< Levitiko 5 >

1 “‘Ngati munthu anayitanidwa ku bwalo kuti akachitire umboni pa zimene anaziona kapena kuzimva koma iye nʼkukana kuchitira umboni, munthu ameneyo wachimwa ndipo ayenera kulangidwa.
Gdyby ktoś zgrzeszył przez to, że usłyszał przekleństwo i był [tego] świadkiem lub widział czy dowiedział się o tym, a tego nie oznajmił, będzie obciążony nieprawością;
2 “‘Munthu akakhudza chinthu chilichonse chodetsedwa, monga nyama yakufa ya mʼthengo, kapena chiweto chakufa kapenanso chokwawa chakufa, ngakhale iyeyo wachikhudza mosadziwa, wasanduka wodetsedwa ndipo wachimwa.
Albo jeśli ktoś dotknął czegoś nieczystego, czy to padliny nieczystego zwierzęcia, czy padliny nieczystego bydlęcia, czy padliny nieczystego zwierzęcia pełzającego, a nie jest tego świadomy, i tak będzie nieczysty i winny;
3 “‘Munthu akakhudza choyipitsa munthu cha mtundu uliwonse, ndipo pochikhudzapo ndi kuyipitsidwa nacho mosadziwa, munthuyo adzakhala wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
Lub jeśli ktoś dotknął jakiejkolwiek nieczystości ludzkiej, przez którą stanie się nieczysty, a nie jest tego świadomy, a potem się o tym dowie, będzie winny;
4 “‘Munthu akalumbira mofulumira kapena mosasamala kuti adzachita chinthu, choyipa kapena chabwino, ngakhale kuti wachita izi mosadziwa kuti nʼkulakwa, pamene wazindira kulakwa kwake, iye adzakhalabe wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
Albo jeśli ktoś przysiągł, mówiąc wargami, że źle lub dobrze uczyni w czymkolwiek, co ów człowiek powie w przysiędze, a nie jest tego świadomy, lecz [potem] sobie uświadomi, będzie winny w jednej z tych rzeczy.
5 “‘Pamene munthu wazindikira kuti wachimwa motere, awulule tchimo limene wachitalo.
Jeśli więc jest winny jednej z tych rzeczy, ma wyznać swój grzech;
6 Pambuyo pake, munthuyo abwere kwa Yehova ndi mwana wankhosa wamkazi kapena mbuzi kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo ndipo wansembe achite mwambo wopepesera tchimo lomwe wachitalo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo.
I przyprowadzi PANU ofiarę za przewinienie z powodu swego grzechu, który popełnił: samicę z trzody, owcę albo kozę na ofiarę za grzech, a kapłan dokona za niego przebłagania za jego grzech.
7 “‘Ngati munthuyo alibe mwana wankhosa, abweretse njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri kwa Yehova ngati chopereka chopepesera tchimo lake. Imodzi ikhale nsembe yopepesera tchimo, ndipo inayo ikhale nsembe yopsereza.
A jeśli nie stać go na owcę, niech przyniesie PANU jako ofiarę za swoje przewinienie, które popełnił, dwie synogarlice lub dwa młode gołębie: jednego na ofiarę za grzech, a drugiego na całopalenie;
8 Tsono abwere nazo kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayambe wapereka mbalame imodzi ngati yopepesera tchimo. Apotole khosi koma osayidula mutu,
I przyniesie je do kapłana, a [on] najpierw złoży [to], co ma być na ofiarę za grzech, i ukręci jego głowę przy szyi, ale jej nie oddzieli.
9 kenaka awaze magazi a chopereka chopepesera tchimocho mʼmbali mwa guwa. Magazi ena onse awathire pa tsinde la guwa. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
I pokropi krwią tej ofiary za grzech ścianę ołtarza, a resztę krwi wyciśnie u podstawy ołtarza. To [jest] ofiara za grzech.
10 Pambuyo pake wansembe apereke mbalame inayo kuti ikhale chopereka chopsereza potsata mwambo wake. Wansembe atatha kupereka nsembe yopepesera tchimo limene munthu uja wachita, wochimwayo adzakhululukidwa.
