< Levitiko 5 >

1 “‘Ngati munthu anayitanidwa ku bwalo kuti akachitire umboni pa zimene anaziona kapena kuzimva koma iye nʼkukana kuchitira umboni, munthu ameneyo wachimwa ndipo ayenera kulangidwa.
Кынд чинева, фиинд пус суб журэмынт ка мартор, ва пэкэтуи неспунынд че а вэзут сау че штие ши ва кэдя астфел суб винэ
2 “‘Munthu akakhudza chinthu chilichonse chodetsedwa, monga nyama yakufa ya mʼthengo, kapena chiweto chakufa kapenanso chokwawa chakufa, ngakhale iyeyo wachikhudza mosadziwa, wasanduka wodetsedwa ndipo wachimwa.
сау кынд чинева, фэрэ сэ штие, се ва атинӂе де чева некурат, фие де хойтул уней фяре сэлбатиче некурате, фие де хойтул уней вите де касэ некурате, фие де хойтул уней тырытоаре некурате, ши ва бэга апой де сямэ ши се ва фаче астфел виноват
3 “‘Munthu akakhudza choyipitsa munthu cha mtundu uliwonse, ndipo pochikhudzapo ndi kuyipitsidwa nacho mosadziwa, munthuyo adzakhala wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
сау кынд чинева, фэрэ сэ я сяма, се ва атинӂе де врео спуркэчуне оменяскэ, де орьче спуркэчуне каре фаче пе чинева некурат, ши ва бэга де сямэ май тырзиу ши се ва фаче астфел виноват
4 “‘Munthu akalumbira mofulumira kapena mosasamala kuti adzachita chinthu, choyipa kapena chabwino, ngakhale kuti wachita izi mosadziwa kuti nʼkulakwa, pamene wazindira kulakwa kwake, iye adzakhalabe wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
сау кынд чинева, ворбинд ку ушуринцэ, журэ кэ аре сэ факэ чева рэу сау бине ши, небэгынд де сямэ ла ынчепут, багэ де сямэ май тырзиу ши се ва фаче астфел виноват –
5 “‘Pamene munthu wazindikira kuti wachimwa motere, awulule tchimo limene wachitalo.
кынд чинева деч се ва фаче виноват де унул дин ачесте лукрурь, требуе сэ-шь мэртурисяскэ пэкатул.
6 Pambuyo pake, munthuyo abwere kwa Yehova ndi mwana wankhosa wamkazi kapena mbuzi kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo ndipo wansembe achite mwambo wopepesera tchimo lomwe wachitalo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo.
Апой, сэ адукэ луй Думнезеу ка жертфэ де винэ пентру пэкатул пе каре л-а фэкут о парте фемеяскэ дин турмэ, ши ануме о оае сау о капрэ, ка жертфэ испэшитоаре, ши преотул сэ факэ пентру ел испэширя пэкатулуй луй.
7 “‘Ngati munthuyo alibe mwana wankhosa, abweretse njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri kwa Yehova ngati chopereka chopepesera tchimo lake. Imodzi ikhale nsembe yopepesera tchimo, ndipo inayo ikhale nsembe yopsereza.
Дакэ ну ва путя сэ адукэ о оае сау о капрэ, сэ адукэ Домнулуй ка жертфэ де винэ пентру пэкатул луй доуэ туртуреле сау дой пуй де порумбел, унул ка жертфэ де испэшире, яр челэлалт ка ардере-де-тот.
8 Tsono abwere nazo kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayambe wapereka mbalame imodzi ngati yopepesera tchimo. Apotole khosi koma osayidula mutu,
Сэ ле адукэ преотулуй, каре ва жертфи ынтый пе чя каре аре сэ служяскэ дрепт жертфэ де испэшире. Преотул сэ-й фрынгэ ку унгия капул де ла грумаз, фэрэ сэ-л деспартэ,
9 kenaka awaze magazi a chopereka chopepesera tchimocho mʼmbali mwa guwa. Magazi ena onse awathire pa tsinde la guwa. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
сэ стропяскэ ун перете ал алтарулуй ку сынӂеле жертфей де испэшире, яр челэлалт сынӂе сэ-л стоаркэ ла пичоареле алтарулуй – ачаста есте о жертфэ де испэшире.
10 Pambuyo pake wansembe apereke mbalame inayo kuti ikhale chopereka chopsereza potsata mwambo wake. Wansembe atatha kupereka nsembe yopepesera tchimo limene munthu uja wachita, wochimwayo adzakhululukidwa.
