< Levitiko 4 >

1 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
Још рече Господ Мојсију говорећи:
2 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Munthu akachimwa mosadziwa ndi kuchita chilichonse chimene Yehova walamula kuti asachite, azichita izi:
Кажи синовима Израиљевим, и реци: Ако ко згреши нехотице и учини штагод што је Господ забранио да се не чини,
3 “‘Ngati wansembe wodzozedwa achimwa, ndi kuchimwitsa anthu onse, iyeyu ayenera kupereka mwana wangʼombe wamphongo wopanda chilema chifukwa cha tchimo limene wachitalo. Imeneyi ndi nsembe ya Yehova yopepesera tchimo lake.
Ако свештеник помазани згреши, те буде на грех народу, нека за грех свој који је учинио принесе теле здраво Господу на жртву за грех.
4 Wansembeyo abwere nayo ngʼombeyo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova. Asanjike dzanja lake pamutu pa ngʼombeyo ndipo ayiphe pamaso pa Yehova.
И доведавши теле на врата шатору од сведочанства пред Господа, нека метне руку своју телету на главу, и закоље теле пред Господом.
5 Kenaka wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano.
И нека узме свештеник помазани крви од телета, и унесе је у шатор од састанка.
6 Iye aviyike chala chake mʼmagazi, ndipo awawaze kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova, patsogolo pa katani yotchinga malo wopatulika.
И нека замочи свештеник прст свој у крв, и крвљу седам пута покропи пред Господом пред завесом од светиње.
7 Kenaka wansembe apake magaziwo pa nyanga za guwa lofukizira lubani limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza, limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
И нека помаже свештеник том крвљу рогове олтару, на коме се кади мирисима пред Господом у шатору од састанка, а осталу крв од телета сву нека излије на подножје олтару, на коме се пале жртве на вратима шатора од састанка.
8 Pambuyo pake achotse mafuta onse a ngʼombe yayimuna yopepesera machimoyo: mafuta okuta zamʼkati kapena mafuta onse amʼkatimo.
И нека извади све сало из телета за грех, сало што покрива црева и све сало што је на цревима;
9 Achotsenso ndi kubwera ndi impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta onse ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi ndi impsyo
И оба бубрега, и сало што је на њима и на слабинама, и мрежицу на јетри с бубрезима нека извади,
10 monga momwe amachotsera mafuta a ngʼombe yoperekedwa kuti ikhale chopereka chachiyanjano. Tsono wansembe atenthe zimenezi pa guwa lansembe zopsereza.
Онако како се вади из говечета за жртву захвалну; и нека запали свештеник на олтару, на коме се жртва пали.
11 Koma chikopa cha ngʼombe yayimunayo ndi mnofu wake wonse, pamodzi ndi mutu ndi miyendo, zamʼkati ndi matumbo,
А кожу од телета и све месо с главом и с ногама и црева и балегу,
12 kapena kuti ngʼombe yonse yotsalayo apite nayo kunja kwa msasa ku malo woyeretsedwa, kumene amatayako phulusa ndi kuyitentha pa nkhuni, pa phulusapo.
И цело теле нека изнесе напоље из логора на чисто место, где се просипа пепео, и нека га спали огњем на дрвима; на месту где се просипа пепео нека се спали.
13 “‘Ngati gulu lonse la Aisraeli lichimwa mosadziwa, nachita chomwe ndi choletsedwa ndi Yehova, ngakhale kuti gulu lonselo silikudziwa kuti lachimwa, anthuwo ndi olakwa ndithu.
Ако ли би сав збор синова Израиљевих згрешио нехотице и не би збор знао за то, и учинили би штагод што је Господ забранио да се не чини, те би скривили,
14 Akazindikira tchimo limene achita, gulu lonse lipereke mwana wangʼombe wamphongo kuti akhale chopereka chopepesera tchimo ndipo abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
Кад се дозна за грех који су учинили, онда нека збор принесе теле, жртву за грех, и нека га доведу пред шатор од састанка.
15 Akuluakulu a anthuwo asanjike manja awo pa mutu pa ngʼombe pamaso pa Yehova, ndipo ayiphe pomwepo pamaso pa Yehova.
И старешине од збора нека метну телету на главу руке своје пред Господом, и свештеник нека закоље теле пред Господом.
16 Tsono wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano.
И свештеник помазани нека унесе крви од телета у шатор од састанка,
17 Aviyike chala chake mʼmagaziwo ndi kuwawaza pamaso pa Yehova kasanu ndi kawiri patsogolo pa nsalu yotchinga.
И нека свештеник замочи прст свој у крв, и седам пута покропи пред Господом пред завесом.
18 Pambuyo pake iye apake magaziwo pa nyanga za guwa limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
И том крвљу нека помаже рогове олтару који је пред Господом у шатору од састанка, а осталу крв сву нека излије на подножје олтару на коме се пали жртва, на вратима шатора од састанка.
