< Levitiko 23 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke unto Moses, saying,
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.
Speak unto the children of Israel, and say unto them, The feasts of the Lord, which ye shall proclaim to be holy convocations, —these are my feasts:
3 “‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.
Six days may work be done; but on the seventh day is the sabbath of rest, a holy convocation; no kind of work shall ye do thereon; it is the sabbath [holy] unto the Lord in all your dwellings.
4 “‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake:
These are the feasts of the Lord, the holy convocations, which ye shall proclaim in their seasons:
5 Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba.
On the fourteenth day of the first month, toward evening, is the passover-lamb to be offered unto the Lord.
6 Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
And on the fifteenth day of the same month is the feast of unleavened bread unto the Lord: seven days must ye eat unleavened bread.
7 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse.
On the first day there shall be a holy convocation unto you; no servile work shall ye do thereon.
8 Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’”
And ye shall offer an offering made by fire unto the Lord seven days: on the seventh day is a holy convocation; no servile work shall ye do.
9 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke unto Moses, saying,
10 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu.
Speak unto the children of Israel, and say unto them, When ye shall have come into the land which I give unto you, and reap the harvest thereof: then shall ye bring an omer full of the first of your harvest unto the priest;
11 Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata.
And he shall wave the omer before the Lord, that it may be favorably received for you; on the morrow after the holy day shall the priest wave it.
12 Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
And ye shall offer on the day when ye wave the omer, a male sheep without blemish of the first year for a burnt-offering unto the Lord.
13 Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka.
And the meat-offering thereof shall be two tenth parts of fine flour mingled with oil, as an offering made by fire unto the Lord, for a sweet savor; with its drink-offering of wine, the fourth part of a hin.
14 Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
And neither bread, nor parched corn, nor green ears, shall ye eat, until the self-same day, until ye have brought the offering of your God: it shall be a statute forever throughout your generations in all your dwellings.
15 “‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu.
And ye shall count unto you from the morrow after the holy day, from the day that ye bring the omer of the wave-offering, [that] it be seven complete weeks:
16 Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova.
Even unto the morrow after the seventh week shall ye number fifty days; and ye shall then offer a new meat-offering unto the Lord.
17 Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha.
Out of your own habitations shall ye bring two wave-loaves of two tenth parts; of fine flour shall they be; leavened shall they be baked; they are the first-fruits unto the Lord.
18 Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova.
And ye shall offer with the bread seven sheep without blemish of the first year, and one young bullock, and two rams: they shall be for a burnt-offering unto the Lord, with their meat-offering, with their drink-offerings, an offering made by fire, of a sweet savor unto the Lord.
19 Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano.
And ye shall sacrifice one he-goat for a sin-offering, and two sheep of the first year for a sacrifice of peace-offering.
20 Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe.
And the priest shall make with them together with the bread of the first-fruits a waving before the Lord, together with the two sheep; holy shall they be to the Lord for the priest.
21 Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
And ye shall proclaim on the self-same day, that it may be a holy convocation unto you; no servile work shall ye do; it shall be a statute for ever in all your dwellings throughout your generations.
22 “‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
And when ye reap the harvest of your land, thou shalt not cut away altogether the corners of thy field when thou reapest, and the gleaning of thy harvest shalt thou not gather up; unto the poor, and to the stranger shalt thou leave them: I am the Lord your God.
23 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke unto Moses, saying,
24 “Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga.
Speak unto the children of Israel, saying, In the seventh month, on the first day of the month, shall ye have a rest, a [day of] memorial of sounding the cornet, a holy convocation.
25 Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’”
No servile work shall ye do: and ye shall offer an offering made by fire unto the Lord.
26 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke unto Moses, saying,
27 “Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova.
But on the tenth day of this seventh month is the day of atonement, a holy convocation shall it be unto you, and ye shall fast; and ye shall offer an offering made by fire unto the Lord.
28 Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
And no manner of work shall ye do on this same day; for it is a day of atonement, to make an atonement for you before the Lord your God.
29 Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
For whatsoever person it be that fasteth not on this same day, shall be cut off from among his people.
30 Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake.
And if there be any person that doth any work on this same day, then will I destroy the same person from among his people.
31 Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
No manner of work shall ye do: it shall he a statute for ever throughout your generations, in all your dwellings.
32 Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”
A sabbath of rest it shall be unto you, and ye shall fast: on the ninth day of the month at evening [shall ye begin], from evening unto evening shall ye celebrate your sabbath.
33 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke unto Moses, saying,
34 “Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova.
Speak unto the children of Israel, saying, On the fifteenth day of this seventh month, shall be the feast of tabernacles for seven days unto the Lord.
35 Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa.
On the first day shall be a holy convocation; no servile work shall ye do.
36 Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.
Seven days shall ye offer an offering made by fire unto the Lord: on the eighth day shall be a holy convocation unto you; and ye shall offer an offering made by fire unto the Lord, it is a solemn assembly; no servile work shall ye do.
37 (“‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku.
These are the feasts of the Lord, which ye shall proclaim to be holy convocations, to offer an offering made by fire unto the Lord, burnt-offering, and meat-offering, sacrifice, and drink-offerings, every thing upon its day:
38 Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)
Beside the sabbaths of the Lord, and beside your gifts, and beside all your vows, and beside all your freewill-offerings, which ye may give unto the Lord.
39 “‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso.
But on the fifteenth day of the seventh month, when ye have gathered in the fruit of the land, shall ye keep the feast of the Lord seven days: on the first day shall be a rest, and on the eighth day shall be a rest.
40 Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri.
And ye shall take unto yourselves on the first day the fruit of the tree hadar, branches of palm-trees, and the boughs of the myrtle-tree, and willows of the brook: and ye shall rejoice before the Lord your God seven days.
41 Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri.
And ye shall keep it as a feast unto the Lord seven days in the year: it shall be a statute for ever throughout your generations; in the seventh month shall ye celebrate it.
42 Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa
In booths shall ye dwell seven days; all that are Israelites born shall dwell in booths.
43 kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
In order that your generations may know, that I caused the children of Israel to dwell in booths, when I brought them forth out of the land of Egypt: I am the Lord your God.
44 Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.
And Moses declared the feasts of the Lord unto the children of Israel.