< Levitiko 19 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the LORD spoke to Moses, saying,
2 “Uza gulu lonse la Aisraeli kuti, ‘Khalani oyera mtima chifukwa Ine, Yehova Mulungu wanu, ndine Woyera.
Speak to all the congregation of the children of Israel, and say to them, You shall be holy: for I the LORD your God am holy.
3 “‘Aliyense mwa inu azilemekeza abambo ake ndi amayi ake. Ndipo muzisunga masabata anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
You shall fear every man his mother, and his father, and keep my sabbaths: I am the LORD your God.
4 “‘Musatembenukire ku mafano kapena kudzipangira nokha milungu ya zitsulo zosungunula. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Turn you not to idols, nor make to yourselves molten gods: I am the LORD your God.
5 “‘Pamene mukupereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, muyipereke mwanjira yoti ilandiridwe.
And if you offer a sacrifice of peace offerings to the LORD, you shall offer it at your own will.
6 Nsembe izidyedwa tsiku lomwe mwayiperekalo kapena mmawa mwake. Chilichonse chotsala mpaka tsiku lachitatu chiyenera kutenthedwa.
It shall be eaten the same day you offer it, and on the morrow: and if any remain until the third day, it shall be burnt in the fire.
7 Ngati mudya choperekacho tsiku lachitatu, ndiye kuti mwachita chonyansa ndipo chakudyacho sichidzalandiridwa.
And if it be eaten at all on the third day, it is abominable; it shall not be accepted.
8 Munthu aliyense amene adya chakudyacho adzasenza machimo ake chifukwa wayipitsa chinthu chimene ndi choyera kwa Yehova. Munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.
Therefore every one that eats it shall bear his iniquity, because he has profaned the hallowed thing of the LORD: and that soul shall be cut off from among his people.
9 “‘Pamene mukolola zinthu mʼmunda mwanu musakolole mpaka mʼmphepete mwa munda, ndipo musatole khunkha lake.
And when you reap the harvest of your land, you shall not wholly reap the corners of your field, neither shall you gather the gleanings of your harvest.
10 Musakolole mphesa zonse mʼmunda wanu wa mpesa kapena kutola mphesa zakugwa mʼmundamo. Zimenezi muzisiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wako.
And you shall not glean your vineyard, neither shall you gather every grape of your vineyard; you shall leave them for the poor and stranger: I am the LORD your God.
11 “‘Musabe. “‘Musamanamizane. “‘Musachitirane zinthu mwachinyengo.
You shall not steal, neither deal falsely, neither lie one to another.
12 “‘Musalumbire mʼdzina langa monyenga popeza kutero ndi kuyipitsa dzina la Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
And you shall not swear by my name falsely, neither shall you profane the name of your God: I am the LORD.
13 “‘Musapsinje mnzanu kapena kumulanda zinthu zake. “‘Musasunge malipiro a munthu wantchito usiku wonse mpaka mmawa.
You shall not defraud your neighbor, neither rob him: the wages of him that is hired shall not abide with you all night until the morning.
14 “‘Musatemberere wosamva kapena kuyikira munthu wosaona chinthu choti apunthwe nacho patsogolo pake, koma muziopa Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
You shall not curse the deaf, nor put a stumbling block before the blind, but shall fear your God: I am the LORD.
15 “‘Musamaweruze mopanda chilungamo. Musachite tsankho pakati pa osauka ndi olemera, koma muweruze mlandu wa mnzanu mwachilungamo.
You shall do no unrighteousness in judgment: you shall not respect the person of the poor, nor honor the person of the mighty: but in righteousness shall you judge your neighbor.
16 “‘Musamapite uku ndi uku kunena bodza pakati pa anthu anu. “‘Musachite kanthu kalikonse kamene kangadzetse imfa kwa mnzanu. Ine ndine Yehova.
You shall not go up and down as a talebearer among your people: neither shall you stand against the blood of your neighbor; I am the LORD.
17 “‘Musamude mʼbale wanu mu mtima mwanu. Koma mudzudzuleni mnzanu moona mtima kuti musakhale wolakwa.
You shall not hate your brother in your heart: you shall in any wise rebuke your neighbor, and not suffer sin on him.
18 “‘Musamubwezere mnzanu choyipa kapena kumusungira kanthu kunkhosi, koma konda mnansi wako monga iwe mwini. Ine ndine Yehova.
You shall not avenge, nor bear any grudge against the children of your people, but you shall love your neighbor as yourself: I am the LORD.
19 “‘Muzisunga malangizo anga. “‘Tsono musamalole kuti ngʼombe zanu zikwerane ndi chiweto cha mtundu wina. “‘Ndiponso musamadzale mbewu za mitundu iwiri mʼmunda umodzi. “‘Musavale chovala chopangidwa ndi nsalu za mitundu iwiri.
You shall keep my statutes. You shall not let your cattle engender with a diverse kind: you shall not sow your field with mingled seed: neither shall a garment mingled of linen and woolen come on you.
