< Levitiko 26 >

1 “‘Musadzipangire mafano ndipo musayimike chifanizo chosema kapena mwala woti mudzipembedza. Musayike mwala wosema mʼdziko mwanu kuti muziwugwadira. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
MAI hana oukou i na akuakii, a me na kii kalaiia no oukou; aole hoi e kukulu i kii ku, aole hoi e hooka i kii pohaku ma ko oukou aina e kulou iho ia ia; no ka mea, owau no Iehova ko oukou Akua.
2 “‘Muzisunga Masabata anga ndipo muzilemekeza malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova.
E malama oukou i ko'u mau Sabati, a e hoano i ko'u keenakapu: owau no Iehova,
3 “‘Mukamayenda motsata malangizo anga ndi kumvera mosamalitsa malamulo anga,
Ina e hele oukou ma ko'u mau kanawai, a e malama hoi i ka'u mau kauoha, a e hana hoi ma ia mau mea;
4 ndidzakupatsani mvula pa nyengo yake. Nthaka yanu idzabala zokolola zake, ndipo mitengo ya mʼmunda idzabala zipatso zake.
Alaila e haawi aku ai au i ka ua no oukou i ka wa pono, a e haawi mai ka aina i kona mea ulu, a e hoohua mai na laau i ko lakou hua.
5 Mudzakhala mukupuntha tirigu mpaka nthawi yothyola mphesa, ndipo mudzakhala mukuthyola mphesa mpaka nthawi yodzala. Mudzadya chakudya chanu mpaka kukhuta ndipo mudzakhala mʼdziko lanu mwamtendere.
A o ko oukou wa e hahi ai ana e hiki aku ia i ka wa e ohi hua waina ai, a o ka wa e ohi hua waina ai e hiki aku ia i ka wa e lulu hua ai; a e ai oukou i ka oukou berena a maona, a e noho maluhia oukou ma ko oukou aiua.
6 “‘Ndidzabweretsa mtendere mʼdziko lanu, ndipo muzidzagona popanda wokuopsezani. Ndidzachotsa nyama zakuthengo zoopsa mʼdziko mwanu, ndipo mʼdzikomo simudzakhala nkhondo.
A e haawi aku no wau i ka malu ma ko oukou aina, a e moe iho oukou ilalo, aohe mea nana oukou e hooweliweli; ae hoopau aku au i na holoholona ino mailoko aku o ko oukou aina; aole hoi e hele ae ka pahikaua mawaena ae o ko oukou aina,
7 Mudzapirikitsa adani anu, ndipo mudzawagonjetsa ndi lupanga pamaso panu.
E alualu oukou i ko oukou poe enemi, a e haule lakou i ka pahikaua mamua o oukou.
8 Anthu asanu mwa inu adzapirikitsa anthu 100, ndipo anthu 100 mwa inu adzathamangitsa anthu 10,000, ndipo adani anuwo mudzawagonjetsa ndi lupanga.
Elima o oukou e alualu i ka haneri, a he haneri o oukou e hooanhee i na tausani he umi; a e haule ko oukou poe enemi imua o oukou i ka pahikaua.
9 “‘Ndidzakukumbukirani ndi kukupatsani ana ambiri ndi kukuchulukitsani. Ndidzasunga pangano langa ndi inu.
No ka mea, e manao aku no au ia oukou, a e hana aku au ia oukou e hua ae, a e hoonui aku au ia oukou, a e hoopaa aku au i kau berita me oukou.
10 Mudzakhala mukudyabe chakudya chogonera ndipo mudzachotse chakudyacho mʼnkhokwe kuti mupezemo malo woyika chakudya china chatsopano.
A e ai oukou i ka mea kahiko, a e lawe mai i ka mea kahiko iwaho, no ka mea hou.
11 Ndidzakhala pakati panu, ndipo sindidzayipidwa nanu.
A e hoonoho au i kuu halelewa iwaena o oukou, aole hoi e hoowahawaha ko'u uhane ia oukou.
12 Ine ndidzayendayenda pakati panu ndipo ndidzakhala Mulungu wanu. Inu mudzakhala anthu anga.
A e hele au iwaena o oukou, a owau no ko oukou Akua, a e noho oukou i kanaka no'u.
13 Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti musakhalenso akapolo a Aigupto. Ndinadula mipiringidzo ya goli lanu ndi kukuthandizani kuti muziyenda momasuka.
Owau no Iehova ko oukou Akua ka mea nana oukou i lawe mai nei, mai ka aina mai o Aigupita, i ole ai oukou e noho kauwa paa no lakou; a ua moku ia'u na mea e paa ai ka oukou auamo, a hookupono ia oukou i ka hele ana.
