< Levitiko 27 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
Домнул а ворбит луй Мойсе ши а зис: „Ворбеште копиилор луй Исраел ши спуне-ле:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati munthu anachita lumbiro lapadera loti adzapereka munthu mnzake kwa Yehova ndipo akufuna kuti amuwombole,
‘Кынд се вор фаче журуинце Домнулуй, дакэ е ворба де оамень, ей сэ фие ай Домнулуй, дупэ прецуиря та.
3 mtengo wake ukhale masekeli a siliva makumi asanu, molingana ndi kawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu, ngati munthuyo ndi wamwamuna wa zaka zapakati pa 20 ndi 60.
Яр прецуиря пе каре о вей фаче унуй бэрбат, де ла доуэзечь пынэ ла шайзечь де ань, сэ фие де чинчзечь де сикли де арӂинт, дупэ сиклул Сфынтулуй Локаш:
4 Ndipo ngati ndi wamkazi, mtengo wake ukhale masekeli makumi atatu.
дакэ есте фемее, прецуиря сэ фие де трейзечь де сикли.
5 Mtengo wa munthu wamwamuna wa zaka zapakati pa zisanu ndi makumi awiri ukhale masekeli makumi awiri ndipo munthu wamkazi ukhale masekeli khumi.
Де ла чинч пынэ ла доуэзечь де ань, прецуиря сэ фие де доуэзечь де сикли пентру ун бэят ши де зече сикли пентру о фатэ.
6 Ngati ndi munthu wamwamuna wa pakati pa mwezi umodzi ndi zaka zisanu, mtengo wa munthu wamwamuna ukhale masekeli asanu a siliva ndipo ngati ndi wamkazi, ukhale masekeli atatu a siliva.
Де ла о лунэ пынэ ла чинч ань, прецуиря сэ фие де чинч сикли де арӂинт пентру ун бэят ши де трей сикли де арӂинт пентру о фатэ.
7 Ngati ndi munthu wa zaka makumi asanu ndi limodzi kapena kuposerapo, mtengo wa wamwamuna ukhale masekeli khumi ndi asanu, ndipo wamkazi ukhale masekeli khumi.
Де ла шайзечь де ань ын сус, прецуиря сэ фие де чинчспрезече сикли пентру ун бэрбат ши де зече сикли пентру о фемее.
8 Ngati munthu amene anachita lumbiro ndi wosauka kwambiri kuti sangathe kulipira ndalama zimenezo, abwere ndi munthu woperekedwa uja kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayike mtengo woti munthu wolumbirayo angathe kulipira.
Дакэ чел че а фэкут журуинца есте пря сэрак ка сэ плэтяскэ прецуиря ачаста фэкутэ де тине, сэ-л адукэ ла преот, сэ-л прецуяскэ, ши преотул сэ факэ о прецуире потривит ку мижлоачеле омулуй ачелуя.
9 “‘Ngati chimene anachitira lumbiro kuti apereke ndi nyama imene amapereka kukhala nsembe kwa Yehova, zonse zimene amapereka kwa Yehova nʼzopatulika.
Дакэ есте ворба де добитоачеле каре пот фи адусе ка жертфэ Домнулуй, орьче добиток каре се ва да Домнулуй ва фи чева сфынт.
10 Munthu asasinthanitse ndi ina kapena kupereka ina yabwino mʼmalo mwa yoyipa, kapena yoyipa mʼmalo mwa yabwino. Ngati asinthitsa nyama ina mʼmalo mwa ina, nyamayo pamodzi ndi inzake wasinthitsayo zikhala zopatulika.
Сэ ну-л скимбе ши сэ ну пунэ унул рэу ын локул унуя бун, нич унул бун ын локул унуя рэу; дакэ с-ар ынтымпла сэ се ынлокуяскэ ун добиток ку алтул, ши унул, ши челэлалт ва фи сфынт.
11 Ngati chimene anachitira lumbiro ndi nyama yodetsedwa, nyama imene siloledwa kuyipereka kukhala nsembe kwa Yehova, nyamayo abwere nayo kwa wansembe,
Дакэ есте ворба де добитоачеле некурате, каре ну пот фи адусе ка жертфэ Домнулуй, сэ адукэ добитокул ла преот,
12 ndipo wansembeyo atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake.
каре-й ва фаче прецуиря дупэ кум ва фи бун сау рэу ши ва рэмыне ла прецуиря преотулуй.