Чялалтэ пасэре с-о прегэтяскэ дрепт ардере-де-тот, дупэ рындуелиле ашезате. Астфел ва фаче преотул пентру омул ачеста испэширя пэкатулуй пе каре л-а фэкут, ши и се ва ерта.
11 “‘Koma ngati munthuyo alibe njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri, abweretse ufa wosalala wokwanira kilogalamu imodzi kuti ukhale chopereka chopepesera tchimo limene wachita. Asathiremo mafuta kapena lubani chifukwa ndi chopereka chopepesera tchimo.
Дакэ ну поате сэ адукэ нич доуэ туртуреле сау дой пуй де порумбел, сэ адукэ пентру пэкатул луй, ка дар, а зечя парте динтр-о ефэ де флоаря фэиний, ши ануме ка дар де испэшире; сэ ну пунэ унтделемн пе еа ши сэ ну адауӂе нич тэмые, кэч есте ун дар де испэшире.
12 Abweretse ufawo kwa wansembe ndipo wansembeyo atapeko dzanja limodzi kuti ukhale ufa wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa pamodzi ndi chopereka chopsereza kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
С-о адукэ ла преот, ши преотул сэ я дин еа ун пумн плин, ка адучере аминте, ши с-о ардэ пе алтар, ка ши пе даруриле де мынкаре мистуите де фок ынаинтя Домнулуй – ачеста есте ун дар де испэшире.
13 Umu ndi mmene wansembe adzachitire mwambo wopepesera machimo ena aliwonse amene munthu wachita, ndipo munthuyo adzakhululukidwa. Zopereka zonse zotsala zidzakhala za wansembeyo monga momwe amachitira ndi chopereka chachakudya.’”
Астфел ва фаче преотул пентру омул ачела испэширя пэкатулуй пе каре л-а фэкут фацэ де унул дин ачесте лукрурь, ши и се ва ерта. Чялалтэ парте каре ва май рэмыне дин дарул ачеста сэ фие а преотулуй, ка ши ла дарул де мынкаре.’”
14 Yehova anawuza Mose kuti,
Домнул а ворбит луй Мойсе ши а зис:
15 “Munthu akachita zinthu mosakhulupirika, nachimwa mosadziwa posapereka zinthu zopatulika zofunika kwa Yehova, munthuyo apereke kwa Yehova nsembe yopepesera machimo ake. Nsembeyo ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale wokwana masekeli oyenera a siliva pakawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu. Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula.
„Кынд чинева ва фаче о нелеӂюире ши ва пэкэтуи фэрэ вое фацэ де лукруриле ынкинате Домнулуй, сэ адукэ Домнулуй ка жертфэ де винэ пентру пэкатул луй ун бербек фэрэ кусур дин турмэ, дупэ прецуиря та, ын сикли де арӂинт, дупэ сиклул Сфынтулуй Локаш.
16 Munthuyo ayenera kubweza zinthu zopatulika zimene sanaperekezo. Awonjezepo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse ndi kuzipereka zonsezo kwa wansembe amene adzachita mwambo wopepesera machimo a munthuyo, popereka nkhosa yayimuna ija ngati nsembe yopepesera ndipo wochimwayo adzakhululukidwa.
Сэ май адауӂе а чинчя парте ла прецул лукрулуй ку каре а ыншелат Сфынтул Локаш ши сэ-л ынкрединцезе преотулуй. Ши преотул сэ факэ испэшире пентру ел ку бербекул адус ка жертфэ пентру винэ, ши и се ва ерта.
17 “Ngati munthu wachimwa mosadziwa pochita chilichonse chimene Yehova salola, munthuyo ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kulangidwa.
Кынд ва пэкэтуи чинева фэкынд, фэрэ сэ штие, ымпотрива унея дин порунчиле Домнулуй лукрурь каре ну требуе фэкуте ши се ва фаче виноват, пуртынду-шь астфел вина,
18 Abwere kwa wansembe ndi chopereka chopepesera kupalamula kwake. Chopereka chikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale woyenera nsembe yopepesera kupalamula kumene anachimwa mosadziwako, ndipo munthuyo adzakhululukidwa.
сэ адукэ преотулуй ка жертфэ пентру винэ ун бербек фэрэ кусур, луат дин турмэ, дупэ прецуиря та. Ши преотул сэ факэ пентру ел испэширя грешелий пе каре а фэкут-о фэрэ сэ штие, ши и се ва ерта.
19 Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula popeza munthuyo wapezeka wolakwa pamaso pa Yehova.”
Ачаста есте о жертфэ пентру винэ. Омул ачеста се фэкусе виноват фацэ де Домнул.”

< Levitiko 5 >