< Levitiko 22 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
LEUM GOD El sapkin nu sel Moses
2 “Uza Aaroni ndi ana ake kuti azilemekeza zinthu zopatulika zimene Aisraeli azipereka kwa Ine, kuti asayipitse dzina langa loyera. Ine ndine Yehova.
elan fahk nu sel Aaron ac wen luo natul, “Kowos fah tia akpusiselye Ine mutal luk, ke ma inge kowos fah aklosye kowos sifacna ke kowos ac orekma ke mwe kisa mutal ma mwet Israel elos kisakin nu sik. Nga LEUM GOD.
3 “Uwawuze kuti ngati wina aliyense mwa zidzukulu zawo mʼmibado yonse imene ikubwera adzayandikira zinthu zopatulika zimene ana a Israeli apereka kwa Yehova, ali wodetsedwa, ameneyo achotsedwe pamaso pa Yehova. Ine ndine Yehova.
Kutena sin fwil nutuwos fin tia nasnas ac el tuku apkuran nu ke mwe kisa mutal su mwet Israel elos kisakin nu sik, na mwet sacn el tia ku in sifilpa kulansap ke loang uh. Oakwuk se inge ac fah ma nu ke pacl nukewa fahsru. Nga LEUM GOD.
4 “Munthu aliyense mwa zidzukulu za Aaroni amene ali ndi khate kapena amatulutsa zoyipa mʼthupi mwake, asadye zinthu zopatulika mpaka atayeretsedwa. Wansembe angakhale wodetsedwa atakhudzana ndi chinthu chimene chadetsedwa ndi chinthu chakufa kapena kukhudza munthu amene wataya umuna,
“Wangin sie sin mwet tol in fwil natul Aaron su oasr mas sensenkinyuk ke mano, ku sroano koluk soror kacl, fah kang kutena mwe kisa mutal nwe ke na el nasnasla. Kutena mwet tol el fah tia nasnas el fin kahlye kutena ma su tia nasnas ke sripen el pusralla monin ma misa, ku fin oasr sroano koluk fahsr kacl,
5 kapena kukhudza chilichonse chokwawa chomwe chimadetsa munthu, kapena kukhudza munthu amene angamudetse, kapenanso kukhudza kanthu kena kalikonse kodetsedwa.
ku el fin pusralla soko kosro ku sie mwet ma tia nasnas.
6 Tsono ngati wansembe angakhudze chilichonse mwa zimenezi ndiye kuti adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Asadye chopereka chilichonse chopatulika mpaka atasamba thupi lake lonse.
Ouinge, kutena mwet tol su tia nasnas el fah mutana in tia nasnas lal nwe ke ekela, ac finne ekela el fah tiana kang kutena mwe kisa mutal nwe ke na el yihla.
7 Munthuyo adzakhala woyeretsedwa pamene dzuwa lalowa, ndipo angathe kudya chopereka chopatulikacho popeza ndi chakudya chake.
Tukun faht uh tili, na el fah nasnasla ac el ku in kang mwe kisa mutal, su pa ingan mwe mongo nal.
8 Wansembe sayenera kudya chinthu chofa chokha kapena chojiwa ndi chirombo kuopa kuti angadzidetse ndi chakudyacho. Ine ndine Yehova.
El fah tia kang ikwen kutena kosro ma sifacna misa ku anwuki sin kosro lemnak; ma inge ac oru el tia nasnas. Nga LEUM GOD.
9 “‘Choncho ansembe azisunga malamulo angawa kuti asapezeke wolakwa ndi kufa chifukwa chopeputsa malamulowa. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.
“Mwet tol nukewa fah liyaung oakwuk ma nga orala inge. Elos fin tia liyaung, na ac fah oasr mwatalos ac elos ac misa, ke sripen elos seakos oakwuk mutal luk. Nga LEUM GOD, ac nga akmutalyalos.
10 “‘Aliyense amene si wabanja la wansembe, kaya ndi mlendo wa wansembe, kapena wantchito wake, asadye chopereka chopatulika.
“Mwet in sou lun mwet tol mukena fah ku in mongo ke mwe kisa mutal; wangin sie mwet saya ku in kang — finne mwet su mutwata walil, ku mwet ma el moli nu se in orekma lal.
