< Levitiko 18 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
UThixo wathi kuMosi,
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
“Tshela abako-Israyeli ukuthi: ‘NginguThixo uNkulunkulu wenu.
3 Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo.
Lingabokwenza lokhu okwenziwa eGibhithe, lapho elalikhona, njalo lingabokwenza abakwenzayo ezweni laseKhenani, lapho engilisa khona. Lingalandeli abakwenzayo.
4 Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Lalelani imithetho yami njalo linanzelele, lilandele izimiso zami. Mina nginguThixo uNkulunkulu wenu.
5 Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.
Gcinani izimiso zami lemithetho yami, ngoba umuntu oyilalelayo uzaphila ngayo. Mina nginguThixo.
6 “‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.
Akungabi lamuntu osondela esihlotsheni sakhe esiseduze ukuthi alale laso. Mina nginguThixo.
7 “‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.
Ungatheleli uyihlo ihlazo ngokulala lonyoko. Ngunyoko; ungalali laye.
8 “‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.
Ungalali lomfazi kayihlo; lokho kuthelela uyihlo ihlazo.
9 “‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.
Ungalali lodadewenu, loba indodakazi kayihlo loba indodakazi kanyoko, kungakhathalekile ukuthi wazalelwa ekhaya loba kwenye indawo.
10 “‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.
Ungalali lendodakazi yendodana yakho loba indodakazi yendodakazi yakho; lokhu kuzakuthelela ihlazo.
11 “‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.
Ungalali lendodakazi yomfazi kayihlo, eyazalwa nguyihlo, ingudadewenu.
12 “‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.
Ungalali lodadewabo kayihlo; uyisihlobo sikayihlo esiseduze kakhulu.
13 “‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.
Ungalali lodadewabo kanyoko, uyisihlobo sikanyoko esiseduzane kakhulu.
14 “‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.
Ungatheleli umfowabo kayihlo ihlazo ngokusondela kumkakhe ukuthi ulale laye, ngoba ungunyoko.
15 “‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.
Ungalali lomalokazana wakho, ngumfazi wendodana yakho; ungalali laye.
16 “‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.
Ungalali lomfazi womfowenu; kuzathelela umfowenu ihlazo.
17 “‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.
Ungalali lowesifazane kanye lendodakazi yakhe. Ungalali lendodakazi yendodana yakhe loba indodakazi yendodakazi yakhe; bayizihlobo zakho eziseduzane. Lokhu kuyikuxhwala.
18 “‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.
Ungathathi udadewabo womkakho ukuthi ulale laye nxa umkakho esaphila.
19 “‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.
Ungasondeli kowesifazane ukuthi ulale laye ngesikhathi esemfuleni ngoba ungcolile.
20 “‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.
Ungalali lomfazi kamakhelwane wakho ngoba uyazingcolisa ngaye.
21 “‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.
Unganikeli loba nguphi wabantwabakho ukuthi abe ngumhlatshelo kunkulunkulu uMoleki, ngoba akufanelanga ukuthi ungcolise ibizo likaNkulunkulu wakho. Mina nginguThixo.
22 “‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.
Ungalali lendoda njengendoda ilala lomfazi; lokhu kuyisinengiso.
23 “‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.
Ungafebi lenyamazana, ngoba uyazingcolisa ngalokho. Owesifazane angafebi lenyamazana, lokhu kuyisinengiso.
24 “‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera.
Lingazingcolisi noma kungayiphi yalezizindlela, ngoba yizo izindlela izizwe engizazidudula phambi kwenu ezazingcolisa ngazo.
25 Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo.
Kwaze kwangcola lelizwe; kungakho ngalijezisa ngesono salo, ilizwe ababehlala kulo labakhafula.
26 Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi,
Kodwa kumele ligcine izimiso zami lemilayo yami. Lina banikazi belizwe labezizwe abaphakathi kwenu, akufanelanga benze lezizinto ezenyanyekayo,
27 pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa.
ngoba zonke lezizinto zenziwa ngabantu ababehlala kulelilizwe lina lingakafiki, ngakho ilizwe langcola.
28 Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.
Nxa lingenza amanyala kulelilizwe, lizalikhafula njengendlela elakhafula ngayo izizwe ezalandulelayo.
29 “‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake.
Loba ngubani owenza lezizinto ezenyanyekayo, kumele axotshwe ebantwini bakibo.
30 Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Gcinani iziqondiso zami, lingalandeli izindlela zamanyala lemikhuba eyayilandelwa ngabantu abalandulelayo, njalo lingazingcolisi ngayo. Mina nginguThixo uNkulunkulu wenu.’”

< Levitiko 18 >