< Levitiko 26 >

1 “‘Musadzipangire mafano ndipo musayimike chifanizo chosema kapena mwala woti mudzipembedza. Musayike mwala wosema mʼdziko mwanu kuti muziwugwadira. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
“‘Lingazenzeli izithombe loba imifanekiso kumbe amatshe akhonzwayo, njalo lingafaki matshe elizweni lenu ukuba liwakhothamele. Mina nginguThixo uNkulunkulu wenu.
2 “‘Muzisunga Masabata anga ndipo muzilemekeza malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova.
Gcinani amaSabatha ami, lihloniphe indlu yami engcwele. Mina nginguThixo.
3 “‘Mukamayenda motsata malangizo anga ndi kumvera mosamalitsa malamulo anga,
Lingalalela izimiso zami, ligcine imilayo yami,
4 ndidzakupatsani mvula pa nyengo yake. Nthaka yanu idzabala zokolola zake, ndipo mitengo ya mʼmunda idzabala zipatso zake.
ngizalehlisela izulu ngesikhathi salo, umhlabathi uthele amabele, lezihlahla zeganga zithele izithelo zazo.
5 Mudzakhala mukupuntha tirigu mpaka nthawi yothyola mphesa, ndipo mudzakhala mukuthyola mphesa mpaka nthawi yodzala. Mudzadya chakudya chanu mpaka kukhuta ndipo mudzakhala mʼdziko lanu mwamtendere.
Ukubhula kwenu kuzaqhubeka kuze kufike isikhathi sokuvunwa kwamavini, kuthi ukuvunwa kwamavini kuqhubeke kuze kufike isikhathi sokuhlanyela, njalo lizakudla konke ukudla elikufunayo lihlale ngokuvikeleka elizweni lenu.
6 “‘Ndidzabweretsa mtendere mʼdziko lanu, ndipo muzidzagona popanda wokuopsezani. Ndidzachotsa nyama zakuthengo zoopsa mʼdziko mwanu, ndipo mʼdzikomo simudzakhala nkhondo.
Ngizaletha ukuthula elizweni lenu, kungekho muntu ozalethusa. Ngizasusa izinyamazana eziyingozi elizweni; inkemba ayiyikwedlula phakathi kwelizwe lenu.
7 Mudzapirikitsa adani anu, ndipo mudzawagonjetsa ndi lupanga pamaso panu.
Lizazixotsha izitha zenu, ziwe ngenkemba phambi kwenu.
8 Anthu asanu mwa inu adzapirikitsa anthu 100, ndipo anthu 100 mwa inu adzathamangitsa anthu 10,000, ndipo adani anuwo mudzawagonjetsa ndi lupanga.
Abahlanu benu bazaxotsha abalikhulu, kuthi abalikhulu benu baxotshe abayinkulungwane, njalo izitha zenu zizakuwa ngenkemba phambi kwenu.
9 “‘Ndidzakukumbukirani ndi kukupatsani ana ambiri ndi kukuchulukitsani. Ndidzasunga pangano langa ndi inu.
Ngizakuba lomusa kini ngilinike inzalo lande; njalo ngizagcina isivumelwano sami lani.
10 Mudzakhala mukudyabe chakudya chogonera ndipo mudzachotse chakudyacho mʼnkhokwe kuti mupezemo malo woyika chakudya china chatsopano.
Lizakudla okwesivuno sanyakenye lapho okuzamele lisisuse ukuze kube lendawo yesivuno esitsha.
11 Ndidzakhala pakati panu, ndipo sindidzayipidwa nanu.
Ngizabeka indawo yami yokuhlala phakathi kwenu, njalo kaliyikunginenga.
12 Ine ndidzayendayenda pakati panu ndipo ndidzakhala Mulungu wanu. Inu mudzakhala anthu anga.
Ngizahamba phakathi kwenu, ngibe nguNkulunkulu wenu lina libe ngabantu bami.
13 Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti musakhalenso akapolo a Aigupto. Ndinadula mipiringidzo ya goli lanu ndi kukuthandizani kuti muziyenda momasuka.
Mina nginguThixo uNkulunkulu wenu owalikhupha elizweni laseGibhithe ukuze lingabi yizigqili zamaGibhithe futhi. Ngizaphule izikeyi zejogwe lenu njalo ngenza ukuba lenelise ukuhamba amakhanda enu ephakeme.’”
