< Levitiko 22 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And he spoke Yahweh to Moses saying.
2 “Uza Aaroni ndi ana ake kuti azilemekeza zinthu zopatulika zimene Aisraeli azipereka kwa Ine, kuti asayipitse dzina langa loyera. Ine ndine Yehova.
Speak to Aaron and to sons his so they may separate themselves from [the] holy things of [the] people of Israel and not they will profane [the] name of holiness my which they [are] setting apart as holy to me I [am] Yahweh.
3 “Uwawuze kuti ngati wina aliyense mwa zidzukulu zawo mʼmibado yonse imene ikubwera adzayandikira zinthu zopatulika zimene ana a Israeli apereka kwa Yehova, ali wodetsedwa, ameneyo achotsedwe pamaso pa Yehova. Ine ndine Yehova.
Say to them to generations your every man - who he will draw near from all offspring your to the holy things which they will set apart as holy [the] people of Israel to Yahweh and uncleanness his [is] on him and it will be cut off the person that from to before me I [am] Yahweh.
4 “Munthu aliyense mwa zidzukulu za Aaroni amene ali ndi khate kapena amatulutsa zoyipa mʼthupi mwake, asadye zinthu zopatulika mpaka atayeretsedwa. Wansembe angakhale wodetsedwa atakhudzana ndi chinthu chimene chadetsedwa ndi chinthu chakufa kapena kukhudza munthu amene wataya umuna,
A man a man from [the] offspring of Aaron and he [is] having a serious skin disease or [is] discharging in the holy things not he will eat until that he will be pure and who [-ever] touches any [thing] unclean of a corpse or anyone whom it will go out from him a laying of seed.
5 kapena kukhudza chilichonse chokwawa chomwe chimadetsa munthu, kapena kukhudza munthu amene angamudetse, kapenanso kukhudza kanthu kena kalikonse kodetsedwa.
Or anyone who he will touch any swarming thing which it is unclean to him or anyone who he is unclean to him to all uncleanness his.
6 Tsono ngati wansembe angakhudze chilichonse mwa zimenezi ndiye kuti adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Asadye chopereka chilichonse chopatulika mpaka atasamba thupi lake lonse.
Anyone who it will touch it and it will be unclean until the evening and not he will eat any of the holy things that except he has washed body his with water.
7 Munthuyo adzakhala woyeretsedwa pamene dzuwa lalowa, ndipo angathe kudya chopereka chopatulikacho popeza ndi chakudya chake.
And it will go the sun and he will be clean and after he will eat any of the holy things for [is] food his it.
8 Wansembe sayenera kudya chinthu chofa chokha kapena chojiwa ndi chirombo kuopa kuti angadzidetse ndi chakudyacho. Ine ndine Yehova.
A carcass and a torn animal not he will eat to become unclean by it I [am] Yahweh.
9 “‘Choncho ansembe azisunga malamulo angawa kuti asapezeke wolakwa ndi kufa chifukwa chopeputsa malamulowa. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.
And they will keep duty my and not they will bear on it sin and they will die by it for they will profane it I [am] Yahweh [who] sets apart as holy them.
10 “‘Aliyense amene si wabanja la wansembe, kaya ndi mlendo wa wansembe, kapena wantchito wake, asadye chopereka chopatulika.
And any stranger not he will eat a holy thing a resident alien of a priest and a hired laborer not he will eat a holy thing.
11 Koma kapolo amene wagulidwa ndi ndalama kapena kubadwira mʼbanja la wansembe angathe kudya chakudya cha wansembeyo.
And a priest if he will acquire a person [the] acquisition of money his he he will eat in it and [the] one born of household his they they will eat in food his.
12 Mwana wamkazi wa wansembe amene wakwatiwa ndi munthu amene si wansembe, asadyeko nsembe zopatulikazo.
And a daughter of a priest if she will belong to a man strange she in [the] contribution of the holy things not she will eat.
13 Koma mwana wamkazi wa wansembe amene ali wamasiye kapena wosudzulidwa, ndipo alibe mwana, komanso anabwerera ku nyumba ya abambo ake monga pa nthawi ya utsikana wake, angathe kudya chakudya cha abambo ake. Mlendo asadye chakudya chopatulika.
And a daughter of a priest if she will be a widow and a divorced [woman] and offspring not [belongs] to her and she will return to [the] house of father her like youth her any of [the] food of father her she will eat and any stranger not he will eat in it.
14 “‘Ngati munthu wina aliyense adya chopereka chopatulika mosadziwa, munthuyo amubwezere wansembe chinthu chopatulikacho ndipo awonjezerepo limodzi la magawo asanu a chinthucho.
And anyone if he will eat a holy thing by inadvertence and he will add fifth its to it and he will give to the priest the holy thing.
15 Choncho ansembe asayipitse zopereka zopatulika za Aisraeli zimene apereka kwa Yehova
And not they will profane [the] holy things of [the] people of Israel which they will lift up to Yahweh.
16 ndipo asachimwitse ndi kupalamulitsa Aisraeli powalola kudya zakudya zawo zopatulika. Ine ndine Yehova amene ndimawayeretsa.’”
