< Levitiko 20 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
OLELO mai la o Iehova ia Mose, i mai la,
2 “Uza Aisraeli kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala mu Israeli wopereka mwana wake kwa Moleki ayenera kuphedwa. Anthu a mʼdera lakelo amuphe ndi miyala.
E olelo hou aku oe i na mamo a Iseraela, O kela kanaka keia kanaka, o na mamo a Iseraela, a o na malihini e noho ana ma ka Iseraela, nana e haawi i kahi keiki ana ia Moleka, e make io no ua kanaka la; na na kanaka o ka aina ia e hailuku aku me na pohaku.
3 Munthu ameneyo ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anzake.’ Popereka mwana wake kwa Moleki, wadetsa malo anga wopatulika ndi kuyipitsa dzina langa loyera.
A e hooku e au i ko'u maka i kela kanaka, a e oki aku hoi au ia ia maiwaena aku o kona poe kanaka, no kona haawi ana i kekahi keiki ana ia Moleka; e hoohaumia i kuu keenakapu, a me ka hoino i ko'u inoa hoano.
4 Ngati anthu a mʼderalo achita ngati sakumuona munthuyo pamene akupereka mwana wake kwa Moleki ndi kusamupha,
A ina e huna iki na kanaka o ka aina i ko lakou mau maka i na kanaka la, i kona wa e haawi ai i kekahi keiki ana ia Moleka, aole hoi hoomake ia ia;
5 Ineyo ndidzamufulatira pamodzi ndi banja lake. Ndidzawachotsa pakati pa anthu anzawo onse amene anamutsatira, nadziyipitsa okha popembedza Moleki.”
Alaila, na'u no e hooku e i kuu maka i ua kanaka la a me kona ohana, a e oki aku au ia ia, a me ka poe a pau e hele moe kolohe mamuli ona, e moe kolohe me Moleka, maiwaena aku o ko lakou poe kanaka.
6 “‘Ngati munthu adzapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena kwa owombeza, nadziyipitsa powatsatira iwowo, Ine ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anthu anzake.
A o ke kanaka huli mamuli o na mea ninau-uhane, a mamuli hoi o na kupua, e hele moe kolohe mamuli o lakou, e hooku e au i kuu maka i kela kanaka, a e oki aku hoi au ia ia maiwaena aku o kona poe kanaka.
7 “‘Chifukwa chake dzipatuleni ndi kukhala woyera popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Nolaila, e huikala oukou ia oukou iho, i hoano hoi oukou: no ka mea, owau no Iehova ko oukou Akua.
8 Ndipo sungani malangizo anga ndi kuwatsata. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani.
E malama oukou i ko'u mau kanawai, a e hana hoi ma ia mau mea: owau no Iehova nana oukou e hoolaa nei.
9 “‘Munthu aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa. Magazi ake adzakhala pamutu pake chifukwa iye watemberera abambo kapena amayi ake.
No ka mea, o kela kanaka keia kanaka i kuamuamu i kona makuakane a i kona makuwahine paha, e make io no ia: ua hoino aku oia i kona makuakane, a i kona makuwahine paha; maluna ona kona koko iho.
10 “‘Ngati munthu wachita chigololo ndi mkazi wa mnzake, mwamunayo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa.
O ke kanaka moe kolohe aku i ka wahine a kekahi kanaka, o ka mea moe kolohe i ka wahine a kona hoalauna, e make io no ke kanaka moe kolohe a me ka wahine moe kolohe.
11 “‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa abambo ake, wachititsa manyazi abambo ake. Munthuyo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa. Magazi awo adzakhala pa mitu pake.
O ke kanaka moe me ka wahine a kona makuakane, ua wehe ae oia i kahi huna o kona makuakane; e make io no laua pu; maluna o laua ko laua koko iho.
12 “‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa mwana wake, awiriwo ayenera kuphedwa. Iwo achita chinthu chonyansa kwambiri. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
Ina e moe ke kanaka me kana hunonawahine, e make io no laua pu, ua hana laua i ka mea haumia hilahila; maluna o laua ko laua koko iho.
13 “‘Ngati munthu agonana ndi mwamuna mnzake ngati akugonana ndi mkazi, ndiye kuti onsewo achita chinthu cha manyazi. Choncho aphedwe. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
Ina e moe aku ke kanaka i ke kane e like me kona moe aku i ka wahine, ua hana pu laua i ka mea haumia hilahila; e make io no laua pu; maluna o laua ko laua koko.
14 “‘Ngati munthu akwatira mkazi, nakwatiranso amayi ake, chimenecho ndi chinthu choyipa kwambiri. Mwamunayo pamodzi ndi akaziwo ayenera kutenthedwa pa moto kuti chinthu choyipa chotere chisapezekenso pakati panu.
Ina e mare ke kanaka i ka wahine a me kona makuwahine, he hewa ia: e puhi pu ia lakou i ke ahi, oia pu me laua la; i ole ai he hewa iwaena o oukou.
15 “‘Ngati mwamuna agonana ndi nyama, iye ayenera kuphedwa, ndipo muyeneranso kupha nyamayo.
A ina e moe ke kanaka i ka holoholona, e make io no ia; a e pepehi oukou ia holoholona.
16 “‘Ngati mkazi agonana ndi nyama, aphedwe pamodzi ndi nyamayo. Mkaziyo ndi nyamayo ayenera kuphedwa, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
A ina e hookokoke aku ka wahine i ka holoholona e moe iho ia ia, e pepehi oe ia wahine, a me ka holoholona: e make io no laua pu; maluna o laua ko laua koko.
