< Levitiko 23 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
Le Seigneur parla encore à Moïse, disant:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.
Parle aux enfants d’Israël, et tu leur diras: Voici les fêtes du Seigneur que vous appellerez saintes.
3 “‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.
Pendant six jours vous travaillerez; le septième jour, parce qu’il est le repos du sabbat, sera appelé saint: vous ne ferez aucun ouvrage en ce jour. C’est le sabbat du Seigneur dans toutes vos habitations.
4 “‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake:
Voici donc les fêtes saintes du Seigneur que vous devez célébrer en leurs temps.
5 Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba.
Au premier mois, au quatorzième jour du mois vers le soir, est la Pâque du Seigneur;
6 Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
Et au quinzième jour de ce mois est la solennité des azymes du Seigneur. Pendant sept jours vous mangerez des azymes.
7 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse.
Le premier jour sera pour vous très solennel et saint; vous ne ferez aucune oeuvre servile en ce jour;
8 Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’”
Mais vous offrirez un sacrifice avec du feu au Seigneur pendant sept jours; mais le septième jour sera plus solennel et plus saint; et vous ne ferez aucune œuvre servile en ce jour.
9 Yehova anawuza Mose kuti,
Le Seigneur parla encore à Moïse, disant:
10 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu.
Parle aux enfants d’Israël, et tu leur diras: Lorsque vous entrerez dans la terre que je vous donnerai moi-même, et que vous aurez moissonné le blé, vous apporterez des gerbes d’épis, prémices de votre moisson, au prêtre,
11 Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata.
Qui élèvera la botte devant le Seigneur, le second jour du sabbat, afin qu’elle soit acceptable en votre faveur, et il la sanctifiera.
12 Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
Et au même jour que la gerbe sera consacrée, un agneau sans tache, d’un an, sera immolé pour l’holocauste du Seigneur.
13 Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka.
Et seront offertes avec lui les libations: deux décimes de fleur de farine arrosée d’huile pour l’holocauste du Seigneur, et en odeur très suave; et aussi les libations de vin, la quatrième partie du hin.
14 Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
Vous ne mangerez ni pain, ni farine desséchée, ni bouillie provenant du blé, jusqu’au jour que vous en offrirez à votre Dieu. C’est un précepte perpétuel en toutes vos générations et en toutes vos habitations.
15 “‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu.
Vous compterez donc depuis le second jour du sabbat dans lequel vous aurez offert la gerbe des prémices, sept semaines pleines,
16 Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova.
Jusqu’au jour d’après la fin de la septième semaine, c’est-à-dire, cinquante jours; et c’est ainsi que vous offrirez un sacrifice nouveau au Seigneur,
17 Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha.
De toutes vos habitations, deux pains de prémices de deux décimes de fleur de farine fermentée, que vous cuirez pour les prémices du Seigneur;
18 Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova.
Et vous offrirez avec les pains sept agneaux sans tache d’un an, et un veau pris du troupeau de gros bétail, et deux béliers, et ils seront avec leurs libations pour un holocauste, en odeur suave pour le Seigneur.
19 Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano.
Vous sacrifierez aussi un bouc pour le péché et deux agneaux d’un an, hosties de sacrifices pacifiques.
20 Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe.
Et lorsque le prêtre les aura élevés avec les pains des prémices devant le Seigneur, ils deviendront à son usage.
21 Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
Et vous appellerez ce jour très solennel et très saint; vous ne ferez aucune œuvre servile en ce jour. Ce sera une loi éternelle en toutes vos habitations et en toutes vos générations.
22 “‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Quand vous moissonnerez le blé de votre terre, vous ne le couperez pas jusqu’au sol, et vous ne ramasserez point les épis restants, mais vous les laisserez pour les pauvres et les étrangers. C’est moi qui suis le Seigneur votre Dieu.
23 Yehova anawuza Mose kuti,
Le Seigneur parla encore à Moïse, disant:
24 “Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga.
Dis aux enfants d’Israël: Au septième mois, au premier jour du mois, sera pour vous un sabbat, un souvenir, les trompettes sonnant; et il sera appelé saint.
25 Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’”
Vous ne ferez aucune œuvre servile en ce jour, et vous offrirez un holocauste au Seigneur.
26 Yehova anawuza Mose kuti,
Le Seigneur parla encore à Moïse, disant:
27 “Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova.
Au dixième jour de ce septième mois, sera le jour très très solennel des expiations, et il sera appelé saint; or, vous affligerez vos âmes en ce jour, et vous offrirez un holocauste au Seigneur.
28 Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
Vous ne ferez aucune œuvre servile pendant tout ce jour, parce que c’est un jour de propitiation, afin que le Seigneur votre Dieu vous devienne propice.
29 Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
Tout homme qui ne sera point affligé en ce jour-là périra du milieu de ses peuples;
30 Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake.
Et celui qui fera quelque œuvre que ce soit, je le retrancherai du milieu de son peuple.
31 Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
Vous ne ferez donc aucune œuvre en ce jour; ce sera une loi perpétuelle pour vous en toutes vos générations et en toutes vos habitations.
32 Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”
C’est un sabbat de repos, et vous affligerez vos âmes au neuvième jour du mois: c’est depuis un soir jusqu’à un soir que vous célébrerez vos sabbats.
33 Yehova anawuza Mose kuti,
Le Seigneur parla encore à Moïse, disant:
34 “Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova.
Dis aux enfants d’Israël: Depuis le quinzième jour de ce septième mois, seront les fêtes des Tabernacles pendant sept jours en l’honneur du Seigneur.
35 Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa.
Le premier jour sera appelé très solennel et très saint: vous ne ferez aucune œuvre servile en ce jour.
36 Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.
Et pendant sept jours vous offrirez des holocaustes au Seigneur: le huitième jour aussi sera très solennel et très saint, et vous offrirez un holocauste au! Seigneur; car c’est une assemblée et des réunions: vous ne ferez aucune œuvre servile en ce jour.
37 (“‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku.
Ce sont là les fêtes du Seigneur que vous appellerez très solennelles et très saintes, et vous y offrirez des oblations au Seigneur, des holocaustes et des libations selon le rite de chaque jour;
38 Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)
Outre le sabbat du Seigneur, et vos dons et les choses que vous offrirez en vertu d’un vœu, ou que vous donnerez spontanément au Seigneur.
39 “‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso.
Depuis donc le quinzième jour du septième mois, quand vous aurez rassemblé tous les fruits de votre terre, vous célébrerez les fêtes du Seigneur pendant sept jours; au premier et au huitième jour sera un sabbat, c’est-à-dire un repos.
40 Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri.
Or, au premier jour vous prendrez des fruits de l’arbre le plus beau, des petites spathes de palmiers, des rameaux d’un arbre au feuillage épais et des saules du torrent, et vous vous réjouirez devant le Seigneur votre Dieu:
41 Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri.
Et vous célébrerez sa solennité pendant sept jours par an: ce sera une loi perpétuelle en vos générations. Au septième mois vous célébrerez ces fêtes,
42 Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa
Et vous habiterez sous les ombrages pendant sept jours. Quiconque est de la race d’Israël demeurera sous les tentes;
43 kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Afin que vos descendants apprennent que c’est sous les tentes que j’ai fait habiter les enfants d’Israël, lorsque je les retirai de la terre d’Egypte. Je suis le Seigneur votre Dieu.
44 Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.
C’est ainsi que Moïse parla sur les solennités du Seigneur aux enfants d’Israël.