< Levitiko 25 >

1 Yehova anawuza Mose pa phiri la Sinai kuti,
UThixo wathi kuMosi entabeni iSinayi,
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukadzalowa mʼdziko limene ndikukupatsani, nthakayo iyenera kumakasunga Sabata la Yehova.
“Khuluma ebantwini bako-Israyeli uthi kubo: ‘Lapho lingena elizweni engizalinika lona, ilizwe lona ngokwalo kumele ligcinele uThixo iSabatha.
3 Pa zaka zisanu ndi chimodzi muzikalima minda yanu, ndipo kwa zaka zisanu ndi chimodzi muzikasadza mitengo yanu ya mpesa ndi kuthyola zipatso zake.
Hlanyelani amasimu enu okweminyaka eyisithupha, kuthi kweminye iminyaka eyisithupha lithene amavini enu.
4 Koma chaka chachisanu ndi chiwiri ndi chaka choti nthaka ipume, chaka cha Sabata la Yehova. Musalime mʼminda yanu kapena kusadza mitengo yanu ya mpesa.
Kodwa ngomnyaka wesikhombisa ilizwe kalibe leSabatha lokuphumula, iSabatha likaThixo. Lingahlanyeli amasimu enu loba lithene izihlahla ezivinini zenu.
5 Musakolole zimene zinamera zokha mʼmunda mwanu. Musakakolole kapena kuthyola mphesa za mʼmitengo imene simunasadze. Chaka chimenechi nʼchoti nthaka ipumule.
Lingavuni imkhukhuzela kumbe likhe izithelo zamavini angalungiselwanga, ilizwe libe lomnyaka wokuphumula.
6 Chaka chimene nthakayo ipumula mudzakhala ndi chakudya chokwanira inuyo, akapolo anu aamuna ndi aakazi, antchito ndi alendo okhala nanu.
Lokho okuzathelwa yilizwe ngomnyaka wesabatha kuzakuba yikudla kwenu, lokwezinceku lezincekukazi zenu, lokwezisebenzi eziqhatshiweyo kanye labemzini abahlala lani,
7 Ziweto zanu pamodzi ndi nyama za mʼdziko lanu zizidzadya zipatso za mʼnthaka.
kanye lokwezifuyo zenu lezinyamazana zeganga elizweni lenu. Konke okuthelwa yilizwe kakudliwe.’”
8 “‘Muzichotsera Masabata asanu ndi awiri a zaka, ndi kuchulukitsa zaka zisanu ndi ziwiri kasanu ndi kawirinso kuti Masabata asanu ndi awiri a zakawo akwane zaka 49.
“‘Balani amasabatha ayisikhombisa eminyaka, iminyaka eyisikhombisa iphindwe kasikhombisa ukuze amasabatha eminyaka eyisikhombisa abe yisibanga seminyaka engamatshumi amane lesificamunwemunye.
9 Ndipo pa tsiku la khumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri mulize lipenga mofuwula. Tsiku lochita mwambo wopepesera machimo muziliza lipenga mʼdziko lanu lonse.
Lapho-ke akutshaywe uphondo ezindaweni zonke ngosuku lwetshumi lwenyanga yesikhombisa; kuthi ngosuku lokuBuyisana kutshaywe uphondo kulolonke ilizwe lenu.
10 Mupatule chaka cha makumi asanu, ndipo mulengeze kuti pakhale ufulu mʼdziko lonse kwa onse amene ali mʼmenemo. Kwa inu chakachi chidzakhala choyimba lipenga la chikondwerero. Aliyense wa inu adzayenera kubwerera pa munda wake, ndipo aliyense wa inu adzabwerera ku fuko lake.
Umnyaka wamatshumi amahlanu wenzeni ube ngcwele, limemezele inkululeko elizweni lonke kubo bonke abahlezi kulo. Uzakuba lijubhili kini. Lowo lalowo wenu kuzamele abuyele emzini wakwabo, esizweni sakibo.
