< Levitiko 25 >

1 Yehova anawuza Mose pa phiri la Sinai kuti,
Mluvil ještě Hospodin k Mojžíšovi na hoře Sinai, řka:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukadzalowa mʼdziko limene ndikukupatsani, nthakayo iyenera kumakasunga Sabata la Yehova.
Mluv synům Izraelským a rci jim: Když vejdete do země, kterouž já dávám vám, odpočívati bude země, nebo sobota jest Hospodinova.
3 Pa zaka zisanu ndi chimodzi muzikalima minda yanu, ndipo kwa zaka zisanu ndi chimodzi muzikasadza mitengo yanu ya mpesa ndi kuthyola zipatso zake.
Šest let osívati budeš rolí svou, a šest let obřezovati budeš vinici svou a sbírati úrody její.
4 Koma chaka chachisanu ndi chiwiri ndi chaka choti nthaka ipume, chaka cha Sabata la Yehova. Musalime mʼminda yanu kapena kusadza mitengo yanu ya mpesa.
Sedmého pak léta sobotu odpočinutí bude míti země, sobotu Hospodinovu; nebudeš na poli svém síti a vinice své řezati.
5 Musakolole zimene zinamera zokha mʼmunda mwanu. Musakakolole kapena kuthyola mphesa za mʼmitengo imene simunasadze. Chaka chimenechi nʼchoti nthaka ipumule.
Což se samo od sebe zrodí obilí tvého, nebudeš toho žíti, a hroznů vinice zanechané od tebe nebudeš sbírati. Rok odpočinutí bude míti země.
6 Chaka chimene nthakayo ipumula mudzakhala ndi chakudya chokwanira inuyo, akapolo anu aamuna ndi aakazi, antchito ndi alendo okhala nanu.
Ale ovoce země toho odpočinutí budete míti ku pokrmu, ty i služebník tvůj, i děvka tvá, i nájemník tvůj, i příchozí tvůj, kterýž bydlí u tebe,
7 Ziweto zanu pamodzi ndi nyama za mʼdziko lanu zizidzadya zipatso za mʼnthaka.
I hovado tvé, i všeliký živočich, kterýž jest v zemi tvé, všecky úrody její budou míti ku pokrmu.
8 “‘Muzichotsera Masabata asanu ndi awiri a zaka, ndi kuchulukitsa zaka zisanu ndi ziwiri kasanu ndi kawirinso kuti Masabata asanu ndi awiri a zakawo akwane zaka 49.
Sečteš také sobě sedm téhodnů let, totiž sedmkrát sedm let, tak aby čas sedmi téhodnů let učinil tobě čtyřidceti devět let.
9 Ndipo pa tsiku la khumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri mulize lipenga mofuwula. Tsiku lochita mwambo wopepesera machimo muziliza lipenga mʼdziko lanu lonse.
Tedy dáš troubiti trubou veselé všudy sedmého měsíce v desátý den; v den očišťování dáš troubiti trubou po vší zemi vaší.
10 Mupatule chaka cha makumi asanu, ndipo mulengeze kuti pakhale ufulu mʼdziko lonse kwa onse amene ali mʼmenemo. Kwa inu chakachi chidzakhala choyimba lipenga la chikondwerero. Aliyense wa inu adzayenera kubwerera pa munda wake, ndipo aliyense wa inu adzabwerera ku fuko lake.
I posvětíte léta padesátého, a vyhlásíte svobodu v zemi té všechněm obyvatelům jejím. Léto milostivé toto míti budete, abyste se navrátili jeden každý k statku svému, a jeden každý k čeledi své zase přijde.
11 Kwa inu chakachi chidzakhaladi chaka choyimba lipenga kukondwerera zaka makumi asanu. Pa chaka chimenechi musadzale kanthu ndipo musakolole mbewu zomera zokha kapenanso kuthyola mphesa pa mitengo yosasadzira.
Ten rok milostivý padesátého léta míti budete; nebudete síti, ani žíti toho, což by samo od sebe vzrostlo, ani sbírati vína opuštěných vinic léta toho.
12 Chimenechi ndi chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Choncho chikhale chaka chopatulika kwa inu. Muzidya zokhazo zimene zakololedwa mʼminda.
Nebo milostivé léto jest, protož za svaté je míti budete; ze všelikého pole jísti budete úrody jeho.
13 “‘Chaka chimenechi ndi choliza lipenga, kukondwerera zaka makumi asanu, ndipo aliyense abwerere pa malo ake.
Toho léta milostivého navrátí se jeden každý k statku svému.
14 “‘Ngati unagulitsa kapena kugula malo ako kwa mnzako wa mʼdzikomo, pasakhale kuchenjeretsana.
