< Levitiko 22 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Og Herren talede til Mose og sagde:
2 “Uza Aaroni ndi ana ake kuti azilemekeza zinthu zopatulika zimene Aisraeli azipereka kwa Ine, kuti asayipitse dzina langa loyera. Ine ndine Yehova.
Sig til Aron og til hans Sønner, at de afholde sig fra Israels Børns hellige Ting og ikke vanhellige mit hellige Navn, naar disse hellige mig noget; jeg er Herren.
3 “Uwawuze kuti ngati wina aliyense mwa zidzukulu zawo mʼmibado yonse imene ikubwera adzayandikira zinthu zopatulika zimene ana a Israeli apereka kwa Yehova, ali wodetsedwa, ameneyo achotsedwe pamaso pa Yehova. Ine ndine Yehova.
Sig til dem: Hvilken som helst Mand i eders Slægter af al eders Sæd, der kommer nær til de hellige Ting, som Israels Børn hellige Herren, og hans Urenhed er paa ham, han skal udryddes fra at være for mit Ansigt; jeg er Herren.
4 “Munthu aliyense mwa zidzukulu za Aaroni amene ali ndi khate kapena amatulutsa zoyipa mʼthupi mwake, asadye zinthu zopatulika mpaka atayeretsedwa. Wansembe angakhale wodetsedwa atakhudzana ndi chinthu chimene chadetsedwa ndi chinthu chakufa kapena kukhudza munthu amene wataya umuna,
Hvo som helst af Arons Sæd, der er spedalsk eller har Flod, han skal ikke æde af de hellige Ting, indtil han vorder ren; og den ikke heller, som rører ved nogen, der er uren formedelst Lig, eller den Mand, fra hvem der gaar Sæd,
5 kapena kukhudza chilichonse chokwawa chomwe chimadetsa munthu, kapena kukhudza munthu amene angamudetse, kapenanso kukhudza kanthu kena kalikonse kodetsedwa.
eller den Mand, som rører ved noget Kryb, som man kan blive uren af, eller ved et Menneske, som man kan blive uren af, hvad Slags Urenhed det end er;
6 Tsono ngati wansembe angakhudze chilichonse mwa zimenezi ndiye kuti adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Asadye chopereka chilichonse chopatulika mpaka atasamba thupi lake lonse.
den Person, som rører ved det, skal være uren indtil Aftenen, og han skal ikke æde af de hellige Ting, men bade sit Legeme i Vand.
7 Munthuyo adzakhala woyeretsedwa pamene dzuwa lalowa, ndipo angathe kudya chopereka chopatulikacho popeza ndi chakudya chake.
Og naar Solen gaar ned, saa er han ren, og siden maa han æde af de hellige Ting; thi det er hans Mad.
8 Wansembe sayenera kudya chinthu chofa chokha kapena chojiwa ndi chirombo kuopa kuti angadzidetse ndi chakudyacho. Ine ndine Yehova.
Han skal ikke æde Aadsel eller det, som er sønderrevet, at blive uren paa det; jeg er Herren.
9 “‘Choncho ansembe azisunga malamulo angawa kuti asapezeke wolakwa ndi kufa chifukwa chopeputsa malamulowa. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.
Og de skulle holde det, jeg vil have holdt, og de skulle ikke bære Synd for den Sags Skyld og dø derfor, naar de vanhellige det; jeg er Herren, som helliger dem.
10 “‘Aliyense amene si wabanja la wansembe, kaya ndi mlendo wa wansembe, kapena wantchito wake, asadye chopereka chopatulika.
Og ingen fremmed skal æde det hellige; den, som bor hos Præsten, og en Daglønner skal ikke æde af det hellige.
11 Koma kapolo amene wagulidwa ndi ndalama kapena kubadwira mʼbanja la wansembe angathe kudya chakudya cha wansembeyo.
Men naar Præsten har købt nogen for sine Penge til Ejendom, da maa denne æde deraf; og hver den, som er født i hans Hus, de maa æde af hans Brød.
12 Mwana wamkazi wa wansembe amene wakwatiwa ndi munthu amene si wansembe, asadyeko nsembe zopatulikazo.
Men naar en Præsts Datter bliver en fremmed Mands Hustru, da skal hun ikke æde af de hellige Ting, som ere en Gave.
13 Koma mwana wamkazi wa wansembe amene ali wamasiye kapena wosudzulidwa, ndipo alibe mwana, komanso anabwerera ku nyumba ya abambo ake monga pa nthawi ya utsikana wake, angathe kudya chakudya cha abambo ake. Mlendo asadye chakudya chopatulika.
Men naar en Præsts Datter bliver Enke eller forskudt, og hun har ingen Afkom, og hun vender tilbage til sin Faders Hus, ligesom i hendes Ungdom, da maa hun æde af sin Faders Brød; men ingen fremmed maa æde deraf.
14 “‘Ngati munthu wina aliyense adya chopereka chopatulika mosadziwa, munthuyo amubwezere wansembe chinthu chopatulikacho ndipo awonjezerepo limodzi la magawo asanu a chinthucho.
Men æder nogen af det hellige uvitterlig, da skal han lægge den femte Del deraf dertil og give Præsten det tillige med det hellige.
15 Choncho ansembe asayipitse zopereka zopatulika za Aisraeli zimene apereka kwa Yehova
Og de skulle ikke vanhellige Israels Børns hellige Ting, dem, som de bringe til Gave for Herren,
16 ndipo asachimwitse ndi kupalamulitsa Aisraeli powalola kudya zakudya zawo zopatulika. Ine ndine Yehova amene ndimawayeretsa.’”
og ikke belade sig med Misgerning og Skyld, naar de æde deres hellige Ting; thi jeg er Herren, som helliger dem.
