< Levitiko 25 >

1 Yehova anawuza Mose pa phiri la Sinai kuti,
And the LORD spoke to Moses in mount Sinai, saying,
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukadzalowa mʼdziko limene ndikukupatsani, nthakayo iyenera kumakasunga Sabata la Yehova.
Speak to the children of Israel, and say to them, When ye come into the land which I give you, then shall the land keep a sabbath to the LORD.
3 Pa zaka zisanu ndi chimodzi muzikalima minda yanu, ndipo kwa zaka zisanu ndi chimodzi muzikasadza mitengo yanu ya mpesa ndi kuthyola zipatso zake.
Six years thou shalt sow thy field, and six years thou shalt prune thy vineyard, and gather in its fruit;
4 Koma chaka chachisanu ndi chiwiri ndi chaka choti nthaka ipume, chaka cha Sabata la Yehova. Musalime mʼminda yanu kapena kusadza mitengo yanu ya mpesa.
But in the seventh year shall be a sabbath of rest to the land, a sabbath for the LORD: thou shalt neither sow thy field, nor prune thy vineyard.
5 Musakolole zimene zinamera zokha mʼmunda mwanu. Musakakolole kapena kuthyola mphesa za mʼmitengo imene simunasadze. Chaka chimenechi nʼchoti nthaka ipumule.
That which groweth of its own accord of thy harvest thou shalt not reap, neither gather the grapes of thy untrimmed vine: for it is a year of rest to the land.
6 Chaka chimene nthakayo ipumula mudzakhala ndi chakudya chokwanira inuyo, akapolo anu aamuna ndi aakazi, antchito ndi alendo okhala nanu.
And the sabbath of the land shall be food for you; for thee, and for thy male servant, and for thy female servant, and for thy hired servant, and for thy stranger that sojourneth with thee,
7 Ziweto zanu pamodzi ndi nyama za mʼdziko lanu zizidzadya zipatso za mʼnthaka.
And for thy cattle, and for the beast that are in thy land, shall all the increase of it be food.
8 “‘Muzichotsera Masabata asanu ndi awiri a zaka, ndi kuchulukitsa zaka zisanu ndi ziwiri kasanu ndi kawirinso kuti Masabata asanu ndi awiri a zakawo akwane zaka 49.
And thou shalt number seven sabbaths of years to thee, seven times seven years; and the space of the seven sabbaths of years shall be to thee forty and nine years.
9 Ndipo pa tsiku la khumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri mulize lipenga mofuwula. Tsiku lochita mwambo wopepesera machimo muziliza lipenga mʼdziko lanu lonse.
Then shalt thou cause the trumpet of the jubilee to sound on the tenth day of the seventh month, in the day of atonement shall ye make the trumpet sound throughout all your land.
10 Mupatule chaka cha makumi asanu, ndipo mulengeze kuti pakhale ufulu mʼdziko lonse kwa onse amene ali mʼmenemo. Kwa inu chakachi chidzakhala choyimba lipenga la chikondwerero. Aliyense wa inu adzayenera kubwerera pa munda wake, ndipo aliyense wa inu adzabwerera ku fuko lake.
And ye shall hallow the fiftieth year, and proclaim liberty throughout all the land to all its inhabitants: it shall be a jubilee to you; and ye shall return every man to his possession, and ye shall return every man to his family.
11 Kwa inu chakachi chidzakhaladi chaka choyimba lipenga kukondwerera zaka makumi asanu. Pa chaka chimenechi musadzale kanthu ndipo musakolole mbewu zomera zokha kapenanso kuthyola mphesa pa mitengo yosasadzira.
A jubilee shall that fiftieth year be to you: ye shall not sow, neither reap that which groweth of itself in it, nor gather the grapes in it of thy untrimmed vine.
12 Chimenechi ndi chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Choncho chikhale chaka chopatulika kwa inu. Muzidya zokhazo zimene zakololedwa mʼminda.
For it is the jubilee; it shall be holy to you: ye shall eat the increase of it out of the field.
13 “‘Chaka chimenechi ndi choliza lipenga, kukondwerera zaka makumi asanu, ndipo aliyense abwerere pa malo ake.