14 “‘Koma mukadzapanda kundimvera ndi kuphwanya malamulo anga onsewa,
Aka ina e lohe ole oukou ia'u, aole hoi e hana ma keia mau kauoha a pau;
15 ndipo ngati mudzanyoza malangizo anga ndi kunyansidwa ndi malamulo anga, ndi kulephera kumvera zonse zimene ndakulamulani, ndi kuswa pangano langa,
A ina e hoowahawaha oukou i ka'u mau kauoha, a e inaina mai ko oukou uhane i ko'u mau kanawai, i ole ai oukou e hana ma ka'u mau kauoha a pau, aka e pale ou kou i ka'u berita;
16 Ine ndidzakuchitirani izi: ndidzabweretsa zoopsa zadzidzidzi monga chifuwa chachikulu chowondetsa ndiponso malungo amene adzawononga maso ndi kufowoketsa moyo wanu. Mudzangovutika kudzala mbewu zanu chifukwa adani anu adzazidya.
Na'u no keia e hana ai ia oukou, e hoomaopopo au maluna o oukou i ka makau, a me ka hokii, a me ka li wela e pau ai na maka, a e ehaeha ai ka naau: a e lulu make hewa oukou i ko oukou hua, no ka mea, na ko oukou mau enemi ia e ai.
17 Ndidzakufulatirani, kotero kuti adani anu adzakugonjetsani. Odana nanu adzakulamulirani ndipo inu muzidzagothawa popanda wokupirikitsani.
E hooku e hoi au i ko'u maka ia oukou, a e lukuia oukou imua o ko oukou poe enemi: a o ka poe inaina ia oukou e alii ae maluna o oukou, a e auhee oukou i ka alualu ole ai o kekahi ia oukou.
18 “‘Ngati simudzandimvera mutaona zonsezi, ndidzakulanganinso mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha kuchimwa kwanu.
A ina aole oukou e hoolohe mai ia'u no keia mea, alaila e hoopai pahiku hou aku au ia oukou no ko oukou mau hewa.
19 Ndidzathyola mphamvu zanu zimene mukunyadirazo, ndipo ndidzasandutsa mitambo kuti ikhale yowuma ngati chitsulo, ndiponso nthaka yanu kuti ikhale ngati mkuwa.
A e wahi aku au i ka haaheo o ko oukou mana; a e hoolilo au i ko oukou lani me he hao la, a i ko oukou honua me he keleawe la.
20 Mphamvu zanu zidzapita pachabe chifukwa nthaka yanu sidzabala kanthu, ngakhale mitengo yake sidzabala zipatso zake.
A e lilo ko oukou ikaika i ole; no ka mea, aole e haawi mai ko oukou aina i kona mea ulu, aole hoi e hoohua na laau o ka aina i ko lakou mau hua,
21 “‘Ngati mudzapitirira kutsutsana nane ndi kukana kundimvera, ndidzachulukitsa masautso anu kasanu ndi kawiri molingana ndi machimo anu.
A ina e hele ku e oukou ia'u, aole hoi e hoolohe mai ia'u, e hooili pahiku hou aku au i na mea ino maiuna o oukou, e like me ko oukou mau hewa.
22 Ndidzabweretsa zirombo zolusa pakati panu, ndipo zidzakulandani ana anu ndi kuwononga ngʼombe zanu. Choncho zidzachepetsa chiwerengero chanu kotero kuti mʼnjira mwanu simudzapita anthu.
E hoouna no hoi au i na holoholona hihiu iwaena o oukou e kaili ae i ka oukou mau keiki, a e luku hoi i ko oukou holoholona, a e houuku ia oukou, a e neoneo ae ko oukou mau alanui.
23 “‘Mukadzapanda kutembenukira kwa Ine ngakhale nditakulangani motere, ndi kumachitabe zotsutsana ndi Ine,
A ina aole oukou e hooponoia e au ma keia mau mea, aka, e hele ku e no oukou ia'u,
24 Ine mwini ndidzalimbana nanu, ndipo ndidzakulangani mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha machimo anu.
Alaila e hele ku e aku au ia oukou, a e hoopai pahiku aku au ia oukou no ko oukou mau hewa.
25 Ndipo ndidzabweretsa lupanga pa inu ndi kukulangani chifukwa chophwanya pangano langa. Mukadzasonkhana mʼmizinda yanu, ndidzatumiza miliri pakati panu ndipo ndidzakuperekani mʼmanja mwa adani anu.