13 Ngati mwini wakeyo akufuna kuwombola nyamayo, awonjezere pa mtengo wake wa nyamayo chimodzi mwa zigawo zisanu zamtengowo.
Дакэ вря сэ-л рэскумпере, сэ май адауӂе о чинчиме ла прецуиря луй.
14 “‘Ngati munthu apereka nyumba yake kuti ikhale yopatulika kwa Yehova, wansembe atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake.
Дакэ чинева ышь ынкинэ Домнулуй каса, хэрэзинд-о Домнулуй ка ун дар сфынт, преотул сэ-й факэ прецуиря дупэ кум ва фи, бунэ сау ря, ши сэ рэмынэ ла прецуиря фэкутэ де преот.
15 Ngati munthu amene wapereka nyumbayo afuna kuyiwombola nyumbayo, awonjezere pamtengo wake wa nyumbayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ndipo nyumbayo idzakhalanso yake.
Дакэ чел че шь-а ынкинат Домнулуй каса вря с-о рэскумпере, сэ адауӂе о чинчиме ла прецул прецуирий ей, ши ва фи а луй.
16 “‘Ngati munthu apereka kwa Yehova mbali ina ya malo a makolo ake, mtengo umene awuyike ukhale wolingana ndi mtengo wa mbewu zimene zimadzabzalidwamo. Zikhale mbewu za barele za makilogalamu makumi awiri ndipo mtengo wake ukhale masekeli makumi asanu.
Дакэ чинева ынкинэ Домнулуй ун огор дин мошия луй, прецуиря та сэ фие дупэ кытимя де сэмынцэ пе каре о дэ, ши ануме чинчзечь де сикли де арӂинт пентру ун омер де сэмынцэ де орз.
17 Ngati munthu apereka munda wake kuyambira chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mtengo wake ukhale umene unakhazikitsidwa.
Дакэ ышь ынкинэ Домнулуй огорул, ку ынчепере кяр дин анул де веселие, сэ рэмынэ ла прецуиря та,
18 Koma ngati apereka mundawo chaka chokondwerera zaka makumi asanu chitapita, wansembe adzatchula mtengo molingana ndi zaka zomwe zatsala kuti chifike chaka china chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo mtengo wake udzakhala wotsikirapo.
дар, дакэ ышь ынкинэ Домнулуй огорул дупэ анул де веселие, атунч преотул сэ-й сокотяскэ прецул дупэ нумэрул анилор каре май рэмын пынэ ла анул де веселие ши сэ-л скадэ дин прецуиря та.
19 Ngati munthu amene wapereka munda afuna kuwuwombola, ayenera kuwonjezera pa mtengo wake wa mundawo, limodzi mwa magawo asanu a mtengowo. Ndipo mundawo udzakhalanso wake.
Дакэ чел че шь-а ынкинат Домнулуй огорул вря сэ-л рэскумпере, атунч сэ май адауӂе о чинчиме ла арӂинтул прецуит де тине, ши огорул сэ рэмынэ ал луй.
20 Koma ngati sawuwombola mundawo, kapena ngati waugulitsa kwa munthu wina, mundawo sudzawomboledwanso.
Дакэ ну-шь рэскумпэрэ огорул, ши-л винде алтуй ом, ну ва май путя фи рэскумпэрат.
21 Mwini mundawo akawusiya mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu ndiye kuti mundawo udzakhala wopatulika monga woperekedwa kwa Yehova: udzakhala munda wa ansembe.
Ши кынд ва еши кумпэрэторул дин ел ла анул де веселие, огорул ачела сэ фие ынкинат Домнулуй, ка огор хэрэзит Луй; сэ фие мошия преотулуй.
22 “‘Ngati munthu apereka kwa Yehova munda umene anagula, umene si malo a makolo ake,
Дакэ чинева ынкинэ Домнулуй ун огор кумпэрат де ел, каре ну фаче парте дин мошия луй,
23 wansembe atchule mtengo wake kufikira pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo munthuyo apereke ndalama zokwanira mtengo wake pa tsikulo monga ndalama zopatulika kwa Yehova.
преотул сэ-й сокотяскэ прецул дупэ кыт фаче прецуиря пынэ ла анул де веселие, ши омул ачела сэ плэтяскэ ын ачеяшь зи прецул хотэрыт де тине, ка лукру ынкинат Домнулуй.