14 “‘Koma mukadzapanda kundimvera ndi kuphwanya malamulo anga onsewa,
“‘Kodwa nxa lingayikungilalela, lingayigcini lemilayo yonke le,
15 ndipo ngati mudzanyoza malangizo anga ndi kunyansidwa ndi malamulo anga, ndi kulephera kumvera zonse zimene ndakulamulani, ndi kuswa pangano langa,
njalo nxa lizakwala izimiso zami, linengwe yimithetho yami, lingenzi okwemilayo yami yonke, ngalokho lephule isivumelwano sami,
16 Ine ndidzakuchitirani izi: ndidzabweretsa zoopsa zadzidzidzi monga chifuwa chachikulu chowondetsa ndiponso malungo amene adzawononga maso ndi kufowoketsa moyo wanu. Mudzangovutika kudzala mbewu zanu chifukwa adani anu adzazidya.
ngizakwenza lokhu kini: Ngizalilethela ukwesaba okukhulu, izifo ezicikizayo, loqhuqho oluzafiphaza amehlo enu, lunciphise impilo yenu. Lizahlanyela inhlanyelo ingasizi ngalutho, ngoba izitha zenu zizayidla.
17 Ndidzakufulatirani, kotero kuti adani anu adzakugonjetsani. Odana nanu adzakulamulirani ndipo inu muzidzagothawa popanda wokupirikitsani.
Ngizaliphendukela lehlulwe yizitha zenu, abalizondayo bazalibusa; lizabaleka lanxa kungekho olixotshayo.
18 “‘Ngati simudzandimvera mutaona zonsezi, ndidzakulanganinso mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha kuchimwa kwanu.
Nxa emva kwakho konke lokhu lingayikungilalela, ngizalijezisa ngokuphindwe kasikhombisa ngenxa yezono zenu.
19 Ndidzathyola mphamvu zanu zimene mukunyadirazo, ndipo ndidzasandutsa mitambo kuti ikhale yowuma ngati chitsulo, ndiponso nthaka yanu kuti ikhale ngati mkuwa.
Ngizabudiliza ubuqholo bokuzazisa kwenu, ngenze umkhathi phezu kwenu ube njengensimbi, kuthi umhlabathi ngaphansi kwenu ube njengethusi.
20 Mphamvu zanu zidzapita pachabe chifukwa nthaka yanu sidzabala kanthu, ngakhale mitengo yake sidzabala zipatso zake.
Amandla enu azachithelwa ize, ngoba umhlabathi wenu awuyikulinika amabele, lezihlahla zelizwe aziyikuthela izithelo zazo.
21 “‘Ngati mudzapitirira kutsutsana nane ndi kukana kundimvera, ndidzachulukitsa masautso anu kasanu ndi kawiri molingana ndi machimo anu.
Lingaqhubeka liyizitha kimi, lale ukungilalela, ngizalithumela inhlupheko zenu kasikhombisa njengokufanele izono zenu.
22 Ndidzabweretsa zirombo zolusa pakati panu, ndipo zidzakulandani ana anu ndi kuwononga ngʼombe zanu. Choncho zidzachepetsa chiwerengero chanu kotero kuti mʼnjira mwanu simudzapita anthu.
Ngizalithumela izilo zeganga, ezizalemuka abantwabenu, zibulale inkomo zenu, zilenze libe balutshwana, imigwaqo yenu ize isale ingaselamuntu.
23 “‘Mukadzapanda kutembenukira kwa Ine ngakhale nditakulangani motere, ndi kumachitabe zotsutsana ndi Ine,
Nxa phezu kwalezizinto lingemukeli iziqondiso zami, liqhubeke liyizitha kimi,
24 Ine mwini ndidzalimbana nanu, ndipo ndidzakulangani mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha machimo anu.
mina ngokwami ngizakuba yisitha kini, ngilitshaye okuphindwe kasikhombisa ngenxa yezono zenu.
25 Ndipo ndidzabweretsa lupanga pa inu ndi kukulangani chifukwa chophwanya pangano langa. Mukadzasonkhana mʼmizinda yanu, ndidzatumiza miliri pakati panu ndipo ndidzakuperekani mʼmanja mwa adani anu.