In the year of this jubilee ye shall return every man to his possession.
14 “‘Ngati unagulitsa kapena kugula malo ako kwa mnzako wa mʼdzikomo, pasakhale kuchenjeretsana.
And if thou shalt sell any to thy neighbour, or buy any thing from thy neighbour’s hand, ye shall not oppress one another:
15 Ugule kwa mnzako potsata chiwerengero cha zaka zimene zatha kuyambira pa chikondwerero cha chaka cha makumi asanu chapita. Ndipo mnzakoyo akugulitse potsata chiwerengero cha zaka zokolola zomwe zatsala.
According to the number of years after the jubilee thou shalt buy of thy neighbour, and according to the number of years of the fruits he shall sell to thee:
16 Zaka zikakhala zochuluka, uwonjezere mtengo, ndipo zaka zikakhala zochepa, uchepetse mtengo, pakuti chimene iye akukugulitsa ndi zaka zokolola.
According to the multitude of years thou shalt increase the price of it, and according to the fewness of years thou shalt diminish the price of it: for according to the number of the years of the fruits doth he sell to thee.
17 Musachenjeretsane koma muope Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Ye shall not therefore oppress one another; but thou shalt fear thy God: for I am the LORD your God.
18 “‘Tsatirani malangizo anga ndipo mverani mosamala malamulo anga ndipo mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere.
Therefore ye shall do my statutes, and keep my judgments, and do them; and ye shall dwell in the land in safety.
19 Ndipo nthaka idzakupatsani zipatso zake. Mudzadya mpaka kukhuta ndiponso mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere.
And the land shall yield her fruit, and ye shall eat your fill, and dwell in it in safety.
20 Mwina nʼkafunsa kuti, ‘Kodi chaka chachisanu ndi chiwiri tidzadya chiyani ngati sitidzala kapena kukolola mbewu zathu?’
And if ye shall say, What shall we eat the seventh year? behold, we shall not sow, nor gather in our increase:
21 Ine ndidzatumiza madalitso ambiri chaka chachisanu ndi chimodzi moti nthaka yanu idzabala zinthu zokwanira kudya zaka zitatu.
Then I will command my blessing upon you in the sixth year, and it shall bring forth fruit for three years.
22 Pamene mukudzala chaka chachisanu ndi chitatu, muzidzadya chakudya chogonera ndipo mudzapitirira kudya mpaka nthawi yokolola mʼchaka chachisanu ndi chinayi.
And ye shall sow the eighth year, and eat of old fruit until the ninth year; until its fruits come in ye shall eat of the old store.
23 “‘Malo asagulitsidwe mpaka muyaya chifukwa dzikolo ndi langa. Inu ndinu alendo okhala ndi Ine.
The land shall not be sold for ever: for the land is mine; for ye are strangers and sojourners with me.
24 Malo onse amene ali mʼmanja mwanu mudzalole kuti amene anakugulitsani awawombole.
And in all the land of your possession ye shall grant a redemption for the land.
25 “‘Ngati Mwisraeli mnzanu wasauka nagulitsako gawo lina la malo ake, mʼbale wake wapaphata abwere kudzawombola malo amene mʼbale wakeyo wagulitsa.
If thy brother shall have become poor, and have sold some of his possession, and if any of his kin shall come to redeem it, then shall he redeem that which his brother sold.
26 Koma ngati munthuyo alibe wachibale woti nʼkuwombola malowo koma pambuyo pake iye mwini nʼkulemera ndi kupeza zokwanira kuwombolera, awombole malowo.
And if the man shall have none to redeem it, and himself be able to redeem it;
27 Awerengerane zaka kuyambira pamene anagulitsa mundawo ndipo amubwezere amene anagulayo ndalama zimene akanayenera kuzipereka mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Atatero angathe kubwerera pa malo ake.
Then let him count the years of the sale of it, and restore the balance to the man to whom he sold it; that he may return to his possession.
28 Koma ngati sakhala nazo zokwanira kuti amubwezere amene anagula malowo, gawo limene anagulitsalo lidzakhala mʼmanja mwa munthu amene anagulayo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Malowo adzabwezedwa chaka chimenechi, ndipo iye adzatha kubwerera pa malo ake.
