< Levitiko 20 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
2 “Uza Aisraeli kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala mu Israeli wopereka mwana wake kwa Moleki ayenera kuphedwa. Anthu a mʼdera lakelo amuphe ndi miyala.
Sig til Israeliterne: Om nogen af Israeliterne eller de fremmede, der bor hos Israel, giver sit Afkom hen til Molok, da skal han lide Døden; Landets Indbyggere skal stene ham,
3 Munthu ameneyo ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anzake.’ Popereka mwana wake kwa Moleki, wadetsa malo anga wopatulika ndi kuyipitsa dzina langa loyera.
og jeg vender selv mit Åsyn imod den Mand og udrydder ham af hans Folk, fordi han gav sit Afkom hen til Molok for at gøre min Helligdom uren og vanhellige mit hellige Navn;
4 Ngati anthu a mʼderalo achita ngati sakumuona munthuyo pamene akupereka mwana wake kwa Moleki ndi kusamupha,
og ser end Landets Indbyggere igennem Fingre med den Mand, når han giver sit Afkom hen til Molok, og undlader at dræbe ham,
5 Ineyo ndidzamufulatira pamodzi ndi banja lake. Ndidzawachotsa pakati pa anthu anzawo onse amene anamutsatira, nadziyipitsa okha popembedza Moleki.”
så vender jeg dog selv mit Åsyn imod den Mand og hans Slægt og udrydder ham og alle dem, der følger i hans Spor og boler med Molok, af deres Folk.
6 “‘Ngati munthu adzapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena kwa owombeza, nadziyipitsa powatsatira iwowo, Ine ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anthu anzake.
Det Menneske, som henvender sig til Genfærd eller Sandsigerånder og boler med dem, mod det Menneske vil jeg vende mit Åsyn og udrydde ham af hans Folk.
7 “‘Chifukwa chake dzipatuleni ndi kukhala woyera popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Helliger eder og vær hellige; thi jeg er HERREN eders Gud!
8 Ndipo sungani malangizo anga ndi kuwatsata. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani.
Hold mine Anordninger og gør efter dem. Jeg er HERREN, som helliger eder!
9 “‘Munthu aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa. Magazi ake adzakhala pamutu pake chifukwa iye watemberera abambo kapena amayi ake.
Thi enhver, som forbander sin Fader og sin Moder, skal lide Døden; han har forbandet sin Fader og sin Moder, derfor hviler der Blodskyld på ham.
10 “‘Ngati munthu wachita chigololo ndi mkazi wa mnzake, mwamunayo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa.
Om nogen bedriver Hor med en anden Mands Hustru, om nogen bedriver Hor med sin Næstes Hustru, da skal de lide Døden, Horkarlen såvel som Horkvinden.
11 “‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa abambo ake, wachititsa manyazi abambo ake. Munthuyo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa. Magazi awo adzakhala pa mitu pake.
Om nogen har Samleje med sin Faders Hustru, har han blottet sin Faders Blusel; de skal begge lide Døden, der hviler Blodskyld på dem.
12 “‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa mwana wake, awiriwo ayenera kuphedwa. Iwo achita chinthu chonyansa kwambiri. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
Om nogen har Samleje med sin Sønnekone, skal de begge lide Døden; de har øvet Skændselsdåd, der hviler Blodskyld på dem.
13 “‘Ngati munthu agonana ndi mwamuna mnzake ngati akugonana ndi mkazi, ndiye kuti onsewo achita chinthu cha manyazi. Choncho aphedwe. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
Om nogen ligger hos en Mand, på samme Måde som man ligger hos en Kvinde, da har de begge øvet en Vederstyggelighed; de skal lide Døden, der hviler Blodskyld på dem.
14 “‘Ngati munthu akwatira mkazi, nakwatiranso amayi ake, chimenecho ndi chinthu choyipa kwambiri. Mwamunayo pamodzi ndi akaziwo ayenera kutenthedwa pa moto kuti chinthu choyipa chotere chisapezekenso pakati panu.
Om nogen ægter en Kvinde og hendes Moder, er det grov Utugt: man skal brænde både ham og begge Kvinderne; der må ikke findes grov Utugt iblandt eder.
15 “‘Ngati mwamuna agonana ndi nyama, iye ayenera kuphedwa, ndipo muyeneranso kupha nyamayo.
Om nogen har Omgang med et Dyr, skal han lide Døden, og Dyret skal I slå ihjel.
16 “‘Ngati mkazi agonana ndi nyama, aphedwe pamodzi ndi nyamayo. Mkaziyo ndi nyamayo ayenera kuphedwa, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
Om en Kvinde kommer noget Dyr nær for at have kønslig Omgang med det, da skal du ihjelslå både Kvinden og Dyret; de skal lide Døden, der hviler Blodskyld på dem.
