< Levitiko 23 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Mluvil opět Hospodin Mojžíšovi, řka:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.
Mluv k synům Izraelským a rci jim: Slavnosti Hospodinovy, kteréž nazývati budete shromáždění svatá, tyto jsou slavnosti mé:
3 “‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.
Šest dní dělati budete, dne pak sedmého sobota odpočinutí jest, shromáždění svaté bude. Žádného díla nedělejte, nebo jest sobota Hospodinova, ve všech příbytcích vašich.
4 “‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake:
Protož tyto jsou slavnosti Hospodinovy, shromáždění svatá, kteréž slaviti budete v časy jich určité:
5 Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba.
Měsíce prvního, čtrnáctého dne téhož měsíce u večer bude Fáze Hospodinovo.
6 Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
A patnáctého dne téhož měsíce svátek přesnic bude Hospodinu; za sedm dní přesné chleby jísti budete.
7 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse.
Dne prvního sbor svatý míti budete; žádného díla robotného nebudete dělati.
8 Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’”
Ale obětovati budete obět ohnivou Hospodinu za sedm dní. Dne také sedmého sbor svatý bude; žádného díla robotného nebudete dělati.
9 Yehova anawuza Mose kuti,
I mluvil Hospodin k Mojžíšovi, řka:
10 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu.
Mluv k synům Izraelským a rci jim: Když vejdete do země, kterouž já dávám vám, a žíti budete obilí její, tedy přinesete snopek prvotiny žně vaší k knězi.
11 Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata.
Kterýž obraceti bude sem i tam snopek ten před Hospodinem, aby byl příjemnou obětí za vás; nazejtří po sobotě obraceti jej bude kněz.
12 Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
Kterého dne obraceti budete snopek ten, téhož zabijete beránka ročního bez poškvrny v obět zápalnou Hospodinu.
13 Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka.
Též i obět suchou jeho, dvě desetiny mouky bělné olejem zadělané, v obět ohnivou Hospodinu u vůni příjemnou, a mokrou obět jeho, vína čtvrtý díl míry hin.
14 Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
Chleba pak, ani pražmy, ani zrní vymnutého nebudete jísti, až právě do toho dne, když obětovati budete obět Bohu svému. Ustanovení to věčné bude v pronárodech vašich, ve všech příbytcích vašich.
15 “‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu.
Počtete sobě také od prvního dne po sobotě, ode dne, v němž jste obětovali snopek sem i tam obracení, (plných sedm téhodnů ať jest),
16 Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova.
Až do prvního dne po sedmém téhodni, sečtete padesáte dní, a tehdy obětovati budete novou obět suchou Hospodinu.
17 Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha.
Z příbytků svých přinesete chleby sem i tam obracení, dva bochníky ze dvou desetin mouky bělné budou; kvašené je upečete, prvotiny jsou Hospodinu.
18 Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova.
A s tím chlebem obětovati budete sedm beránků ročních bez vady, a volka mladého jednoho, a skopce dva; obět zápalná budou Hospodinu, s obětmi svými suchými i mokrými, obět ohnivá vůně spokojující Hospodina.
19 Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano.
Zabijete také kozla jednoho za hřích, a dva beránky roční k oběti pokojné.
20 Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe.
I bude je kněz sem i tam obraceti s chleby prvotin v obět sem i tam obracení před Hospodinem, i s těmi dvěma beránky; a budou svaté věci Hospodinu, a dostanou se knězi.
21 Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
I vyhlásíte v ten den slavnost, shromáždění svaté míti budete, žádného díla robotného nebudete dělati. Ustanovení to bude věčné ve všech příbytcích vašich, v pronárodech vašich.
22 “‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
A když budete žíti obilé krajiny vaší, nesežneš všeho až do konce pole svého, a pozůstalých klasů po žni své nebudeš sbírati; chudému a příchozímu zanecháš jich: Já jsem Hospodin Bůh váš.
23 Yehova anawuza Mose kuti,
Mluvil ještě Hospodin k Mojžíšovi, řka:
24 “Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga.
Mluv synům Izraelským takto: Měsíce sedmého, v první den téhož měsíce, budete míti odpočinutí, památku troubení, shromáždění svaté držíce.
25 Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’”
Žádného díla robotného nebudete dělati, a budete obětovati obět ohnivou Hospodinu.
26 Yehova anawuza Mose kuti,
Mluvil také Hospodin k Mojžíšovi, řka:
27 “Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova.
Desátý pak den každého měsíce sedmého den očišťování jest. Shromáždění svaté míti budete, a ponižovati budete životů svých, a obětovati obět ohnivou Hospodinu.
28 Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
Žádného díla nebudete dělati v ten den; nebo den očišťování jest, k očišťování vás před Hospodinem Bohem vaším.
29 Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
A všeliká duše, kteráž by neponižovala se toho dne, vyhlazena bude z lidu svého.
30 Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake.
Kdož by koli dílo nějaké dělal toho dne, zatratím člověka toho z lidu jeho.
31 Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
Žádného díla nedělejte. Ustanovení to bude věčné v pronárodech vašich, ve všech příbytcích vašich.
32 Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”
Sobotu odpočinutí míti budete, když ponižovati budete duší svých, devátého dne téhož měsíce u večer; od večera až do druhého večera držeti budete sobotu svou.
33 Yehova anawuza Mose kuti,
Mluvil také Hospodin k Mojžíšovi, řka:
34 “Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova.
Mluv synům Izraelským a rci: Každého patnáctého dne měsíce sedmého slavnost stánků za sedm dní bude Hospodinu.
35 Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa.
Dne prvního shromáždění svaté bude; žádného díla robotného nebudete dělati.
36 Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.
Za sedm dní obětovati budete obět ohnivou Hospodinu. Dne osmého shromáždění svaté míti budete, a obětovati budete obět ohnivou Hospodinu; svátek jest, žádného díla robotného nebudete dělati.
37 (“‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku.
To jsou slavnosti Hospodinovy, kteréž slaviti budete, mívajíce shromáždění svatá, abyste v nich obětovali obět ohnivou Hospodinu, zápal, obět suchou, obět pokojnou, a oběti mokré, jedno každé ve dni svém,
38 Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)
Kromě sobot Hospodinových, a kromě darů vašich, i všech slibů vašich a kromě všech dobrovolných obětí vašich, kteréž dávati budete Hospodinu.
39 “‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso.
A však dne patnáctého toho měsíce sedmého, když byste shromáždili úrody země, světiti budete svátek Hospodinův za sedm dní. Dne prvního odpočinutí bude, tolikéž dne osmého bude odpočinutí.
40 Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri.
A naberouce sobě dne prvního ovoce z stromů krásných, a ratolestí palmových, a větvoví z stromů hustých, a vrbí od potoku, veseliti se budete před Hospodinem Bohem svým za sedm dní.
41 Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri.
A tak držeti budete ten svátek Hospodinův za sedm dní každého roku. Ustanovení to bude věčné v pronárodech vašich; každého měsíce sedmého slaviti jej budete.
42 Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa
V staních zůstanete za sedm dní. Kdožkoli doma zrozený jest v Izraeli, v staních zůstávati budete,
43 kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Aby věděli potomci vaši, že jsem choval v staních syny Izraelské, když jsem je vyvedl z země Egyptské: Já Hospodin Bůh váš.
44 Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.
I oznámil Mojžíš slavnosti Hospodinovy synům Izraelským.

< Levitiko 23 >