< Levitiko 2 >
1 “‘Munthu wina aliyense akabwera ndi nsembe ya chakudya kwa Yehova, chopereka chake chizikhala ufa wosalala. Ufawo ausakanize ndi mafuta ndi lubani,
And when any one bringeth a meal-offering unto the LORD, his offering shall be of fine flour; and he shall pour oil upon it, and put frankincense thereon.
2 ndipo apite nawo kwa ansembe, ana a Aaroni. Atapeko modzazitsa dzanja ufa wosalala uja kuti ukhale wachikumbutso pamodzi ndi mafuta ndi lubani ndipo atenthe zonsezi pa guwa lansembe kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa chopereka chonse. Iyi ndi nsembe yotentha pa moto ndiponso fungo lokomera Yehova.
And he shall bring it to Aaron's sons the priests; and he shall take thereout his handful of the fine flour thereof, and of the oil thereof, together with all the frankincense thereof; and the priest shall make the memorial-part thereof smoke upon the altar, an offering made by fire, of a sweet savour unto the LORD.
3 Zotsala za nsembe ya chakudyazo ndi za Aaroni pamodzi ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
But that which is left of the meal-offering shall be Aaron's and his sons'; it is a thing most holy of the offerings of the LORD made by fire.
4 “‘Ukabweretsa nsembe ya chakudya chophika mu uvuni, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta, kapena timitanda ta buledi topyapyala, topanda yisiti koma topaka mafuta.
And when thou bringest a meal-offering baked in the oven, it shall be unleavened cakes of fine flour mingled with oil, or unleavened wafers spread with oil.
5 Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophika pa chitsulo chamoto, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta.
And if thy offering be a meal-offering baked on a griddle, it shall be of fine flour unleavened, mingled with oil.
6 Umuduledule bulediyo ndi kumupaka mafuta; imeneyo ndi nsembe yachakudya.
Thou shalt break it in pieces, and pour oil thereon; it is a meal-offering.
7 Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophikidwa pa chiwaya, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
And if thy offering be a meal-offering of the stewing-pan, it shall be made of fine flour with oil.
8 Munthu azibwera ndi nsembe za chakudya zimene wapanga ndi zinthu zimenezi. Atachipereka kwa wansembe, iyeyu adzipita nacho ku guwa.
And thou shalt bring the meal-offering that is made of these things unto the LORD; and it shall be presented unto the priest, and he shall bring it unto the altar.
9 Wansembeyo atengeko gawo lina la nsembeyo kukhala ufa wachikumbutso kuti ilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse ndipo ayitenthe pa moto monga nsembe yopsereza ya fungo lokomera Yehova.
And the priest shall take off from the meal-offering the memorial-part thereof, and shall make it smoke upon the altar — an offering made by fire, of a sweet savour unto the LORD.
10 Zotsala za nsembe ya chakudyayo zikhale za Aaroni ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
But that which is left of the meal-offering shall be Aaron's and his sons'; it is a thing most holy of the offerings of the LORD made by fire.
11 “‘Nsembe ya chakudya chilichonse imene ubweretsa kwa Yehova ikhale yopanda yisiti, pakuti suyenera kupereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto imene ili ndi yisiti kapena uchi.
No meal-offering, which ye shall bring unto the LORD, shall be made with leaven; for ye shall make no leaven, nor any honey, smoke as an offering made by fire unto the LORD.
12 Ziwirizi ungathe kubwera nazo kwa Yehova ngati chopereka cha zokolola zoyambirira. Koma usazitenthe pa guwa kuti zikhale fungo lokomera Yehova.
As an offering of first-fruits ye may bring them unto the LORD; but they shall not come up for a sweet savour on the altar.
13 Zopereka zako zonse zachakudya uzithire mchere. Usayiwale kuthira mchere pa chopereka chako popeza mcherewo ukusonyeza pangano pakati pa iwe ndi Mulungu wako. Tsono uzinthira mchere pa chopereka chako chilichonse.
And every meal-offering of thine shalt thou season with salt; neither shalt thou suffer the salt of the covenant of thy God to be lacking from thy meal-offering; with all thy offerings thou shalt offer salt.
14 “‘Mukamapereka kwa Yehova chopereka cha chakudya choyamba kucha, choperekacho chikhale cha chipatso chatsopano chokazinga pa moto ndi chopunthapuntha.
And if thou bring a meal-offering of first-fruits unto the LORD, thou shalt bring for the meal-offering of thy first-fruits corn in the ear parched with fire, even groats of the fresh ear.
15 Uchithire mafuta ndi lubani pakuti ndi chopereka cha chakudya.
And thou shalt put oil upon it, and lay frankincense thereon; it is a meal-offering.
16 Tsono wansembe atenthe gawo la chopereka chopunthapuntha chija kuti chikhala ufa wachikumbutso ndi cha mafuta pamodzi ndi lubani yense kuti Yehova alandire mʼmalo mwa zopereka zonse. Ichi ndi chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
And the priest shall make the memorial-part of it smoke, even of the groats thereof, and of the oil thereof, with all the frankincense thereof; it is an offering made by fire unto the LORD.