< Levitiko 5 >

1 “‘Ngati munthu anayitanidwa ku bwalo kuti akachitire umboni pa zimene anaziona kapena kuzimva koma iye nʼkukana kuchitira umboni, munthu ameneyo wachimwa ndipo ayenera kulangidwa.
“‘Ngʼato angʼata ma nokwongʼre kata ma notamre mar hulo wach moro mosewinjo kata moseneno, en bende nobed jaketho, kendo nyaka kume mi ochul.
2 “‘Munthu akakhudza chinthu chilichonse chodetsedwa, monga nyama yakufa ya mʼthengo, kapena chiweto chakufa kapenanso chokwawa chakufa, ngakhale iyeyo wachikhudza mosadziwa, wasanduka wodetsedwa ndipo wachimwa.
“‘Kata ka ngʼato omulo gimoro makwero, bed ni en le mar bungu motho kata gik mamol motho, ka ok ongʼeyo, mi ofwenye achien, to enodok jaketho.
3 “‘Munthu akakhudza choyipitsa munthu cha mtundu uliwonse, ndipo pochikhudzapo ndi kuyipitsidwa nacho mosadziwa, munthuyo adzakhala wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
Kata ka orere kuom gimoro makwero moa kuom dhano ka ok ongʼeyo, mi ofwenyo achien, to enodok jaketho.
4 “‘Munthu akalumbira mofulumira kapena mosasamala kuti adzachita chinthu, choyipa kapena chabwino, ngakhale kuti wachita izi mosadziwa kuti nʼkulakwa, pamene wazindira kulakwa kwake, iye adzakhalabe wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
Ka ngʼato ohedhore ma okwongʼore mar timo gimoro, maber kata marach ka ok ongʼeyo, (e wach moro ma ngʼato thoro hedhore ka kwongʼore) mi bangʼe achien ofwenyo, to enodok jaketho.
5 “‘Pamene munthu wazindikira kuti wachimwa motere, awulule tchimo limene wachitalo.
Ka ngʼato angʼata en jaketho e achiel kuom wechegi, to nyaka ohul kaka oseketho,
6 Pambuyo pake, munthuyo abwere kwa Yehova ndi mwana wankhosa wamkazi kapena mbuzi kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo ndipo wansembe achite mwambo wopepesera tchimo lomwe wachitalo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo.
kendo nyaka okel ni Jehova Nyasaye rombo kata diel madhako kaka misango mar golo richo kuom ketho mosetimo; bangʼe jadolo nopwodhnego kethoneno.
7 “‘Ngati munthuyo alibe mwana wankhosa, abweretse njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri kwa Yehova ngati chopereka chopepesera tchimo lake. Imodzi ikhale nsembe yopepesera tchimo, ndipo inayo ikhale nsembe yopsereza.
“‘To ka ok onyal chiwo nyarombo, to nokel akuche odugla ariyo kata nyithi akuru ariyo ni Jehova Nyasaye kuom richo mosetimono. Kuom mano, akuru achiel notimnego misango mar golo richo, to machielo to notimnego misango miwangʼo pep.
8 Tsono abwere nazo kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayambe wapereka mbalame imodzi ngati yopepesera tchimo. Apotole khosi koma osayidula mutu,
Enokelgi ne jadolo, eka jadolo nokwong ochiw winyo mar misango mar golo richo. Enomak wiye komino ngʼute, to ok nochode chuth,
9 kenaka awaze magazi a chopereka chopepesera tchimocho mʼmbali mwa guwa. Magazi ena onse awathire pa tsinde la guwa. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
kendo nokir remb winyono moko e kor kendo mar misango, to remo modongʼ to mondo ochwer e tiend kendono, nikech en misango mar golo richo.
10 Pambuyo pake wansembe apereke mbalame inayo kuti ikhale chopereka chopsereza potsata mwambo wake. Wansembe atatha kupereka nsembe yopepesera tchimo limene munthu uja wachita, wochimwayo adzakhululukidwa.