11 Koma kapolo amene wagulidwa ndi ndalama kapena kubadwira mʼbanja la wansembe angathe kudya chakudya cha wansembeyo.
Tusruktu sie mwet foko lun mwet tol, su el molela ke mani lal sifacna, ku su ma isusla in lohm sel, fah ku in mongo ke mwe mongo ma itukyang nun mwet tol.
12 Mwana wamkazi wa wansembe amene wakwatiwa ndi munthu amene si wansembe, asadyeko nsembe zopatulikazo.
Sie acn nutin mwet tol su payuk sin sie mwet su tia mwet tol, fah tia ku in kang kutena mwe kisa mutal.
13 Koma mwana wamkazi wa wansembe amene ali wamasiye kapena wosudzulidwa, ndipo alibe mwana, komanso anabwerera ku nyumba ya abambo ake monga pa nthawi ya utsikana wake, angathe kudya chakudya cha abambo ake. Mlendo asadye chakudya chopatulika.
Tusruktu sie acn nutin mwet tol ma wangin tulik natu ac el katinmasla, ku su ma mukul tuma uh sisla, ac el foloko in tuh muta inpoun papa tumal in lohm sel, el ku in kang mongo itukyang nun papa tumal ke sripen el sie mwet tol. Mwet na in sou lun mwet tol mukena pa ku in kang ma inge.
14 “‘Ngati munthu wina aliyense adya chopereka chopatulika mosadziwa, munthuyo amubwezere wansembe chinthu chopatulikacho ndipo awonjezerepo limodzi la magawo asanu a chinthucho.
“Kutena mwet su tia ma in sou lun mwet tol fin mongo ke mwe kisa mutal ke tia etu lal, el fah moli nu sin mwet tol molin ma el kangla, ac laesla ke percent longoul.
15 Choncho ansembe asayipitse zopereka zopatulika za Aisraeli zimene apereka kwa Yehova
Mwet tol el fah tia aklusrongtenye mwe kisa mutal,
16 ndipo asachimwitse ndi kupalamulitsa Aisraeli powalola kudya zakudya zawo zopatulika. Ine ndine Yehova amene ndimawayeretsa.’”
ke el lela kutena mwet su tia fal in mongo kac in kang. Ouiya se inge ac fah sang mwata ac kalya nu sin kain mwet se inge. Nga LEUM GOD, ac nga oru kisa inge in mutal.”
17 Yehova anawuza Mose kuti,
LEUM GOD El sapkin nu sel Moses
18 “Yankhula ndi Aaroni, ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse, ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati wina aliyense wa inu, Mwisraeli kapena mlendo amene akukhala mu Israeli abwera ndi mphatso ya nsembe yopsereza kwa Yehova, kupereka chimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu,
elan sang nu sel Aaron, wen natul kewa, ac nu sin mwet Israel nukewa oakwuk inge. Pacl se kutena sin mwet Israel, ku mwetsac su muta in facl Israel, oru sie kisa firir, finne ma in akfalye sie wulela, ku ke engan na lal in oru, kosro mwe kisa uh ac fah tia oasr kutena ma koluk ke manol.
19 ndiye kuti abwere ndi ngʼombe yayimuna, nkhosa yayimuna kapena mbuzi yayimuna. Izi zikhale zopanda chilema kuti zilandiridwe.
In oru tuh mwe kisa uh in ohi sin God, enenu in kosro mukul soko su wanginna ma koluk ke mano.
20 Musapereke nyama iliyonse yokhala ndi chilema chifukwa sidzalandiridwa mʼmalo mwanu.
Kom fin kisakin kutena kosro su oasr ma koluk ke mano, LEUM GOD El ac tia insewowo kac.
21 Pamene wina aliyense abweretsa ngʼombe kapena nkhosa kuti ikhale nsembe yachiyanjano kwa Yehova, kukwaniritsa zimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu, nyamayo iyenera kukhala yangwiro ndi yopanda chilema kuti ilandiridwe.
Mwet se fin oru sie kisa in akinsewowo nu sin LEUM GOD, finne ma in akfalye sie wulela, ku sie mwe sang ke insewowo na lal, kosro in kisa uh fah tia oasr kutena ma koluk ke mano, in mau wo sin LEUM GOD.
