< Levitiko 2 >

1 “‘Munthu wina aliyense akabwera ndi nsembe ya chakudya kwa Yehova, chopereka chake chizikhala ufa wosalala. Ufawo ausakanize ndi mafuta ndi lubani,
"Jos joku tahtoo tuoda Herralle lahjaksi ruokauhrin, olkoon hänen uhrilahjanaan lestyjä jauhoja; ja hän vuodattakoon siihen öljyä ja pankoon sen päälle suitsuketta
2 ndipo apite nawo kwa ansembe, ana a Aaroni. Atapeko modzazitsa dzanja ufa wosalala uja kuti ukhale wachikumbutso pamodzi ndi mafuta ndi lubani ndipo atenthe zonsezi pa guwa lansembe kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa chopereka chonse. Iyi ndi nsembe yotentha pa moto ndiponso fungo lokomera Yehova.
ja vieköön sen papeille, Aaronin pojille, ja pappi ottakoon kourallisen niitä jauhoja ja sitä öljyä ynnä kaiken suitsukkeen ja polttakoon tämän alttariuhriosan alttarilla suloisesti tuoksuvana uhrina Herralle.
3 Zotsala za nsembe ya chakudyazo ndi za Aaroni pamodzi ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
Mutta se, mikä jää tähteeksi ruokauhrista, olkoon Aaronin ja hänen poikiensa oma; se on korkeasti-pyhää, Herran uhria.
4 “‘Ukabweretsa nsembe ya chakudya chophika mu uvuni, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta, kapena timitanda ta buledi topyapyala, topanda yisiti koma topaka mafuta.
Mutta jos tahdot tuoda ruokauhrilahjan uunissa paistetusta, olkoon uhrinasi lestyistä jauhoista valmistetut, öljyyn leivotut happamattomat kakut tai öljyllä voidellut happamattomat ohukaiset.
5 Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophika pa chitsulo chamoto, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta.
Jos taas uhrilahjasi on ruokauhri, joka leivinlevyllä paistetaan, olkoon se valmistettu lestyistä jauhoista, öljyyn leivottu ja happamaton.
6 Umuduledule bulediyo ndi kumupaka mafuta; imeneyo ndi nsembe yachakudya.
Paloittele se palasiksi ja vuodata öljyä sen päälle; se on ruokauhri.
7 Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophikidwa pa chiwaya, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
Ja jos uhrilahjasi on ruokauhri, joka paistetaan pannussa, valmistettakoon se lestyistä jauhoista ynnä öljystä.
8 Munthu azibwera ndi nsembe za chakudya zimene wapanga ndi zinthu zimenezi. Atachipereka kwa wansembe, iyeyu adzipita nacho ku guwa.
Ja vie ruokauhri, joka näin on valmistettu, Herralle; se vietäköön papille, ja hän tuokoon sen alttarin ääreen.
9 Wansembeyo atengeko gawo lina la nsembeyo kukhala ufa wachikumbutso kuti ilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse ndipo ayitenthe pa moto monga nsembe yopsereza ya fungo lokomera Yehova.
Ja pappi erottakoon ruokauhrista alttariuhriosan ja polttakoon sen alttarilla suloisesti tuoksuvana uhrina Herralle.
10 Zotsala za nsembe ya chakudyayo zikhale za Aaroni ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
Mutta se, mikä jää tähteeksi ruokauhrista, olkoon Aaronin ja hänen poikiensa oma; se on korkeasti-pyhää, Herran uhria.
11 “‘Nsembe ya chakudya chilichonse imene ubweretsa kwa Yehova ikhale yopanda yisiti, pakuti suyenera kupereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto imene ili ndi yisiti kapena uchi.
Mitään ruokauhria, jonka te tuotte Herralle, älköön valmistettako happamesta; älkää polttako uhria Herralle mistään happamesta taikinasta tai hunajasta.
12 Ziwirizi ungathe kubwera nazo kwa Yehova ngati chopereka cha zokolola zoyambirira. Koma usazitenthe pa guwa kuti zikhale fungo lokomera Yehova.
Uutisuhrilahjana saatte tuoda niitä Herralle, mutta älkööt ne tulko alttarille suloiseksi tuoksuksi.
13 Zopereka zako zonse zachakudya uzithire mchere. Usayiwale kuthira mchere pa chopereka chako popeza mcherewo ukusonyeza pangano pakati pa iwe ndi Mulungu wako. Tsono uzinthira mchere pa chopereka chako chilichonse.
Ja jokainen ruokauhrilahjasi suolaa suolalla, äläkä anna Jumalasi liitonsuolan puuttua ruokauhristasi; jokaiseen uhrilahjaasi sinun on tuotava suolaa.
14 “‘Mukamapereka kwa Yehova chopereka cha chakudya choyamba kucha, choperekacho chikhale cha chipatso chatsopano chokazinga pa moto ndi chopunthapuntha.
Mutta jos tahdot tuoda uutisesta ruokauhrin Herralle, niin tuo uutisruokauhrinasi tulessa paahdettuja tähkäpäitä tai survottuja jyviä tuleentumattomasta viljasta.
15 Uchithire mafuta ndi lubani pakuti ndi chopereka cha chakudya.
Ja vuodata siihen öljyä ja pane siihen suitsuketta; se on ruokauhri.
16 Tsono wansembe atenthe gawo la chopereka chopunthapuntha chija kuti chikhala ufa wachikumbutso ndi cha mafuta pamodzi ndi lubani yense kuti Yehova alandire mʼmalo mwa zopereka zonse. Ichi ndi chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
Ja pappi polttakoon alttariuhriosan survotuista jyvistä ja öljystä ynnä kaiken suitsukkeen uhrina Herralle."

< Levitiko 2 >