Njalo ngizaletha lenkemba phezu kwenu ukuba kuphindiselwe ukwephulwa kwesivumelwano. Lingahlehlela emadolobheni enu, ngizathumela isifo phakathi kwenu, linikelwe lezandleni zezitha.
26 Ndikadzachepetsa buledi wanu, akazi khumi adzaphika buledi wawo mu uvuni umodzi, ndipo adzakugawirani bulediyo pangʼonopangʼono. Choncho mudzadya koma wosakhuta.
Lapho sengimise ukulethwa kwezinkwa zenu, abesifazane abalitshumi bazapheka izinkwa zenu eziko elilodwa, babele izinkwa zenu ngobunzima bazo; lizakudla kodwa lingasuthi.
27 “‘Mukadzapanda kundimvera ngakhale nditakulangani motere, ndi kumatsutsanabe ndi Ine,
Nxa lingaqhubeka lingangilaleli, liqhubeka liyizitha kimi,
28 pamenepo ndidzalimbana nanu mwaukali, ndipo Ine mwini ndidzakulangani mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha kuchimwa kwanu.
lami ngolaka lwami ngizakuba yisitha kini, njalo mina ngokwami ngizalijezisa okuphindwe kasikhombisa ngenxa yezono zenu.
29 Mudzadya ana anu aamuna ndiponso mudzadya ana anu aakazi.
Lizakudla inyama yemizimba yamadodana enu, lidle lenyama yemizimba yamadodakazi enu.
30 Ine ndidzawononga malo anu opembedzera mafano a ku mapiri. Ndidzagwetsa maguwa anu ofukizira lubani, ndipo ndidzawunjika pamodzi mitembo ya mafano anu wopanda moyowo, ndipo ndidzanyansidwa nanu.
Ngizabhidliza izindawo zenu eziphakemeyo, ngidilize lama-alithare enu empepha, besengibuthelela izidumbu zenu phezu kwezithombe zenu ezingaphiliyo, nginengeke ngani.
31 Ndidzasandutsa mizinda yanu kukhala mabwinja ndi kuwononga malo anu wopatulika. Sindidzakondweranso ndi fungo lokoma la zopereka zanu.
Ngizakwenza amadolobho enu abe ngamanxiwa, ngidilize izindlu zenu ezingcwele, njalo angiyikuthokoziswa yikunuka mnandi kwephunga leminikelo yenu.
32 Ndidzawononga dziko kotero kuti adani anu mʼmenemo adzadabwa.
Ilizwe ngizalitshabalalisa kuze kumangale izitha zenu ezihlala kulo.
33 Ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina ya anthu ndipo ndidzasolola lupanga langa ndi kukupirikitsani. Dziko lanu lidzawonongedwa, ndipo mizinda yanu idzasanduka mabwinja.
Ngizalihlakazela phakathi kwezizwe, ngikhokhe inkemba yami, ngilixotshe. Ilizwe lenu lizatshabalaliswa, amadolobho enu abe ngamanxiwa.
34 Nthawi imeneyo nthaka idzasangalalira kuyipumitsa kwake nthawi yonse imene idzakhala yosalimidwa, pamene inu mudzakhala muli mʼdziko la adani anu. Pa nthawi imeneyo dziko lidzapumula ndi kukondwerera kulipumuza kwake.
Lapho-ke ilizwe lizathokoziswa ngamasabatha alo ngesikhathi sonke lichithekile, lina liselizweni lezitha zenu. Emva kwalokho, ilizwe lizaphumula lithokoze ngamasabatha alo.
35 Nthawi zonse pamene dzikolo lidzakhala lopanda anthu, nthaka idzapumula. Mpumulo umenewu udzakhala umene nthakayo sinapumulepo pa nthawi zimene inu munkapumula muli mʼdzikomo.
Ngasosonke lesosikhathi ilizwe lichithekile lizakuba lokuphumula elingazange libe lakho ngamasabatha esikhathi lina lisahlala kulo.
36 “‘Kunena za amene adzatsale, ndidzayika mantha mʼmitima mwawo mʼdziko la adani awo kotero kuti adzathawa ngakhale mtswatswa wa tsamba lowuluka ndi mphepo. Adzathawa ngati akuthawa lupanga, ndipo adzagwa pansi ngakhale padzakhale wopanda kuwapirikitsa.
