< Levitiko 22 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahweh spoke to Moses, saying,
2 “Uza Aaroni ndi ana ake kuti azilemekeza zinthu zopatulika zimene Aisraeli azipereka kwa Ine, kuti asayipitse dzina langa loyera. Ine ndine Yehova.
“Speak to Aaron and to his sons, tell them to keep away from the holy things of the people of Israel, which they set apart to me. They must not profane my holy name. I am Yahweh.
3 “Uwawuze kuti ngati wina aliyense mwa zidzukulu zawo mʼmibado yonse imene ikubwera adzayandikira zinthu zopatulika zimene ana a Israeli apereka kwa Yehova, ali wodetsedwa, ameneyo achotsedwe pamaso pa Yehova. Ine ndine Yehova.
Say to them, 'If any of your descendants throughout your generations approaches the holy things that the people of Israel have set apart to Yahweh, while he is unclean, that person must be cut off from before me: I am Yahweh.
4 “Munthu aliyense mwa zidzukulu za Aaroni amene ali ndi khate kapena amatulutsa zoyipa mʼthupi mwake, asadye zinthu zopatulika mpaka atayeretsedwa. Wansembe angakhale wodetsedwa atakhudzana ndi chinthu chimene chadetsedwa ndi chinthu chakufa kapena kukhudza munthu amene wataya umuna,
None of the descendants of Aaron who has an infectious skin disease, or an infection flowing from his body, may eat any of the sacrifices made to Yahweh until he is clean. Whoever touches anything unclean through contact with the dead, or by contact with a man who has a flow of semen,
5 kapena kukhudza chilichonse chokwawa chomwe chimadetsa munthu, kapena kukhudza munthu amene angamudetse, kapenanso kukhudza kanthu kena kalikonse kodetsedwa.
or whoever touches any creeping animal that makes him unclean, or any person who makes him unclean, whatever kind of uncleanness it may be—
6 Tsono ngati wansembe angakhudze chilichonse mwa zimenezi ndiye kuti adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Asadye chopereka chilichonse chopatulika mpaka atasamba thupi lake lonse.
then the priest who touches anything unclean will be unclean until evening. He must not eat any of the holy things, unless he has bathed his body in water.
7 Munthuyo adzakhala woyeretsedwa pamene dzuwa lalowa, ndipo angathe kudya chopereka chopatulikacho popeza ndi chakudya chake.
When the sun has set, he will then be clean. After sunset he may eat from the holy things, because they are his food.
8 Wansembe sayenera kudya chinthu chofa chokha kapena chojiwa ndi chirombo kuopa kuti angadzidetse ndi chakudyacho. Ine ndine Yehova.
He must not eat anything found dead or killed by wild animals, by which he would defile himself. I am Yahweh.
9 “‘Choncho ansembe azisunga malamulo angawa kuti asapezeke wolakwa ndi kufa chifukwa chopeputsa malamulowa. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.
The priests must follow my instructions, or they will be guilty of sin and could die for profaning me. I am Yahweh who makes them holy.
10 “‘Aliyense amene si wabanja la wansembe, kaya ndi mlendo wa wansembe, kapena wantchito wake, asadye chopereka chopatulika.
No one outside the priest's family, including guests of a priest or his hired servants, may eat anything that is holy.
11 Koma kapolo amene wagulidwa ndi ndalama kapena kubadwira mʼbanja la wansembe angathe kudya chakudya cha wansembeyo.
But if a priest buys any slave with his own money, that slave may eat from the things set apart to Yahweh. The priest's family members and slaves born in his house, they also may eat with him from those things.
12 Mwana wamkazi wa wansembe amene wakwatiwa ndi munthu amene si wansembe, asadyeko nsembe zopatulikazo.
If a priest's daughter married someone who is not a priest, she may not eat any of the holy contribution offerings.
13 Koma mwana wamkazi wa wansembe amene ali wamasiye kapena wosudzulidwa, ndipo alibe mwana, komanso anabwerera ku nyumba ya abambo ake monga pa nthawi ya utsikana wake, angathe kudya chakudya cha abambo ake. Mlendo asadye chakudya chopatulika.
But if a priest's daughter is a widow, or divorced, and if she has no child, and if she returns to live in her father's house as in her youth, she may eat from her father's food. But no one who is not in the priestly family may eat from the priest's food.
14 “‘Ngati munthu wina aliyense adya chopereka chopatulika mosadziwa, munthuyo amubwezere wansembe chinthu chopatulikacho ndipo awonjezerepo limodzi la magawo asanu a chinthucho.
If a man eats a holy food without knowing it, then he must repay the priest for it; he must add one-fifth to it and give it back to the priest.
15 Choncho ansembe asayipitse zopereka zopatulika za Aisraeli zimene apereka kwa Yehova
The people of Israel must not profane the holy things that they have raised high and presented to Yahweh,
16 ndipo asachimwitse ndi kupalamulitsa Aisraeli powalola kudya zakudya zawo zopatulika. Ine ndine Yehova amene ndimawayeretsa.’”
and cause themselves to carry the sin that would make them guilty of eating the holy food, for I am Yahweh who makes them holy.'”
