< Levitiko 20 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
INkosi yasikhuluma kuMozisi isithi:
2 “Uza Aisraeli kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala mu Israeli wopereka mwana wake kwa Moleki ayenera kuphedwa. Anthu a mʼdera lakelo amuphe ndi miyala.
Tshono futhi ebantwaneni bakoIsrayeli uthi: Ngulowo lalowo wabantwana bakoIsrayeli, loba owabezizweni abahlala njengabezizwe koIsrayeli, onikela okwenzalo yakhe kuMoleki, uzabulawa lokubulawa, abantu belizwe bazamkhanda ngamatshe.
3 Munthu ameneyo ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anzake.’ Popereka mwana wake kwa Moleki, wadetsa malo anga wopatulika ndi kuyipitsa dzina langa loyera.
Mina-ke ngizamisa ubuso bami bumelane lalowomuntu, ngimqume asuke phakathi kwabantu bakibo, ngoba enikele okwenzalo yakhe kuMoleki, ukuze angcolise indlu yami engcwele, eyise ibizo lami elingcwele.
4 Ngati anthu a mʼderalo achita ngati sakumuona munthuyo pamene akupereka mwana wake kwa Moleki ndi kusamupha,
Uba-ke abantu belizwe befihla lokufihla amehlo abo kulowomuntu nxa enikela okwenzalo yakhe kuMoleki, ukuze bangambulali,
5 Ineyo ndidzamufulatira pamodzi ndi banja lake. Ndidzawachotsa pakati pa anthu anzawo onse amene anamutsatira, nadziyipitsa okha popembedza Moleki.”
mina ngizamisa ubuso bami bumelane lalowomuntu njalo bumelane losapho lwakhe, ngimqume labo bonke abaphinga emva kwakhe, ukuthi baphinge belandela uMoleki, basuke phakathi kwabantu bakibo.
6 “‘Ngati munthu adzapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena kwa owombeza, nadziyipitsa powatsatira iwowo, Ine ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anthu anzake.
Umphefumulo, ophendukela-ke kulabo abalamadlozi lakwabalumbayo ukuphinga ubalandela, ngizamisa ubuso bami bumelane lalowomphefumulo, ngiwuqume usuke phakathi kwabantu bakibo.
7 “‘Chifukwa chake dzipatuleni ndi kukhala woyera popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Ngakho zingcweliseni libe ngcwele, ngoba ngiyiNkosi uNkulunkulu wenu.
8 Ndipo sungani malangizo anga ndi kuwatsata. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani.
Njalo gcinani izimiso zami, lizenze. NgiyiNkosi elingcwelisayo.
9 “‘Munthu aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa. Magazi ake adzakhala pamutu pake chifukwa iye watemberera abambo kapena amayi ake.
Ngoba ngulowo lalowo othuka uyise kumbe unina uzabulawa lokubulawa; uthukile uyise kumbe unina; igazi lakhe liphezu kwakhe.
10 “‘Ngati munthu wachita chigololo ndi mkazi wa mnzake, mwamunayo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa.
Lendoda efeba lomfazi womuntu, efeba lomkamakhelwane wayo, izabulawa lokubulawa, isifebe lesifebekazi.
11 “‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa abambo ake, wachititsa manyazi abambo ake. Munthuyo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa. Magazi awo adzakhala pa mitu pake.
Lendoda elala lomkayise yembule ubunqunu bukayise; bobabili bazabulawa lokubulawa; igazi labo liphezu kwabo.
12 “‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa mwana wake, awiriwo ayenera kuphedwa. Iwo achita chinthu chonyansa kwambiri. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
Lendoda elala lomalokazana wayo, bobabili bazabulawa lokubulawa; benze ingxube; igazi labo liphezu kwabo.
13 “‘Ngati munthu agonana ndi mwamuna mnzake ngati akugonana ndi mkazi, ndiye kuti onsewo achita chinthu cha manyazi. Choncho aphedwe. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
Lendoda elala lowesilisa njengokulala lowesifazana, bobabili benze isinengiso; bazabulawa lokubulawa; igazi labo liphezu kwabo.
14 “‘Ngati munthu akwatira mkazi, nakwatiranso amayi ake, chimenecho ndi chinthu choyipa kwambiri. Mwamunayo pamodzi ndi akaziwo ayenera kutenthedwa pa moto kuti chinthu choyipa chotere chisapezekenso pakati panu.
Lendoda ethatha umfazi kanye lonina, kuyinkohlakalo. Bazatshiswa ngomlilo, yena labo, ukuze kungabi khona inkohlakalo phakathi kwenu.
15 “‘Ngati mwamuna agonana ndi nyama, iye ayenera kuphedwa, ndipo muyeneranso kupha nyamayo.
Lendoda elala lenyamazana, izabulawa lokubulawa, futhi lizayibulala inyamazana.
16 “‘Ngati mkazi agonana ndi nyama, aphedwe pamodzi ndi nyamayo. Mkaziyo ndi nyamayo ayenera kuphedwa, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
Lowesifazana osondela lakuyiphi inyamazana ukulala layo, uzabulala owesifazana lenyamazana; bazabulawa lokubulawa; igazi labo liphezu kwabo.