But if he shall not be able to restore it to him, then that which is sold shall remain in the hand of him that hath bought it until the year of jubilee: and in the jubilee it shall go out, and he shall return to his possession.
29 “‘Ngati munthu agulitsa nyumba ya mu mzinda umene uli mu linga, angathe kuyiwombola nyumbayo chisanathe chaka chathunthu chigulitsire. Mu nthawi imeneyi wogulitsayo atha kuyiwombola.
And if a man shall sell a dwelling house in a walled city, then he may redeem it within a whole year after it is sold; within a full year may he redeem it.
30 Ngati nyumbayo siwomboledwa chisanathe chaka chimodzicho, nyumbayo idzakhala ya amene anagulayo ndi zidzukulu zake mpaka muyaya. Sidzabwezedwanso kwa mwini wake mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu.
And if it shall not be redeemed within the space of a full year, then the house that is in the walled city shall be established for ever to him that bought it throughout his generations: it shall not go out in the jubilee.
31 Koma nyumba za mʼmizinda yosazingidwa ndi linga ziwomboledwe monga mmene achitira ndi minda ya mʼdzikomo.
But the houses of the villages which have no walls around them shall be counted as the fields of the country: they may be redeemed, and they shall go out in the jubilee.
32 “‘Alevi ali ndi ufulu owombola nyumba zawo za mʼmidzi yawo nthawi ina iliyonse.
However the cities of the Levites, and the houses of the cities of their possession, may the Levites redeem at any time.
33 Koma ngati Mlevi sawombola nyumba imene inagulitsidwa mʼmudzi mwake, ndiye kuti idzabwezedwe mʼchaka choliza lipenga pokondwerera zaka makumi asanu, popeza nyumba zimenezi zili mʼmidzi ya Alevi ndi yawo pakati pa Aisraeli.
And if a man shall purchase of the Levites, then the house that was sold, and the city of his possession, shall go out in the year of jubilee: for the houses of the cities of the Levites are their possession among the children of Israel.
34 Koma malo owetera ziweto a mʼmidzi yawoyo sayenera kugulitsidwa. Awa ndi malo awo mpaka muyaya.
But the field of the common land of their cities may not be sold; for it is their perpetual possession.
35 “‘Ngati mʼbale wako akhala wosauka kuti sangathe kudzisamalira yekha, umuthandize. Ukhale naye ngati mlendo kapena ngati munthu amene ukhala naye kwa kanthawi.
And if thy brother shall have become poor, and falleth into poverty among you; then thou shalt relieve him: yea, though he may be a stranger, or a sojourner; that he may live with thee.
36 Usalandire chiwongoladzanja chilichonse kuchokera kwa iye kapena kuwonjezerapo kanthu kena, koma uziopa Mulungu kuti mʼbale wakoyo akhale nawe.
Take thou no interest of him, or increase: but fear thy God; that thy brother may live with thee.
37 Musakongoze mnzanu ndalama kuti mulandire chiwongoladzanja, kapena kumugulitsa chakudya kuti mupeze phindu.
Thou shalt not give him thy money upon interest, nor lend him thy food for increase.
38 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikupatseni dziko la Kanaani ndi kuti ndikhale Mulungu wanu.
I am the LORD your God, who brought you out of the land of Egypt, to give you the land of Canaan, and to be your God.
39 “‘Ngati mʼbale wanu asauka ndipo adzigulitsa yekha kwa inu, musamugwiritse ntchito ngati kapolo.
And if thy brother that dwelleth by thee shall have become poor, and be sold to thee; thou shalt not compel him to serve as a slave:
40 Akhale ngati wantchito kapena ngati mlendo. Akugwirireni ntchito mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu.
But as an hired servant, and as a sojourner, he shall be with thee, and shall serve thee to the year of jubilee:
41 Kenaka iye ndi ana ake achoke, ndipo apite ku fuko lake ndi kubwerera ku malo a makolo ake.
And then shall he depart from thee, both he and his children with him, and shall return to his own family, and to the possession of his fathers shall he return.
42 Chifukwa Aisraeli ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto, asagulitsidwe ngati akapolo.
For they are my servants, which I brought out of the land of Egypt: they shall not be sold as slaves.
