< Levitiko 4 >
1 Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
Mluvil také Hospodin k Mojžíšovi, řka:
2 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Munthu akachimwa mosadziwa ndi kuchita chilichonse chimene Yehova walamula kuti asachite, azichita izi:
Mluv synům Izraelským a rci: Když by kdo zhřešil z poblouzení proti některému ze všech přikázaní Hospodinových, čině, čehož býti nemá, a přestoupil by jedno z nich;
3 “‘Ngati wansembe wodzozedwa achimwa, ndi kuchimwitsa anthu onse, iyeyu ayenera kupereka mwana wangʼombe wamphongo wopanda chilema chifukwa cha tchimo limene wachitalo. Imeneyi ndi nsembe ya Yehova yopepesera tchimo lake.
Jestliže by kněz pomazaný zhřešil hříchem jiných lidí: tedy obětovati bude za hřích svůj, kterýmž zhřešil, volka mladého bez poškvrny Hospodinu v obět za hřích.
4 Wansembeyo abwere nayo ngʼombeyo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova. Asanjike dzanja lake pamutu pa ngʼombeyo ndipo ayiphe pamaso pa Yehova.
I přivede volka toho ke dveřím stánku úmluvy před oblíčej Hospodinův, a položí ruku svou na hlavu volka toho, a zabije ho před oblíčejem Hospodinovým.
5 Kenaka wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano.
Tedy vezme kněz pomazaný krve z toho volka, a vnese ji do stánku úmluvy.
6 Iye aviyike chala chake mʼmagazi, ndipo awawaze kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova, patsogolo pa katani yotchinga malo wopatulika.
Potom omočí kněz prst svůj v té krvi, a kropiti jí bude sedmkráte před Hospodinem, před oponou svatyně.
7 Kenaka wansembe apake magaziwo pa nyanga za guwa lofukizira lubani limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza, limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
Pomaže také kněz tou krví rohů oltáře, na němž se kadí vonnými věcmi před Hospodinem, kterýž jest v stánku úmluvy, a ostatek krve volka toho vyleje k spodku oltáře zápalu, kterýž jest u dveří stánku úmluvy.
8 Pambuyo pake achotse mafuta onse a ngʼombe yayimuna yopepesera machimoyo: mafuta okuta zamʼkati kapena mafuta onse amʼkatimo.
Všecken pak tuk volka toho za hřích vyjme z něho, totiž tuk přikrývající střeva a všecken tuk, kterýž jest na nich,
9 Achotsenso ndi kubwera ndi impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta onse ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi ndi impsyo
Též obě dvě ledvinky s tukem, kterýž jest na nich i na slabinách, tolikéž i branici, kteráž jest na jatrách, s ledvinkami odejme ji,
10 monga momwe amachotsera mafuta a ngʼombe yoperekedwa kuti ikhale chopereka chachiyanjano. Tsono wansembe atenthe zimenezi pa guwa lansembe zopsereza.
Tak jako se odjímá od volka oběti pokojné, a páliti to bude kněz na oltáři zápalu.
11 Koma chikopa cha ngʼombe yayimunayo ndi mnofu wake wonse, pamodzi ndi mutu ndi miyendo, zamʼkati ndi matumbo,
Kůži pak volka toho, i všecko maso jeho s hlavou i s nohami jeho, střeva jeho i s lejny jeho,
12 kapena kuti ngʼombe yonse yotsalayo apite nayo kunja kwa msasa ku malo woyeretsedwa, kumene amatayako phulusa ndi kuyitentha pa nkhuni, pa phulusapo.
A tak celého volka vynese ven za stany na místo čisté, tam kdež se popel vysýpá, a spálí jej na dříví ohněm; na místě, kdež se popel vysýpá, spálen bude.
13 “‘Ngati gulu lonse la Aisraeli lichimwa mosadziwa, nachita chomwe ndi choletsedwa ndi Yehova, ngakhale kuti gulu lonselo silikudziwa kuti lachimwa, anthuwo ndi olakwa ndithu.
Jestliže by pak všecko množství Izraelské pobloudilo, a byla by ta věc skrytá před očima shromáždění toho, a učinili by proti některému ze všech přikázaní Hospodinových, čehož by býti nemělo, tak že by vinni byli,
14 Akazindikira tchimo limene achita, gulu lonse lipereke mwana wangʼombe wamphongo kuti akhale chopereka chopepesera tchimo ndipo abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
A byl by poznán hřích, kterýmž zhřešili: tedy obětovati bude shromáždění volka mladého v obět za hřích, a přivedou ho před stánek úmluvy.
15 Akuluakulu a anthuwo asanjike manja awo pa mutu pa ngʼombe pamaso pa Yehova, ndipo ayiphe pomwepo pamaso pa Yehova.
I položí starší shromáždění toho ruce své na hlavu volka před Hospodinem, a zabije volka před Hospodinem.
16 Tsono wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano.
I vnese kněz pomazaný z krve volka toho do stánku úmluvy,
17 Aviyike chala chake mʼmagaziwo ndi kuwawaza pamaso pa Yehova kasanu ndi kawiri patsogolo pa nsalu yotchinga.
A omoče kněz prst svůj v té krvi, kropiti jí bude sedmkráte před Hospodinem, před oponou.
18 Pambuyo pake iye apake magaziwo pa nyanga za guwa limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
Pomaže také kněz tou krví rohů oltáře, kterýž jest před Hospodinem v stánku úmluvy; potom všecku krev pozůstávající vyleje k spodku oltáře zápalu, kterýž jest u dveří stánku úmluvy.