11 Kwa inu chakachi chidzakhaladi chaka choyimba lipenga kukondwerera zaka makumi asanu. Pa chaka chimenechi musadzale kanthu ndipo musakolole mbewu zomera zokha kapenanso kuthyola mphesa pa mitengo yosasadzira.
Umnyaka wamatshumi amahlanu uzakuba lijubhili kini. Lingahlanyeli lutho, njalo lingavuni imikhukhuzela kumbe likhe izithelo zamavini angalungiselwanga.
12 Chimenechi ndi chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Choncho chikhale chaka chopatulika kwa inu. Muzidya zokhazo zimene zakololedwa mʼminda.
Ngoba uliJubhili, uzakuba ngcwele kini; dlanini kuphela lokho elikuthethe emasimini.
13 “‘Chaka chimenechi ndi choliza lipenga, kukondwerera zaka makumi asanu, ndipo aliyense abwerere pa malo ake.
Ngalo umnyaka weJubhili, umuntu wonke kuzamele abuyele emzini wakwabo.
14 “‘Ngati unagulitsa kapena kugula malo ako kwa mnzako wa mʼdzikomo, pasakhale kuchenjeretsana.
Nxa uthengisela umuntu welizwe lakini isiqinti, kumbe usithenga kuye, lingaqilibezelani.
15 Ugule kwa mnzako potsata chiwerengero cha zaka zimene zatha kuyambira pa chikondwerero cha chaka cha makumi asanu chapita. Ndipo mnzakoyo akugulitse potsata chiwerengero cha zaka zokolola zomwe zatsala.
Nxa uthenga emuntwini welizwe lakini kuzakuya ngokuthi mingaki iminyaka eseyadlulayo emva kweJubhili. Yena uzakuthengisela ngokuthi mingaki iminyaka eseleyo ukuthi kuvunwe amabele.
16 Zaka zikakhala zochuluka, uwonjezere mtengo, ndipo zaka zikakhala zochepa, uchepetse mtengo, pakuti chimene iye akukugulitsa ndi zaka zokolola.
Nxa iminyaka iminengi uzakhweza intengo, kuthi nxa iminyaka imilutshwana wehlise intengo, ngoba okuyikho akuthengisela khona linani lezivuno zamabele.
17 Musachenjeretsane koma muope Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Lingaqilibezelani; kodwa mesabeni uNkulunkulu wenu. NginguThixo uNkulunkulu wenu.
18 “‘Tsatirani malangizo anga ndipo mverani mosamala malamulo anga ndipo mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere.
Gcinani izimiso zami, lilalele imithetho yami ngokunanzelela ukuze lihlale livikelekile elizweni.
19 Ndipo nthaka idzakupatsani zipatso zake. Mudzadya mpaka kukhuta ndiponso mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere.
Ilizwe lizathela izithelo zalo, lina lidle lisuthe, lihlale kulo livikelekile.
20 Mwina nʼkafunsa kuti, ‘Kodi chaka chachisanu ndi chiwiri tidzadya chiyani ngati sitidzala kapena kukolola mbewu zathu?’
Lingabuza lithi, “Pho sizakudlani ngomnyaka wesikhombisa nxa singahlanyeli kumbe sivune amabele ethu na?”
21 Ine ndidzatumiza madalitso ambiri chaka chachisanu ndi chimodzi moti nthaka yanu idzabala zinthu zokwanira kudya zaka zitatu.
Mina ngizalilethela isibusiso ngomnyaka wesithupha, ilizwe lithele izithelo zeminyaka emithathu.
22 Pamene mukudzala chaka chachisanu ndi chitatu, muzidzadya chakudya chogonera ndipo mudzapitirira kudya mpaka nthawi yokolola mʼchaka chachisanu ndi chinayi.
Lapho selilima ngomnyaka wesificaminwembili lizakube lisidla amabele amadala, liqhubeke lisidla wona kuze kufike isivuno somnyaka wesificamunwemunye.
23 “‘Malo asagulitsidwe mpaka muyaya chifukwa dzikolo ndi langa. Inu ndinu alendo okhala ndi Ine.