Když nějakou věc prodáš bližnímu svému, aneb koupíš něco od bližního svého, nikoli neutiskujte jeden druhého.
15 Ugule kwa mnzako potsata chiwerengero cha zaka zimene zatha kuyambira pa chikondwerero cha chaka cha makumi asanu chapita. Ndipo mnzakoyo akugulitse potsata chiwerengero cha zaka zokolola zomwe zatsala.
Vedlé počtu let po létu milostivém koupíš od bližního svého, a vedlé počtu let, v kterýchž úrody bráti máš, prodá tobě.
16 Zaka zikakhala zochuluka, uwonjezere mtengo, ndipo zaka zikakhala zochepa, uchepetse mtengo, pakuti chimene iye akukugulitsa ndi zaka zokolola.
Èím více bude let, tím větší placení bude, a čím méně let, tím, menší placení bude; nebo počet úrod prodá tobě.
17 Musachenjeretsane koma muope Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Protož nikoli neoklamávejte jeden druhého, ale boj se každý Boha svého; nebo já jsem Hospodin Bůh váš.
18 “‘Tsatirani malangizo anga ndipo mverani mosamala malamulo anga ndipo mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere.
Ostříhejte ustanovení mých, a soudy mé zachovávejte a čiňte je, a bydliti budete v zemi té bezpečně.
19 Ndipo nthaka idzakupatsani zipatso zake. Mudzadya mpaka kukhuta ndiponso mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere.
A přinese vám země úrody své; i budete jísti až do sytosti, bydlíce bezpečně v ní.
20 Mwina nʼkafunsa kuti, ‘Kodi chaka chachisanu ndi chiwiri tidzadya chiyani ngati sitidzala kapena kukolola mbewu zathu?’
Pakli díte: Co budeme jísti léta sedmého, jestliže nebudeme síti, ani shromažďovati užitků svých?
21 Ine ndidzatumiza madalitso ambiri chaka chachisanu ndi chimodzi moti nthaka yanu idzabala zinthu zokwanira kudya zaka zitatu.
Dám požehnání své vám léta šestého, tak že přinese úrody na tři léta.
22 Pamene mukudzala chaka chachisanu ndi chitatu, muzidzadya chakudya chogonera ndipo mudzapitirira kudya mpaka nthawi yokolola mʼchaka chachisanu ndi chinayi.
I budete síti léta osmého, a jísti úrody staré až do léta devátého; dokudž by nezrostly úrody jeho, jísti budete staré.
23 “‘Malo asagulitsidwe mpaka muyaya chifukwa dzikolo ndi langa. Inu ndinu alendo okhala ndi Ine.
Země pak nebude prodávána v manství; nebo má jest země, a vy jste příchozí a podruzi u mne.
24 Malo onse amene ali mʼmanja mwanu mudzalole kuti amene anakugulitsani awawombole.
A po vší zemi vládařství svého dopustíte dávati výplatu země.
25 “‘Ngati Mwisraeli mnzanu wasauka nagulitsako gawo lina la malo ake, mʼbale wake wapaphata abwere kudzawombola malo amene mʼbale wakeyo wagulitsa.
Jestliže by ochudl bratr tvůj, tak že by prodal něco z statku svého, tedy přijde příbuzný jeho, nejbližší jeho, a vyplatí prodanou věc od bratra svého.
26 Koma ngati munthuyo alibe wachibale woti nʼkuwombola malowo koma pambuyo pake iye mwini nʼkulemera ndi kupeza zokwanira kuwombolera, awombole malowo.
Pakli kdo nemaje výplatce, mohl by tomu sám dosti učiniti, tak že shledal by, což potřebí k vyplacení:
27 Awerengerane zaka kuyambira pamene anagulitsa mundawo ndipo amubwezere amene anagulayo ndalama zimene akanayenera kuzipereka mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Atatero angathe kubwerera pa malo ake.
Tedy počte léta prodaje svého, a navrátí, což zůstane, tomu, jemuž prodal; tak zase přijde k statku svému.
28 Koma ngati sakhala nazo zokwanira kuti amubwezere amene anagula malowo, gawo limene anagulitsalo lidzakhala mʼmanja mwa munthu amene anagulayo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Malowo adzabwezedwa chaka chimenechi, ndipo iye adzatha kubwerera pa malo ake.
Pakli by nemohl shledati toho, což by navrátiti měl, tedy zůstane věc prodaná v rukou toho, kterýž ji koupil, až do léta milostivého. I postoupí mu ji v čas léta milostivého, a on navrátí se zase k dědictví svému.