43 Musawalamulire mwankhanza koma wopani Mulungu wanu.
Thou shalt not rule over him with rigour; but shalt fear thy God.
44 “‘Kunena za akapolo aamuna ndi aakazi, amenewa mungathe kuwagula kuchokera kwa mitundu ya anthu imene yakuzungulirani.
Both thy male and female slaves, which thou shalt have, shall be from the heathen that are around you; from them shall ye buy male and female slaves.
45 Mungathenso kugula akapolo kuchokera kwa alendo amene akukhala nanu kapena kuchokera ku mabanja amene mukukhala nawo amene ndi mbadwa za mʼdziko lanu. Iwowa akhoza kukhala akapolo anu.
Moreover of the children of the strangers that sojourn among you, of them shall ye buy, and of their families that are with you, whom they begat in your land: and they shall be your possession.
46 Akapolowo mungathe kuwasiya mʼmanja mwa ana anu inu mutafa kuti akhale cholowa chawo moyo wawo wonse. Koma musawalamulire mwankhanza Aisraeli anzanu.
And ye shall take them as an inheritance for your children after you, to inherit them for a possession; they shall be your slaves for ever: but over your brethren the children of Israel, ye shall not rule one over another with rigour.
47 “‘Ngati mlendo kapena munthu amene akukhala nanu kwa kanthawi kochepa alemera ndipo mmodzi wa abale anu amene akukhala naye pafupi nʼkusauka, nadzigulitsa yekha kwa mlendo amene akukhala pakati panuyo kapena kwa mmodzi wa fuko la munthu wongokhala pafupi nayeyo,
And if a sojourner or a stranger shall become rich by thee, and thy brother that dwelleth by him shall become poor, and sell himself to the stranger or sojourner by thee, or to the stock of the stranger’s family:
48 wodzigulitsayo ali ndi ufulu wowomboledwa. Mmodzi mwa abale ake angathe kumuwombola:
After that he is sold he may be redeemed again; one of his brethren may redeem him:
49 amalume ake kapena mwana wa amalume ake, kapena wachibale wa mu fuko lake. Kapena ngati iye mwini alemera, atha kudziwombola yekha.
Either his uncle, or his uncle’s son, may redeem him, or any that is near of kin to him of his family may redeem him; or if he is able, he may redeem himself.
50 Iye pamodzi ndi munthu amene anamugulayo awerengerane kuyambira chaka chimene anadzigulitsa kwa iyeyo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Mtengo wodziwombolera ukhale wofanana ndi zakazo. Ndipo nthawi imene anali ndi mbuye wakeyo iwerengedwe ngati nthawi ya munthu wantchito.
And he shall reckon with him that bought him from the year that he was sold to him to the year of jubilee: and the price of his sale shall be according to the number of years, according to the time of an hired servant shall it be with him.
51 Ngati patsala zaka zambiri, iye ayenera kulipira mtengo woposera umene anamugulira.
If there shall be yet many years behind, according to them he shall give again the price of his redemption out of the money that he was bought for.
52 Ngati kwatsala zaka zochepa kuti ifike nthawi ya chaka chokondwerera zaka makumi asanu, iye awerengerane ndi mbuye wake, ndipo apereke ndalama za zowomboledwera molingana ndi zaka zotsalazo.
And if there shall remain but few years to the year of jubilee, then he shall count with him, and according to his years shall he give him again the price of his redemption.
53 Azikhala naye ngati wantchito wolembedwa chaka ndi chaka. Ndipo muonetsetse kuti mbuye wakeyo sakumulamulira mwankhanza.
And as a yearly hired servant shall he be with him: and the other shall not rule with rigour over him in thy sight.
54 “‘Ngakhale munthuyo atapanda kuwomboledwa mwa njira zimenezi, iye ndi ana ake ayenera kumasulidwa mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu,
And if he shall not be redeemed in these years, then he shall go out in the year of jubilee, both he, and his children with him.
55 pakuti Aisraeli ndi atumiki anga. Iwo ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
For to me the children of Israel are servants; they are my servants whom I brought out of the land of Egypt: I am the LORD your God.

< Levitiko 25 >