< Levitiko 20 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Og Herren talede til Mose og sagde:
2 “Uza Aisraeli kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala mu Israeli wopereka mwana wake kwa Moleki ayenera kuphedwa. Anthu a mʼdera lakelo amuphe ndi miyala.
Og du skal sige til Israels Børn: Hvo som helst af Israels Børn eller af de fremmede, som opholde sig i Israel, der hengiver nogen af sin Sæd til Molek, skal visselig dødes; Folket i Landet skulle stene ham med Stene.
3 Munthu ameneyo ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anzake.’ Popereka mwana wake kwa Moleki, wadetsa malo anga wopatulika ndi kuyipitsa dzina langa loyera.
Og jeg vil sætte mit Ansigt imod denne Mand, og jeg vil udrydde ham midt af sit Folk, fordi han hengav af sin Sæd til Molek, til at gøre min Helligdom uren og at vanhellige mit hellige Navn.
4 Ngati anthu a mʼderalo achita ngati sakumuona munthuyo pamene akupereka mwana wake kwa Moleki ndi kusamupha,
Og dersom Folket i Landet ser igennem Fingre med det samme Menneske, naar han hengiver nogen af sin Sæd til Molek, saa at de ikke ihjelslaa ham,
5 Ineyo ndidzamufulatira pamodzi ndi banja lake. Ndidzawachotsa pakati pa anthu anzawo onse amene anamutsatira, nadziyipitsa okha popembedza Moleki.”
da vil jeg sætte mit Ansigt imod det Menneske og imod hans Slægt; og ham og alle dem, som efterfølge hans Bolen med at bole med Molek, vil jeg udrydde midt af deres Folk.
6 “‘Ngati munthu adzapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena kwa owombeza, nadziyipitsa powatsatira iwowo, Ine ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anthu anzake.
Og naar en Person vender sig til Spaakvinder eller til Tegnsudlæggere, til at bole med dem, da vil jeg sætte mit Ansigt imod denne Person, og jeg vil udrydde ham fra hans Folk.
7 “‘Chifukwa chake dzipatuleni ndi kukhala woyera popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Derfor helliger eder og værer hellige; thi jeg er Herren eders Gud.
8 Ndipo sungani malangizo anga ndi kuwatsata. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani.
Og holder mine Skikke, og gører dem; jeg er Herren, som gør eder hellige.
9 “‘Munthu aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa. Magazi ake adzakhala pamutu pake chifukwa iye watemberera abambo kapena amayi ake.
Thi hvo som helst der bander sin Fader eller sin Moder, skal visselig dødes; han bandede sin Fader eller sin Moder, hans Blod være over ham.
10 “‘Ngati munthu wachita chigololo ndi mkazi wa mnzake, mwamunayo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa.
Og en Mand, som bedriver Hor med en Mands Hustru, den, som bedriver Hor med sin Næstes Hustru, den Horkarl og den Horekone skal visselig dødes.
11 “‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa abambo ake, wachititsa manyazi abambo ake. Munthuyo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa. Magazi awo adzakhala pa mitu pake.
Og en Mand, som ligger hos sin Faders Hustru, han har blottet sin Faders Blusel; de skulle begge visselig dødes, deres Blod skal være over dem.
12 “‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa mwana wake, awiriwo ayenera kuphedwa. Iwo achita chinthu chonyansa kwambiri. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
Og naar en Mand ligger hos sin Søns Hustru, da skulle de begge visselig dødes; de have gjort en Skændighed, deres Blod skal være over dem.
13 “‘Ngati munthu agonana ndi mwamuna mnzake ngati akugonana ndi mkazi, ndiye kuti onsewo achita chinthu cha manyazi. Choncho aphedwe. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
Og naar en Mand ligger hos en Mandsperson, som man ligger hos en Kvinde, da have de begge gjort en Vederstyggelighed; de skulle visselig dødes, deres Blod skal være over dem.
14 “‘Ngati munthu akwatira mkazi, nakwatiranso amayi ake, chimenecho ndi chinthu choyipa kwambiri. Mwamunayo pamodzi ndi akaziwo ayenera kutenthedwa pa moto kuti chinthu choyipa chotere chisapezekenso pakati panu.
Og naar en Mand tager en Kvinde og hendes Moder til Ægte, er det en Skændsel; de skulle brænde baade ham og dem med Ild, og der skal ikke være nogen Skændsel iblandt eder.
15 “‘Ngati mwamuna agonana ndi nyama, iye ayenera kuphedwa, ndipo muyeneranso kupha nyamayo.
Og en Mand, som ligger hos et Dyr, skal visselig dødes, og Dyret skulle I dræbe.
16 “‘Ngati mkazi agonana ndi nyama, aphedwe pamodzi ndi nyamayo. Mkaziyo ndi nyamayo ayenera kuphedwa, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
Og naar en Kvinde kommer nær til noget Dyr, at det har Fællesskab med hende, da skal du ihjelslaa baade Kvinden og Dyret; de skulle visselig dødes, deres Blod skal være over dem.
