< Levitiko 24 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
and to speak: speak LORD to(wards) Moses to/for to say
2 “Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale, a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
to command [obj] son: descendant/people Israel and to take: bring to(wards) you oil olive pure beaten to/for light to/for to ascend: offer up lamp continually
3 Kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, mʼchihema cha msonkhano, Aaroni azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa, nthawi zonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yonse.
from outside to/for curtain [the] testimony in/on/with tent meeting to arrange [obj] him Aaron from evening till morning to/for face: before LORD continually statute forever: enduring to/for generation your
4 Aaroni ayatse nyale zimene zili pa choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri kuti zikhale zoyaka nthawi zonse pamaso pa Yehova.
upon [the] lampstand [the] pure to arrange [obj] [the] lamp to/for face: before LORD continually
5 “Mutenge ufa wosalala ndipo muphike makeke khumi ndi awiri ndipo keke iliyonse ikhale ya ufa wa makilogalamu awiri.
and to take: take fine flour and to bake [obj] her two ten bun two tenth to be [the] bun [the] one
6 Muwayike pa tebulo la golide wabwino kwambiri pamaso pa Yehova mʼmizere iwiri. Mzere uliwonse ukhale wa makeke asanu ndi imodzi.
and to set: make [obj] them two row six [the] row upon [the] table [the] pure to/for face: before LORD
7 Pa mzere uliwonse muyikepo lubani wafungo lokoma kuti pamodzi ndi bulediyo akhale wachikumbutso cha nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova.
and to give: put upon [the] row frankincense pure and to be to/for food: bread to/for memorial food offering to/for LORD
8 Sabata ndi sabata nthawi zonse Aaroni aziyika makeke amenewa pamaso pa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti akhale pangano lamuyaya.
in/on/with day [the] Sabbath in/on/with day [the] Sabbath to arrange him to/for face: before LORD continually from with son: descendant/people Israel covenant forever: enduring
9 Chakudyacho ndi cha Aaroni ndi ana ake ndipo azidyera ku malo wopatulika chifukwa kwa iye chakudyacho ndi chopatulika kwambiri chochokera pa chopereka chopsereza cha Yehova.”
and to be to/for Aaron and to/for son: child his and to eat him in/on/with place holy for holiness holiness he/she/it to/for him from food offering LORD statute: portion forever: enduring
10 Tsiku lina munthu wina wamwamuna amene amayi ake anali Mwisraeli koma abambo ake anali Mwigupto anapita kwa Aisraeli ndipo anakangana ndi Mwisraeli wina ku msasa.
and to come out: come son: child woman Israelite and he/she/it son: child man Egyptian in/on/with midst son: descendant/people Israel and to struggle in/on/with camp son: child [the] Israelite and man [the] Israelite
11 Munthu uja ananyoza dzina la Yehova ndi kulitemberera. Choncho anabwera naye kwa Mose. Dzina la amayi ake linali Selomiti, mwana wa Dibiri, wa fuko la Dani.
and to pierce son: child [the] woman [the] Israelite [obj] [the] name and to lighten and to come (in): bring [obj] him to(wards) Moses and name mother his Shelomith daughter Dibri to/for tribe Dan
12 Anamuyika mʼndende mpaka atadziwa bwino chofuna cha Yehova.
and to rest him in/on/with custody to/for to declare to/for them upon lip: word LORD
13 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
and to speak: speak LORD to(wards) Moses to/for to say
14 “Pita naye kunja kwa msasa munthu wotembererayo. Onse amene anamumva akutemberera asanjike manja awo pamutu pake ndipo gulu lonse la anthu limugende miyala.
to come out: send [obj] [the] to lighten to(wards) from outside to/for camp and to support all [the] to hear: hear [obj] hand their upon head his and to stone [obj] him all [the] congregation
15 Choncho uza Aisraeli kuti, ‘Aliyense wotemberera Mulungu wake alangidwe.
and to(wards) son: descendant/people Israel to speak: speak to/for to say man man for to lighten God his and to lift: guilt sin his
16 Aliyense wonyoza dzina la Yehova, mlendo ngakhale mbadwa, aphedwe. Gulu lonse la anthu limuponye miyala.
and to curse name LORD to die to die to stone to stone in/on/with him all [the] congregation like/as sojourner like/as born in/on/with to curse he name to die
17 “‘Ngati munthu wina aliyense achotsa moyo wa munthu mnzake, munthuyo ayenera kuphedwa.
and man: anyone for to smite all soul: life man to die to die
18 Aliyense wopha chiweto cha mnzake ayenera kulipira china. Moyo kulipa moyo.
and to smite soul: life animal to complete her soul: life underneath: instead soul: life
19 Ngati munthu avulaza mnzake, nayenso amuchite zomwe wachitira mnzakeyo:
and man: anyone for to give: do blemish in/on/with neighbor his like/as as which to make: do so to make: do to/for him
20 kuthyola fupa kulipira kuthyola fupa, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino. Monga momwe anavulazira mnzake, amuvulaze chimodzimodzinso.
breaking underneath: instead breaking eye underneath: instead eye tooth underneath: instead tooth like/as as which to give: give blemish in/on/with man so to give: give in/on/with him
21 Aliyense wopha chiweto cha mnzake, alipire chiweto china, koma aliyense wopha munthu ayenera kuphedwa.
and to smite animal to complete her and to smite man to die
22 Lamulo la mlendo ndi mbadwa ndi limodzi lomweli. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
justice: judgement one to be to/for you like/as sojourner like/as born to be for I LORD God your
23 Pamenepo Mose anawuza Aisraeli zimenezi, ndipo iwo anatulutsira munthu wotembererayo kunja kwa msasa ndi kumugenda miyala. Aisraeli anachita zimene Yehova analamula Mose.
and to speak: speak Moses to(wards) son: descendant/people Israel and to come out: send [obj] [the] to lighten to(wards) from outside to/for camp and to stone [obj] him stone and son: descendant/people Israel to make: do like/as as which to command LORD [obj] Moses