22 Musapereke kwa Yehova nyama zakhungu, zovulala kapena zolumala, kapena nyama zimene zikutulutsa mafinya mʼthupi mwake, kapena zimene zili ndi nthenda yonyerenyetsa, kapena zimene zili ndi mphere. Nyama zotere musaziyike pa guwa kuti zikhale nsembe yopsereza kwa Yehova.
Nimet kisakin nu sin LEUM GOD kutena kosro ma kunla muta, ku sukapasla, ku kanteyuki, ku oasr sronin faf kac, ku aryurla, ku turupweni mano. Nimet kisakin kain kosro ingan fin loang uh nu ke mwe kisa mongo.
23 Koma mungathe kupereka ngʼombe yayimuna kapena nkhosa imene ili ndi chiwalo chachitali kapena chachifupi kukhala nsembe yaufulu. Koma simungayipereke ngati nsembe yoperekera zimene munalumbirira chifukwa sidzalandiridwa.
Tusruktu fin mwe kisa ke lungse na lom, kom ku in sang soko kosro ma isusla tuh sufas mano, ku matkang, a tia ma in akfalye sie wulela.
24 Nyama iliyonse imene mavalo ake ndi onyuka kapena ophwanyika, ongʼambika kapena oduka, musamayipereke kwa Yehova mʼdziko lanu.
Nimet sang nu sin LEUM GOD kutena kosro ma atrol itatu, ku mihsalik, ku futunla, ku laslasla. Ma inge tia lela in kisakinyuk in facl suwos.
25 Ndipo musalandire nyama zotere kuchokera kwa mlendo ndi kuzipereka kukhala zakudya za Mulungu wanu. Zimenezi sizidzalandiridwa mʼmalo mwanu chifukwa zili ndi chilema ndipo ndi zolumala.’”
Nimet sang kutena kosro ma kowos eis sin mwetsac tuh in mwe kisa in mwe mongo. Kain kosro ingan lumweyuk mu oasr ma koluk ke manol ac God tia insewowo kac.
26 Yehova anawuza Mose kuti,
LEUM GOD El fahk nu sel Moses,
27 “Pamene mwana wangʼombe, mwana wankhosa kapena mwana wambuzi wabadwa, akhale ndi make kwa masiku asanu ndi awiri. Kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu mpaka mʼtsogolo mwake, angathe kulandiridwa kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
“Ke pacl se osweyukla soko cow ku soko sheep ku soko nani, kosro fusr soko ah enenu in mutana yurin nina kial ke len itkos, ac ke len se akoalkosr fahla, el fah ku in ituk nu ke mwe kisa firir nu sin LEUM GOD.
28 Musaphe ngʼombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wake tsiku limodzi. Muyidye pa tsiku lomwelo; musasiyeko ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
Nimet kisakin soko cow ac cow fusr natul, ku soko sheep ac sheep fusr natul, ku soko nani ac nani fusr natul ke len sefanna.
29 “Pamene mupereka nsembe yoyamika kwa Yehova, muyipereke mwakufuna kwanu mu njira yoti ilandiridwe mʼmalo mwanu.
Ke pacl kom oru sie kisa in sang kulo nu sin LEUM GOD, oru in fal nu ke oakwuk ma orekla nu kac an, tuh kisa lom in fah mwe insewowo nu sel:
30 Muyidye pa tsiku lomwelo, wosasiyako ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
kangla ke len sacna, ac tia filiye kutu nu ke len tok an.”
31 “Choncho sungani malamulo anga ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.
LEUM GOD El fahk, “Akos ma nga sapkin. Nga LEUM GOD.
32 Musanyoze dzina langa loyera. Koma lilemekezedwe pakati pa Aisraeli. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani
Nimet aklusrongtenye Ine mutal luk. Mwet Israel nukewa enenu in akilen lah nga mutal. Nga LEUM GOD, ac nga oru kowos in mutal;
33 ndipo ndine amene ndinakutulutsani mu Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.”
ac nga uskowosme liki acn Egypt tuh nga fah God lowos. Nga LEUM GOD.”

< Levitiko 22 >