Jadolo nochiw winyo machielo modongʼ kaka misango miwangʼo pep e yo ma chik dwaro kendo mondo opwodhego kuom richo mosetimo mi nowene.
11 “‘Koma ngati munthuyo alibe njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri, abweretse ufa wosalala wokwanira kilogalamu imodzi kuti ukhale chopereka chopepesera tchimo limene wachita. Asathiremo mafuta kapena lubani chifukwa ndi chopereka chopepesera tchimo.
“‘To ka ok onyal yudo kata mana akuche odugla ariyo kata nyithi akuru ariyo, to chunoni nyaka ochiw kilo angʼwen mar mogo mayom kaka misango mar golo richo. Kik oolie mo kata kik oketie ubani, nikech en misango mar golo richo.
12 Abweretse ufawo kwa wansembe ndipo wansembeyo atapeko dzanja limodzi kuti ukhale ufa wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa pamodzi ndi chopereka chopsereza kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
Eka enokel mogono ni jadolo eka jadolo nojuke sanja kaka rapar, mi nowangʼe e kendo mar misango ewi misengini miwangʼo gi mach ni Jehova Nyasaye. Mano en misango mar golo richo.
13 Umu ndi mmene wansembe adzachitire mwambo wopepesera machimo ena aliwonse amene munthu wachita, ndipo munthuyo adzakhululukidwa. Zopereka zonse zotsala zidzakhala za wansembeyo monga momwe amachitira ndi chopereka chachakudya.’”
Kamano e kaka jadolo notimne pwodhruok kuom richo mosetimo kendo nowene. Mana kaka chiwo mag cham, chiwo mamoko nobed mag jadolo.’”
14 Yehova anawuza Mose kuti,
Jehova Nyasaye nowacho ne Musa niya,
15 “Munthu akachita zinthu mosakhulupirika, nachimwa mosadziwa posapereka zinthu zopatulika zofunika kwa Yehova, munthuyo apereke kwa Yehova nsembe yopepesera machimo ake. Nsembeyo ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale wokwana masekeli oyenera a siliva pakawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu. Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula.
“Ka ngʼato oketho mi otimo richo mar oyiem kaluwore gi chike maler mag Jehova Nyasaye, to nyaka okel ne Jehova Nyasaye im maonge songa kendo man-gi nengo kaluwore gi rapim mar shekel mar kama ler mar lemo. En misango michiwo mar pwodhruok e ketho.
16 Munthuyo ayenera kubweza zinthu zopatulika zimene sanaperekezo. Awonjezepo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse ndi kuzipereka zonsezo kwa wansembe amene adzachita mwambo wopepesera machimo a munthuyo, popereka nkhosa yayimuna ija ngati nsembe yopepesera ndipo wochimwayo adzakhululukidwa.
Nyaka ochul nengo mar gima ne ok ochiwo kaluwore gi chike maler, kendo bende omedi achiel kuom abich mar nengono kendo ochiwe duto ne jadolo, mabiro kawo imno kendo otimnego misango mar pwodhruok e ketho eka nowene richone.
17 “Ngati munthu wachimwa mosadziwa pochita chilichonse chimene Yehova salola, munthuyo ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kulangidwa.
“Ka ngʼata otimo richo kendo otimo gima okwer e chik moro amora mar Jehova Nyasaye, kata obedo ni ok ongʼeye, to en richo kendo en okwane jaketho.
18 Abwere kwa wansembe ndi chopereka chopepesera kupalamula kwake. Chopereka chikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale woyenera nsembe yopepesera kupalamula kumene anachimwa mosadziwako, ndipo munthuyo adzakhululukidwa.
Nyaka okelne jadolo im man-gi nengo kendo maonge songa kaka misango mipwodhogo ketho. Kamano jadolo nopwodhe kuom ketho mosetimo kokia kendo nowene.
19 Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula popeza munthuyo wapezeka wolakwa pamaso pa Yehova.”
En misango mar pwodhruok e ketho; nikech osetimo marach e nyim Jehova Nyasaye.”

< Levitiko 5 >