< Levitiko 21 >
1 Yehova anawuza Mose kuti, “Yankhula ndi ansembe, ana a Aaroni, ndipo uwawuze kuti, ‘Wansembe asadzidetse pokhudza munthu wakufa pakati pa abale ake.
and to say LORD to(wards) Moses to say to(wards) [the] priest son: child Aaron and to say to(wards) them to/for soul: dead not to defile in/on/with kinsman his
2 Koma akhoza kukhudza thupi lakufa la amayi ake, abambo ake, mwana wake wamwamuna, mwana wake wamkazi, mchimwene wake,
that if: except if: except to/for flesh his [the] near to(wards) him to/for mother his and to/for father his and to/for son: child his and to/for daughter his and to/for brother: male-sibling his
3 kapena mlongo wake wosakwatiwa amene amadalira iye chifukwa sanakwatiwe. Iye akhoza kudzidetsa pokhudza thupi lakufa la mchemwali wake wosakwatiwa yekha.
and to/for sister his [the] virgin [the] near to(wards) him which not to be to/for man: husband to/for her to defile
4 Koma wansembe asadzidetse chifukwa cha anthu amene ali nawo pa ubale obwera chifukwa cha ukwati.
not to defile master: husband in/on/with kinsman his to/for to profane/begin: profane him
5 “‘Ansembe asamete tsitsi kumutu kwawo kapena mʼmphepete mwa ndevu zawo, kapenanso kudzichekacheka pa thupi lawo.
not (to make bald *Q(k)*) bald spot in/on/with head their and side beard their not to shave and in/on/with flesh their not to incise incision
6 Ayenera kukhala oyera pamaso pa Mulungu wawo ndipo asachititse manyazi dzina la Mulungu wawo. Popeza amapereka nsembe zotentha pa moto kwa Yehova, chakudya cha Mulungu wawo, iwo azikhala woyera.
holy to be to/for God their and not to profane/begin: profane name God their for [obj] food offering LORD food: bread God their they(masc.) to present: bring and to be holiness
7 “‘Asakwatire akazi amene adzidetsa ndi chiwerewere kapena akazi amene amuna awo awasudzula, chifukwa ansembe ndi oyera pamaso pa Mulungu wawo.
woman to fornicate and profaned not to take: marry and woman to drive out: divorce from man: husband her not to take: marry for holy he/she/it to/for God his
8 Iwo akhale oyera chifukwa amapereka nsembe kwa Mulungu wanu. Muziwaona kuti ndi oyera, popeza Ine Yehova amene ndimawayeretsa ndine woyera, nawonso akhale oyera.
and to consecrate: consecate him for [obj] food: bread God your he/she/it to present: bring holy to be to/for you for holy I LORD to consecrate: consecate you
9 “‘Ngati mwana wamkazi wa wansembe adziyipitsa pochita zachiwerewere, ndiye kuti iye akuchititsa manyazi abambo ake; mwanayo atenthedwe pa moto.
and daughter man priest for to profane/begin: profane to/for to fornicate [obj] father her he/she/it to profane/begin: profane in/on/with fire to burn
10 “‘Munthu amene ali mkulu wa ansembe pakati pa abale ake, amene anamudzoza pomutsanulira mafuta pamutu pake, ndiponso amene anapatulidwa pomuveka zovala zaunsembe, asalekerere tsitsi lake kapena kungʼamba zovala zake kusonyeza kuti ali pa chisoni.
and [the] priest [the] great: large from brother: male-relative his which to pour: pour upon head his oil [the] anointing and to fill [obj] hand: donate his to/for to clothe [obj] [the] garment [obj] head his not to neglect and garment his not to tear
11 Asalowe mʼnyumba mmene muli munthu wakufa ngakhale womwalirayo ndi amayi ake kapena abambo ake.
and upon all soul: dead to die not to come (in): come to/for father his and to/for mother his not to defile
12 Asadzidetse potulukira kunja kwa malo opatulika popeza mafuta womupatula kukhala wansembe ali pamutu pake. Ine ndine Yehova.
and from [the] sanctuary not to come out: come and not to profane/begin: profane [obj] sanctuary God his for consecration: crown oil anointing God his upon him I LORD
13 “‘Iye akwatire namwali wosadziwa mwamuna.
and he/she/it woman: wife in/on/with virginity her to take: marry
14 Asakwatire mkazi wamasiye, mkazi wosudzulidwa, kapena mkazi wachiwerewere, koma akwatire namwali wosadziwa mwamuna pakati pa anthu a mtundu wake,
widow and to drive out: divorce and profaned to fornicate [obj] these not to take: marry that if: except if: except virgin from kinsman his to take: marry woman: wife
15 kuti mtundu wake usakhale wodetsedwa pakati pa abale popeza ndine Yehova, amene ndimamuyeretsa.’”
and not to profane/begin: profane seed: children his in/on/with kinsman his for I LORD to consecrate: consecate him
16 Yehova anawuza Mose kuti,
and to speak: speak LORD to(wards) Moses to/for to say
17 “Muwuze Aaroni kuti, ‘Munthu aliyense mwa zidzukulu zake ku mibado yawo yonse ikubwera akakhala ndi chilema asabwere kudzapereka nsembe kwa Mulungu wake.
to speak: speak to(wards) Aaron to/for to say man from seed: children your to/for generation their which to be in/on/with him blemish not to present: come to/for to present: bring food: bread God his
18 Munthu aliyense wachilema motere: munthu wakhungu kapena wolumala miyendo, munthu wolumala nkhope kapena waziwalo zambiri,
for all man which in/on/with him blemish not to present: come man blind or lame or to slash or to extend
19 munthu wa phazi lolumala kapena dzanja lolumala,
or man which to be in/on/with him breaking foot or breaking hand
20 kapena munthu wokhota msana kapena wamfupi kwambiri, kapena wolumala maso, munthu wa nthenda yonyerenyetsa, kapena wamphere, kapenanso wophwanyika mavalo, sayenera kusendera pafupi.
or humpbacked or thin or defect in/on/with eye: seeing his or scab or scab or crushed testicle
21 Mdzukulu aliyense wa Aaroni wansembe, amene ali ndi chilema asadzayandikire kukapereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Popeza kuti ali ndi chilema, asayandikire kudzapereka nsembe ya chakudya kwa Mulungu wake.
all man which in/on/with him blemish from seed: children Aaron [the] priest not to approach: approach to/for to present: bring [obj] food offering LORD blemish in/on/with him [obj] food: bread God his not to approach: approach to/for to present: bring
22 Koma iye angathe kudya chakudya chopatulika kwambiri chija, ngakhalenso chakudya chotsala pa nsembe zopatulika.
food: bread God his from holiness [the] holiness and from [the] holiness to eat
23 Koma chifukwa cha kulumala kwake, sayenera kuyandikira katani kapena kufika pa guwa kuti angadetse malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.’”
surely to(wards) [the] curtain not to come (in): come and to(wards) [the] altar not to approach: approach for blemish in/on/with him and not to profane/begin: profane [obj] sanctuary my for I LORD to consecrate: consecate them
24 Choncho Mose anawuza Aaroni ndi ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse zimenezi.
and to speak: speak Moses to(wards) Aaron and to(wards) son: child his and to(wards) all son: descendant/people Israel