< Levitiko 22 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
И рече Господь к Моисеовы, глаголя:
2 “Uza Aaroni ndi ana ake kuti azilemekeza zinthu zopatulika zimene Aisraeli azipereka kwa Ine, kuti asayipitse dzina langa loyera. Ine ndine Yehova.
рцы Аарону и сыном его, да внимают от святынь сынов Израилевых, и да не осквернят имене святаго Моего, елика они освящают Ми: Аз Господь.
3 “Uwawuze kuti ngati wina aliyense mwa zidzukulu zawo mʼmibado yonse imene ikubwera adzayandikira zinthu zopatulika zimene ana a Israeli apereka kwa Yehova, ali wodetsedwa, ameneyo achotsedwe pamaso pa Yehova. Ine ndine Yehova.
Рцы им: в роды вашя всяк человек, иже аще приступит от всякаго семене вашего ко святым, елика аще освятят сынове Израилевы Господу, и нечистота его на нем будет, потребится душа оная от Мене: Аз Господь Бог ваш.
4 “Munthu aliyense mwa zidzukulu za Aaroni amene ali ndi khate kapena amatulutsa zoyipa mʼthupi mwake, asadye zinthu zopatulika mpaka atayeretsedwa. Wansembe angakhale wodetsedwa atakhudzana ndi chinthu chimene chadetsedwa ndi chinthu chakufa kapena kukhudza munthu amene wataya umuna,
И человек от семене Аарона жерца, и сей прокажен, или семя изливает, от святых да не снест, дондеже очистится: и прикасаяйся всякой нечистоте души, или человек, емуже аще изыдет от его ложа семя,
5 kapena kukhudza chilichonse chokwawa chomwe chimadetsa munthu, kapena kukhudza munthu amene angamudetse, kapenanso kukhudza kanthu kena kalikonse kodetsedwa.
или иже аще прикоснется всякому гаду нечисту, иже осквернит его, или человеку, иже осквернит его, по всякой нечистоте его:
6 Tsono ngati wansembe angakhudze chilichonse mwa zimenezi ndiye kuti adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Asadye chopereka chilichonse chopatulika mpaka atasamba thupi lake lonse.
душа, яже аще прикоснется их, нечиста будет до вечера: да не снест от святых, аще не омыет тела своего водою,
7 Munthuyo adzakhala woyeretsedwa pamene dzuwa lalowa, ndipo angathe kudya chopereka chopatulikacho popeza ndi chakudya chake.
и зайдет солнце, и чист будет: и тогда да снест от святых, яко хлеб его есть.
8 Wansembe sayenera kudya chinthu chofa chokha kapena chojiwa ndi chirombo kuopa kuti angadzidetse ndi chakudyacho. Ine ndine Yehova.
Мертвечины и звероядины да не снест, еже осквернитися ему в них: Аз Господь.
9 “‘Choncho ansembe azisunga malamulo angawa kuti asapezeke wolakwa ndi kufa chifukwa chopeputsa malamulowa. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.
И да сохранят повеления Моя, да не приимут сих ради греха, и измрут за них, аще осквернят их: Аз Господь Бог освящаяй их.
10 “‘Aliyense amene si wabanja la wansembe, kaya ndi mlendo wa wansembe, kapena wantchito wake, asadye chopereka chopatulika.
И всяк иноплеменник да не снест святынь: приселник иереев или наемник да не снест святынь.
11 Koma kapolo amene wagulidwa ndi ndalama kapena kubadwira mʼbanja la wansembe angathe kudya chakudya cha wansembeyo.
Аще же жрец пристяжет душу пристяжаную сребром, сия да снест хлебы его: и домочадцы его, и сии да снедят хлебы его.
12 Mwana wamkazi wa wansembe amene wakwatiwa ndi munthu amene si wansembe, asadyeko nsembe zopatulikazo.
И дщерь человека жерца, аще посягнет за мужа иноплеменника, сия от начатков святых да не снест.
13 Koma mwana wamkazi wa wansembe amene ali wamasiye kapena wosudzulidwa, ndipo alibe mwana, komanso anabwerera ku nyumba ya abambo ake monga pa nthawi ya utsikana wake, angathe kudya chakudya cha abambo ake. Mlendo asadye chakudya chopatulika.
И дщерь жерца аще будет вдова или отпущена, плода же не будет ей, возвратится в дом отца своего, по юности своей, от хлебов отца своего да снест: всяк же иноплеменник да не снест от них.
14 “‘Ngati munthu wina aliyense adya chopereka chopatulika mosadziwa, munthuyo amubwezere wansembe chinthu chopatulikacho ndipo awonjezerepo limodzi la magawo asanu a chinthucho.
И человек, иже аще яст святая по неведению, и да приложит пятую свою часть ко истому, и да даст сие жерцу святое.
15 Choncho ansembe asayipitse zopereka zopatulika za Aisraeli zimene apereka kwa Yehova
И да не осквернят святынь сынов Израилевых, ихже они отделяют Господу:
16 ndipo asachimwitse ndi kupalamulitsa Aisraeli powalola kudya zakudya zawo zopatulika. Ine ndine Yehova amene ndimawayeretsa.’”
