< Levitiko 27 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
І Госпо́дь промовляв до Мойсея, говорячи:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati munthu anachita lumbiro lapadera loti adzapereka munthu mnzake kwa Yehova ndipo akufuna kuti amuwombole,
„Промовляй до Ізраїлевих синів та й скажеш їм: Коли хто складає обі́тницю Богові за твоєю оці́нкою душ для Господа,
3 mtengo wake ukhale masekeli a siliva makumi asanu, molingana ndi kawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu, ngati munthuyo ndi wamwamuna wa zaka zapakati pa 20 ndi 60.
то буде твоя оці́нка: чоловіка від віку двадцяти́ літ і аж до віку шости́десяти літ, — і буде твоя оці́нка п'ятдеся́т ше́клів срібла на міру ше́клем святині;
4 Ndipo ngati ndi wamkazi, mtengo wake ukhale masekeli makumi atatu.
а якщо жінка вона, то буде твоя оці́нка тридцять шеклів.
5 Mtengo wa munthu wamwamuna wa zaka zapakati pa zisanu ndi makumi awiri ukhale masekeli makumi awiri ndipo munthu wamkazi ukhale masekeli khumi.
А якщо від віку п'яти літ і до віку двадцяти літ, то буде твоя оці́нка: чоловіка — двадцять шеклів, а для жінки — десять шеклів.
6 Ngati ndi munthu wamwamuna wa pakati pa mwezi umodzi ndi zaka zisanu, mtengo wa munthu wamwamuna ukhale masekeli asanu a siliva ndipo ngati ndi wamkazi, ukhale masekeli atatu a siliva.
А якщо від віку місяця й аж до віку п'яти літ, то буде твоя оці́нка: чоловіка — п'ять шеклів срібла, а для жінки твоя оцінка — три шеклі срібла.
7 Ngati ndi munthu wa zaka makumi asanu ndi limodzi kapena kuposerapo, mtengo wa wamwamuna ukhale masekeli khumi ndi asanu, ndipo wamkazi ukhale masekeli khumi.
А якщо від віку шостидесяти літ і вище: якщо чоловік, то буде твоя оці́нка п'ятна́дцять шеклів, а для жінки — десять шеклів.
8 Ngati munthu amene anachita lumbiro ndi wosauka kwambiri kuti sangathe kulipira ndalama zimenezo, abwere ndi munthu woperekedwa uja kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayike mtengo woti munthu wolumbirayo angathe kulipira.
А якщо він обіднілий проти твоєї оцінки, то поставить його перед священиком, і священик оціну́є його, — за тим, що спроможна рука того, хто обіцяв, оціну́є його священик.
9 “‘Ngati chimene anachitira lumbiro kuti apereke ndi nyama imene amapereka kukhala nsembe kwa Yehova, zonse zimene amapereka kwa Yehova nʼzopatulika.
А якщо буде худоба, що з неї прино́сять жертву для Господа, — усе, що дається із неї для Господа, буде святощами.
10 Munthu asasinthanitse ndi ina kapena kupereka ina yabwino mʼmalo mwa yoyipa, kapena yoyipa mʼmalo mwa yabwino. Ngati asinthitsa nyama ina mʼmalo mwa ina, nyamayo pamodzi ndi inzake wasinthitsayo zikhala zopatulika.
Не вільно обміняти її, ані заступити її, добру — злою, або злу — доброю; а якщо справді заступить худобу худобою, то буде вона та засту́пство її — буде святощами.
11 Ngati chimene anachitira lumbiro ndi nyama yodetsedwa, nyama imene siloledwa kuyipereka kukhala nsembe kwa Yehova, nyamayo abwere nayo kwa wansembe,
А якщо та всяка худоба нечиста, що з неї не приносять жертов для Господа, то він поставить ту худобу перед священиком,
12 ndipo wansembeyo atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake.
і священик оціну́є її чи то добре, чи недобре. Як оціну́є священик, так нехай буде.
13 Ngati mwini wakeyo akufuna kuwombola nyamayo, awonjezere pa mtengo wake wa nyamayo chimodzi mwa zigawo zisanu zamtengowo.
А якщо він справді викупить її, то додасть п'яту частину її над оці́нку твою́.
14 “‘Ngati munthu apereka nyumba yake kuti ikhale yopatulika kwa Yehova, wansembe atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake.
А коли хто посвятить дім свій на святість для Господа, то священик оціну́є його чи то добре, чи недобре. Як оціну́є його священик, так стане.
15 Ngati munthu amene wapereka nyumbayo afuna kuyiwombola nyumbayo, awonjezere pamtengo wake wa nyumbayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ndipo nyumbayo idzakhalanso yake.
А якщо той, хто посвячує, викупить свого дома, то додасть п'яту частину срібла твоєї оцінки над нього, — і буде його.
16 “‘Ngati munthu apereka kwa Yehova mbali ina ya malo a makolo ake, mtengo umene awuyike ukhale wolingana ndi mtengo wa mbewu zimene zimadzabzalidwamo. Zikhale mbewu za barele za makilogalamu makumi awiri ndipo mtengo wake ukhale masekeli makumi asanu.
А якщо хтось посвятить Господе́ві з поля своєї посілости, то буде оці́нка твоя посівом його, — по́сів хомера ячме́ню за п'ятдеся́т шеклів срібла.
17 Ngati munthu apereka munda wake kuyambira chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mtengo wake ukhale umene unakhazikitsidwa.
Якщо він посвятить своє поле від ювілейного року, то воно стане за оці́нкою твоєю.