29 “‘Ngati munthu agulitsa nyumba ya mu mzinda umene uli mu linga, angathe kuyiwombola nyumbayo chisanathe chaka chathunthu chigulitsire. Mu nthawi imeneyi wogulitsayo atha kuyiwombola.
Když by kdo prodal dům k bydlení v městě hrazeném, bude míti právo k vyplacení jeho, dokudž nevyplní se rok prodaje jeho. Za celý rok bude míti právo k vyplacení jeho.
30 Ngati nyumbayo siwomboledwa chisanathe chaka chimodzicho, nyumbayo idzakhala ya amene anagulayo ndi zidzukulu zake mpaka muyaya. Sidzabwezedwanso kwa mwini wake mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu.
Pakliť ho nevyplatí dříve, než vyjde ten celý rok, tedy zůstane dům ten v městě hrazeném tomu, kterýž jej koupil, dědičně v pronárodech jeho, aniž ho postoupí v létě milostivém.
31 Koma nyumba za mʼmizinda yosazingidwa ndi linga ziwomboledwe monga mmene achitira ndi minda ya mʼdzikomo.
Domové pak ve vsech, kteréž nejsou zdí ohrazené, tak jako pole země počítati se budou. Budou moci býti vyplacováni, a léta milostivého navráceni budou.
32 “‘Alevi ali ndi ufulu owombola nyumba zawo za mʼmidzi yawo nthawi ina iliyonse.
Ale města Levítská, a domové v městech dědictví jejich, ti vždycky vyplaceni mohou býti od Levítů.
33 Koma ngati Mlevi sawombola nyumba imene inagulitsidwa mʼmudzi mwake, ndiye kuti idzabwezedwe mʼchaka choliza lipenga pokondwerera zaka makumi asanu, popeza nyumba zimenezi zili mʼmidzi ya Alevi ndi yawo pakati pa Aisraeli.
Ten pak, kdož vyplacuje, ať jest z Levítů. Aneb ať vyjde kupec z koupeného domu a města dědictví jeho v čas léta milostivého; nebo domové měst Levítských jsou dědictví jejich mezi syny Izraelskými.
34 Koma malo owetera ziweto a mʼmidzi yawoyo sayenera kugulitsidwa. Awa ndi malo awo mpaka muyaya.
Pole pak na předměstí měst jejich nebude prodáváno, nebo dědictví jejich věčné jest.
35 “‘Ngati mʼbale wako akhala wosauka kuti sangathe kudzisamalira yekha, umuthandize. Ukhale naye ngati mlendo kapena ngati munthu amene ukhala naye kwa kanthawi.
Jestliže by schudl bratr tvůj, a ustaly by ruce jeho u tebe, posilníš ho; též příchozí aneb podruh živiti se bude při tobě.
36 Usalandire chiwongoladzanja chilichonse kuchokera kwa iye kapena kuwonjezerapo kanthu kena, koma uziopa Mulungu kuti mʼbale wakoyo akhale nawe.
Nevezmeš od něho lichvy aneb úroku, ale báti se budeš Boha svého, aby se mohl bratr tvůj živiti u tebe.
37 Musakongoze mnzanu ndalama kuti mulandire chiwongoladzanja, kapena kumugulitsa chakudya kuti mupeze phindu.
Peněz svých nedáš jemu na lichvu, aniž pro zisk půjčovati budeš obilí svého.
38 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikupatseni dziko la Kanaani ndi kuti ndikhale Mulungu wanu.
Já jsem Hospodin Bůh váš, kterýž jsem vyvedl vás z země Egyptské, abych vám dal zemi Kananejskou, a byl vám za Boha.
39 “‘Ngati mʼbale wanu asauka ndipo adzigulitsa yekha kwa inu, musamugwiritse ntchito ngati kapolo.
Jestliže by pak schudl bratr tvůj u tebe, tak že by se prodal tobě, nebudeš ho podrobovati v dílo otrocké.
40 Akhale ngati wantchito kapena ngati mlendo. Akugwirireni ntchito mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu.
Jakožto nájemník a jako podruh bude při tobě; až do léta milostivého sloužiti bude u tebe.
41 Kenaka iye ndi ana ake achoke, ndipo apite ku fuko lake ndi kubwerera ku malo a makolo ake.
Potom vyjde od tebe s dětmi svými, a navrátí se k čeledi své, a v dědictví otců svých navrátí se.
42 Chifukwa Aisraeli ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto, asagulitsidwe ngati akapolo.
Nebo jsou služebníci moji, kteréž jsem vyvedl z země Egyptské; nebudou prodáváni tak jako jiní služebníci.
43 Musawalamulire mwankhanza koma wopani Mulungu wanu.
Nebudeš panovati nad ním tvrdě, ale báti se budeš Boha svého.