17 “‘Ngati munthu akakwatira mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake, kapena mwana wamkazi wa amayi ake, ndipo iwo nʼkugonana, ndiye kuti achita chinthu chochititsa manyazi. Onse awiri ayenera kuchotsedwa pa gulu la abale awo. Tsono popeza munthuyo wachititsa manyazi mlongo wake, adzayenera kulandira chilango.
A ina e lawe ke kanaka i kona kaikuwahine, i ke kaikamahine a kona makuakane, a i ke kaikamahine a kona makuwahine paha, a ike aku i kona wahi huna, a ike mai kela i kona wahi huna, he mea hewa io no ia; e okiia laua ma ke alo o ko laua poe kanaka: ua wehe oia i kahi huna o kona kaikuwahine; e kau no kona hewa maluna ona.
18 “‘Ngati munthu agonana ndi mkazi pa nthawi yake yosamba, ndiye kuti wavula msambo wake, ndipo mkaziyo wadzivulanso. Onse awiri achotsedwe pakati pa anthu anzawo.
A ina e moe aku ke kanaka i ka wahine i kona mai ana, a wehe ae i kona wahi huna; ua wehe ae ia i kona punawai, a ua wehe ae ia wahine i ke kumu o kona koko, e oki pu ia'ku hoi laua maiwaena aku o ko laua poe kanaka.
19 “‘Musagonane ndi mchemwali wa amayi anu kapena abambo anu, pakuti kutero ndi kuchititsa manyazi mʼbale wanu. Nonse mudzalipira mlandu wanu.
Mai wehe oe i kahi huna o ka hoahanauwahine o kou makuwahine, a o ke kaikuwahine a kou makuakane paha; no ka mea, oia ka wehe i kona io iho; e kau no ko laua hewa maluna o laua.
20 “‘Ngati munthu agonana ndi azakhali ake, munthuyo wachititsa manyazi a malume ake. Onse adzalipira mlandu wawo. Onsewo adzafa wopanda mwana.
A ina e moe aku ke kanaka me ka wahine a ka hoahanaukane o kona makuakane, ua wehe ae oia i kahi huna o kela makuakane; e kau no ko laua hewa maluna o laua, e make keiki ole laua.
21 “‘Munthu akakwatira mkazi wa mchimwene wake ndiye kuti wachita chinthu chonyansa. Wachititsa manyazi mʼbale wakeyo. Onse awiriwo adzakhala wopanda mwana.
A ina e lawe ke kanaka, i ka wahine a kona hoahanaukane, he mea haumia ia; ua wehe ae oia i kahi huna o kona hoahanaukane, aole aku keiki a laua.
22 “‘Nʼchifukwa chake muzisunga malangizo anga onse ndi malamulo anga ndipo muwatsatire kuti ku dziko limene Ine ndikupita nanu kuti mukakhalemo lisakakusanzeni.
Nolaila, e malama oukou I ka'u mau kauoha a pau, a me ko'u mau kanawai a pau; i ole ai ka aina kahi a'u e lawe aku ai ia oukou e noho malaila, e luai aku ia oukou.
23 Musatsanzire miyambo ya mitundu ya anthu imene ndi kuyipirikitsa inu mukufika. Chifukwa iwo anachita zinthu zonsezi, ndipo Ine ndinanyansidwa nawo.
Mai hele oukou ma na oihana a na lahuikanaka, a'u e kiola aku ai imua o oukou: no ka mea, ua hana lakou i keia mau mea a pau, nolaila i hoowahawaha aku ai au ia lakou.
24 Koma Ine ndinakuwuzani kuti, ‘Mudzatenga dziko lawo. Ine ndidzakupatsani dzikolo kuti likhale cholowa chanu, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’ Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndakupatulani pakati pa mitundu yonse ya anthu.
Aka, ua olelo aku au ia oukou, e loaa ia oukou ko lakou aina; na'u ia e haawi aku no oukou ponoi, he aina e kahe ai ka waiu a me ka meli: owau no Iehova ko oukou Akua nana oukou i hookaawale ae mai na lahuikanaka e ae.
25 “‘Chifukwa chake muzisiyanitsa pakati pa nyama zoyeretsedwa ndi nyama zodetsedwa ndiponso pakati pa mbalame zoyeretsedwa ndi mbalame zodetsedwa. Musadzidetse pakudya nyama iliyonse kapena mbalame, kapena chilichonse chimene chimakwawa pansi, chimene Ine ndachipatula kuti chikhale chodetsedwa kwa inu.
Nolaila e hookaawale ae oukou iwaena o na holoholona maemae, a me ka haumia, a mawaena o na manu haumia, a me ka maemae: mai hoohaumia i ko oukou mau uhane ma kahi holoholona, a me kahi manu, a me kahi mea e kolo ana ma ka lepo, na mea a'u i hookaawale ae mai o oukou ae, me he haumia la.
26 Muzikhala woyera pamaso panga chifukwa Ine Yehova, ndine woyera ndipo ndakupatulani pakati pa anthu a mitundu yonse kuti mukhale anthu anga.
E hoano hoi oukou no'u; no ka mea, he hoano no wau, o Iehova, a ua hookaawale ae au ia oukou mai na lahuikanaka e i lilo oukou no'u.
27 “‘Mwamuna kapena mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena wanyanga pakati panu ayenera kuphedwa. Muwagende ndi miyala, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.’”
O ke kanaka, a o ka wahine paha, he ninau-uhane, a he kupua paha, e make no ia; e hailuku lakou ia laua me na pohaku; e kau no ko laua koko maluna o laua.