17 “‘Ngati munthu akakwatira mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake, kapena mwana wamkazi wa amayi ake, ndipo iwo nʼkugonana, ndiye kuti achita chinthu chochititsa manyazi. Onse awiri ayenera kuchotsedwa pa gulu la abale awo. Tsono popeza munthuyo wachititsa manyazi mlongo wake, adzayenera kulandira chilango.
Og naar en Mand tager sin Søster, sin Faders Datter eller sin Moders Datter, til Ægte, og ser hendes Blusel, og hun ser hans Blusel, saa er det en gruelig Ting, og de skulle udryddes for deres Folks Børns Øjne; han blottede sin Søsters Blusel, han skal bære sin Misgerning.
18 “‘Ngati munthu agonana ndi mkazi pa nthawi yake yosamba, ndiye kuti wavula msambo wake, ndipo mkaziyo wadzivulanso. Onse awiri achotsedwe pakati pa anthu anzawo.
Og naar en Mand ligger hos en Hustru, som er svag, og blotter hendes Blusel, blotter hendes Kilde, og hun blotter sin Blods Kilde, da skulle de begge udryddes af deres Folk.
19 “‘Musagonane ndi mchemwali wa amayi anu kapena abambo anu, pakuti kutero ndi kuchititsa manyazi mʼbale wanu. Nonse mudzalipira mlandu wanu.
Og du skal ikke blotte din Moders Søsters og din Faders Søsters Blusel; thi en saadan har blottet sin næste Slægt, de skulle bære deres Misgerning.
20 “‘Ngati munthu agonana ndi azakhali ake, munthuyo wachititsa manyazi a malume ake. Onse adzalipira mlandu wawo. Onsewo adzafa wopanda mwana.
Og naar en Mand ligger hos sin Farbroders Hustru, han har blottet sin Farbroders Blusel; de skulle bære deres Synd, de skulle dø barnløse.
21 “‘Munthu akakwatira mkazi wa mchimwene wake ndiye kuti wachita chinthu chonyansa. Wachititsa manyazi mʼbale wakeyo. Onse awiriwo adzakhala wopanda mwana.
Og dersom en Mand tager sin Broders Hustru til Ægte, det er en slem Gerning; han blottede sin Broders Blusel, de skulle være barnløse.
22 “‘Nʼchifukwa chake muzisunga malangizo anga onse ndi malamulo anga ndipo muwatsatire kuti ku dziko limene Ine ndikupita nanu kuti mukakhalemo lisakakusanzeni.
Saa skulle I holde alle mine Skikke og alle mine Bud og gøre dem, at Landet, som jeg vil føre eder ind udi, til at bo derudi, ikke skal udspy eder.
23 Musatsanzire miyambo ya mitundu ya anthu imene ndi kuyipirikitsa inu mukufika. Chifukwa iwo anachita zinthu zonsezi, ndipo Ine ndinanyansidwa nawo.
Og I skulle ikke vandre i det Folks Skikke, hvilket jeg skal udkaste for eder; thi alle disse Ting have de gjort, og jeg væmmedes ved dem.
24 Koma Ine ndinakuwuzani kuti, ‘Mudzatenga dziko lawo. Ine ndidzakupatsani dzikolo kuti likhale cholowa chanu, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’ Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndakupatulani pakati pa mitundu yonse ya anthu.
Men jeg siger eder: I skulle eje deres Land, og jeg vil give eder det til Eje, et Land, som flyder med Mælk og Honning. Jeg er Herren eders Gud, som har udskilt eder fra Folkene.
25 “‘Chifukwa chake muzisiyanitsa pakati pa nyama zoyeretsedwa ndi nyama zodetsedwa ndiponso pakati pa mbalame zoyeretsedwa ndi mbalame zodetsedwa. Musadzidetse pakudya nyama iliyonse kapena mbalame, kapena chilichonse chimene chimakwawa pansi, chimene Ine ndachipatula kuti chikhale chodetsedwa kwa inu.
Og I skulle gøre Skilsmisse imellem rene og urene Dyr og imellem urene og rene Fugle; og I skulle ikke gøre eders Sjæle vederstyggelige med Dyr og med Fugle og med alt det, som kryber paa Jorden, hvilket jeg har fraskilt for eder, at I skulle holde det urent.
26 Muzikhala woyera pamaso panga chifukwa Ine Yehova, ndine woyera ndipo ndakupatulani pakati pa anthu a mitundu yonse kuti mukhale anthu anga.
Derfor skulle I være mig hellige, thi jeg Herren er hellig; og jeg har udskilt eder fra Folkene til at høre mig til.
27 “‘Mwamuna kapena mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena wanyanga pakati panu ayenera kuphedwa. Muwagende ndi miyala, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.’”
Og naar af Mand eller Kvinde nogen er en Spaamand eller Tegnsudlægger, skulle de visselig dødes; de skulle stene dem ihjel, deres Blod være over dem.

< Levitiko 20 >