< Levitiko 18 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahvé dit à Moïse:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Parle aux enfants d'Israël, et dis-leur: « Je suis Yahvé, votre Dieu.
3 Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo.
Vous ne ferez pas comme on fait dans le pays d'Égypte, où vous avez vécu. Vous ne ferez pas comme eux dans le pays de Canaan, où je vous conduis. Tu ne suivras pas leurs lois.
4 Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Vous observerez mes ordonnances. Tu observeras mes lois et tu marcheras selon elles. Je suis Yahvé, ton Dieu.
5 Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.
Tu observeras donc mes lois et mes ordonnances; si un homme les met en pratique, il vivra en elles. Je suis Yahvé.
6 “‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.
"'Aucun de vous ne s'approchera d'un proche parent pour découvrir sa nudité: Je suis Yahvé.
7 “‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.
"'Tu ne découvriras pas la nudité de ton père, ni la nudité de ta mère: elle est ta mère. Tu ne découvriras pas sa nudité.
8 “‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.
"'Tu ne découvriras pas la nudité de la femme de ton père. C'est la nudité de ton père.
9 “‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.
"'Tu ne découvriras pas la nudité de ta sœur, fille de ton père ou fille de ta mère, qu'elle soit née dans le pays ou à l'étranger.
10 “‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.
"'Tu ne découvriras pas la nudité de la fille de ton fils ou de la fille de ta fille, même leur nudité; car leur nudité est la tienne.
11 “‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.
"'Tu ne découvriras pas la nudité de la fille de la femme de ton père, conçue par ton père, puisqu'elle est ta sœur.
12 “‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.
"'Tu ne découvriras pas la nudité de la sœur de ton père. Elle est la proche parente de ton père.
13 “‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.
"'Tu ne découvriras pas la nudité de la sœur de ta mère, car elle est la proche parente de ta mère.
14 “‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.
"'Tu ne découvriras pas la nudité du frère de ton père. Tu ne t'approcheras pas de sa femme. Elle est ta tante.
15 “‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.
"'Tu ne découvriras pas la nudité de ta belle-fille. Elle est la femme de ton fils. Tu ne découvriras pas sa nudité.
16 “‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.
"'Tu ne découvriras pas la nudité de la femme de ton frère. C'est la nudité de ton frère.
17 “‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.
"'Tu ne découvriras pas la nudité d'une femme et de sa fille. Tu ne prendras pas la fille de son fils, ni la fille de sa fille, pour découvrir sa nudité. Elles sont proches parentes. C'est de la méchanceté.
18 “‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.
"'Tu ne prendras pas une femme en plus de sa sœur, pour être une rivale, pour découvrir sa nudité, tant que sa sœur est encore en vie.
19 “‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.
"'Tu ne t'approcheras pas d'une femme pour découvrir sa nudité, tant qu'elle est souillée par son impureté.
20 “‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.
"'Tu ne coucheras pas charnellement avec la femme de ton prochain, et tu ne te souilleras pas avec elle.
21 “‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.
"'Tu ne donneras aucun de tes enfants en sacrifice à Moloch. Tu ne profaneras pas le nom de ton Dieu. Je suis Yahvé.
22 “‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.
"'Tu ne coucheras pas avec un homme comme avec une femme. C'est une chose détestable.
23 “‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.
"'Tu ne coucheras pas avec un animal pour te souiller avec lui. Aucune femme ne peut se donner à un animal, pour se coucher avec lui: c'est une perversion.
24 “‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera.
« Ne vous souillez par aucune de ces choses, car c'est par toutes ces choses que se sont souillées les nations que je chasse devant vous.
25 Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo.
Le pays s'est souillé. J'ai donc puni son iniquité, et le pays a vomi ses habitants.
26 Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi,
Vous observerez donc mes lois et mes ordonnances, et vous ne commettrez aucune de ces abominations, ni le natif, ni l'étranger qui vit au milieu de vous
27 pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa.
(car les hommes du pays qui était avant vous ont commis toutes ces abominations, et le pays s'est souillé),
28 Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.
afin que le pays ne vous vomisse pas aussi, quand vous le souillerez, comme il a vomi la nation qui était avant vous.
29 “‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake.
"'Car quiconque commettra l'une de ces abominations, les âmes qui les commettent seront retranchées du milieu de leur peuple.
30 Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
C'est pourquoi vous observerez mes prescriptions, afin de ne pratiquer aucune de ces coutumes abominables qui ont été pratiquées avant vous, et de ne pas vous souiller par elles. Je suis Yahvé, ton Dieu. »

< Levitiko 18 >