< Levitiko 19 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
Le Seigneur parla à Moïse, disant:
2 “Uza gulu lonse la Aisraeli kuti, ‘Khalani oyera mtima chifukwa Ine, Yehova Mulungu wanu, ndine Woyera.
Parle à toute l’assemblée des enfants d’Israël, et tu leur diras: Soyez saints, parce que je suis saint, moi, le Seigneur votre Dieu.
3 “‘Aliyense mwa inu azilemekeza abambo ake ndi amayi ake. Ndipo muzisunga masabata anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Que chacun craigne son père et sa mère. Gardez mes sabbats. Je suis le Seigneur votre Dieu.
4 “‘Musatembenukire ku mafano kapena kudzipangira nokha milungu ya zitsulo zosungunula. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Ne vous tournez point vers les idoles, et ne vous faites point de dieux de fonte. Je suis le Seigneur votre Dieu.
5 “‘Pamene mukupereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, muyipereke mwanjira yoti ilandiridwe.
Si vous immolez une hostie de sacrifices pacifiques au Seigneur, afin qu’il se laisse fléchir,
6 Nsembe izidyedwa tsiku lomwe mwayiperekalo kapena mmawa mwake. Chilichonse chotsala mpaka tsiku lachitatu chiyenera kutenthedwa.
Au même jour qu’elle aura été immolée, vous la mangerez, et au jour suivant; mais ce qui sera de reste au troisième jour, vous le brûlerez au feu.
7 Ngati mudya choperekacho tsiku lachitatu, ndiye kuti mwachita chonyansa ndipo chakudyacho sichidzalandiridwa.
Si quelqu’un en mange après deux jours, il sera profane et coupable d’impiété;
8 Munthu aliyense amene adya chakudyacho adzasenza machimo ake chifukwa wayipitsa chinthu chimene ndi choyera kwa Yehova. Munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.
Et il portera son iniquité, parce qu’il a souillé la chose sainte du Seigneur, et cette âme périra du milieu de son peuple.
9 “‘Pamene mukolola zinthu mʼmunda mwanu musakolole mpaka mʼmphepete mwa munda, ndipo musatole khunkha lake.
Lorsque tu moissonneras les blés de la terre, tu ne couperas point jusqu’au sol, ce qui sera à la superficie de la terre, et tu ne ramasseras point les épis restants.
10 Musakolole mphesa zonse mʼmunda wanu wa mpesa kapena kutola mphesa zakugwa mʼmundamo. Zimenezi muzisiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wako.
Et, dans ta vigne, tu ne cueilleras point les grappes et les grains qui tombent, mais tu les laisseras recueillir aux pauvres et aux étrangers. Je suis le Seigneur votre Dieu.
11 “‘Musabe. “‘Musamanamizane. “‘Musachitirane zinthu mwachinyengo.
Vous ne ferez point de vol, vous ne mentirez point, et nul ne trompera son prochain.
12 “‘Musalumbire mʼdzina langa monyenga popeza kutero ndi kuyipitsa dzina la Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
Tu ne feras point de faux serment en mon nom, et tu ne souilleras point le nom de ton Dieu. Je suis le Seigneur.
13 “‘Musapsinje mnzanu kapena kumulanda zinthu zake. “‘Musasunge malipiro a munthu wantchito usiku wonse mpaka mmawa.
Tu ne calomnieras point ton prochain, tu ne l’opprimeras point par la violence. Le travail de ton mercenaire ne demeurera point chez toi jusqu’au matin.
14 “‘Musatemberere wosamva kapena kuyikira munthu wosaona chinthu choti apunthwe nacho patsogolo pake, koma muziopa Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
Tu ne maudiras point le sourd, et devant l’aveugle, tu ne mettras pas de pierre d’achoppement; mais tu craindras le Seigneur ton Dieu, parce que c’est moi qui suis le Seigneur.
15 “‘Musamaweruze mopanda chilungamo. Musachite tsankho pakati pa osauka ndi olemera, koma muweruze mlandu wa mnzanu mwachilungamo.
Tu ne feras point ce qui est inique, et tu ne jugeras point injustement. Ne considère point la personne du pauvre, et n’honore point le visage de l’homme puissant. Juge justement ton prochain.
16 “‘Musamapite uku ndi uku kunena bodza pakati pa anthu anu. “‘Musachite kanthu kalikonse kamene kangadzetse imfa kwa mnzanu. Ine ndine Yehova.
Tu ne seras point accusateur, ni médisant parmi le peuple. Tu ne t’élèveras point contre le sang de ton prochain. Je suis le Seigneur.
17 “‘Musamude mʼbale wanu mu mtima mwanu. Koma mudzudzuleni mnzanu moona mtima kuti musakhale wolakwa.
Ne hais point ton frère en ton cœur, mais reprends-le publiquement, afin que tu n’aies pas de péché à son sujet.
18 “‘Musamubwezere mnzanu choyipa kapena kumusungira kanthu kunkhosi, koma konda mnansi wako monga iwe mwini. Ine ndine Yehova.
Ne cherche point la vengeance, et tu ne te souviendras pas de l’injure de tes concitoyens. Tu aimeras ton ami comme toi-même. Je suis le Seigneur.
19 “‘Muzisunga malangizo anga. “‘Tsono musamalole kuti ngʼombe zanu zikwerane ndi chiweto cha mtundu wina. “‘Ndiponso musamadzale mbewu za mitundu iwiri mʼmunda umodzi. “‘Musavale chovala chopangidwa ndi nsalu za mitundu iwiri.
