< Levitiko 6 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
The Lord spoke to Moses, saying:
2 “Ngati munthu wina aliyense achimwa, nachita zinthu mosakhulupirika kwa Yehova chifukwa cha kunyenga mnzake pokana kumubwezera zimene anamusungitsa, kapena kumubera kapenanso kumulanda,
The soul who will have sinned, and, despising the Lord, will have denied to his neighbor the deposit which he had entrusted to his safekeeping, or who will have extorted anything by force, or who will have made a false accusation,
3 kapena ndi kunama kuti sanatole chinthu chimene chinatayika, kapena kulumbira mwachinyengo pa chinthu chilichonse chimene munthu akachita amachimwa nacho,
or who will have found a lost thing and then also withheld it by swearing falsely, or who will have done any other of the many things by which men usually sin:
4 ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kubweza zimene anabazo, zimene analanda mwachinyengozo, zimene anamusungitsazo, zimene anatolazo
being convicted of the offense, he shall restore
5 kapena zimene analumbira monyengazo. Pa tsiku limene apezeke kuti wapalamuladi, iye ayenera kumubwezera mwini wake zinthu zonsezi ndi kuwonjezerapo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse.
all that he wanted to obtain by fraud, the whole plus an additional fifth part, to the owner against whom he brought the damage.
6 Pambuyo pake apereke kwa Yehova nsembe yopalamula. Nsembe yake ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake wogwirizana ndi nsembe yopepesera machimo.
Then, on behalf of his sin, he shall offer an immaculate ram from the flock, and he shall give it to the priest, according to the estimation and measure of the offense.
7 Kenaka wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo pamaso pa Yehova, ndipo adzakhululukidwa chilichonse chomwe anachita kuti akhale wopalamula.”
And he shall pray for him in the sight of the Lord, and he shall be released from any one of those things that he did when he sinned.
8 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke to Moses, saying:
9 “Lamula Aaroni ndi ana ake kuti, ‘Lamulo la nsembe yopsereza ndi ili: Nsembe yopserezayo izikhala pa moto pa guwa usiku wonse mpaka mmawa, ndipo moto wa paguwapo uzikhala ukuyaka nthawi zonse.
Instruct Aaron and his sons: This is the law of a holocaust. It shall be burned upon the altar, all night until morning. The fire shall be from the same altar.
10 Tsono wansembe avale mkanjo wake wa nsalu yofewa ndi yosalala. Mʼkati avalenso kabudula wofewa, wosalala. Pambuyo pake atenge phulusa la nyama imene yatenthedwa pa guwa lansembe paja ndi kulithira pambali pa guwa lomwelo.
The priest shall be vested with the tunic and the linen undergarments. And he shall take up the ashes of that which the devouring fire has consumed, and, placing them next to the altar,
11 Akatero avule zovala zakezo ndi kuvala zovala zina. Kenaka atulutse phulusalo ndi kukaliyika pa malo woyeretsedwa kunja kwa chithando.
he shall strip off his former vestments, and being clothed with others, he shall carry them beyond the camp, and he shall cause them to be consumed, even to glowing embers, in a very clean place.
12 Moto wa pa guwa uzikhala ukuyaka nthawi zonse, usamazime. Mmawa uliwonse wansembe aziwonjezerapo nkhuni pa motopo ndi kukonza nsembe yopsereza, ndi kutentha mafuta a nsembe yachiyanjano pamenepo.
But the fire on the altar shall burn always, for the priest shall nourish it by placing wood under it each day in the morning. And, laying down the holocaust, he shall burn the fat of the peace offerings upon it.
13 Moto uzikhala ukuyaka pa guwa nthawi zonse ndipo usazimepo.
This is the perpetual fire which shall never fail upon the altar.
14 “‘Lamulo la nsembe yachakudya ndi ili: ana a Aaroni azibwera nayo nsembeyo pamaso pa Yehova, patsogolo pa guwa.
This is the law of the sacrifice and the libations, which the sons of Aaron shall offer in the sight of the Lord, and before the altar.
15 Wansembe mmodzi atapeko dzanja limodzi la ufa wosalala wa nsembe yachakudya ija kuti ukhala ufa wachikumbutso ndi mafuta pamodzi ndi lubani yense amene ali pa nsembe ya chakudyacho, ndipo azitenthe pa guwa kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse kuti zikhale nsembe ya fungo lokomera Yehova.
The priest shall take a handful of fine wheat flour, which has been sprinkled with oil, and all the frankincense, which has been placed upon the flour, and he shall burn it upon the altar as a memorial of most sweet odor to the Lord.
16 Aaroni ndi ana ake azidya zimene zatsala koma azidya zopanda yisiti ku malo wopatulika, ku bwalo la tenti ya msonkhano.