19 Kenaka achotse mafuta onse a ngʼombeyo ndi kuwatentha pa guwa,
Všecken také tuk jeho vyjme z něho, a páliti bude na oltáři.
20 ndipo achite ndi ngʼombe yayimunayi monga anachitira ndi ngʼombe yayimuna yopepesera machimo. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera anthu, ndipo machimo awo adzakhululukidwa.
S tím pak volkem tak učiní, jako učinil s volkem za hřích obětovaným, rovně tak učiní s ním. A tak očistí je kněz, i bude jim odpuštěno.
21 Kenaka atulutse ngʼombeyo kunja kwa msasa ndi kuyitentha monga anatenthera ngʼombe yoyamba ija. Imeneyi ndiyo nsembe yopepesera machimo a gulu lonse.
Volka pak vynese ven z táboru a spálí jej, jako spálil volka prvního; nebo obět za hřích shromáždění jest.
22 “‘Ngati mtsogoleri achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova Mulungu wake, ndiye kuti wapalamula.
Jestliže pak kníže zhřeší, a učiní proti některému ze všech přikázaní Hospodina Boha svého, čehož býti nemělo, a to z poblouzení, tak že vinen bude,
23 Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, iye abwere ndi mbuzi yayimuna yopanda chilema kuti ikhale chopereka chake.
A byl by znám hřích jeho, jímž zhřešil: tedy přivede obět svou z koz, samce bez poškvrny.
24 Asanjike dzanja lake pa mutu wa mbuziyo ndi kuyiphera pamalo pamene amaphera zopereka zopsereza pamaso pa Yehova. Ichi ndi chopereka chopepesera tchimo.
I položí ruku svou na hlavu toho kozla a zabije ho na místě, kdež se bijí oběti zápalné před Hospodinem; obět za hřích jest.
25 Pambuyo pake wansembe atengeko magazi a chopereka chopepesera tchimocho ndi chala chake, ndipo awapake pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Athire magazi otsalawo pa tsinde la guwalo.
A vezma kněz z krve oběti za hřích na prst svůj, pomaže rohů oltáře zápalu, ostatek pak krve jeho vyleje k spodku oltáře zápalu.
26 Wansembeyo atenthe mafuta onse pa guwapo monga amatenthera chopereka chachiyanjano. Pochita zimenezi, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo, ndipo adzakhululukidwa.
Všecken také tuk jeho páliti bude na oltáři, jako i tuk obětí pokojných. A tak očistí jej kněz od hříchu jeho, a odpuštěn bude jemu.
27 “‘Ngati munthu wamba achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova, ndiye kuti wapalamula.
Jestliže pak zhřeší člověk z lidu obecného z poblouzení, učině proti některému přikázaní Hospodinovu, čehož by nemělo býti, tak že vinen bude,
28 Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, abweretse mbuzi yayikazi yopanda chilema kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo.
A byl by znám hřích jeho, kterýmž zhřešil: tedy přivede obět svou z koz, samici bez poškvrny, za hřích svůj, jímž zhřešil.
29 Asanjike dzanja lake pamutu pa mbuziyo ndipo ayiphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza.
I položí ruku svou na hlavu oběti té za hřích a zabije tu obět za hřích na místě obětí zápalných.
30 Ndipo wansembe atenge magazi ndi chala chake ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza ndi kuthira magazi wotsalawo pa tsinde la guwalo.
A vezma kněz z krve její na prst svůj, pomaže rohů oltáře zápalu, a ostatek krve její vyleje u spodku oltáře.
31 Kenaka iye achotse mafuta onse monga momwe anachotsera mafuta a chopereka chachiyanjano, ndipo awatenthe pa guwa kuti akhale fungo lokomera Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo ndipo adzakhululukidwa.
Všecken také tuk její odejme, jako se odjímá tuk od obětí pokojných, a páliti jej bude kněz na oltáři u vůni příjemnou Hospodinu. A tak očistí jej kněz, a bude mu odpuštěno.
32 “‘Ngati munthu apereka mwana wankhosa ngati chopereka chopepesera tchimo lake, abwere ndi mwana wankhosa wamkazi wopanda chilema.
Pakli by z ovcí přinesl obět svou za hřích, samici bez poškvrny přinese.
33 Asanjike dzanja lake pa mutu wa mwana wankhosayo ndipo amuphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza.
A vloží ruku svou na hlavu té oběti za hřích a zabije ji v obět za hřích na místě, kdež se bijí oběti zápalné.
34 Kenaka wansembe atengeko ndi chala chake magazi a mwana wankhosa uja ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Magazi otsalawo athire pa tsinde la guwalo.
Potom vezma kněz krve z oběti té za hřích na prst svůj, pomaže rohů oltáře zápalu, ostatek pak krve její vyleje k spodku oltáře.
35 Iye achotse mafuta onse, monga amachotsera mafuta a mwana wankhosa wa chopereka chachiyanjano, ndipo wansembe awatenthe pa guwa pamodzi ndi zopereka zina zopsereza za Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo limene munthuyo anachita ndipo adzakhululukidwa.
Všecken také tuk její odejme, jakž se odjímá tuk beránka z obětí pokojných, a páliti jej bude kněz na oltáři v obět ohnivou Hospodinu. A tak očistí jej kněz od hříchu jeho, kterýmž zhřešil, a odpuštěn bude jemu.