A e lawe au i ka pahikaua maluna o oukou e hoopai ana no ka berita; a akoakoa oukou iloko o ko oukou mau kulanakauhale, e hoouua aku au i ka mai ahulau iwaena o oukou; a e haawiia'ku oukou i ka lima o ka enemi.
26 Ndikadzachepetsa buledi wanu, akazi khumi adzaphika buledi wawo mu uvuni umodzi, ndipo adzakugawirani bulediyo pangʼonopangʼono. Choncho mudzadya koma wosakhuta.
Aia haki ia'u ke kookoo o ka oukou berena, alaila e kahumu na wahine he umi i ka oukou berena ma ka umu hookahi, a e haawi hou lakou i ka oukou berena ia oukou, ma ke kaupaona; a e ai hoi oukou, aole hoi e maona.
27 “‘Mukadzapanda kundimvera ngakhale nditakulangani motere, ndi kumatsutsanabe ndi Ine,
A ina aole oukou e hoolohe mai ia'u no keia, aka, e hele ku e no oukou ia'u;
28 pamenepo ndidzalimbana nanu mwaukali, ndipo Ine mwini ndidzakulangani mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha kuchimwa kwanu.
Alaila e hele ku e aku au ia oukou, me ka huhu; a na'u, na'u no oukou e hahau pahiku aku no ko oukou hewa,
29 Mudzadya ana anu aamuna ndiponso mudzadya ana anu aakazi.
A e ai oukou i ka io o ka oukou mau keikikane, a o ka io no o ka oukou mau kaikamahine ka oukou e ai ai.
30 Ine ndidzawononga malo anu opembedzera mafano a ku mapiri. Ndidzagwetsa maguwa anu ofukizira lubani, ndipo ndidzawunjika pamodzi mitembo ya mafano anu wopanda moyowo, ndipo ndidzanyansidwa nanu.
A e hoopau aku au i ko oukou mau wahi kiekie, a e kua iho au i ko oukou mau kii, a e hoolei aku wau i ko oukou mau kupapau maluna iho o na kupapau o ko oukou mau kii a e hoowahawaha aku ko'u uhane ia oukou.
31 Ndidzasandutsa mizinda yanu kukhala mabwinja ndi kuwononga malo anu wopatulika. Sindidzakondweranso ndi fungo lokoma la zopereka zanu.
A e hooneoneo aku au i ko oukou mau kulanakauhale, a e hookae no au i ko oukou mau keenakapu, aole hoi au e honi aku i ke ala o ko oukou mea ala.
32 Ndidzawononga dziko kotero kuti adani anu mʼmenemo adzadabwa.
A e hooneoneo aku au i ka aina, a, nolaila e ilihia'i ko oukou poe enemi e noho ana malaila.
33 Ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina ya anthu ndipo ndidzasolola lupanga langa ndi kukupirikitsani. Dziko lanu lidzawonongedwa, ndipo mizinda yanu idzasanduka mabwinja.
A e hooleilei aku au ia oukou iwaena o na lahuikanaka, a e unuhi ae au i ka pahikaua mahope o oukou; a e neoneo ae ko oukou aina, a e noho ole ia ko oukou mau kulanakauhale.
34 Nthawi imeneyo nthaka idzasangalalira kuyipumitsa kwake nthawi yonse imene idzakhala yosalimidwa, pamene inu mudzakhala muli mʼdziko la adani anu. Pa nthawi imeneyo dziko lidzapumula ndi kukondwerera kulipumuza kwake.
Alaila e loaa i ka aina kona mau Sabati, i kona mau la e neoneo ai, a e noho ai hoi oukou ma ka aina o ko oukou mau enemi; alaila e maha ai ka aina, a e loaa ia ia kona mau Sabati.
35 Nthawi zonse pamene dzikolo lidzakhala lopanda anthu, nthaka idzapumula. Mpumulo umenewu udzakhala umene nthakayo sinapumulepo pa nthawi zimene inu munkapumula muli mʼdzikomo.
I kona mau la e neoneo ai, e maha no ia; no ka mea, aole ia i maha i ko oukou mau Sabati, ia oukou i noho ai maluna ona.
36 “‘Kunena za amene adzatsale, ndidzayika mantha mʼmitima mwawo mʼdziko la adani awo kotero kuti adzathawa ngakhale mtswatswa wa tsamba lowuluka ndi mphepo. Adzathawa ngati akuthawa lupanga, ndipo adzagwa pansi ngakhale padzakhale wopanda kuwapirikitsa.
