< Levitiko 7 >

1 “‘Malamulo a nsembe yopepesera kupalamula imene ndi nsembe yopatulika kwambiri ndi awa:
and this instruction [the] guilt (offering) holiness holiness he/she/it
2 Nsembe yopepesera machimo iziphedwa pamalo pomwe amaphera nsembe yopsereza ndipo awaze magazi ake mbali zonse za guwa.
in/on/with place which to slaughter [obj] [the] burnt offering to slaughter [obj] [the] guilt (offering) and [obj] blood his to scatter upon [the] altar around: side
3 Tsono apereke mafuta ake onse: mchira wamafuta ndi mafuta amene amakuta matumbo.
and [obj] all fat his to present: bring from him [obj] [the] fat tail and [obj] [the] fat [the] to cover [obj] [the] entrails: inner parts
4 Aperekenso impsyo ziwiri, mafuta ake pamodzi ndi mafuta onse amene ali chamʼchiwuno, ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi.
and [obj] two [the] kidney and [obj] [the] fat which upon them which upon [the] loin and [obj] [the] lobe upon [the] liver upon [the] kidney to turn aside: remove her
5 Wansembe azitenthe pa guwa kuti zikhale nsembe yotentha pa moto, yoperekedwa kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo lopalamula.
and to offer: burn [obj] them [the] priest [the] altar [to] food offering to/for LORD guilt (offering) he/she/it
6 Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kudyako nsembeyo koma adyere ku malo opatulika. Imeneyi ndi nsembe yopatulika kwambiri.
all male in/on/with priest to eat him in/on/with place holy to eat holiness holiness he/she/it
7 “‘Nsembe yopepesera tchimo lopalamula ndi yofanana ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo. Ndipo nsembe ziwiri zonsezi zili ndi lamulo limodzi lokha. Wansembe amene wachita mwambo wa nsembe yopepesera machimo a kupalamula atenge nyamayo ngati yake.
like/as sin: sin offering like/as guilt (offering) instruction one to/for them [the] priest which to atone in/on/with him to/for him to be
8 Wansembe wopereka nsembe yopsereza ya munthu wina aliyense, atenge chikopa cha nsembe yopserezayo kuti chikhale chake.
and [the] priest [the] to present: bring [obj] burnt offering man: anyone skin [the] burnt offering which to present: bring to/for priest to/for him to be
9 Chopereka chilichonse cha chakudya chophika mu uvuni kapena chokazinga mu mʼphika kapena mu chiwaya ndi cha wansembe amene wapereka nsembezo.
and all offering which to bake in/on/with oven and all to make in/on/with pan and upon griddle to/for priest [the] to present: bring [obj] her to/for him to be
10 Ndipo chopereka china chilichonse cha chakudya chosakaniza ndi mafuta kapena chowuma, chikhale cha ana onse a Aaroni ndipo anawo achigawane mofanana.
and all offering to mix in/on/with oil and dry to/for all son: child Aaron to be man: anyone like/as brother: compatriot his
11 “‘Malamulo a nsembe ya chiyanjano imene munthu angathe kupereka kwa Yehova ndi awa:
and this instruction sacrifice [the] peace offering which to present: bring to/for LORD
12 “‘Ngati munthuyo apereka chifukwa cha kuthokoza, apereke nsembeyo pamodzi ndi makeke wopanda yisiti, osakaniza ndi mafuta; timitanda ta buledi wopanda yisiti, topyapyala, topaka mafuta, ndiponso makeke a ufa wosalala wophikidwa bwino, wosakaniza ndi mafuta.
if upon thanksgiving to present: bring him and to present: bring upon sacrifice [the] thanksgiving bun unleavened bread to mix in/on/with oil and flatbread unleavened bread to anoint in/on/with oil and fine flour to stir bun to mix in/on/with oil
13 Pamodzi ndi nsembe yachiyanjano yothokozerayo abwerenso ndi makeke opangidwa ndi yisiti ngati chopereka chake.
upon bun food: bread leaven to present: bring offering his upon sacrifice thanksgiving peace offering his
14 Munthuyo atenge mtanda umodzi pa mtanda wa buledi wa mtundu uliwonse kuti ukhale nsembe yopereka kwa Yehova. Tsono mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe yachiyanjano.