17 “‘Ngati munthu akakwatira mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake, kapena mwana wamkazi wa amayi ake, ndipo iwo nʼkugonana, ndiye kuti achita chinthu chochititsa manyazi. Onse awiri ayenera kuchotsedwa pa gulu la abale awo. Tsono popeza munthuyo wachititsa manyazi mlongo wake, adzayenera kulandira chilango.
Om en Mand tager sin Søster, sin Faders eller sin Moders Datter, til Ægte, så han ser hendes Blusel, og hun hans, da er det en skammelig Gerning; de skal udryddes i deres Landsmænds Påsyn; han har blottet sin Søsters Blusel, han skal undgælde for sin Brøde.
18 “‘Ngati munthu agonana ndi mkazi pa nthawi yake yosamba, ndiye kuti wavula msambo wake, ndipo mkaziyo wadzivulanso. Onse awiri achotsedwe pakati pa anthu anzawo.
Om en Mand har Samleje med en Kvinde under hendes månedlige Svaghed og blotter hendes Blusel, idet han afdækker hendes Kilde, og hun afdækker sit Blods Kilde, da skal de begge udryddes af deres Folk.
19 “‘Musagonane ndi mchemwali wa amayi anu kapena abambo anu, pakuti kutero ndi kuchititsa manyazi mʼbale wanu. Nonse mudzalipira mlandu wanu.
Du må ikke blotte din Mosters og din Fasters Blusel, thi den, der gør det, afdækker sin kødelige Slægtnings Blusel; de skal undgælde for deres Brøde.
20 “‘Ngati munthu agonana ndi azakhali ake, munthuyo wachititsa manyazi a malume ake. Onse adzalipira mlandu wawo. Onsewo adzafa wopanda mwana.
Om nogen har Samleje med sin Farbroders Hustru, da har han blottet sin Farbroders Blusel, de skal undgælde for deres Synd og dø barnløse.
21 “‘Munthu akakwatira mkazi wa mchimwene wake ndiye kuti wachita chinthu chonyansa. Wachititsa manyazi mʼbale wakeyo. Onse awiriwo adzakhala wopanda mwana.
Om nogen tager sin Broders Hustru til Ægte, da er det en uren Gerning; han har blottet sin Broders Blusel; de skal blive barnløse.
22 “‘Nʼchifukwa chake muzisunga malangizo anga onse ndi malamulo anga ndipo muwatsatire kuti ku dziko limene Ine ndikupita nanu kuti mukakhalemo lisakakusanzeni.
Hold alle mine Anordninger og Lovbud og gør efter dem, at ikke Landet, jeg føler eder ind at bo i, skal udspy eder.
23 Musatsanzire miyambo ya mitundu ya anthu imene ndi kuyipirikitsa inu mukufika. Chifukwa iwo anachita zinthu zonsezi, ndipo Ine ndinanyansidwa nawo.
Følg ikke det Folks Skikke, som jeg driver bort foran eder, thi de har øvet alt dette; derfor væmmedes jeg ved dem
24 Koma Ine ndinakuwuzani kuti, ‘Mudzatenga dziko lawo. Ine ndidzakupatsani dzikolo kuti likhale cholowa chanu, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’ Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndakupatulani pakati pa mitundu yonse ya anthu.
og sagde til eder: I skal få deres Land i Eje; jeg giver eder det i Eje, et Land, der flyder med Mælk og Honning. Jeg er HERREN eders Gud, som har udskilt eder fra alle andre Folkeslag.
25 “‘Chifukwa chake muzisiyanitsa pakati pa nyama zoyeretsedwa ndi nyama zodetsedwa ndiponso pakati pa mbalame zoyeretsedwa ndi mbalame zodetsedwa. Musadzidetse pakudya nyama iliyonse kapena mbalame, kapena chilichonse chimene chimakwawa pansi, chimene Ine ndachipatula kuti chikhale chodetsedwa kwa inu.
I skal skelne mellem rene og urene Dyr og mellem urene og rene Fugle for ikke at gøre eder selv til en Vederstyggelighed ved de Dyr og de Fugle og alt, hvad der rører sig på Jorden, alt, hvad jeg har udskilt for eder og erklæret for urent.
26 Muzikhala woyera pamaso panga chifukwa Ine Yehova, ndine woyera ndipo ndakupatulani pakati pa anthu a mitundu yonse kuti mukhale anthu anga.
Og I skal være mig hellige, thi jeg HERREN er hellig, og jeg har udskilt eder fra alle andre Folkeslag til at høre mig til.
27 “‘Mwamuna kapena mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena wanyanga pakati panu ayenera kuphedwa. Muwagende ndi miyala, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.’”
Når der i en Mand eller Kvinde er en Genfærdsånd eller en Sandsigerånd, skal de lide Døden; de skal stenes, der hviler Blodskyld på dem.

< Levitiko 20 >