< Levitiko 18 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Le Seigneur parla à Moïse, disant:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Parle aux enfants d’Israël et tu leur diras: Je suis le Seigneur votre Dieu:
3 Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo.
Vous ne vous conduirez point selon la coutume de la terre d’Egypte, dans laquelle vous avez habité; et vous n’agirez point selon les mœurs du pays de Chanaan, dans lequel je dois moi-même vous introduire, et vous ne marcherez point dans leurs lois.
4 Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Vous exécuterez mes ordonnances, vous observerez mes préceptes et vous y marcherez. Je suis le Seigneur votre Dieu.
5 Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.
Gardez mes lois et mes ordonnances; l’homme qui les accomplit, vivra par elles. Je suis le Seigneur.
6 “‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.
Nul homme ne s’approchera d’une femme qui est de son sang pour révéler sa nudité. Je suis le Seigneur.
7 “‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.
Tu ne découvriras point la nudité de ton père et la nudité de ta mère: c’est ta mère; tu ne révéleras pas sa nudité.
8 “‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.
Tu ne découvriras point la nudité de la femme de ton père; car c’est la nudité de ton père.
9 “‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.
Tu ne révéleras point la nudité de ta sœur de père ou de mère, qui est née dans la maison ou au dehors.
10 “‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.
Tu ne révéleras point la nudité de la fille de ton fils ou de la fille de ta fille; parce que c’est ta nudité.
11 “‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.
Tu ne révéleras point la nudité de la fille de la femme de ton père, qu’elle a enfantée à ton père; car elle est ta sœur.
12 “‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.
Tu ne découvriras point la nudité de la sœur de ton père, parce que c’est la chair de ton père.
13 “‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.
Tu ne révéleras point la nudité de la sœur de la mère, parce que c’est la chair de ta mère.
14 “‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.
Tu ne révéleras point la nudité de ton oncle paternel, et tu ne t’approcheras point de sa femme, qui t’est unie par affinité.
15 “‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.
Tu ne révéleras point la nudité de ta belle-fille, parce que c’est la femme de ton fils, et tu ne découvriras point son ignominie.
16 “‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.
Tu ne révéleras point la nudité de la femme de ton frère, parce que c’est la nudité de ton frère.
17 “‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.
Tu ne révéleras point la nudité de ta femme et de sa fille. Tu ne prendras point la fille de son fils et la fille de sa fille, pour révéler son ignominie, parce qu’elles sont sa chair, et une telle union est un inceste.
18 “‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.
Tu ne prendras point la sœur de ta femme conjointement avec elle, et tu ne révéleras point sa nudité, elle encore vivante.
19 “‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.
Tu ne t’approcheras point de la femme qui a ses mois, et tu ne révéleras point son impureté.
20 “‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.
Tu ne t’approcheras point de la femme de ton prochain, et tu ne te souilleras point par un mélange de sang.
21 “‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.
Tu ne donneras point de tes enfants pour être consacrés à l’idole de Moloch, et tu ne souilleras point le nom de ton Dieu. Je suis le Seigneur.
22 “‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.
Tu ne t’approcheras point d’un homme comme d’une femme, parce que c’est une abomination.
23 “‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.
Tu ne t’approcheras d’aucune bête, et tu ne te souilleras point avec elle. Une femme n’ira point vers une bête et ne s’unira point avec elle, parce que c’est un crime.
24 “‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera.
Ne soyez point souillés d’aucune de ces choses, dont ont été souillées toutes les nations, que je chasserai moi-même devant vous,
25 Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo.
Et dont a été souillée cette terre de laquelle je visiterai moi-même les crimes, afin qu’elle vomisse ses habitants.
26 Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi,
Gardez mes lois et mes ordonnances, et ne faites aucune de ces abominations, tant l’indigène, que le colon qui séjournent chez vous.
27 pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa.
Car toutes ces exécrations, ils les ont commises, les habitants de cette terre qui ont été avant vous, et ils l’ont souillée.
28 Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.
Prenez donc garde qu’elle ne vous vomisse vous aussi de même, lorsque vous ferez de pareilles choses, comme elle a vomi la nation qui a été avant vous.
29 “‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake.
Tout homme qui fera quelque chose de ces abominations, périra du milieu de son peuple.
30 Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Gardez mes commandements. Ne faites point les choses qu’ont faites ceux qui ont été avant vous et ne soyez point souillés par elles. Je suis le Seigneur votre Dieu

< Levitiko 18 >