And the remaining portion of the flour, Aaron shall eat with his sons, without leaven. And he shall eat it in the holy place, in the atrium of the tabernacle.
17 Poziphika asathire yisiti. Ndawapatsa zotsalazo kuti zikhale gawo lawo la nsembe zanga zopsereza. Zonsezi ndi zopatulika kwambiri monga nsembe yopepesera tchimo ndiponso nsembe yopepesera machimo.
Yet for this reason, it shall not be leavened, because part of it is offered as an incense of the Lord. The Holy of holies shall it be, just as what is offered on behalf of sin and of transgression.
18 Mwana aliyense wamwamuna wa Aaroni azidyako za nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova. Ndi gawo lake lokhazikika la chopereka chopsereza kwa Yehova pa mibado yanu yonse. Chilichonse chimene chidzakhudza nsembezo chidzakhala chopatulika.’”
Only the males of the stock of Aaron shall eat it. This shall be an everlasting ordinance in your generations concerning the sacrifices of the Lord. All who will touch these shall be sanctified.
19 Yehova anawuzanso Mose kuti,
And the Lord spoke to Moses, saying:
20 “Nsembe imene Aaroni ndi ana ake ayenera kupereka kwa Yehova pa tsiku limene wansembe akudzozedwa ndi iyi: ufa wosalala kilogalamu imodzi ngati chopereka chachakudya cha nthawi zonse. Azipereka theka limodzi mmawa ndipo theka linalo madzulo.
This is the oblation of Aaron and of his sons, which they must offer to the Lord in the day of their anointing. They shall offer a tenth part of an ephah of fine wheat flour as a perpetual sacrifice, half of it in the morning, and half of it in the evening.
21 Ipangidwe ndi mafuta pa chiwaya ndipo ubwere nayo ili yosakaniza bwino, yophikidwa mitandamitanda monga amachitira ndi nsembe yachakudya. Iphikidwe moti itulutse fungo lokomera Yehova.
It shall be sprinkled with oil and fried in a frying pan. Then it shall be offered hot, as a most sweet odor to the Lord,
22 Mwana wa fuko la Aaroni amene adzadzozedwe kukhala wansembe kulowa mʼmalo mwa Aaroni ndiye amene azidzakonza ndi kupereka nsembeyi kwa Yehova nthawi zonse monga kunalembedwera.
by the priest who by law succeeds his father. And it shall be entirely burned on the altar.
23 Nsembe iliyonse yachakudya ya wansembe izitenthedwa kwathunthu, isamadyedwe.”
For every sacrifice of the priest shall be consumed by fire; neither shall anyone eat from it.
24 Yehova anawuza Mose kuti
Then the Lord spoke to Moses, saying:
25 “Uza Aaroni ndi ana ake kuti, ‘Malamulo a nsembe ya tchimo ndi awa: Nsembeyi iziphedwa pamaso pa Yehova pa malo pamene mumaphera nsembe yopsereza popeza ndi nsembe yopatulika.
Say to Aaron and his sons: This is the law of the victim for sin. In the place where the holocaust is offered, it shall be immolated in the sight of the Lord. It is the Holy of holies.
26 Wansembe amene apereke nsembeyi adyere ku malo wopatulika ndiye kuti mʼbwalo la tenti ya msonkhano.
The priest who offers it shall eat it in the holy place, in the atrium of the tabernacle.
27 Chilichonse chimene chidzakhudza nsembeyo chidzakhala chopatulika, ndipo ngati magazi ake agwera pa chovala, muchape chovalacho pa malo opatulika.
Whatever will touch its flesh shall be sanctified. If a garment will be sprinkled with its blood, it shall be washed in a holy place.
28 Mʼphika wadothi umene aphikira nyamayo auphwanye. Koma ngati yaphikidwa mu mʼphika wa mkuwa, awukweche ndi kuwutsukuluza ndi madzi.
Then the earthen vessel, in which it was soaked, shall be broken. But if the vessel will be of brass, it shall be scoured and washed with water.
29 Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kuyidya popeza nsembeyi ndi yopatulika kwambiri.
Every male of priestly descent shall feed on its flesh, because it is the Holy of holies.
30 Koma nsembe yopepesera tchimo imene magazi ake amabwera nawo mu tenti ya msonkhano kudzachita mwambo wopepesera tchimo ku malo opatulika isadyedwe, mʼmalo mwake itenthedwe.’”
For the victim that is slain for sin, whose blood is carried into the tabernacle of the testimony, for expiation in the Sanctuary, shall not be eaten, but it shall be consumed by fire.

< Levitiko 6 >