Ilizwe akumelanga lithengiswe kuze kube nininini, ngoba ilizwe ngelami njalo lihlala elizweni lami njengabezizweni.
24 Malo onse amene ali mʼmanja mwanu mudzalole kuti amene anakugulitsani awawombole.
Kulolonke ilizwe elingelenu, lungiselani ukuthi wonke umhlaba owathengwayo uhlengwe.
25 “‘Ngati Mwisraeli mnzanu wasauka nagulitsako gawo lina la malo ake, mʼbale wake wapaphata abwere kudzawombola malo amene mʼbale wakeyo wagulitsa.
Nxa omunye wakini esebe ngumyanga eseze ethengisa okunye kwempahla yakhe, isihlobo sakhe kasisize sihlenge lokho osekuthengiswe ngumuntu wakibo.
26 Koma ngati munthuyo alibe wachibale woti nʼkuwombola malowo koma pambuyo pake iye mwini nʼkulemera ndi kupeza zokwanira kuwombolera, awombole malowo.
Kodwa-ke nxa umuntu engelaye ongamhlengela khona, abesebuya enotha yena ngokwakhe azuze okwanele ukuthi azihlengele,
27 Awerengerane zaka kuyambira pamene anagulitsa mundawo ndipo amubwezere amene anagulayo ndalama zimene akanayenera kuzipereka mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Atatero angathe kubwerera pa malo ake.
kabale imali elingana leminyaka leyo kusukela impahla leyo ithengisiwe, abuyisele imali esalayo kulowomuntu ayemthengisele, abesethatha impahla yakhe.
28 Koma ngati sakhala nazo zokwanira kuti amubwezere amene anagula malowo, gawo limene anagulitsalo lidzakhala mʼmanja mwa munthu amene anagulayo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Malowo adzabwezedwa chaka chimenechi, ndipo iye adzatha kubwerera pa malo ake.
Kodwa-ke nxa engelamali eyaneleyo yokuyibuyisa leyompahla ayithengisayo, kayihlale kulowo owayithengayo kuze kufike umnyaka weJubhili. Izabuyiselwa kuye ngeJubhili, kulapho-ke azayithatha khona impahla yakhe.
29 “‘Ngati munthu agulitsa nyumba ya mu mzinda umene uli mu linga, angathe kuyiwombola nyumbayo chisanathe chaka chathunthu chigulitsire. Mu nthawi imeneyi wogulitsayo atha kuyiwombola.
Nxa umuntu ethengisa indlu edolobheni elihonqolozelwe ngomthangala ulelungelo lokuyihlenga emva komnyaka ithengisiwe. Phakathi kwalesosikhathi angayihlenga.
30 Ngati nyumbayo siwomboledwa chisanathe chaka chimodzicho, nyumbayo idzakhala ya amene anagulayo ndi zidzukulu zake mpaka muyaya. Sidzabwezedwanso kwa mwini wake mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu.
Nxa ingahlengwanga kuze kuphele umnyaka ogcweleyo, indlu esedolobheni elihonqolozelwe ngomthangala izakuba ngeyalowo owayithengayo, ibe ngeyakhe kokuphela lowo owayithengayo kanye lezizukulwane zakhe. Kayiyikubuyiselwa kowayengumniniyo ngeJubhili.
31 Koma nyumba za mʼmizinda yosazingidwa ndi linga ziwomboledwe monga mmene achitira ndi minda ya mʼdzikomo.
Kodwa izindlu ezisemizini engahonqolozelwanga zizabalwa njengeganga elingelalutho. Kazihlengwe, njalo kumele zibuyiselwe kubanikazi ngeJubhili.
32 “‘Alevi ali ndi ufulu owombola nyumba zawo za mʼmidzi yawo nthawi ina iliyonse.
AmaLevi ahlezi elelungelo lokuhlenga izindlu zawo emadolobheni angawamaLevi.
33 Koma ngati Mlevi sawombola nyumba imene inagulitsidwa mʼmudzi mwake, ndiye kuti idzabwezedwe mʼchaka choliza lipenga pokondwerera zaka makumi asanu, popeza nyumba zimenezi zili mʼmidzi ya Alevi ndi yawo pakati pa Aisraeli.