44 “‘Kunena za akapolo aamuna ndi aakazi, amenewa mungathe kuwagula kuchokera kwa mitundu ya anthu imene yakuzungulirani.
Služebník pak tvůj aneb děvka tvá, kteréž míti budeš, budou z národů těch, kteříž jsou vůkol vás; z nich kupovati budete služebníky a děvky.
45 Mungathenso kugula akapolo kuchokera kwa alendo amene akukhala nanu kapena kuchokera ku mabanja amene mukukhala nawo amene ndi mbadwa za mʼdziko lanu. Iwowa akhoza kukhala akapolo anu.
I od synů bydlitelů, kteříž jsou u vás pohostinu, od těch kupovati budete, a z čeledí těch, kteříž jsou s vámi, kteréž zplodili v zemi vaší, a budou vám v dědictví.
46 Akapolowo mungathe kuwasiya mʼmanja mwa ana anu inu mutafa kuti akhale cholowa chawo moyo wawo wonse. Koma musawalamulire mwankhanza Aisraeli anzanu.
A vládnouti budete jimi právem dědičným, i synové vaší po vás, abyste je dědičně obdrželi. Na věčnost služby jejich užívati budete, ale nad bratřími svými, syny Izraelskými, nižádný nad bratrem svým nebude tvrdě panovati.
47 “‘Ngati mlendo kapena munthu amene akukhala nanu kwa kanthawi kochepa alemera ndipo mmodzi wa abale anu amene akukhala naye pafupi nʼkusauka, nadzigulitsa yekha kwa mlendo amene akukhala pakati panuyo kapena kwa mmodzi wa fuko la munthu wongokhala pafupi nayeyo,
Jestliže by pak zbohatl příchozí aneb host, kterýž bydlí s tebou, a bratr tvůj přišel by na chudobu při něm, tak že by se prodal příchozímu aneb hosti tvému, aneb obyvateli, kterýž jest z čeledi cizí,
48 wodzigulitsayo ali ndi ufulu wowomboledwa. Mmodzi mwa abale ake angathe kumuwombola:
Když by se tedy prodal, může zase vyplacen býti. Někdo z bratří jeho vyplatí ho.
49 amalume ake kapena mwana wa amalume ake, kapena wachibale wa mu fuko lake. Kapena ngati iye mwini alemera, atha kudziwombola yekha.
Buďto strýc jeho, aneb syn strýce jeho vyplatí jej, aneb někdo z přátel krevních jeho, z rodiny jeho, vyplatí ho; aneb jestli potom sám bude moci s to býti, vyplatí se.
50 Iye pamodzi ndi munthu amene anamugulayo awerengerane kuyambira chaka chimene anadzigulitsa kwa iyeyo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Mtengo wodziwombolera ukhale wofanana ndi zakazo. Ndipo nthawi imene anali ndi mbuye wakeyo iwerengedwe ngati nthawi ya munthu wantchito.
I počte se s tím, kterýž ho koupil, od léta, v kterémž se jemu prodal, až do léta milostivého, aby peníze, za něž jest prodán, byly vedlé počtu let; a jakožto s nájemníkem, tak se s ním stane.
51 Ngati patsala zaka zambiri, iye ayenera kulipira mtengo woposera umene anamugulira.
Jestliže ještě mnoho let zůstává k létu milostivému, vedlé nich navrátí výplatu svou z peněz, za něž koupen jest.
52 Ngati kwatsala zaka zochepa kuti ifike nthawi ya chaka chokondwerera zaka makumi asanu, iye awerengerane ndi mbuye wake, ndipo apereke ndalama za zowomboledwera molingana ndi zaka zotsalazo.
Pakli málo zůstává let do léta milostivého, tedy počte se s ním, a vedlé počtu let jeho navrátí výplatu svou.
53 Azikhala naye ngati wantchito wolembedwa chaka ndi chaka. Ndipo muonetsetse kuti mbuye wakeyo sakumulamulira mwankhanza.
Tak jako s čeledínem ročním nakládáno bude s ním; nebude nad ním tvrdě panovati před očima tvýma.
54 “‘Ngakhale munthuyo atapanda kuwomboledwa mwa njira zimenezi, iye ndi ana ake ayenera kumasulidwa mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu,
Pakli by se nevyplatil v těch letech, tedy vyjde léta milostivého on, i synové jeho s ním.
55 pakuti Aisraeli ndi atumiki anga. Iwo ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Nebo synové Izraelští jsou moji služebníci, služebníci moji jsou, kteréž jsem vyvedl z země Egyptské: Já Hospodin Bůh váš.

< Levitiko 25 >