и да не наведут на себе беззаконие преступления, внегда ясти им святыню их, яко Аз Господь освящаяй их.
17 Yehova anawuza Mose kuti,
И рече Господь к Моисею, глаголя:
18 “Yankhula ndi Aaroni, ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse, ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati wina aliyense wa inu, Mwisraeli kapena mlendo amene akukhala mu Israeli abwera ndi mphatso ya nsembe yopsereza kwa Yehova, kupereka chimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu,
глаголи Аарону и сыном его и всему сонму Израилеву и речеши к ним: человек человек от сынов Израилевых, или от пришлец прилежащих к ним во Израили, иже аще принесет дары своя по всякому исповеданию своему, или по всякому изволению своему, елика аще принесут Господу на всесожжение,
19 ndiye kuti abwere ndi ngʼombe yayimuna, nkhosa yayimuna kapena mbuzi yayimuna. Izi zikhale zopanda chilema kuti zilandiridwe.
приятны вам непорочны мужеск пол от стад волов, или от овен и от коз:
20 Musapereke nyama iliyonse yokhala ndi chilema chifukwa sidzalandiridwa mʼmalo mwanu.
всех, елика аще имут порок на себе, да не принесут Господу, понеже неприятно будет вам.
21 Pamene wina aliyense abweretsa ngʼombe kapena nkhosa kuti ikhale nsembe yachiyanjano kwa Yehova, kukwaniritsa zimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu, nyamayo iyenera kukhala yangwiro ndi yopanda chilema kuti ilandiridwe.
И человек иже аще принесет жертву спасения Господу, отлучив обет или по изволению, или в праздники вашя, от стад волов или от овец, непорочно да будет в приятие, всяк порок да не будет на нем:
22 Musapereke kwa Yehova nyama zakhungu, zovulala kapena zolumala, kapena nyama zimene zikutulutsa mafinya mʼthupi mwake, kapena zimene zili ndi nthenda yonyerenyetsa, kapena zimene zili ndi mphere. Nyama zotere musaziyike pa guwa kuti zikhale nsembe yopsereza kwa Yehova.
слепо, или сокрушено, или язык урезан имущо, или червиво, или крастово, или лишаво, да не принесут тех Господу, и в жертву не дадите от них на олтарь Господви:
23 Koma mungathe kupereka ngʼombe yayimuna kapena nkhosa imene ili ndi chiwalo chachitali kapena chachifupi kukhala nsembe yaufulu. Koma simungayipereke ngati nsembe yoperekera zimene munalumbirira chifukwa sidzalandiridwa.
и телца или овцу ухорезну, или безхвостну, в заколение сотвориши я себе (по изволению), в обет же твой да не приимется:
24 Nyama iliyonse imene mavalo ake ndi onyuka kapena ophwanyika, ongʼambika kapena oduka, musamayipereke kwa Yehova mʼdziko lanu.
емуже суть ятра сокрушена, и емуже раздавлена, и изрезана, и исторжена, да не принесете сих Господу, и в земли вашей да не сотворите.
25 Ndipo musalandire nyama zotere kuchokera kwa mlendo ndi kuzipereka kukhala zakudya za Mulungu wanu. Zimenezi sizidzalandiridwa mʼmalo mwanu chifukwa zili ndi chilema ndipo ndi zolumala.’”
И от руки иноплеменника да не принесете даров Богу вашему от всех сих, яко вреждения суть на них, порок на них, не приимутся сия от вас.
26 Yehova anawuza Mose kuti,
И рече Господь к Моисею, глаголя:
27 “Pamene mwana wangʼombe, mwana wankhosa kapena mwana wambuzi wabadwa, akhale ndi make kwa masiku asanu ndi awiri. Kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu mpaka mʼtsogolo mwake, angathe kulandiridwa kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
телец, или овча, или козля, егда родится, да будет седмь дний под материю своею, в день же осмый и далее принесется в дар, принос Господу:
28 Musaphe ngʼombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wake tsiku limodzi. Muyidye pa tsiku lomwelo; musasiyeko ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
и телца и овчате вкупе с материю да не заколете в един день,
29 “Pamene mupereka nsembe yoyamika kwa Yehova, muyipereke mwakufuna kwanu mu njira yoti ilandiridwe mʼmalo mwanu.
аше же пожреши жертву обет радования Господви, приятно вам пожрите е:
30 Muyidye pa tsiku lomwelo, wosasiyako ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
сия в тойже день да снестся, да не оставите от мяс на утрие: Аз есмь Господь.
31 “Choncho sungani malamulo anga ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.
И сохраните заповеди Моя и сотворите я: Аз Господь:
32 Musanyoze dzina langa loyera. Koma lilemekezedwe pakati pa Aisraeli. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani
и не оскверните имене Святаго, и освящуся посреде сынов Израилевых: Аз Господь освящаяй вас,
33 ndipo ndine amene ndinakutulutsani mu Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.”
изведый вы из земли Египетския, яко быти вам в Бога: Аз Господь.

< Levitiko 22 >