< Levitiko 21 >
1 Yehova anawuza Mose kuti, “Yankhula ndi ansembe, ana a Aaroni, ndipo uwawuze kuti, ‘Wansembe asadzidetse pokhudza munthu wakufa pakati pa abale ake.
And Yahweh said unto Moses, Say unto the priests, the sons of Aaron, —yea thou shalt say unto them, For a dead person, shall no one make himself unclean among his people:
2 Koma akhoza kukhudza thupi lakufa la amayi ake, abambo ake, mwana wake wamwamuna, mwana wake wamkazi, mchimwene wake,
Saving for his kin, that are near unto him, for his mother or for his father, or for his son or for his daughter, or for his brother;
3 kapena mlongo wake wosakwatiwa amene amadalira iye chifukwa sanakwatiwe. Iye akhoza kudzidetsa pokhudza thupi lakufa la mchemwali wake wosakwatiwa yekha.
or for his sister, a virgin who is near unto him, who belongeth not unto a husband, —for her, he may make himself unclean:
4 Koma wansembe asadzidetse chifukwa cha anthu amene ali nawo pa ubale obwera chifukwa cha ukwati.
He shall not make himself unclean being a chief among his people, —by profaning himself:
5 “‘Ansembe asamete tsitsi kumutu kwawo kapena mʼmphepete mwa ndevu zawo, kapenanso kudzichekacheka pa thupi lawo.
They shall not make a baldness behind in their head, And the border of their beard, shall they not cut off, —And, in their flesh, shall they not make incisions.
6 Ayenera kukhala oyera pamaso pa Mulungu wawo ndipo asachititse manyazi dzina la Mulungu wawo. Popeza amapereka nsembe zotentha pa moto kwa Yehova, chakudya cha Mulungu wawo, iwo azikhala woyera.
Holy persons, shall they be unto their God, and not profane the name of their God, —for, the altar-flames of Yahweh, the food of their God, do they bring near—Therefore shall they be holy.
7 “‘Asakwatire akazi amene adzidetsa ndi chiwerewere kapena akazi amene amuna awo awasudzula, chifukwa ansembe ndi oyera pamaso pa Mulungu wawo.
A woman that is unchaste or dishonoured, shall they not take, And a woman divorced from her husband, shall they not take, —For holy, he is unto his God.
8 Iwo akhale oyera chifukwa amapereka nsembe kwa Mulungu wanu. Muziwaona kuti ndi oyera, popeza Ine Yehova amene ndimawayeretsa ndine woyera, nawonso akhale oyera.
Therefore shalt thou hold him as holy, for the food of thy God, doth he bring near, —Holy, shall he be to thee, For, holy, am I—Yahweh, who am making you holy.
9 “‘Ngati mwana wamkazi wa wansembe adziyipitsa pochita zachiwerewere, ndiye kuti iye akuchititsa manyazi abambo ake; mwanayo atenthedwe pa moto.
And, the daughter of any priest, when she profaneth herself by unchastity, Her father, she, doth profane, with fire, shall she be consumed.
10 “‘Munthu amene ali mkulu wa ansembe pakati pa abale ake, amene anamudzoza pomutsanulira mafuta pamutu pake, ndiponso amene anapatulidwa pomuveka zovala zaunsembe, asalekerere tsitsi lake kapena kungʼamba zovala zake kusonyeza kuti ali pa chisoni.
And, as for the high priest from among his brethren upon whose head is poured the anointing oil, and who is installed, by putting on the garments, His head, shall he not bare, And, his garments, shall he not rend;
11 Asalowe mʼnyumba mmene muli munthu wakufa ngakhale womwalirayo ndi amayi ake kapena abambo ake.
And, unto no persons of the dead, shall he go in, —For his father or for his mother, shall he not make himself unclean;
12 Asadzidetse potulukira kunja kwa malo opatulika popeza mafuta womupatula kukhala wansembe ali pamutu pake. Ine ndine Yehova.
And, out of the sanctuary, shall he not go forth, so shall he not profane the sanctuary of his God, —for the consecration of the anointing oil of his God is upon him—I, am Yahweh.
13 “‘Iye akwatire namwali wosadziwa mwamuna.
But, he, shall take a woman in her virginity:
14 Asakwatire mkazi wamasiye, mkazi wosudzulidwa, kapena mkazi wachiwerewere, koma akwatire namwali wosadziwa mwamuna pakati pa anthu a mtundu wake,
A widow or a divorced woman or one dishonoured—an unchaste woman, these, shall he not take, But, a virgin from among his own kinsfolk, shall he take to wife;
15 kuti mtundu wake usakhale wodetsedwa pakati pa abale popeza ndine Yehova, amene ndimamuyeretsa.’”
So shall he not profane his seed, among his kinsfolk, —For I—Yahweh, do hallow him.
16 Yehova anawuza Mose kuti,
And Yahweh spake unto Moses, saying:
17 “Muwuze Aaroni kuti, ‘Munthu aliyense mwa zidzukulu zake ku mibado yawo yonse ikubwera akakhala ndi chilema asabwere kudzapereka nsembe kwa Mulungu wake.
Speak unto Aaron, saying, —No man of thy seed, unto their generations in whom shall be any blemish, shall come near, to present the food of his God.
18 Munthu aliyense wachilema motere: munthu wakhungu kapena wolumala miyendo, munthu wolumala nkhope kapena waziwalo zambiri,
Surely, no man in whom is any blemish, shall come near, —No man who is blind or lame, or hath a flat nose, or is lanky;
19 munthu wa phazi lolumala kapena dzanja lolumala,
nor any man who hath a broken foot, —or a broken hand;
20 kapena munthu wokhota msana kapena wamfupi kwambiri, kapena wolumala maso, munthu wa nthenda yonyerenyetsa, kapena wamphere, kapenanso wophwanyika mavalo, sayenera kusendera pafupi.
or is hump-backed or a dwarf, or hath defective vision, —or hath scurvy or scab, or is crushed in the stones:
21 Mdzukulu aliyense wa Aaroni wansembe, amene ali ndi chilema asadzayandikire kukapereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Popeza kuti ali ndi chilema, asayandikire kudzapereka nsembe ya chakudya kwa Mulungu wake.
No, man in whom is a blemish of the seed of Aaron the priest, shall approach, to bring near the altar-flames of Yahweh, —a blemish, is in him, the food of his God, shall he not approach to bring near:
22 Koma iye angathe kudya chakudya chopatulika kwambiri chija, ngakhalenso chakudya chotsala pa nsembe zopatulika.
Of the food of his God, both of the most holy, —and the holy, may he eat:
23 Koma chifukwa cha kulumala kwake, sayenera kuyandikira katani kapena kufika pa guwa kuti angadetse malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.’”
Only, unto the veil, shall he not come in and unto the altar, shall he not approach—because, a blemish, is in him, so shall he not profane my sanctuaries, For, I—Yahweh, am hallowing them.
24 Choncho Mose anawuza Aaroni ndi ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse zimenezi.
And Moses spake [these things] unto Aaron, and unto his sons, —and unto all the sons of Israel.