< Levitiko 2 >

1 “‘Munthu wina aliyense akabwera ndi nsembe ya chakudya kwa Yehova, chopereka chake chizikhala ufa wosalala. Ufawo ausakanize ndi mafuta ndi lubani,
Lorsqu’un homme offrira une oblation de sacrifice au Seigneur, c’est de fleur de farine que sera son oblation; et il répandra de l’huile sur elle, et il mettra de l’encens;
2 ndipo apite nawo kwa ansembe, ana a Aaroni. Atapeko modzazitsa dzanja ufa wosalala uja kuti ukhale wachikumbutso pamodzi ndi mafuta ndi lubani ndipo atenthe zonsezi pa guwa lansembe kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa chopereka chonse. Iyi ndi nsembe yotentha pa moto ndiponso fungo lokomera Yehova.
Puis il la portera aux fils d’Aaron, prêtres, dont l’un prendra une pleine poignée de fleur de farine et d’huile et tout l’encens, et il le posera comme un souvenir sur l’autel, en odeur très suave pour le Seigneur.
3 Zotsala za nsembe ya chakudyazo ndi za Aaroni pamodzi ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
Mais ce qui sera de reste du sacrifice, appartiendra à Aaron et à ses fils, comme une chose très sainte des oblations du Seigneur.
4 “‘Ukabweretsa nsembe ya chakudya chophika mu uvuni, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta, kapena timitanda ta buledi topyapyala, topanda yisiti koma topaka mafuta.
Et lorsque tu offriras le sacrifice d’une chose cuite au four, elle sera de fleur de farine, c’est-à-dire, de pains sans levain, arrosés d’huile, et de beignets azymes oints d’huile,
5 Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophika pa chitsulo chamoto, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta.
Si ton oblation se fait d’une chose cuite dans la poêle, de fleur de farine arrosée d’huile et sans levain,
6 Umuduledule bulediyo ndi kumupaka mafuta; imeneyo ndi nsembe yachakudya.
Tu la couperas en petits morceaux, et tu répandras sur elle de l’huile.
7 Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophikidwa pa chiwaya, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
Mais si c’est d’une chose cuite sur le gril que se fait le sacrifice, la fleur de farine sera également arrosée d’huile;
8 Munthu azibwera ndi nsembe za chakudya zimene wapanga ndi zinthu zimenezi. Atachipereka kwa wansembe, iyeyu adzipita nacho ku guwa.
Et l’offrant au Seigneur, tu la remettras aux mains du prêtre,
9 Wansembeyo atengeko gawo lina la nsembeyo kukhala ufa wachikumbutso kuti ilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse ndipo ayitenthe pa moto monga nsembe yopsereza ya fungo lokomera Yehova.
Qui, lorsqu’il l’aura offerte, prendra une partie du sacrifice comme un souvenir, et il la brûlera sur l’autel, en odeur de suavité pour le Seigneur:
10 Zotsala za nsembe ya chakudyayo zikhale za Aaroni ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
Mais tout ce qui sera de reste, appartiendra à Aaron et à ses fils, comme une chose très sainte des oblations du Seigneur.
11 “‘Nsembe ya chakudya chilichonse imene ubweretsa kwa Yehova ikhale yopanda yisiti, pakuti suyenera kupereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto imene ili ndi yisiti kapena uchi.
Toute oblation qui sera offerte au Seigneur, se fera sans levain, et rien en fait de levain et de miel ne sera brûlé, quand on sacrifiera au Seigneur.
12 Ziwirizi ungathe kubwera nazo kwa Yehova ngati chopereka cha zokolola zoyambirira. Koma usazitenthe pa guwa kuti zikhale fungo lokomera Yehova.
Vous les offrirez seulement comme des prémices et des dons; mais ils ne seront pas mis sur l’autel en odeur de suavité.
13 Zopereka zako zonse zachakudya uzithire mchere. Usayiwale kuthira mchere pa chopereka chako popeza mcherewo ukusonyeza pangano pakati pa iwe ndi Mulungu wako. Tsono uzinthira mchere pa chopereka chako chilichonse.
Tout ce que tu offriras en sacrifice, tu l’assaisonneras de sel, et tu n’ôteras pas de ton sacrifice le sel de l’alliance de ton Dieu. Dans toute oblation tu offriras du sel.
14 “‘Mukamapereka kwa Yehova chopereka cha chakudya choyamba kucha, choperekacho chikhale cha chipatso chatsopano chokazinga pa moto ndi chopunthapuntha.
Mais si tu offres au Seigneur un présent de tes premiers grains, des épis encore verts, tu les rôtiras au feu, et tu les briseras à la manière du froment, et c’est ainsi que tu offriras tes prémices au Seigneur,
15 Uchithire mafuta ndi lubani pakuti ndi chopereka cha chakudya.
Répandant de l’huile dessus, et mettant de l’encens, parce que c’est une oblation du Seigneur,
16 Tsono wansembe atenthe gawo la chopereka chopunthapuntha chija kuti chikhala ufa wachikumbutso ndi cha mafuta pamodzi ndi lubani yense kuti Yehova alandire mʼmalo mwa zopereka zonse. Ichi ndi chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
Dans laquelle le prêtre brûlera, en mémoire du présent une partie du froment brisé et de l’huile, et tout l’encens.

< Levitiko 2 >