< Levitiko 22 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
L'Éternel parla encore à Moise, en disant:
2 “Uza Aaroni ndi ana ake kuti azilemekeza zinthu zopatulika zimene Aisraeli azipereka kwa Ine, kuti asayipitse dzina langa loyera. Ine ndine Yehova.
Parle à Aaron et à ses fils afin qu'ils s'abstiennent des choses saintes des enfants d'Israël, et qu'ils ne profanent point le nom de ma sainteté dans les choses qu'ils me consacrent: Je suis l'Éternel.
3 “Uwawuze kuti ngati wina aliyense mwa zidzukulu zawo mʼmibado yonse imene ikubwera adzayandikira zinthu zopatulika zimene ana a Israeli apereka kwa Yehova, ali wodetsedwa, ameneyo achotsedwe pamaso pa Yehova. Ine ndine Yehova.
Dis-leur: Tout homme, dans toute votre postérité et vos générations, qui, étant souillé, s'approchera des choses saintes que les enfants d'Israël auront consacrées à l'Éternel, cet homme-là sera retranché de devant moi: Je suis l'Éternel.
4 “Munthu aliyense mwa zidzukulu za Aaroni amene ali ndi khate kapena amatulutsa zoyipa mʼthupi mwake, asadye zinthu zopatulika mpaka atayeretsedwa. Wansembe angakhale wodetsedwa atakhudzana ndi chinthu chimene chadetsedwa ndi chinthu chakufa kapena kukhudza munthu amene wataya umuna,
Quiconque de la postérité d'Aaron sera lépreux ou aura un flux, ne mangera point des choses consacrées jusqu'à ce qu'il soit purifié. De même celui qui aura touché une personne souillée par le contact d'un cadavre, ou l'homme qui aura une perte séminale;
5 kapena kukhudza chilichonse chokwawa chomwe chimadetsa munthu, kapena kukhudza munthu amene angamudetse, kapenanso kukhudza kanthu kena kalikonse kodetsedwa.
Ou celui qui aura touché quelque reptile qui l'ait rendu souillé, ou un homme qui l'ait rendu souillé, quelle que soit cette souillure.
6 Tsono ngati wansembe angakhudze chilichonse mwa zimenezi ndiye kuti adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Asadye chopereka chilichonse chopatulika mpaka atasamba thupi lake lonse.
Celui qui touchera ces choses sera souillé jusqu'au soir; il ne mangera point des choses consacrées, mais il lavera son corps dans l'eau.
7 Munthuyo adzakhala woyeretsedwa pamene dzuwa lalowa, ndipo angathe kudya chopereka chopatulikacho popeza ndi chakudya chake.
Et après le coucher du soleil il sera pur, et ensuite il pourra manger des choses saintes, car c'est sa nourriture.
8 Wansembe sayenera kudya chinthu chofa chokha kapena chojiwa ndi chirombo kuopa kuti angadzidetse ndi chakudyacho. Ine ndine Yehova.
Il ne mangera point d'une bête morte d'elle-même, ou déchirée, afin de ne pas en être souillé: Je suis l'Éternel.
9 “‘Choncho ansembe azisunga malamulo angawa kuti asapezeke wolakwa ndi kufa chifukwa chopeputsa malamulowa. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.
Qu'ils observent donc ce que j'ai ordonné, de peur qu'ils ne portent leur péché, et qu'ils ne meurent pour avoir profané les choses saintes: Je suis l'Éternel qui les sanctifie.
10 “‘Aliyense amene si wabanja la wansembe, kaya ndi mlendo wa wansembe, kapena wantchito wake, asadye chopereka chopatulika.
Or nul étranger ne mangera des choses consacrées; celui qui demeure chez un sacrificateur, et le mercenaire, ne mangeront point des choses saintes.
11 Koma kapolo amene wagulidwa ndi ndalama kapena kubadwira mʼbanja la wansembe angathe kudya chakudya cha wansembeyo.
Mais la personne que le sacrificateur aura achetée de son argent, en mangera; de même que celui qui sera né dans sa maison; ceux-là mangeront de sa nourriture.
12 Mwana wamkazi wa wansembe amene wakwatiwa ndi munthu amene si wansembe, asadyeko nsembe zopatulikazo.
Si une fille de sacrificateur est mariée à un étranger, elle ne mangera point des choses consacrées, offertes par élévation.
13 Koma mwana wamkazi wa wansembe amene ali wamasiye kapena wosudzulidwa, ndipo alibe mwana, komanso anabwerera ku nyumba ya abambo ake monga pa nthawi ya utsikana wake, angathe kudya chakudya cha abambo ake. Mlendo asadye chakudya chopatulika.
Mais si une fille de sacrificateur, étant veuve, ou répudiée, et sans enfants, retourne à la maison de son père, comme dans sa jeunesse, elle mangera de la nourriture de son père; mais nul étranger n'en mangera.
14 “‘Ngati munthu wina aliyense adya chopereka chopatulika mosadziwa, munthuyo amubwezere wansembe chinthu chopatulikacho ndipo awonjezerepo limodzi la magawo asanu a chinthucho.
Si quelqu'un mange par erreur d'une chose consacrée, il y ajoutera un cinquième, et donnera au sacrificateur la chose consacrée.
15 Choncho ansembe asayipitse zopereka zopatulika za Aisraeli zimene apereka kwa Yehova
Les sacrificateurs ne profaneront point les choses consacrées des enfants d'Israël, ce qu'ils offrent par élévation à l'Éternel.
16 ndipo asachimwitse ndi kupalamulitsa Aisraeli powalola kudya zakudya zawo zopatulika. Ine ndine Yehova amene ndimawayeretsa.’”