Ngakho-ke, impahla yamaLevi iyahlengeka, lokhu kutsho indlu ethengiswe loba kukuliphi idolobho elingelabo, kumele ibuyiselwe ngeJubhili, ngoba izindlu ezisemadolobheni amaLevi zililifa lawo ebantwini labako-Israyeli.
34 Koma malo owetera ziweto a mʼmidzi yawoyo sayenera kugulitsidwa. Awa ndi malo awo mpaka muyaya.
Kodwa amadlelo angaphandle kwamadolobho awo akumelanga athengiswe ngoba ayilifa lawo kuze kube nininini.
35 “‘Ngati mʼbale wako akhala wosauka kuti sangathe kudzisamalira yekha, umuthandize. Ukhale naye ngati mlendo kapena ngati munthu amene ukhala naye kwa kanthawi.
Nxa omunye wabantu bakini esiba ngumyanga owehluleka ukuziphilisa phakathi kwenu, msizeni njengelingakwenza kowezizweni kumbe ohlezi lani okwesikhatshana, ukuze aqhubeke ehlala lani.
36 Usalandire chiwongoladzanja chilichonse kuchokera kwa iye kapena kuwonjezerapo kanthu kena, koma uziopa Mulungu kuti mʼbale wakoyo akhale nawe.
Akungabi lanzuzo eliyithatha kuye, kodwa mesabeni uNkulunkulu wenu, ukuze umuntu wakini aqhubeke ehlala lani.
37 Musakongoze mnzanu ndalama kuti mulandire chiwongoladzanja, kapena kumugulitsa chakudya kuti mupeze phindu.
Lingameboleki imali ezalayo kumbe limthengisele ukudla kulenzuzo.
38 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikupatseni dziko la Kanaani ndi kuti ndikhale Mulungu wanu.
Mina nginguThixo uNkulunkulu wenu owalikhupha elizweni laseGibhithe, ukuba ngilinike ilizwe laseKhenani, ngibe nguNkulunkulu wenu.
39 “‘Ngati mʼbale wanu asauka ndipo adzigulitsa yekha kwa inu, musamugwiritse ntchito ngati kapolo.
Nxa omunye wakini ko-Israyeli esiba ngumyanga phakathi kwenu aze azithengise kuwe, ungamsebenzisi njengesigqili.
40 Akhale ngati wantchito kapena ngati mlendo. Akugwirireni ntchito mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu.
Kumele umphathe njengesisebenzi esiqhatshiweyo kumbe umuntu ohlezi okwesikhatshana phakathi kwenu. Kakusebenzele kuze kufike umnyaka weJubhili.
41 Kenaka iye ndi ana ake achoke, ndipo apite ku fuko lake ndi kubwerera ku malo a makolo ake.
Lapho-ke yena labantwabakhe bazakhululwa, babuyele kwabosendo lwakibo lemfuyweni yabokhokho babo.
42 Chifukwa Aisraeli ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto, asagulitsidwe ngati akapolo.
Ngenxa yokuthi abako-Israyeli bazinceku zami engazikhupha elizweni laseGibhithe, akumelanga bathengiswe njengezigqili.
43 Musawalamulire mwankhanza koma wopani Mulungu wanu.
Ungababusi ngochuku, kodwa mesabe uNkulunkulu wakho.
44 “‘Kunena za akapolo aamuna ndi aakazi, amenewa mungathe kuwagula kuchokera kwa mitundu ya anthu imene yakuzungulirani.
Iziqgili zenu zesilisa lezesifazane zizavela ezizweni ezilihonqolezeleyo; kuzo yikho lapho elingathenga khona izigqili.
45 Mungathenso kugula akapolo kuchokera kwa alendo amene akukhala nanu kapena kuchokera ku mabanja amene mukukhala nawo amene ndi mbadwa za mʼdziko lanu. Iwowa akhoza kukhala akapolo anu.