20 “‘Ngati munthu agonana ndi kapolo wamkazi amene wafunsidwa mbeta ndi munthu wina, koma sanawomboledwe kapenanso kulandira ufulu wake, alangidwe. Koma onsewa asaphedwe, chifukwa mkaziyo anali asanalandire ufulu wake.
And whoever lies carnally with a woman, that is a female slave, betrothed to an husband, and not at all redeemed, nor freedom given her; she shall be scourged; they shall not be put to death, because she was not free.
21 Koma mwamunayo abwere ndi nsembe yopepesera kupalamula kwa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano. Nsembe yake ikhale nkhosa yayimuna
And he shall bring his trespass offering to the LORD, to the door of the tabernacle of the congregation, even a ram for a trespass offering.
22 ndipo wansembe achite nayo mwambo wopepesera chifukwa cha kupalamula kumene anachita pamaso pa Yehova. Akatero tchimo lake lidzakhululukidwa.
And the priest shall make an atonement for him with the ram of the trespass offering before the LORD for his sin which he has done: and the sin which he has done shall be forgiven him.
23 “‘Mukadzalowa mʼdzikomo ndi kudzala mtengo wa mtundu uliwonse wa zipatso, zipatso zakezo mudzaziyese ngati zodetsedwa. Ndiye kuti kwa zaka zitatu zidzakhale zoletsedwa kwa inu. Musadzazidye nthawi imeneyi.
And when you shall come into the land, and shall have planted all manner of trees for food, then you shall count the fruit thereof as uncircumcised: three years shall it be as uncircumcised to you: it shall not be eaten of.
24 Chaka chachinayi, zipatso zake zonse zidzakhala zopatulika, ndipo zidzakhala chopereka cha matamando kwa Yehova.
But in the fourth year all the fruit thereof shall be holy to praise the LORD with.
25 Koma chaka chachisanu, mudzatha kudya zipatso zake kuti mitengoyo idzakubalireni zochuluka. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
And in the fifth year shall you eat of the fruit thereof, that it may yield to you the increase thereof: I am the LORD your God.
26 “‘Musadye nyama ya magazi. “‘Musamawombeze kapena kuchita zamatsenga.
You shall not eat any thing with the blood: neither shall you use enchantment, nor observe times.
27 “‘Musamamete mduliro kapena kumeta mʼmphepete mwa ndevu zanu.
You shall not round the corners of your heads, neither shall you mar the corners of your beard.
28 “‘Musadzichekecheke pathupi panu chifukwa cha munthu wakufa kapena kudzitema mphini pa thupi lanu. Ine ndine Yehova.
You shall not make any cuttings in your flesh for the dead, nor print any marks on you: I am the LORD.
29 “‘Musamuyipitse mwana wanu wamkazi pomusandutsa mkazi wachiwerewere. Mukatero dziko lidzasanduka la anthu achiwerewere ndi lodzaza ndi zoyipa.
Do not prostitute your daughter, to cause her to be a whore; lest the land fall to prostitution, and the land become full of wickedness.
30 “‘Muzisunga Masabata anga ndipo muzilemekeza malo anga opatulika. Ine ndine Yehova.
You shall keep my sabbaths, and reverence my sanctuary: I am the LORD.
31 “‘Musamapite kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kapena kwa owombeza. Musamawafunefune kuti angakuyipitseni. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Regard not them that have familiar spirits, neither seek after wizards, to be defiled by them: I am the LORD your God.
32 “‘Muzikhala mwa ulemu pamaso pa munthu wachikulire, ndipo muzichitira ulemu munthu wokalamba. Kumeneko ndiye kuopa Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.
You shall rise up before the hoary head, and honor the face of the old man, and fear your God: I am the LORD.
33 “‘Pamene mlendo akhala nanu mʼdziko mwanu, musamuzunze.
And if a stranger sojourn with you in your land, you shall not vex him.
34 Mlendo amene akhala nanu akhale ngati mmodzi mwa mbadwa zanu. Mumukonde monga momwe mumadzikondera inu nomwe. Paja inu munali alendo mʼdziko la Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
But the stranger that dwells with you shall be to you as one born among you, and you shall love him as yourself; for you were strangers in the land of Egypt: I am the LORD your God.
35 “‘Musamachite za chinyengo poweruza mlandu, kapena poyeza utali, kulemera ngakhalenso kuchuluka kwa zinthu.
You shall do no unrighteousness in judgment, in length, in weight, or in measure.
36 Miyeso ya sikelo, miyeso yoyezera kulemera kwa zinthu, miyeso yotchedwa efa ndi miyeso yotchedwa hini zikhale zolungama. Ine ndine Yehova, Mulungu wanu amene ndinakutulutsani ku dziko la Igupto.
Just balances, just weights, a just ephah, and a just hin, shall you have: I am the LORD your God, which brought you out of the land of Egypt.
37 “‘Choncho muzisunga malangizo ndi malamulo angawa ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.’”
Therefore shall you observe all my statutes, and all my judgments, and do them: I am the LORD.

< Levitiko 19 >