< Levitiko 24 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Jahve reče Mojsiju:
2 “Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale, a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
“Naredi Izraelcima da ti za svijećnjak donose čistoga ulja od istupanih maslina, da se uvijek održava svjetlo.
3 Kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, mʼchihema cha msonkhano, Aaroni azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa, nthawi zonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yonse.
Neka ga Aron svagda sprema pred Jahvom od večeri do jutra u Šatoru sastanka, pred zavjesom Svjedočanstva. Neka je ovo trajan zakon vašim naraštajima.
4 Aaroni ayatse nyale zimene zili pa choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri kuti zikhale zoyaka nthawi zonse pamaso pa Yehova.
Neka Aron neprekidno održava svjetlila na čistome svijećnjaku pred Jahvom.”
5 “Mutenge ufa wosalala ndipo muphike makeke khumi ndi awiri ndipo keke iliyonse ikhale ya ufa wa makilogalamu awiri.
“Potom uzmi najboljeg brašna i od njega ispeci dvanaest pogača. Neka u svakoj pogači budu dvije desetine efe.
6 Muwayike pa tebulo la golide wabwino kwambiri pamaso pa Yehova mʼmizere iwiri. Mzere uliwonse ukhale wa makeke asanu ndi imodzi.
Onda ih poredaj u dva reda - po šest u redu - na čistome stolu što je pred Jahvom.
7 Pa mzere uliwonse muyikepo lubani wafungo lokoma kuti pamodzi ndi bulediyo akhale wachikumbutso cha nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova.
Na svaki red stavi čistoga tamjana. Neka to bude hrana prinesena kao spomen - paljena žrtva Jahvi.
8 Sabata ndi sabata nthawi zonse Aaroni aziyika makeke amenewa pamaso pa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti akhale pangano lamuyaya.
Svake subote, bez prijekida, neka se postavljaju pred Jahvu. To neka Izraelci vrše zbog vječnoga Saveza.
9 Chakudyacho ndi cha Aaroni ndi ana ake ndipo azidyera ku malo wopatulika chifukwa kwa iye chakudyacho ndi chopatulika kwambiri chochokera pa chopereka chopsereza cha Yehova.”
Neka pripadnu Aronu i njegovim sinovima. Oni ih imaju blagovati na posvećenu mjestu. To je njemu vrlo svet dio Jahvinih paljenih žrtava. To neka bude trajna odredba.”
10 Tsiku lina munthu wina wamwamuna amene amayi ake anali Mwisraeli koma abambo ake anali Mwigupto anapita kwa Aisraeli ndipo anakangana ndi Mwisraeli wina ku msasa.
A sin jedne Izraelke, komu otac bijaše Egipćanin, iziđe među Izraelce i zametne u taboru svađu s nekim Izraelcem.
11 Munthu uja ananyoza dzina la Yehova ndi kulitemberera. Choncho anabwera naye kwa Mose. Dzina la amayi ake linali Selomiti, mwana wa Dibiri, wa fuko la Dani.
Uto sin Izraelke pogrdi Ime i opsuje ga. Tada ga dovedu Mojsiju. - Mati mu se zvala Šelomit, a bila je kći Dibrijeva iz plemena Danova. -
12 Anamuyika mʼndende mpaka atadziwa bwino chofuna cha Yehova.
Stave ga u zatvor dok im se ne očituje volja Jahvina.
13 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
Onda Jahve reče Mojsiju:
14 “Pita naye kunja kwa msasa munthu wotembererayo. Onse amene anamumva akutemberera asanjike manja awo pamutu pake ndipo gulu lonse la anthu limugende miyala.
“Izvedi psovača iz tabora. Potom svi oni koji su ga čuli neka stave svoje ruke na njegovu glavu. A onda neka ga sva zajednica kamenuje.
15 Choncho uza Aisraeli kuti, ‘Aliyense wotemberera Mulungu wake alangidwe.
Poslije toga ćeš ovako prozboriti Izraelcima: Tko god opsuje Boga svoga neka snosi svoju krivnju;
16 Aliyense wonyoza dzina la Yehova, mlendo ngakhale mbadwa, aphedwe. Gulu lonse la anthu limuponye miyala.
tko izgovori hulu na ime Jahvino neka se smakne - neka ga sva zajednica kamenuje; bio stranac ili domorodac, ako pohuli ime Jahvino, mora mrijeti.
17 “‘Ngati munthu wina aliyense achotsa moyo wa munthu mnzake, munthuyo ayenera kuphedwa.
Ako čovjek zada smrtan udarac drugome, mora se smaknuti.
18 Aliyense wopha chiweto cha mnzake ayenera kulipira china. Moyo kulipa moyo.
Tko usmrti živinče mora ga nadomjestiti: život za život.
19 Ngati munthu avulaza mnzake, nayenso amuchite zomwe wachitira mnzakeyo:
Tko ozlijedi svoga bližnjega neka mu se učini kako je on učinio:
20 kuthyola fupa kulipira kuthyola fupa, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino. Monga momwe anavulazira mnzake, amuvulaze chimodzimodzinso.
lom za lom, oko za oko, zub za zub - rana koju je on zadao drugome neka se zada i njemu.
21 Aliyense wopha chiweto cha mnzake, alipire chiweto china, koma aliyense wopha munthu ayenera kuphedwa.
Tko usmrti živinče mora ga nadoknaditi, ali tko ubije čovjeka mora umrijeti.
22 Lamulo la mlendo ndi mbadwa ndi limodzi lomweli. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Neka vam je jednak sud i strancu i domorocu. Jer ja sam Jahve, Bog vaš.”
23 Pamenepo Mose anawuza Aisraeli zimenezi, ndipo iwo anatulutsira munthu wotembererayo kunja kwa msasa ndi kumugenda miyala. Aisraeli anachita zimene Yehova analamula Mose.
Pošto je Mojsije to izložio Izraelcima, oni izvedu psovača izvan tabora i zaspu ga kamenjem. Učine, dakle, Izraelci kako je Jahve Mojsiju naredio.

< Levitiko 24 >