Lingathenga lezakhamizi ezihlezi phakathi kwenu okwesikhatshana, labomndeni wazo abazalelwa elizweni lenu.
46 Akapolowo mungathe kuwasiya mʼmanja mwa ana anu inu mutafa kuti akhale cholowa chawo moyo wawo wonse. Koma musawalamulire mwankhanza Aisraeli anzanu.
Lingabenza babe yilifa labantwabenu, libenze babe yizigqili zabo okwanininini, kodwa akumelanga libuse abako-Israyeli benu ngochuku.
47 “‘Ngati mlendo kapena munthu amene akukhala nanu kwa kanthawi kochepa alemera ndipo mmodzi wa abale anu amene akukhala naye pafupi nʼkusauka, nadzigulitsa yekha kwa mlendo amene akukhala pakati panuyo kapena kwa mmodzi wa fuko la munthu wongokhala pafupi nayeyo,
Nxa owezizweni, kumbe umuntu ohlezi phakathi kwenu okwesikhatshana enotha, kuthi owakini abe ngumyanga azithengise kowezizweni ohlala phakathi kwenu loba kolilunga lomndeni wezizweni,
48 wodzigulitsayo ali ndi ufulu wowomboledwa. Mmodzi mwa abale ake angathe kumuwombola:
ulokhu elalo ilungelo lokuhlengwa emva kokuzithengisa kwakhe. Omunye wezihlobo zakhe angamhlenga.
49 amalume ake kapena mwana wa amalume ake, kapena wachibale wa mu fuko lake. Kapena ngati iye mwini alemera, atha kudziwombola yekha.
Umalumakhe kumbe umzawakhe, loba esinye isihlobo somdeni wakhe singamhlenga. Loba nxa enotha, angazihlenga yena ngokwakhe.
50 Iye pamodzi ndi munthu amene anamugulayo awerengerane kuyambira chaka chimene anadzigulitsa kwa iyeyo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Mtengo wodziwombolera ukhale wofanana ndi zakazo. Ndipo nthawi imene anali ndi mbuye wakeyo iwerengedwe ngati nthawi ya munthu wantchito.
Yena lomthengi wakhe kababale isikhathi kusukela ngomnyaka azithengisa ngawo kusiyafika emnyakeni weJubhili. Intengo yokukhululwa kwakhe izakuhambelana lenani elinikwa umuntu oqhatshiweyo okwalesosikhathi seminyaka.
51 Ngati patsala zaka zambiri, iye ayenera kulipira mtengo woposera umene anamugulira.
Nxa kusele iminyaka eminengi, kumele ahlawulele ukuhlengwa kwakhe ngentengo eyingxenye enengi yentengo ayethengwe ngawo.
52 Ngati kwatsala zaka zochepa kuti ifike nthawi ya chaka chokondwerera zaka makumi asanu, iye awerengerane ndi mbuye wake, ndipo apereke ndalama za zowomboledwera molingana ndi zaka zotsalazo.
Nxa sekusele iminyaka emilutshwana ukuba kufike umnyaka weJubhili, uzabala lokho, akhuphe intengo yokuhlengwa kwakhe okulingana leyominyaka.
53 Azikhala naye ngati wantchito wolembedwa chaka ndi chaka. Ndipo muonetsetse kuti mbuye wakeyo sakumulamulira mwankhanza.
Uzabalwa njengomuntu oqhatshiweyo kusukela komunye umnyaka kusiya komunye. Kumele libone ukuthi lowo owamthengayo kambusi ngochuku.
54 “‘Ngakhale munthuyo atapanda kuwomboledwa mwa njira zimenezi, iye ndi ana ake ayenera kumasulidwa mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu,
Nxa engahlengwanga ngenye yalezizindlela, yena labantwabakhe bazakhululwa ngomnyaka weJubhili,
55 pakuti Aisraeli ndi atumiki anga. Iwo ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
ngoba abako-Israyeli ngabami, bazinceku zami. Bazinceku zami engazikhupha elizweni laseGibhithe. Mina nginguThixo uNkulunkulu wenu.’”

< Levitiko 25 >