Mayelana lalabo abasele bephila, ngizakwenza inhliziyo zabo zibe lokwesaba okukhulu bekhonale emazweni ezitha zabo baze babalekele lomsindo wehlamvu liphetshulwa ngumoya. Bazagijima angathi babalekela inkemba; bazakuwa lanxa kungekho muntu obaxotshayo.
37 Iwo adzaphunthwitsana ngati akuthawa nkhondo, ngakhale padzakhale popanda wowapirikitsa. Choncho simudzatha kuyima pamaso pa adani anu.
Bazagwenxana angathi babalekela inkemba, lanxa kungekho muntu obaxotshayo. Ngakho aliyikuba lamandla okumelana lezitha zenu.
38 Mudzatheratu pakati pa mitundu ya anthu. Dziko la adani anu lidzakudyani.
Lizabhubha phakathi kwezizwe, lidliwe yilizwe lezitha zenu.
39 Ngakhale iwo amene adzatsale adzatheratu mʼdziko la adani awo chifukwa cha machimo awo ndi machimo a makolo awo.
Abenu labo abasalayo bazahlala behlulukelwe emazweni ezitha zabo ngenxa yezono zabo, njalo bazahlulukelwa ngenxa yezono zaboyise.
40 “‘Tsono adzawulula machimo awo ndi machimo a makolo awo, kusakhulupirika kwawo ndi mayendedwe awo otsutsana nane,
Kodwa bangavuma izono zabo lezono zaboyise, inkohliso abayenza kimi, lokumelana kwabo lami,
41 zomwe zinandipangitsa kuwafulatira ndi kuwapereka mʼmanja mwa adani awo. Ndipo mitima yawo yowumayo ikadzadzichepetsa ndi kuvomera kulangidwa chifukwa cha machimo awo,
okwenza lami ngaba yisitha kubo ngaze ngabasa elizweni lezitha zabo, kuthi lapho inhliziyo zabo ezingasokwanga sezithobekile, behlawulela lezono zabo futhi,
42 Ine ndidzakumbukira pangano langa ndi Yakobo, pangano langa ndi Isake, pangano langa ndi Abrahamu. Ndidzakumbukiranso dzikolo.
ngizasikhumbula isivumelwano sami loJakhobe, lesivumelwano sami lo-Isaka, lesivumelwano sami lo-Abhrahama, besengilikhumbula ilizwe.
43 Pakuti adzasiya dziko lawo lopanda anthu, nthaka idzakondwerera zaka zake zoyipumuza pamene iwo kudzakhala kulibe. Koma adzalangidwa chifukwa cha machimo awo popeza anakana malamulo anga ndipo mitima yawo inkayipidwa nawo malangizo anga.
Ngoba ilizwe bazalitshiya lithokoze ngamasabatha alo lapho lichithekile, bengekho kulo. Bazahlawulela izono zabo ngoba imithetho yami bayala, benengeka ngezimiso zami.
44 Komabe ngakhale adzachite zonsezi ali mʼdziko la adani awo, Ine sindidzawakana kapena kuyipidwa nawo kwakuti nʼkuwawononga kwathunthu ndi kuthetsa pangano langa ndi iwo. Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
Ikanti lanxa kunjalo, nxa sebeselizweni lezitha zabo angiyikubalahla loba nginengeke ngabo, besengibatshabalalisa ngephule lesivumelwano sami labo. Mina nginguThixo uNkulunkulu wabo.
45 Koma powachitira chifundo, ndidzakumbukira pangano langa ndi makolo awo amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mitundu ina ikuona kuti Ine ndikhale Mulungu wawo. Ine ndine Yehova.’”
Kodwa ngenxa yabo ngizasikhumbula isivumelwano sami labokhokho babo engabakhupha elizweni laseGibhithe, izizwe zikhangele ukuba ngibe nguNkulunkulu wabo. Mina nginguThixo.’”
46 Amenewa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anawayika pakati pa Iye mwini ndi Aisraeli pa Phiri la Sinai kudzera mwa Mose.
Lezi yizimiso, imithetho lemilayo eyabekwa nguThixo ngoMosi entabeni iSinayi phakathi kwakhe labako-Israyeli.

< Levitiko 26 >