And they will cause to bear them iniquity of guilt when eat they holy things their for I [am] Yahweh [who] sets apart as holy them.
17 Yehova anawuza Mose kuti,
And he spoke Yahweh to Moses saying.
18 “Yankhula ndi Aaroni, ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse, ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati wina aliyense wa inu, Mwisraeli kapena mlendo amene akukhala mu Israeli abwera ndi mphatso ya nsembe yopsereza kwa Yehova, kupereka chimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu,
Speak to Aaron and to sons his and to all [the] people of Israel and you will say to them a person a person from [the] house of Israel and of the sojourner[s] in Israel who he will present present his for all vows their and for all freewill offerings their which they will present to Yahweh to a burnt offering.
19 ndiye kuti abwere ndi ngʼombe yayimuna, nkhosa yayimuna kapena mbuzi yayimuna. Izi zikhale zopanda chilema kuti zilandiridwe.
For acceptance your unblemished a male among the cattle among the young rams and among the goats.
20 Musapereke nyama iliyonse yokhala ndi chilema chifukwa sidzalandiridwa mʼmalo mwanu.
All that [is] in it a blemish not you will present for not for acceptance it will be of you.
21 Pamene wina aliyense abweretsa ngʼombe kapena nkhosa kuti ikhale nsembe yachiyanjano kwa Yehova, kukwaniritsa zimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu, nyamayo iyenera kukhala yangwiro ndi yopanda chilema kuti ilandiridwe.
And anyone if he will present a sacrifice of peace offering to Yahweh to fulfill a vow or to a freewill offering in the herd or in the flock unblemished it will be for acceptance any blemish not it will be in it.
22 Musapereke kwa Yehova nyama zakhungu, zovulala kapena zolumala, kapena nyama zimene zikutulutsa mafinya mʼthupi mwake, kapena zimene zili ndi nthenda yonyerenyetsa, kapena zimene zili ndi mphere. Nyama zotere musaziyike pa guwa kuti zikhale nsembe yopsereza kwa Yehova.
Blindness or a fracture or a mutilation or a wart or eczema or scabs not you will present these to Yahweh and a fire offering not you must give any of them on the altar to Yahweh.
23 Koma mungathe kupereka ngʼombe yayimuna kapena nkhosa imene ili ndi chiwalo chachitali kapena chachifupi kukhala nsembe yaufulu. Koma simungayipereke ngati nsembe yoperekera zimene munalumbirira chifukwa sidzalandiridwa.
And an ox and a sheep [having] something enlarged and [having] something stunted a freewill offering you will offer it and for a vow not it will be accepted.
24 Nyama iliyonse imene mavalo ake ndi onyuka kapena ophwanyika, ongʼambika kapena oduka, musamayipereke kwa Yehova mʼdziko lanu.
And [one which] is squashed and [one which] is crushed and [one which] is torn and [one which] is cut not you will present to Yahweh and in land your not you will do [it].
25 Ndipo musalandire nyama zotere kuchokera kwa mlendo ndi kuzipereka kukhala zakudya za Mulungu wanu. Zimenezi sizidzalandiridwa mʼmalo mwanu chifukwa zili ndi chilema ndipo ndi zolumala.’”
And from [the] hand of a son of foreignness not you must present [the] food of God your any of all these [animals] for disfigurement their [is] in them a blemish [is] in them not they will be accepted for you.
26 Yehova anawuza Mose kuti,
And he spoke Yahweh to Moses saying.
27 “Pamene mwana wangʼombe, mwana wankhosa kapena mwana wambuzi wabadwa, akhale ndi make kwa masiku asanu ndi awiri. Kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu mpaka mʼtsogolo mwake, angathe kulandiridwa kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
An ox or a young ram or a goat if it will be born and it will be seven days under mother its and from [the] day eighth and onwards it will be accepted to a present of a fire offering to Yahweh.
28 Musaphe ngʼombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wake tsiku limodzi. Muyidye pa tsiku lomwelo; musasiyeko ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
And an ox or a sheep it and young its not you must cut [the] throat of in a day one.
29 “Pamene mupereka nsembe yoyamika kwa Yehova, muyipereke mwakufuna kwanu mu njira yoti ilandiridwe mʼmalo mwanu.
And if you will sacrifice a sacrifice of thanksgiving to Yahweh for acceptance your you will sacrifice [it].
30 Muyidye pa tsiku lomwelo, wosasiyako ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
On the day that it will be eaten not you will leave over any of it until morning I [am] Yahweh.
31 “Choncho sungani malamulo anga ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.
And you will keep commandments my and you will do them I [am] Yahweh.
32 Musanyoze dzina langa loyera. Koma lilemekezedwe pakati pa Aisraeli. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani
And not you will profane [the] name of holiness my and I will show myself holy in among [the] people of Israel I [am] Yahweh [who] sets apart as holy you.
33 ndipo ndine amene ndinakutulutsani mu Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.”
Who brought out you from [the] land of Egypt to become for you God I [am] Yahweh.

< Levitiko 22 >