Ils leur feraient porter l'iniquité de leur culpabilité en mangeant ainsi leurs choses consacrées; car je suis l'Éternel, qui les sanctifie.
17 Yehova anawuza Mose kuti,
L'Éternel parla aussi à Moïse, en disant:
18 “Yankhula ndi Aaroni, ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse, ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati wina aliyense wa inu, Mwisraeli kapena mlendo amene akukhala mu Israeli abwera ndi mphatso ya nsembe yopsereza kwa Yehova, kupereka chimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu,
Parle à Aaron et à ses fils, et à tous les enfants d'Israël, et dis-leur: Quiconque de la maison d'Israël, ou des étrangers en Israël, offrira son offrande, soit pour un vœu, soit comme offrande volontaire qu'on offre en holocauste à l'Éternel, pour que vous soyez agréés,
19 ndiye kuti abwere ndi ngʼombe yayimuna, nkhosa yayimuna kapena mbuzi yayimuna. Izi zikhale zopanda chilema kuti zilandiridwe.
Qu'il offre un mâle sans défaut, d'entre le gros bétail, les agneaux ou les chèvres.
20 Musapereke nyama iliyonse yokhala ndi chilema chifukwa sidzalandiridwa mʼmalo mwanu.
Vous n'offrirez rien qui ait un défaut; car ce ne serait point agréé pour vous.
21 Pamene wina aliyense abweretsa ngʼombe kapena nkhosa kuti ikhale nsembe yachiyanjano kwa Yehova, kukwaniritsa zimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu, nyamayo iyenera kukhala yangwiro ndi yopanda chilema kuti ilandiridwe.
Et quand un homme offrira à l'Éternel un sacrifice de prospérités, de gros ou de menu bétail, pour s'acquitter d'un vœu, ou en offrande volontaire, pour être agréée la victime sera sans défaut; qu'il n'y ait en elle aucun défaut.
22 Musapereke kwa Yehova nyama zakhungu, zovulala kapena zolumala, kapena nyama zimene zikutulutsa mafinya mʼthupi mwake, kapena zimene zili ndi nthenda yonyerenyetsa, kapena zimene zili ndi mphere. Nyama zotere musaziyike pa guwa kuti zikhale nsembe yopsereza kwa Yehova.
Vous n'en offrirez point à l'Éternel qui soit aveugle, ou estropiée, ou mutilée, ou affectée d'ulcères, de la gale ou d'une dartre; et vous n'en ferez point sur l'autel un sacrifice par le feu, à l'Éternel.
23 Koma mungathe kupereka ngʼombe yayimuna kapena nkhosa imene ili ndi chiwalo chachitali kapena chachifupi kukhala nsembe yaufulu. Koma simungayipereke ngati nsembe yoperekera zimene munalumbirira chifukwa sidzalandiridwa.
Tu pourras sacrifier comme offrande volontaire un bœuf ou un agneau ayant quelque membre trop long ou trop court; mais il ne sera point agréé pour un vœu.
24 Nyama iliyonse imene mavalo ake ndi onyuka kapena ophwanyika, ongʼambika kapena oduka, musamayipereke kwa Yehova mʼdziko lanu.
Vous n'offrirez point à l'Éternel, et vous ne sacrifierez point dans votre pays un animal dont les testicules ont été froissés, écrasés, arrachés ou coupés.
25 Ndipo musalandire nyama zotere kuchokera kwa mlendo ndi kuzipereka kukhala zakudya za Mulungu wanu. Zimenezi sizidzalandiridwa mʼmalo mwanu chifukwa zili ndi chilema ndipo ndi zolumala.’”
Vous n'accepterez de la main d'un étranger aucune de ces victimes pour l'offrir comme aliment de votre Dieu; car leur mutilation est un défaut en elles; elles ne seront point agréées en votre faveur.
26 Yehova anawuza Mose kuti,
L'Éternel parla encore à Moïse, en disant:
27 “Pamene mwana wangʼombe, mwana wankhosa kapena mwana wambuzi wabadwa, akhale ndi make kwa masiku asanu ndi awiri. Kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu mpaka mʼtsogolo mwake, angathe kulandiridwa kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
Quand un veau, un agneau ou un chevreau naîtra, il sera sept jours avec sa mère; et à partir du huitième jour et les suivants, il sera agréé en offrande de sacrifice fait par le feu à l'Éternel.
28 Musaphe ngʼombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wake tsiku limodzi. Muyidye pa tsiku lomwelo; musasiyeko ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
Soit gros soit menu bétail, vous n'égorgerez pas un animal et son petit le même jour.
29 “Pamene mupereka nsembe yoyamika kwa Yehova, muyipereke mwakufuna kwanu mu njira yoti ilandiridwe mʼmalo mwanu.
Et quand vous offrirez un sacrifice d'actions de grâces à l'Éternel, vous le sacrifierez de manière qu'il soit agréé en votre faveur.
30 Muyidye pa tsiku lomwelo, wosasiyako ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
Il sera mangé le jour même, vous n'en laisserez rien jusqu'au matin: Je suis l'Éternel.
31 “Choncho sungani malamulo anga ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.
Gardez donc mes commandements, et accomplissez-les: Je suis l'Éternel.
32 Musanyoze dzina langa loyera. Koma lilemekezedwe pakati pa Aisraeli. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani
Et ne profanez point mon saint nom, et je serai sanctifié au milieu des enfants d'Israël: Je suis l'Éternel, qui vous sanctifie,
33 ndipo ndine amene ndinakutulutsani mu Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.”
Qui vous ai fait sortir du pays d'Égypte pour être votre Dieu. Je suis l'Éternel.

< Levitiko 22 >