17 Yehova anawuza Mose kuti,
Og Herren talede til Mose og sagde:
18 “Yankhula ndi Aaroni, ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse, ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati wina aliyense wa inu, Mwisraeli kapena mlendo amene akukhala mu Israeli abwera ndi mphatso ya nsembe yopsereza kwa Yehova, kupereka chimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu,
Tal til Aron og til hans Sønner og til alle Israels Børn, og sig til dem: Naar nogen som helst af Israels Hus eller af de fremmede i Israel vil ofre sit Offer, enten det er efter deres Løfte, eller deres frivillige Offer, som de ville ofre Herren til et Brændoffer,
19 ndiye kuti abwere ndi ngʼombe yayimuna, nkhosa yayimuna kapena mbuzi yayimuna. Izi zikhale zopanda chilema kuti zilandiridwe.
da skal det, for at blive til en Behagelighed for eder, være uden Lyde, en Han af stort Kvæg, af Faarene eller af Gederne.
20 Musapereke nyama iliyonse yokhala ndi chilema chifukwa sidzalandiridwa mʼmalo mwanu.
I skulle intet ofre af det, som der er Lyde paa; thi det bliver ikke til en Behagelighed for eder.
21 Pamene wina aliyense abweretsa ngʼombe kapena nkhosa kuti ikhale nsembe yachiyanjano kwa Yehova, kukwaniritsa zimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu, nyamayo iyenera kukhala yangwiro ndi yopanda chilema kuti ilandiridwe.
Og naar nogen vil ofre et Takoffer for Herren til at indfrie et Løfte eller til et frivilligt Offer af stort Kvæg eller smaat Kvæg, da skal det være uden Lyde, at det kan være til en Behagelighed; der skal slet ingen Lyde være paa det.
22 Musapereke kwa Yehova nyama zakhungu, zovulala kapena zolumala, kapena nyama zimene zikutulutsa mafinya mʼthupi mwake, kapena zimene zili ndi nthenda yonyerenyetsa, kapena zimene zili ndi mphere. Nyama zotere musaziyike pa guwa kuti zikhale nsembe yopsereza kwa Yehova.
Det, som er blindt eller benbrudt eller lemlæstet, eller som har flydende Saar eller Skurv eller Fnat, det skulle I ikke ofre Herren, og I skulle ikke bringe Ildoffer deraf paa Alteret til Herren.
23 Koma mungathe kupereka ngʼombe yayimuna kapena nkhosa imene ili ndi chiwalo chachitali kapena chachifupi kukhala nsembe yaufulu. Koma simungayipereke ngati nsembe yoperekera zimene munalumbirira chifukwa sidzalandiridwa.
Baade en Okse og et Faar, som har et Lem for stort eller for lidet, deraf maa du gøre et frivilligt Offer; men til et Løfte kan det ikke vorde behageligt.
24 Nyama iliyonse imene mavalo ake ndi onyuka kapena ophwanyika, ongʼambika kapena oduka, musamayipereke kwa Yehova mʼdziko lanu.
Og I skulle ikke ofre Herren noget, som er blevet krystet eller stødt eller sønderrevet eller afskaaret, og I skulle ikke gøre sligt i eders Land.
25 Ndipo musalandire nyama zotere kuchokera kwa mlendo ndi kuzipereka kukhala zakudya za Mulungu wanu. Zimenezi sizidzalandiridwa mʼmalo mwanu chifukwa zili ndi chilema ndipo ndi zolumala.’”
Og I skulle heller ikke ofre af en fremmeds Haand eders Guds Brød af noget af disse Ting; thi der er Skade paa dem, der er Lyde paa dem; de skulle ikke blive behagelige for eder.
26 Yehova anawuza Mose kuti,
Og Herren talede til Mose og sagde:
27 “Pamene mwana wangʼombe, mwana wankhosa kapena mwana wambuzi wabadwa, akhale ndi make kwa masiku asanu ndi awiri. Kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu mpaka mʼtsogolo mwake, angathe kulandiridwa kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
Naar en Okse eller et Faar eller en Ged fødes, da skal den være i syv Dage hos sin Moder, og fra den ottende Dag og derefter skal den være behagelig til et Ildoffer for Herren.
28 Musaphe ngʼombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wake tsiku limodzi. Muyidye pa tsiku lomwelo; musasiyeko ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
Hvad enten det er Okse eller Faar, da skal man ikke slagte det paa een Dag med dets Affødning.
29 “Pamene mupereka nsembe yoyamika kwa Yehova, muyipereke mwakufuna kwanu mu njira yoti ilandiridwe mʼmalo mwanu.
Men naar I slagte Herren et Lovoffer, skulle I slagte det for eder til en Behagelighed.
30 Muyidye pa tsiku lomwelo, wosasiyako ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
Det skal ædes paa den samme Dag, I skulle ikke levne deraf til om Morgenen; jeg er Herren.
31 “Choncho sungani malamulo anga ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.
Derfor skulle I holde mine Bud og gøre dem; jeg er Herren.
32 Musanyoze dzina langa loyera. Koma lilemekezedwe pakati pa Aisraeli. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani
Og I skulle ikke vanhellige mit hellige Navn, at jeg maa vorde helliget midt iblandt Israels Børn. Jeg er Herren, som helliger eder,
33 ndipo ndine amene ndinakutulutsani mu Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.”
og som udførte eder af Ægyptens Land, at være eders Gud; jeg er Herren.

< Levitiko 22 >