18 Koma ngati apereka mundawo chaka chokondwerera zaka makumi asanu chitapita, wansembe adzatchula mtengo molingana ndi zaka zomwe zatsala kuti chifike chaka china chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo mtengo wake udzakhala wotsikirapo.
А якщо посвятить поле своє по ювілеї, то священик облічить йому те срібло за роками, позосталими до ювілейного року, і те буде відняте від оці́нки твоєї.
19 Ngati munthu amene wapereka munda afuna kuwuwombola, ayenera kuwonjezera pa mtengo wake wa mundawo, limodzi mwa magawo asanu a mtengowo. Ndipo mundawo udzakhalanso wake.
А якщо справді викупить те поле той, хто посвячує його, то додасть п'яту частину срібла оці́нки над нього, — і стане воно його.
20 Koma ngati sawuwombola mundawo, kapena ngati waugulitsa kwa munthu wina, mundawo sudzawomboledwanso.
А якщо він не викупить поля того, і якщо він продасть те поле кому іншому, то вже не буде воно ви́куплене.
21 Mwini mundawo akawusiya mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu ndiye kuti mundawo udzakhala wopatulika monga woperekedwa kwa Yehova: udzakhala munda wa ansembe.
І буде те поле, коли воно вийде в ювілеї, святість для Господа, як поле закля́ття, — для священика буде посілість ним.
22 “‘Ngati munthu apereka kwa Yehova munda umene anagula, umene si malo a makolo ake,
А якщо він посвятить Господе́ві поле купі́влі своєї, що не з поля посілости його,
23 wansembe atchule mtengo wake kufikira pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo munthuyo apereke ndalama zokwanira mtengo wake pa tsikulo monga ndalama zopatulika kwa Yehova.
то священик облічить йому суму твоєї оцінки аж до ювілейного року, і дасть твою оцінку того дня, як святість для Господа.
24 Pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mundawo udzabwezedwa kwa munthu amene anawugulitsayo, amene malowo anali ake.
В ювілейному році ве́рнеться те поле до того, від кого купив його, що його посілість тієї землі.
25 Potchula mtengo uliwonse wansembe awerengere molingana ndi mtengo wa sekeli wa ku Nyumba ya Mulungu: magera makumi awiri pa sekeli imodzi.
А вся оці́нка твоя буде ше́клем святині, — двадцять ґер буде ше́кель.
26 “‘Koma pasapezeke munthu wopereka mwana woyamba kubadwa wa nyama, popeza mwana woyamba kubadwa ali kale wa Yehova, kaya ndi ngʼombe kapena nkhosa, zimenezi ndi za Yehova.
Тільки перворі́дного в худобі, що визнане, як перворі́дне для Господа, ніхто не посвятить його, — чи то віл, чи то овечка, — Господе́ві воно!
27 Ngati ili nyama yodetsedwa, ayiwombole pa mtengo umene wansembe wawuyika, ndi kuwonjezeranso pa mtengo wake wa nyamayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ngati sayiwombola, igulitsidwe pa mtengo umene wansembe awuyike.
А якщо в худобі нечистій, то викупить за твоєю оцінкою, і додасть п'яту частину над нього. А якщо не буде ви́куплене, то буде про́дане за оці́нкою твоєю.
28 “‘Koma chinthu chilichonse choperekedwa kwa Yehova, kaya ndi munthu, nyama, kaya ndi malo a makolo, chimenechi chisagulitsidwe kapena kuwomboledwa. Choperekedwa kwa Yehova motere nʼchopatulika kwambiri.
Тільки ко́жне закля́ття, що люди́на заклене́ Господе́ві зо всього, що його, — від люди́ни, і худоби, і від поля його посілости, не буде про́дане й не буде ви́куплене, — воно найсвятіше для Господа.
29 “‘Munthu amene waperekedwa kotheratu sangawomboledwe. Munthuyo ayenera kuphedwa.
Ко́жне закля́ття, що буде оголошене за закляття з-посеред людей, не буде ви́куплене, — буде конче забите.
30 “‘Chakhumi chilichonse chochokera mʼdziko, kaya ndi tirigu wochokera mʼnthaka kapena chipatso cha mʼmitengo ndi za Yehova. Chimenecho ndi chopatulika kwa Yehova.
А всяка десятина з землі, з насіння землі, з пло́ду дерева, — Господе́ві воно, святощі для Господа!
31 Ngati munthu afuna kuwombola chakhumi chilichonse, awonjezere pamtengo wake chimodzi mwa zigawo zisanu za mtengowo.
А якщо дійсно викупить хтось свою десятину, — той додасть п'яту частину її над неї.
32 Chakhumi cha ngʼombe ndi nkhosa, kapena kuti nyama iliyonse ya khumi imene mʼbusa wayiwerenga idzakhala yopatulikira kwa Yehova.
А всяка десятина худоби великої та худоби дрібної, усе, що пере́йде під палицею, — десяте буде святість для Господа.
33 Palibe amene adzaloledwa kusankha nyama yomwe ili yabwino kapena kusinthitsa. Ngati asinthitsa, nyamayo pamodzi ndi inzakeyo zidzakhala zopatulika ndipo sangaziwombole.’”
Не буде перебирати між добрим та злим, і не замінить його. А якщо справді заступить його, то буде воно та засту́пство його, — буде святість, не буде ви́куплене“.
34 Amenewa ndi malamulo amene Yehova anamupatsa Mose pa Phiri la Sinai kuti awuze Aisraeli.

< Levitiko 27 >