< Levitiko 23 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahweh said to Moses/me,
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.
“Tell the Israeli people about the festivals that I have chosen, the days when you all must gather together [to worship me].”
3 “‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.
“You may work for six days [each week], but on the seventh day you must not do any work. You must rest. It is a sacred/holy day when you must gather together [to worship me]. Wherever you live, you must rest on that day.”
4 “‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake:
“There are festivals that I have established for you. Those will also be sacred/holy days when you must gather together [to worship me].
5 Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba.
[The first festival is] (the Passover/when you remember that I spared your ancestors when I killed all the firstborn Egyptian sons). That festival will begin at twilight/dusk/sunset on the chosen day (each spring/in March or April each year), [and end on the following day].
6 Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
The next day, the Festival of Eating Bread That Has No Yeast will begin. That festival will continue for seven days. During that time, the bread that you eat must be made without yeast.
7 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse.
On the first day of that festival, you all must stop your regular work and you must gather together [to worship me].
8 Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’”
On each of the seven days, you must present to me [several animals to be] an offering/sacrifice to be completely burned [on the altar]. On the seventh day, you all must again stop your regular work and gather to worship me.”
9 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahweh also told Moses/me
10 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu.
to tell the Israeli people [about other festivals]. He said, “When you arrive in the land which I am giving to you, and you harvest your crops [for the first time] there, bring to the priest some of the first grain that you harvest.
11 Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata.
On the day after the [next] Sabbath/rest day, the priest will lift it up [high to dedicate it] to me, in order that I will accept it as your [gift].
12 Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
That same day, you must sacrifice to me a one-year-old male lamb that has no defects. You must burn it [on the altar].
13 Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka.
You must also burn an offering of grain. That offering must consist of (three quarts/3.5 liters) of good flour mixed with [olive] oil. The smell [of those things burning] will be very pleasing to me. Along with that, you must also offer one quart/liter of wine, which will be a liquid offering.
14 Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
Do not eat any bread or any roasted grain or unroasted grain on that day until after you have brought those offerings to me, your God. You must always obey [LIT] those commands, wherever you live.”
15 “‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu.
“Seven weeks after the priest offers that grain to me,
16 Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova.
on the next/50th day after he offers it, [each family] must bring to me an offering from the new crop of grain.
17 Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha.
From your homes, bring two loaves of bread [to the priest]. He will lift them up [high to dedicate them] as an offering to me. Those loaves must be baked from three quarts/liters of good flour that has yeast mixed with it. That bread will be an offering to me from the first wheat that you harvest [each year].
18 Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova.
Along with this bread, you must present to me seven one-year-old lambs with no defects, one young bull, and two rams. They must all be completely burned [on the altar]. All those offerings, with the grain offering and the wine offering, will be burned, and the smell [of all those things burning] will be very pleasing to me.
19 Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano.
Then you must also kill one male goat to be an offering/sacrifice for your sins, and two one-year-old male lambs to be an offering to enable you to maintain fellowship with me.
20 Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe.
The priest will lift up these offerings [high to dedicate them] to me. He will also offer the loaves of bread that were baked from the first wheat that you harvest. Those offerings are sacred to me, but they are for the priests [to eat].
21 Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
On that day, you must stop your regular work and gather to worship me. You must always obey those instructions/commands, and you must obey them wherever you live.
22 “‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
“When you harvest the grain in your fields, do not harvest the grain along the edges of the fields, and do not pick up the grain that the harvesters drop. Leave that grain for the poor people and for the foreigners who are living among you. [Do not forget that it is] I, Yahweh your God, [who am commanding those things]!”
23 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahweh also told Moses/me
24 “Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga.
to give these instructions/commands to the Israeli people: “[Each year] in September, on the day that I have chosen, you all must celebrate it by completely resting. You must not do any work on that day. When [the priests] blow their trumpets loudly, you all must gather together to worship me.
25 Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’”
All of you must not do your regular work on that day. Instead, you must present offerings to me that will be burned [on the altar].”
26 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahweh also said to Moses/me,
27 “Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova.
“You must celebrate a day [on which you request that I] forgive you for the sins that you have committed. That day will be nine days after the festival [when the priests blow] the trumpets. On that day you must (fast/abstain from eating food). You must gather together to worship me and present offerings to me that will be burned [on the altar].
28 Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
You must not do any work on that day, because it is the day when the priests will offer sacrifices to me to (atone for/ask me to forgive) your sins.
29 Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
You must expel from your group anyone who does not (fast/abstain from eating food) on that day.
30 Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake.
I will get rid of anyone who does any kind of work on that day.
31 Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
You must not work at all! You must always obey those instructions/commands, and you must obey them wherever you live.
32 Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”
That day will be a day of complete rest for all of you, and on that day you must (fast/abstain from eating food) [to show that you are sorry for having sinned]. That day of rest and (fasting/abstaining from eating food) will begin on the evening before the day in which you ask me to forgive you for your sins, and it will end on the evening of the following day.”
33 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahweh also said to Moses/me,
34 “Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova.
“Tell the Israeli people that [each year] they must also celebrate a festival of living in temporary shelters. That festival will begin five days after the day in which they request me to forgive them for their sins. It will last for seven days.
35 Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa.
On the first day of that festival, the people must gather together to worship me, and they must not do any regular work on that day.
36 Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.
On each of the seven days of the festival, they must present to me an offering [of animals] that will be burned [on the altar]. On the next day, they must gather again to worship me and present to me another animal that will be burned [on the altar]. That also will be a sacred gathering, and they must not work on that day, either.
37 (“‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku.
“[To summarize], those are the festivals that I have appointed. Celebrate those sacred festivals by gathering together to present to me all the various offerings that will be burned [on the altar]—animals that will be burned completely, and offerings of grain, and offerings to enable the Israeli people to maintain fellowship with me, and offerings of wine. Each offering must be brought on the day that I have indicated.
38 Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)
(Those festivals must be celebrated/You must celebrate those festivals) in addition to [worshiping on] the (Sabbath days/days of rest). And all those offerings must be given in addition to the offerings that people personally decide to give, and in addition to the offerings that people make to accompany the solemn promises that they have made, or offerings that people make (voluntarily/because they themselves want to).
39 “‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso.
“[Returning to my instructions about] the Festival of Living in Temporary Shelters, you must celebrate this festival after you have harvested all the crops. On the first day and on the last day of that festival, you must rest completely.
40 Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri.
But on the first day, you are permitted to pick fruit from trees. Cut palm fronds/branches and other leafy branches from trees or from bushes that grow by the streams, [and make shelters/huts to live in for that week]. Then rejoice in my presence for those seven days.
41 Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri.
You must celebrate this festival for seven days every year. You must never stop obeying my commands/instructions for that festival. You must celebrate it in September.
42 Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa
During the seven days of that festival, all of you people who have been Israelis your entire lives must live in shelters/huts.
43 kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
That will remind your descendants that their ancestors lived in shelters [for many years] after I rescued them from Egypt. [Do not forget that] I, Yahweh your God, [am the one who is commanding this].”
44 Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.
So Moses/I gave to the Israeli people all those instructions concerning the festivals that Yahweh [wanted them to celebrate] each year.