< Levitiko 21 >

1 Yehova anawuza Mose kuti, “Yankhula ndi ansembe, ana a Aaroni, ndipo uwawuze kuti, ‘Wansembe asadzidetse pokhudza munthu wakufa pakati pa abale ake.
The Lord told Moses, “Tell Aaron's sons, the priests: A priest is not to make himself unclean by touching the dead body of any of his relatives.
2 Koma akhoza kukhudza thupi lakufa la amayi ake, abambo ake, mwana wake wamwamuna, mwana wake wamkazi, mchimwene wake,
The only exceptions are for his immediate family. This includes his mother, father, son, daughter, or brother,
3 kapena mlongo wake wosakwatiwa amene amadalira iye chifukwa sanakwatiwe. Iye akhoza kudzidetsa pokhudza thupi lakufa la mchemwali wake wosakwatiwa yekha.
or his unmarried sister since she is a close relative because she doesn't have a husband.
4 Koma wansembe asadzidetse chifukwa cha anthu amene ali nawo pa ubale obwera chifukwa cha ukwati.
He must not make himself unclean for those only related to him by marriage—he is not to make himself ceremonially impure.
5 “‘Ansembe asamete tsitsi kumutu kwawo kapena mʼmphepete mwa ndevu zawo, kapenanso kudzichekacheka pa thupi lawo.
Priests are not to shave bald spots on their heads, trim the sides of their beards, or cut their bodies.
6 Ayenera kukhala oyera pamaso pa Mulungu wawo ndipo asachititse manyazi dzina la Mulungu wawo. Popeza amapereka nsembe zotentha pa moto kwa Yehova, chakudya cha Mulungu wawo, iwo azikhala woyera.
They must be holy to their God and not disgrace their God's reputation. They are the one who present the food offerings to the Lord, the food of their God. Consequently they must be holy.
7 “‘Asakwatire akazi amene adzidetsa ndi chiwerewere kapena akazi amene amuna awo awasudzula, chifukwa ansembe ndi oyera pamaso pa Mulungu wawo.
A priest is not to marry a woman made unclean through prostitution or who is divorced by her husband, for the priest must be holy to his God.
8 Iwo akhale oyera chifukwa amapereka nsembe kwa Mulungu wanu. Muziwaona kuti ndi oyera, popeza Ine Yehova amene ndimawayeretsa ndine woyera, nawonso akhale oyera.
You shall consider him holy because he presents the food offerings to your God. He shall be holy to you, because I am holy. I am the Lord, and I chose you as my special people.
9 “‘Ngati mwana wamkazi wa wansembe adziyipitsa pochita zachiwerewere, ndiye kuti iye akuchititsa manyazi abambo ake; mwanayo atenthedwe pa moto.
A priest's daughter who makes herself unclean through prostitution makes her father unclean. She must be executed by burning.
10 “‘Munthu amene ali mkulu wa ansembe pakati pa abale ake, amene anamudzoza pomutsanulira mafuta pamutu pake, ndiponso amene anapatulidwa pomuveka zovala zaunsembe, asalekerere tsitsi lake kapena kungʼamba zovala zake kusonyeza kuti ali pa chisoni.
The high priest has the highest place among the other priests. He has been anointed with olive oil poured on his head and has been ordained to wear the priestly clothing. He must not leave his hair uncombed or tear his clothes.
11 Asalowe mʼnyumba mmene muli munthu wakufa ngakhale womwalirayo ndi amayi ake kapena abambo ake.
He is not to go near any dead body. He must not make himself unclean, even it is for his own father or mother.
12 Asadzidetse potulukira kunja kwa malo opatulika popeza mafuta womupatula kukhala wansembe ali pamutu pake. Ine ndine Yehova.
He must not leave to deal with someone who has died or make the sanctuary of his God unclean because he has been dedicated by the anointing oil of his God. I am the Lord.
13 “‘Iye akwatire namwali wosadziwa mwamuna.
He can only marry a virgin.
14 Asakwatire mkazi wamasiye, mkazi wosudzulidwa, kapena mkazi wachiwerewere, koma akwatire namwali wosadziwa mwamuna pakati pa anthu a mtundu wake,
He must not marry a widow, a divorced woman, or one made unclean through prostitution. He has to marry a virgin from his own people,
15 kuti mtundu wake usakhale wodetsedwa pakati pa abale popeza ndine Yehova, amene ndimamuyeretsa.’”
so that he doesn't make his children unclean among his people, for I am the Lord who makes him holy.”
16 Yehova anawuza Mose kuti,
The Lord told Moses,
17 “Muwuze Aaroni kuti, ‘Munthu aliyense mwa zidzukulu zake ku mibado yawo yonse ikubwera akakhala ndi chilema asabwere kudzapereka nsembe kwa Mulungu wake.
“Tell Aaron: These rules apply for all future generations. If any of your descendants has a physical defect, he is not allowed to come and present the food offerings of his God.
18 Munthu aliyense wachilema motere: munthu wakhungu kapena wolumala miyendo, munthu wolumala nkhope kapena waziwalo zambiri,
No man is allowed to do this if he has any defects, including anyone who is blind, crippled, facially disfigured, or has deformities,
19 munthu wa phazi lolumala kapena dzanja lolumala,
anyone who has a broken foot or arm,
20 kapena munthu wokhota msana kapena wamfupi kwambiri, kapena wolumala maso, munthu wa nthenda yonyerenyetsa, kapena wamphere, kapenanso wophwanyika mavalo, sayenera kusendera pafupi.
anyone who is a hunchback or dwarf, or who has cataracts, skin sores or scabs, or a damaged testicle.
21 Mdzukulu aliyense wa Aaroni wansembe, amene ali ndi chilema asadzayandikire kukapereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Popeza kuti ali ndi chilema, asayandikire kudzapereka nsembe ya chakudya kwa Mulungu wake.
No descendant of Aaron the priest who has a defect is allowed to come and present the food offerings to the Lord. Because he has a defect, he must not come and offer the food of his God.
22 Koma iye angathe kudya chakudya chopatulika kwambiri chija, ngakhalenso chakudya chotsala pa nsembe zopatulika.
He is still allowed to eat the food from the Most Holy Place of his God and also from the sanctuary,
23 Koma chifukwa cha kulumala kwake, sayenera kuyandikira katani kapena kufika pa guwa kuti angadetse malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.’”
but because he has a defect, he is not allowed to go near the curtain or the altar, so that my sanctuary and everything in it are not made unclean, because I am the Lord who makes them holy.”
24 Choncho Mose anawuza Aaroni ndi ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse zimenezi.
Moses repeated this to Aaron and his sons, and to all the Israelites.

< Levitiko 21 >