24 Pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mundawo udzabwezedwa kwa munthu amene anawugulitsayo, amene malowo anali ake.
Ын анул де веселие, огорул сэ се ынтоаркэ ла ачела де ла каре фусесе кумпэрат ши дин мошия кэруя фэчя парте.
25 Potchula mtengo uliwonse wansembe awerengere molingana ndi mtengo wa sekeli wa ku Nyumba ya Mulungu: magera makumi awiri pa sekeli imodzi.
Тоате прецуириле сэ се факэ ын сиклий Сфынтулуй Локаш: сиклул аре доуэзечь де гере.
26 “‘Koma pasapezeke munthu wopereka mwana woyamba kubadwa wa nyama, popeza mwana woyamba kubadwa ali kale wa Yehova, kaya ndi ngʼombe kapena nkhosa, zimenezi ndi za Yehova.
Нимень ну ва путя сэ ынкине Домнулуй пе ынтыюл нэскут дин вита луй, каре кяр есте ал Домнулуй ка ынтый нэскут; фие боу, фие мел, есте ал Домнулуй.
27 Ngati ili nyama yodetsedwa, ayiwombole pa mtengo umene wansembe wawuyika, ndi kuwonjezeranso pa mtengo wake wa nyamayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ngati sayiwombola, igulitsidwe pa mtengo umene wansembe awuyike.
Дакэ есте ворба ынсэ де ун добиток некурат, сэ-л рэскумпере ку прецул прецуит де тине, май адэугынд ынкэ о чинчиме; дакэ ну есте рэскумпэрат, сэ фие вындут дупэ прецуиря та.
28 “‘Koma chinthu chilichonse choperekedwa kwa Yehova, kaya ndi munthu, nyama, kaya ndi malo a makolo, chimenechi chisagulitsidwe kapena kuwomboledwa. Choperekedwa kwa Yehova motere nʼchopatulika kwambiri.
Тот че ва дэруи ун ом Домнулуй прин фэгэдуинцэ, дин че аре, ну ва путя нич сэ се вындэ, нич сэ се рэскумпере: фие ом, фие добиток, фие ун огор дин мошия луй; тот че ва фи дэруит Домнулуй прин фэгэдуинцэ ва фи ун лукру прясфынт, пентру Домнул.
29 “‘Munthu amene waperekedwa kotheratu sangawomboledwe. Munthuyo ayenera kuphedwa.
Ничун ом ынкинат Домнулуй прин фэгэдуинцэ ну ва путя фи рэскумпэрат, чи ва фи оморыт.
30 “‘Chakhumi chilichonse chochokera mʼdziko, kaya ndi tirigu wochokera mʼnthaka kapena chipatso cha mʼmitengo ndi za Yehova. Chimenecho ndi chopatulika kwa Yehova.
Орьче зечуялэ дин пэмынт, фие дин роаделе пэмынтулуй, фие дин родул помилор, есте а Домнулуй; есте ун лукру ынкинат Домнулуй.
31 Ngati munthu afuna kuwombola chakhumi chilichonse, awonjezere pamtengo wake chimodzi mwa zigawo zisanu za mtengowo.
Дакэ вря чинева сэ рэскумпере чева дин зечуяла луй, сэ май адауӂе о чинчиме.
32 Chakhumi cha ngʼombe ndi nkhosa, kapena kuti nyama iliyonse ya khumi imene mʼbusa wayiwerenga idzakhala yopatulikira kwa Yehova.
Орьче зечуялэ дин чирезь ши дин турме, дин тот че трече суб тояг, сэ фие о зечуялэ ынкинатэ Домнулуй.
33 Palibe amene adzaloledwa kusankha nyama yomwe ili yabwino kapena kusinthitsa. Ngati asinthitsa, nyamayo pamodzi ndi inzakeyo zidzakhala zopatulika ndipo sangaziwombole.’”
Сэ ну се черчетезе дакэ добитокул есте бун сау рэу ши сэ ну се скимбе; дакэ се ынлокуеште ун добиток ку ун алтул, ши унул, ши челэлалт вор фи сфинте ши ну вор путя фи рэскумпэрате.’”
34 Amenewa ndi malamulo amene Yehova anamupatsa Mose pa Phiri la Sinai kuti awuze Aisraeli.
Ачестя сунт порунчиле пе каре ле-а дат луй Мойсе Домнул пентру копиий луй Исраел, пе мунтеле Синай.