Gardez mes lois. Tu n’accoupleras point la bête de somme avec des animaux d’une autre espèce. Tu ne sèmeras point ton champ de diverse semence. Tu ne te vêtiras point d’un vêtement qui est tissu de fils différents.
20 “‘Ngati munthu agonana ndi kapolo wamkazi amene wafunsidwa mbeta ndi munthu wina, koma sanawomboledwe kapenanso kulandira ufulu wake, alangidwe. Koma onsewa asaphedwe, chifukwa mkaziyo anali asanalandire ufulu wake.
Si un homme dort avec une femme, qui soit servante, même nubile, mais non rachetée à prix d’argent, ni mise en liberté, ils seront battus tous deux, et ils ne mourront point, parce qu’elle n’était pas libre.
21 Koma mwamunayo abwere ndi nsembe yopepesera kupalamula kwa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano. Nsembe yake ikhale nkhosa yayimuna
Mais pour son défit, l’homme offrira au Seigneur à la porte du tabernacle de témoignage un bélier;
22 ndipo wansembe achite nayo mwambo wopepesera chifukwa cha kupalamula kumene anachita pamaso pa Yehova. Akatero tchimo lake lidzakhululukidwa.
Et le prêtre priera pour lui et pour son péché devant le Seigneur; et il lui redeviendra propice, et son péché sera remis.
23 “‘Mukadzalowa mʼdzikomo ndi kudzala mtengo wa mtundu uliwonse wa zipatso, zipatso zakezo mudzaziyese ngati zodetsedwa. Ndiye kuti kwa zaka zitatu zidzakhale zoletsedwa kwa inu. Musadzazidye nthawi imeneyi.
Quand vous serez entrés dans la terre, et que vous y aurez planté des arbres fruitiers, vous les émonderez: les fruits qu’ils produisent vous seront impurs, et vous n’en mangerez point.
24 Chaka chachinayi, zipatso zake zonse zidzakhala zopatulika, ndipo zidzakhala chopereka cha matamando kwa Yehova.
Mais à la quatrième année tout leur fruit sera consacré au Seigneur au milieu des louanges.
25 Koma chaka chachisanu, mudzatha kudya zipatso zake kuti mitengoyo idzakubalireni zochuluka. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Et, à la cinquième année, vous mangerez les fruits, recueillant ceux que les arbres porteront. Je suis le Seigneur votre Dieu.
26 “‘Musadye nyama ya magazi. “‘Musamawombeze kapena kuchita zamatsenga.
Vous ne mangerez rien avec le sang. Vous ne consulterez point les augures, et vous n’observerez point les songes.
27 “‘Musamamete mduliro kapena kumeta mʼmphepete mwa ndevu zanu.
Vous ne couperez point vos cheveux en rond, et vous ne raserez point votre barbe.
28 “‘Musadzichekecheke pathupi panu chifukwa cha munthu wakufa kapena kudzitema mphini pa thupi lanu. Ine ndine Yehova.
Vous ne ferez point d’incisions en votre chair à cause d’un mort, et vous ne ferez aucune figure ou de marques sur vous. Je suis le Seigneur.
29 “‘Musamuyipitse mwana wanu wamkazi pomusandutsa mkazi wachiwerewere. Mukatero dziko lidzasanduka la anthu achiwerewere ndi lodzaza ndi zoyipa.
Ne prostitue point ta fille, et afin que la terre ne soit pas souillée et qu’elle ne soit pas remplie d’impiété.
30 “‘Muzisunga Masabata anga ndipo muzilemekeza malo anga opatulika. Ine ndine Yehova.
Gardez mes sabbats, et craignez mon sanctuaire. Je suis le Seigneur.
31 “‘Musamapite kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kapena kwa owombeza. Musamawafunefune kuti angakuyipitseni. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Vous n’irez point vers les magiciens et vous ne demanderez rien aux devins, pour que vous soyez souillés par eux. Je suis le Seigneur votre Dieu.
32 “‘Muzikhala mwa ulemu pamaso pa munthu wachikulire, ndipo muzichitira ulemu munthu wokalamba. Kumeneko ndiye kuopa Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
Lève-toi devant une tête blanche, et honore la personne d’un vieillard: et crains le Seigneur ton Dieu. Je suis le Seigneur.
33 “‘Pamene mlendo akhala nanu mʼdziko mwanu, musamuzunze.
Si un étranger habite en votre terre, et s’il demeure parmi vous, ne lui faites point de reproches;
34 Mlendo amene akhala nanu akhale ngati mmodzi mwa mbadwa zanu. Mumukonde monga momwe mumadzikondera inu nomwe. Paja inu munali alendo mʼdziko la Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Mais qu’il soit parmi vous comme un indigène; et vous l’aimerez comme vous-mêmes; car vous avez été, vous aussi, étrangers dans la terre d’Egypte. Je suis le Seigneur votre Dieu.
35 “‘Musamachite za chinyengo poweruza mlandu, kapena poyeza utali, kulemera ngakhalenso kuchuluka kwa zinthu.
Ne faites rien d’inique dans le jugement, dans la règle, dans le poids, dans la mesure.
36 Miyeso ya sikelo, miyeso yoyezera kulemera kwa zinthu, miyeso yotchedwa efa ndi miyeso yotchedwa hini zikhale zolungama. Ine ndine Yehova, Mulungu wanu amene ndinakutulutsani ku dziko la Igupto.
Que la balance soit juste, les poids justes, le boisseau juste et le setier juste. Je suis le Seigneur votre Dieu, qui vous ai retirés de la terre d’Egypte.
37 “‘Choncho muzisunga malangizo ndi malamulo angawa ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.’”
Gardez tous mes préceptes et toutes mes ordonnances et exécutez-les. Je suis le Seigneur.