19 Kenaka achotse mafuta onse a ngʼombeyo ndi kuwatentha pa guwa,
А све сало извадивши из њега нека запали на олтару.
20 ndipo achite ndi ngʼombe yayimunayi monga anachitira ndi ngʼombe yayimuna yopepesera machimo. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera anthu, ndipo machimo awo adzakhululukidwa.
И с тим телетом нека чини онако како чини с телетом за свој грех, тако нека учини с њим; тако ће их свештеник очистити од греха, и опростиће им се.
21 Kenaka atulutse ngʼombeyo kunja kwa msasa ndi kuyitentha monga anatenthera ngʼombe yoyamba ija. Imeneyi ndiyo nsembe yopepesera machimo a gulu lonse.
А теле нека изнесе напоље из логора, и спали га као и прво теле; то је жртва за грех свега збора.
22 “‘Ngati mtsogoleri achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova Mulungu wake, ndiye kuti wapalamula.
Ако ли поглавар згреши, и учини нехотице штагод што је Господ Бог његов забранио да се не чини, те скриви,
23 Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, iye abwere ndi mbuzi yayimuna yopanda chilema kuti ikhale chopereka chake.
Кад дозна за грех свој, који је учинио, тада нека доведе на жртву јаре мушко, здраво.
24 Asanjike dzanja lake pa mutu wa mbuziyo ndi kuyiphera pamalo pamene amaphera zopereka zopsereza pamaso pa Yehova. Ichi ndi chopereka chopepesera tchimo.
И нека метне руку своју јарету на главу, и свештеник нека га закоље где се коље жртва паљеница пред Господом; то је жртва за грех.
25 Pambuyo pake wansembe atengeko magazi a chopereka chopepesera tchimocho ndi chala chake, ndipo awapake pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Athire magazi otsalawo pa tsinde la guwalo.
И нека узме свештеник крви од жртве за грех на прст свој, и помаже рогове олтару на коме се жртва пали; а осталу крв нека излије на подножје олтару на коме се жртва пали.
26 Wansembeyo atenthe mafuta onse pa guwapo monga amatenthera chopereka chachiyanjano. Pochita zimenezi, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo, ndipo adzakhululukidwa.
А све сало нека запали на олтару као сало од жртве захвалне; и тако ће га очистити свештеник од греха његовог, и опростиће му се.
27 “‘Ngati munthu wamba achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova, ndiye kuti wapalamula.
Ако ли ко из простог народа згреши нехотице, и учини штагод што је Господ забранио да се не чини, те скриви,
28 Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, abweretse mbuzi yayikazi yopanda chilema kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo.
Кад дозна за грех свој, који је учинио, тада нека доведе на жртву јаре женско здраво за грех, који је учинио.
29 Asanjike dzanja lake pamutu pa mbuziyo ndipo ayiphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza.
И нека метне руку своју на главу жртви за грех, и нека је свештеник закоље на месту где се коље жртва паљеница.
30 Ndipo wansembe atenge magazi ndi chala chake ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza ndi kuthira magazi wotsalawo pa tsinde la guwalo.
И нека узме свештеник крви од ње на прст свој, И помаже рогове олтару на коме се пали жртва; а осталу крв сву нека излије на подножје олтару.
31 Kenaka iye achotse mafuta onse monga momwe anachotsera mafuta a chopereka chachiyanjano, ndipo awatenthe pa guwa kuti akhale fungo lokomera Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo ndipo adzakhululukidwa.
И све сало из ње нека извади као што се вади сало из жртве захвалне, и нека га запали свештеник на олтару за угодни мирис Господу; а тако ће га очистити од греха свештеник, И опростиће му се.
32 “‘Ngati munthu apereka mwana wankhosa ngati chopereka chopepesera tchimo lake, abwere ndi mwana wankhosa wamkazi wopanda chilema.
Ако ли би довео између оваца на жртву за грех, нека доведе женско здраво.
33 Asanjike dzanja lake pa mutu wa mwana wankhosayo ndipo amuphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza.
И нека метне руку своју на главу жртви за грех, и нека је свештеник закоље на месту где се коље жртва паљеница.
34 Kenaka wansembe atengeko ndi chala chake magazi a mwana wankhosa uja ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Magazi otsalawo athire pa tsinde la guwalo.
И нека узме свештеник крви од жртве за грех на прст свој, и нека помаже рогове олтару на коме се пали жртва; а осталу крв сву нека излије на подножје олтару.
35 Iye achotse mafuta onse, monga amachotsera mafuta a mwana wankhosa wa chopereka chachiyanjano, ndipo wansembe awatenthe pa guwa pamodzi ndi zopereka zina zopsereza za Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo limene munthuyo anachita ndipo adzakhululukidwa.
И све сало нека извади као што се вади сало из јагњета за жртву захвалну; и нека га свештеник запали на олтару за жртву огњену Господу; и тако ће га очистити свештеник од греха његовог, који је учинио, и опростиће му се.

< Levitiko 4 >