A maluna o ko oukou poe e koe ana, e hooili ai au i ka maule ana iloko o ko lakou mau naau, ma na aina o ko lakou mau enemi; a o ka leo o ka lau i puehuia e hooauhee aku ia lakou, a e auhee lakou, me he auhee ana la mai ka pahikaua aku; a haule no lakou i ka wa e ole ai he mea alualu.
37 Iwo adzaphunthwitsana ngati akuthawa nkhondo, ngakhale padzakhale popanda wowapirikitsa. Choncho simudzatha kuyima pamaso pa adani anu.
A e hina lakou kekahi maluna o kekahi me he mea la mamua o ka pahikaua, i ka wa e ole ai he mea alualu; aole hoi e hiki iki ia oukou ke ku imua o ko oukou poe enemi.
38 Mudzatheratu pakati pa mitundu ya anthu. Dziko la adani anu lidzakudyani.
A e make oukou mawaena o na lahuikanaka, a e ai no ka aina o ko oukou poe enemi ia oukou.
39 Ngakhale iwo amene adzatsale adzatheratu mʼdziko la adani awo chifukwa cha machimo awo ndi machimo a makolo awo.
A o ke koena o oukou, e mae ae lakou iloko o ko lakou hewa, ma na aina o ko oukou poe enemi; a iloko hoi o ka hewa o ko lakou mau makua lakou e mae pu ai me lakou.
40 “‘Tsono adzawulula machimo awo ndi machimo a makolo awo, kusakhulupirika kwawo ndi mayendedwe awo otsutsana nane,
Ina e hai mai lakou i ko lakou hewa, a me ka hewa o ko lakou mau makua, a me ka lawehala a lakou i hana hewa mai ai ia'u, a ua hele ku e hoi lakou ia'u;
41 zomwe zinandipangitsa kuwafulatira ndi kuwapereka mʼmanja mwa adani awo. Ndipo mitima yawo yowumayo ikadzadzichepetsa ndi kuvomera kulangidwa chifukwa cha machimo awo,
A hele ku e hoi au ia lakou, a ua lawo ae hoi ia lakou ma ka aina o ko lakou poe enemi; ina hoi e hoohaahaaia ko lakou mau naau okipoepoe ole ia, a ilaila e ae ai lakou i ka hoopai ana i ko lakou hewa;
42 Ine ndidzakumbukira pangano langa ndi Yakobo, pangano langa ndi Isake, pangano langa ndi Abrahamu. Ndidzakumbukiranso dzikolo.
Alaila e hoomanao aku au i kuu berita me Iakoba, a me kuu berita hoi me Isaaka, a me kuu berita hoi me Aberahama ka'u e hoomanao ai, a e hoomanao hoi au i ka aina.
43 Pakuti adzasiya dziko lawo lopanda anthu, nthaka idzakondwerera zaka zake zoyipumuza pamene iwo kudzakhala kulibe. Koma adzalangidwa chifukwa cha machimo awo popeza anakana malamulo anga ndipo mitima yawo inkayipidwa nawo malangizo anga.
E haaleleia hoi ka aina e lakou, a e loaa ia ia kona mau Sabati, i kona wa e waiho neoneo ai, aole o lakou; a e ae lakou i ka hoopai ana i ko lakou hewa; no keia, o ko lakou hoowahawaha ana i kuu mau kanawai, a no ko lakou inaina ana i kuu mau kauoha.
44 Komabe ngakhale adzachite zonsezi ali mʼdziko la adani awo, Ine sindidzawakana kapena kuyipidwa nawo kwakuti nʼkuwawononga kwathunthu ndi kuthetsa pangano langa ndi iwo. Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
Oia la, aka i ko lakou noho ana ma ka aina o ko lakou poe enemi, aole au e kiola loa ia lakou, aole hoi au e inaina aku ia lakou, e luku loa ai ia lakou, a e uhaki ai i kuu berita me lakou; no ka mea, owau no Iehova ko lakou Akua.
45 Koma powachitira chifundo, ndidzakumbukira pangano langa ndi makolo awo amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mitundu ina ikuona kuti Ine ndikhale Mulungu wawo. Ine ndine Yehova.’”
Aka, no lakou, e hoomanao ai au i ka berita o ko lakou mau kupuna, a'u i lawe mai nei mai ka aina mai o Aigupita imua o na maka o na lahuikanaka, i Akua au no lakou: owau no Iehova.
46 Amenewa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anawayika pakati pa Iye mwini ndi Aisraeli pa Phiri la Sinai kudzera mwa Mose.
Oia na kapu, a me na kauoha, a me na kanawai a Iehova i haawi mai ai iwaena ona a me na mamo a Iseraela, i ka mauna Sinai, ma ka lima o Mose.

< Levitiko 26 >