17 “‘Ngati munthu akakwatira mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake, kapena mwana wamkazi wa amayi ake, ndipo iwo nʼkugonana, ndiye kuti achita chinthu chochititsa manyazi. Onse awiri ayenera kuchotsedwa pa gulu la abale awo. Tsono popeza munthuyo wachititsa manyazi mlongo wake, adzayenera kulandira chilango.
Lendoda ethatha udadewabo, indodakazi kayise loba indodakazi kanina, ibone ubunqunu bakhe, laye abone ubunqunu bayo, kulihlazo; njalo bazaqunywa emehlweni abantwana babantu bakibo; yembule ubunqunu bukadadewabo; izathwala ububi bayo.
18 “‘Ngati munthu agonana ndi mkazi pa nthawi yake yosamba, ndiye kuti wavula msambo wake, ndipo mkaziyo wadzivulanso. Onse awiri achotsedwe pakati pa anthu anzawo.
Lendoda elala lowesifazana ogulayo, yembule ubunqunu bakhe, inqunule umthombo wakhe, laye wembule umthombo wegazi lakhe, bobabili bazaqunywa basuke phakathi kwabantu bakibo.
19 “‘Musagonane ndi mchemwali wa amayi anu kapena abambo anu, pakuti kutero ndi kuchititsa manyazi mʼbale wanu. Nonse mudzalipira mlandu wanu.
Njalo ungembuli ubunqunu bukadadewabo kanyoko, loba obukadadewabo kayihlo; ngoba wembule isihlobo sakhe; bazathwala ububi babo.
20 “‘Ngati munthu agonana ndi azakhali ake, munthuyo wachititsa manyazi a malume ake. Onse adzalipira mlandu wawo. Onsewo adzafa wopanda mwana.
Lendoda elala lomkamfowabo kayise, yembule ubunqunu bomfowabo kayise; bazathwala isono sabo; bafe bengelabantwana.
21 “‘Munthu akakwatira mkazi wa mchimwene wake ndiye kuti wachita chinthu chonyansa. Wachititsa manyazi mʼbale wakeyo. Onse awiriwo adzakhala wopanda mwana.
Lendoda ethatha umkamfowabo, kuyikungcola; yembule ubunqunu bukamfowabo; bazakuba ngabangelabantwana.
22 “‘Nʼchifukwa chake muzisunga malangizo anga onse ndi malamulo anga ndipo muwatsatire kuti ku dziko limene Ine ndikupita nanu kuti mukakhalemo lisakakusanzeni.
Ngakho gcinani zonke izimiso zami lezahlulelo zonke zami, lizenze, ukuze ilizwe engililetha kulo ukuhlala kulo lingalihlanzi.
23 Musatsanzire miyambo ya mitundu ya anthu imene ndi kuyipirikitsa inu mukufika. Chifukwa iwo anachita zinthu zonsezi, ndipo Ine ndinanyansidwa nawo.
Njalo lingahambi ngezimiso zesizwe engisixotshayo phambi kwenu; ngoba benze zonke lezizinto; ngakho nganengwa yibo.
24 Koma Ine ndinakuwuzani kuti, ‘Mudzatenga dziko lawo. Ine ndidzakupatsani dzikolo kuti likhale cholowa chanu, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’ Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndakupatulani pakati pa mitundu yonse ya anthu.
Kodwa ngathi kini: Lizakudla ilifa lelizwe labo; mina ngizalinika ukuthi lidle ilifa lalo, ilizwe eligeleza uchago loluju. NgiyiNkosi uNkulunkulu wenu, olehlukanise labezizwe.
25 “‘Chifukwa chake muzisiyanitsa pakati pa nyama zoyeretsedwa ndi nyama zodetsedwa ndiponso pakati pa mbalame zoyeretsedwa ndi mbalame zodetsedwa. Musadzidetse pakudya nyama iliyonse kapena mbalame, kapena chilichonse chimene chimakwawa pansi, chimene Ine ndachipatula kuti chikhale chodetsedwa kwa inu.
Ngakho yehlukanisani phakathi kwenyamazana ezihlambulukileyo lezingahlambulukanga, laphakathi kwezinyoni ezingahlambulukanga lezihlambulukileyo; lingenzi imiphefumulo yenu inengeke ngezinyamazana loba ngezinyoni loba ngakuphi okuhuquzelayo emhlabathini, engikwehlukanise lani njengokungcolileyo.
26 Muzikhala woyera pamaso panga chifukwa Ine Yehova, ndine woyera ndipo ndakupatulani pakati pa anthu a mitundu yonse kuti mukhale anthu anga.
Njalo lizakuba ngcwele kimi, ngoba mina Nkosi ngingcwele; ngilehlukanisile labezizwe ukuze libe ngabami.
27 “‘Mwamuna kapena mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena wanyanga pakati panu ayenera kuphedwa. Muwagende ndi miyala, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.’”
Njalo owesilisa loba owesifazana, abalamadlozi loba abalumbayo, bazabulawa lokubulawa, bazabakhanda ngamatshe; igazi labo liphezu kwabo.

< Levitiko 20 >