and to present: bring from him one from all offering contribution to/for LORD to/for priest [the] to scatter [obj] blood [the] peace offering to/for him to be
15 Nyama ya nsembe yachiyanjano yothokozera idyedwe pa tsiku lomwe nsembeyo yaperekedwa ndipo isatsaleko mpaka mmawa.
and flesh sacrifice thanksgiving peace offering his in/on/with day offering his to eat not to rest from him till morning
16 “‘Koma ngati nsembe yakeyo apereka chifukwa cha lumbiro kapena mwaufulu, nsembeyo adye tsiku lomwe yaperekedwalo. Koma yotsala angathe kuyidya mmawa mwake.
and if vow or voluntariness sacrifice offering his in/on/with day to present: bring he [obj] sacrifice his to eat and from morrow and [the] to remain from him to eat
17 Ngati nyama ina ya nsembe yatsalabe mpaka tsiku lachitatu, imeneyo itenthedwe pa moto.
and [the] to remain from flesh [the] sacrifice in/on/with day [the] third in/on/with fire to burn
18 Ngati munthu adya nyama yachiyanjano pa tsiku lachitatu, nsembeyo sidzalandiridwa. Amene wayipereka nsembeyo Mulungu sadzamulandira ndipo nsembeyo idzakhala yonyansa pamaso pa Mulungu, yosamupindulira kanthu woperekayo.
and if to eat to eat from flesh sacrifice peace offering his in/on/with day [the] third not to accept [the] to present: bring [obj] him not to devise: count to/for him refuse to be and [the] soul: myself [the] to eat from him iniquity: crime her to lift: guilt
19 “‘Nyama imene yakhudza chilichonse chodetsedwa, munthu asayidye, koma itenthedwe pa moto. Aliyense amene ali woyeretsedwa angathe kudya nyama inayo.
and [the] flesh which to touch in/on/with all unclean not to eat in/on/with fire to burn and [the] flesh all pure to eat flesh
20 Koma ngati munthu wina amene ndi wosayeretsedwa adya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.
and [the] soul: person which to eat flesh from sacrifice [the] peace offering which to/for LORD and uncleanness his upon him and to cut: eliminate [the] soul: person [the] he/she/it from kinsman her
21 Ndipo ngati munthu wina akhudza chinthu chodetsedwa, kaya chonyansa cha munthu kapena cha nyama, kapenanso chonyansa china chilichonse, ndipo kenaka nʼkudya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati anthu a mtundu wake.’”
and soul: person for to touch in/on/with all unclean in/on/with uncleanness man or in/on/with animal unclean or in/on/with all detestation unclean and to eat from flesh sacrifice [the] peace offering which to/for LORD and to cut: eliminate [the] soul: person [the] he/she/it from kinsman her
22 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
and to speak: speak LORD to(wards) Moses to/for to say
23 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Musadye mafuta a ngʼombe, nkhosa kapenanso mbuzi.
to speak: speak to(wards) son: descendant/people Israel to/for to say all fat cattle and sheep and goat not to eat
24 Mafuta a nyama yofa yokha, kapena mafuta a nyama yophedwa ndi zirombo akhoza kuwagwiritsa ntchito iliyonse, koma inu musadye mafuta amenewo.
and fat carcass and fat torn animal to make: do to/for all work and to eat not to eat him
25 Pakuti munthu wakudya mafuta a nyama yoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe yotentha pa moto, ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
for all to eat fat from [the] animal which to present: bring from her food offering to/for LORD and to cut: eliminate [the] soul: person [the] to eat from kinsman her
26 Ndipo kulikonse kumene mukakhale musakadye magazi a mbalame iliyonse kapena magazi a nyama iliyonse.
and all blood not to eat in/on/with all seat your to/for bird and to/for animal
27 Ngati munthu aliyense adya magazi achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.’”
all soul: myself which to eat all blood and to cut: eliminate [the] soul: person [the] he/she/it from kinsman her
28 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
and to speak: speak LORD to(wards) Moses to/for to say
29 “Awuze Aisraeli kuti, Aliyense amene apereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, abwere ndi gawo la nsembeyo kwa Yehova.