Drugiego zaś złoży jako całopalenie według przepisu. W ten sposób kapłan dokona za niego przebłagania za jego grzech, który popełnił, i będzie mu przebaczony.
11 “‘Koma ngati munthuyo alibe njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri, abweretse ufa wosalala wokwanira kilogalamu imodzi kuti ukhale chopereka chopepesera tchimo limene wachita. Asathiremo mafuta kapena lubani chifukwa ndi chopereka chopepesera tchimo.
A jeśli nie stać go na dwie synogarlice lub dwa młode gołębie, niech ten, który zgrzeszył, przyniesie na swoją ofiarę dziesiątą część efy mąki pszennej na ofiarę za swój grzech. Nie naleje jednak na nią oliwy ani nie położy na nią kadzidła, gdyż jest to ofiara za grzech.
12 Abweretse ufawo kwa wansembe ndipo wansembeyo atapeko dzanja limodzi kuti ukhale ufa wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa pamodzi ndi chopereka chopsereza kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
Przyniesie ją do kapłana, a kapłan nabierze z niej pełną garść jako pamiątkę i spali ją na ołtarzu na ofiarach całopalnych dla PANA. To [jest] ofiara za grzech.
13 Umu ndi mmene wansembe adzachitire mwambo wopepesera machimo ena aliwonse amene munthu wachita, ndipo munthuyo adzakhululukidwa. Zopereka zonse zotsala zidzakhala za wansembeyo monga momwe amachitira ndi chopereka chachakudya.’”
I kapłan dokona za niego przebłagania za jego grzech, który popełnił w jednej z tych spraw, i będzie mu przebaczony. [Reszta] zaś będzie dla kapłana, jak przy ofierze pokarmowej.
14 Yehova anawuza Mose kuti,
PAN powiedział jeszcze do Mojżesza:
15 “Munthu akachita zinthu mosakhulupirika, nachimwa mosadziwa posapereka zinthu zopatulika zofunika kwa Yehova, munthuyo apereke kwa Yehova nsembe yopepesera machimo ake. Nsembeyo ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale wokwana masekeli oyenera a siliva pakawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu. Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula.
Jeśli ktoś popełni przewinienie i zgrzeszy nieświadomie [przy] rzeczach poświęconych PANU, to przyprowadzi PANU jako ofiarę za swoje przewinienie barana bez skazy z trzody oraz twoje oszacowanie w syklach srebra według sykla świątynnego na ofiarę za przewinienie.
16 Munthuyo ayenera kubweza zinthu zopatulika zimene sanaperekezo. Awonjezepo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse ndi kuzipereka zonsezo kwa wansembe amene adzachita mwambo wopepesera machimo a munthuyo, popereka nkhosa yayimuna ija ngati nsembe yopepesera ndipo wochimwayo adzakhululukidwa.
I odda kapłanowi za to, czym przewinił przy rzeczach poświęconych, i dołoży do tego jedną piątą. I kapłan dokona za niego przebłagania baranem, będącym ofiarą za przewinienie, a będzie mu przebaczone.
17 “Ngati munthu wachimwa mosadziwa pochita chilichonse chimene Yehova salola, munthuyo ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kulangidwa.
Jeśli ktoś zgrzeszy i przekroczy nieświadomie którekolwiek z przykazań PANA, czyniąc to, czego nie wolno, stanie się winny i będzie obciążony nieprawością.
18 Abwere kwa wansembe ndi chopereka chopepesera kupalamula kwake. Chopereka chikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale woyenera nsembe yopepesera kupalamula kumene anachimwa mosadziwako, ndipo munthuyo adzakhululukidwa.
Przyprowadzi do kapłana barana z trzody bez skazy według twojego oszacowania na ofiarę za przewinienie. A kapłan dokona za niego przebłagania za jego uchybienie, którego nieświadomie się dopuścił, i będzie mu przebaczone.
19 Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula popeza munthuyo wapezeka wolakwa pamaso pa Yehova.”
Jest to ofiara za przewinienie, gdyż w istocie zawinił przeciwko PANU.

< Levitiko 5 >