17 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahweh spoke to Moses, saying,
18 “Yankhula ndi Aaroni, ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse, ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati wina aliyense wa inu, Mwisraeli kapena mlendo amene akukhala mu Israeli abwera ndi mphatso ya nsembe yopsereza kwa Yehova, kupereka chimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu,
“Speak to Aaron and his sons, and to all the people of Israel. Say to them, 'Any Israelite, or an alien living in Israel, when they present a sacrifice—whether it is to fulfill a vow, or whether it is a freewill offering, or they present to Yahweh a burnt offering,
19 ndiye kuti abwere ndi ngʼombe yayimuna, nkhosa yayimuna kapena mbuzi yayimuna. Izi zikhale zopanda chilema kuti zilandiridwe.
if it is to be accepted, they must offer a male animal without blemish from the cattle, sheep, or goats.
20 Musapereke nyama iliyonse yokhala ndi chilema chifukwa sidzalandiridwa mʼmalo mwanu.
But you must not offer whatever has a blemish. I will not accept it on your behalf.
21 Pamene wina aliyense abweretsa ngʼombe kapena nkhosa kuti ikhale nsembe yachiyanjano kwa Yehova, kukwaniritsa zimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu, nyamayo iyenera kukhala yangwiro ndi yopanda chilema kuti ilandiridwe.
Whoever offers a sacrifice of fellowship offerings from the herd or the flock to Yahweh to fulfill a vow, or as a freewill offering, it must be unblemished to be accepted. There must be no defect in the animal.
22 Musapereke kwa Yehova nyama zakhungu, zovulala kapena zolumala, kapena nyama zimene zikutulutsa mafinya mʼthupi mwake, kapena zimene zili ndi nthenda yonyerenyetsa, kapena zimene zili ndi mphere. Nyama zotere musaziyike pa guwa kuti zikhale nsembe yopsereza kwa Yehova.
You must not offer animals that are blind, disabled, or maimed, or that have warts, sores, or scabs. You must not offer these to Yahweh as a sacrifice by fire on the altar.
23 Koma mungathe kupereka ngʼombe yayimuna kapena nkhosa imene ili ndi chiwalo chachitali kapena chachifupi kukhala nsembe yaufulu. Koma simungayipereke ngati nsembe yoperekera zimene munalumbirira chifukwa sidzalandiridwa.
You may present as a freewill offering an ox or a lamb that is deformed or small, but an offering like that will not be accepted for a vow.
24 Nyama iliyonse imene mavalo ake ndi onyuka kapena ophwanyika, ongʼambika kapena oduka, musamayipereke kwa Yehova mʼdziko lanu.
Do not offer any animal to Yahweh that has bruised, crushed, torn, or cut testicles. Do not do this within your land.
25 Ndipo musalandire nyama zotere kuchokera kwa mlendo ndi kuzipereka kukhala zakudya za Mulungu wanu. Zimenezi sizidzalandiridwa mʼmalo mwanu chifukwa zili ndi chilema ndipo ndi zolumala.’”
You must not present the bread of your God from the hand of a foreigner. Those animals are deformed and have defects in them, they will not be accepted for you.'”
26 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahweh spoke to Moses and said,
27 “Pamene mwana wangʼombe, mwana wankhosa kapena mwana wambuzi wabadwa, akhale ndi make kwa masiku asanu ndi awiri. Kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu mpaka mʼtsogolo mwake, angathe kulandiridwa kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
“When a calf or a sheep or a goat is born, it must remain seven days with its mother. Then from the eighth day on, it may be accepted as a sacrifice for an offering made by fire to Yahweh.
28 Musaphe ngʼombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wake tsiku limodzi. Muyidye pa tsiku lomwelo; musasiyeko ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
Do not kill a cow or ewe along with its young, both on the same day.
29 “Pamene mupereka nsembe yoyamika kwa Yehova, muyipereke mwakufuna kwanu mu njira yoti ilandiridwe mʼmalo mwanu.
When you sacrifice a thank offering to Yahweh, you must sacrifice it in an acceptable way.
30 Muyidye pa tsiku lomwelo, wosasiyako ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
It must be eaten on the same day that it is sacrificed. You must leave none of it until the next morning. I am Yahweh.
31 “Choncho sungani malamulo anga ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.
So you must keep my commandments and carry them out. I am Yahweh.
32 Musanyoze dzina langa loyera. Koma lilemekezedwe pakati pa Aisraeli. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani
You must not profane my holy name. I must be acknowledged as holy by the people of Israel. I am Yahweh who makes you holy,
33 ndipo ndine amene ndinakutulutsani mu Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.”
who brought you out of the land of Egypt to be your God: I am Yahweh.”

< Levitiko 22 >