to speak: speak to(wards) son: descendant/people Israel to/for to say [the] to present: bring [obj] sacrifice peace offering his to/for LORD to come (in): bring [obj] offering his to/for LORD from sacrifice peace offering his
30 Atenge ndi manja ake zigawo za chopereka zoyenera kuzitentha pa moto ngati chopereka kwa Yehova. Abweretse mafuta, pamodzi ndi chidale chomwe, ndipo chidalecho achiweyule kuti chikhale chopereka choweyula kwa Yehova.
hand his to come (in): bring [obj] food offering LORD [obj] [the] fat upon [the] breast to come (in): bring him [obj] [the] breast to/for to wave [obj] him wave offering to/for face: before LORD
31 Wansembe atenthe mafutawo pa guwa koma chidalecho chikhale cha Aaroni ndi ana ake.
and to offer: burn [the] priest [obj] [the] fat [the] altar [to] and to be [the] breast to/for Aaron and to/for son: child his
32 Mumupatse wansembe ntchafu ya kumanja ya nsembe yanu yachiyanjano kuti ikhale chopereka chanu kwa iye.
and [obj] leg [the] right to give: give contribution to/for priest from sacrifice peace offering your
33 Mwana wa Aaroni amene amapereka magazi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano, adzitenga ntchafu ya kumanja kukhala gawo lake.
[the] to present: bring [obj] blood [the] peace offering and [obj] [the] fat from son: child Aaron to/for him to be leg [the] right to/for portion
34 Choncho pa zopereka zachiyanjano za Aisraeli, Ine ndatengapo chidale chomwe amaweyula ndi ntchafu zimene amapereka nsembe ndipo ndazipereka kwa wansembe Aaroni ndi ana ake. Izi ndizo gawo lawo nthawi zonse pa zopereka za Aisraeli.”
for [obj] breast [the] wave offering and [obj] leg [the] contribution to take: take from with son: descendant/people Israel from sacrifice peace offering their and to give: give [obj] them to/for Aaron [the] priest and to/for son: child his to/for statute: portion forever: enduring from with son: descendant/people Israel
35 Zimenezi ndi chigawo cha Aaroni ndi ana ake chotapidwa pa zopereka kwa Yehova zoti zitenthedwe pa moto zimene zinaperekedwa pa tsiku limene anapatulidwa kuti akhale ansembe otumikira Yehova.
this anointing Aaron and anointing son: child his from food offering LORD in/on/with day to present: bring [obj] them to/for to minister to/for LORD
36 Yehova ndiye analamulira kuti pa zopereka za Aisraeli azitapapo zimenezi ndi kuwapatsa ansembe ngati gawo lawo. Yehovayo analamula zimenezi pa tsiku limene ansembewo anapatulidwa ndipo anachikhazikitsa ngati lamulo la nthawi zonse.
which to command LORD to/for to give: give to/for them in/on/with day to anoint he [obj] them from with son: descendant/people Israel statute forever: enduring to/for generation their
37 Awa ndi malamulo a nsembe izi: nsembe yopsereza, nsembe yachakudya, nsembe yopepesera machimo, nsembe yopepesera kupalamula, nsembe ya mwambo wodzoza ndi nsembe yachiyanjano.
this [the] instruction to/for burnt offering to/for offering and to/for sin: sin offering and to/for guilt (offering) and to/for setting and to/for sacrifice [the] peace offering
38 Malamulo amenewa Yehova anapereka kwa Mose pa Phiri la Sinai pa tsiku limene Yehova analamulira Aisraeli kuti abwere ndi zopereka za kwa Yehova, ku chipululu cha Sinai kuja.
which to command LORD [obj] Moses in/on/with mountain: mount Sinai in/on/with day to command he [obj] son: descendant/people Israel to/for to present: bring [obj] offering their to/for LORD in/on/with Wilderness (of Sinai) Sinai

< Levitiko 7 >