< Levitiko 18 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke unto Moses, saying,
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Speak unto the children of Israel, and say unto them, I am the Lord your God.
3 Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo.
After the doings of the Land of Egypt, wherein ye have dwelt, shall ye not do; and after the doings of the land of Canaan whither I am bringing you, shall ye not do; and in their customs shall ye not walk.
4 Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
My ordinances shall ye do, and my statutes shall ye keep, to walk therein: I am the Lord your God.
5 Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.
And ye shall keep my statutes, and my ordinances, which if a man do, he shall live in them: I am the Lord.
6 “‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.
None of you shall approach to any that are near of kin to him, to uncover their nakedness: I am the Lord.
7 “‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.
The nakedness of thy father, or the nakedness of thy mother, shalt thou not uncover: she is thy mother, thou shalt not uncover her nakedness.
8 “‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.
The nakedness of thy father's wife shalt thou not uncover: it is thy father's nakedness.
9 “‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.
The nakedness of thy sister, the daughter of thy father, or the daughter of thy mother, whether she be born at home, or born abroad, —even the nakedness of any of these shalt thou not uncover.
10 “‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.
The nakedness of thy son's daughter, or of thy daughter's daughter, —even the nakedness of any of these, shalt thou not uncover; for theirs is thy own nakedness.
11 “‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.
The nakedness of thy father's wife's daughter, begotten of thy father, she is thy sister, —thou shalt not uncover her nakedness.
12 “‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.
The nakedness of thy father's sister shalt thou not uncover: she is thy father's near kinswoman.
13 “‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.
The nakedness of thy mother's sister shalt thou not uncover; for she is thy mother's near kinswoman.
14 “‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.
The nakedness of thy father's brother shalt thou not uncover: his wife shalt thou not approach, she is thy aunt.
15 “‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.
The nakedness of thy daughter-in-law shalt thou not uncover: she is thy son's wife, thou shalt not uncover her nakedness.
16 “‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.
The nakedness of thy brother's wife shalt thou not uncover: it is thy brother's nakedness.
17 “‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.
The nakedness of a woman and her daughter shalt thou not uncover: her son's daughter, or her daughter's daughter shalt thou not take, to uncover her nakedness; for they are near kinswomen; it is incest.
18 “‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.
And a woman together with her sister shalt thou not take, to vex her, to uncover her nakedness, beside the other, in her lifetime.
19 “‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.
And a woman in the separation of her uncleanness shalt thou not approach, to uncover her nakedness.
20 “‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.
And with thy neighbor's wife shalt thou not lie carnally, to defile thyself with her.
21 “‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.
And any of thy seed shalt thou not let pass through [the fire] to Molech, and thou shalt not profane the name of thy God: I am the Lord.
22 “‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.
And with a man shalt thou not lie, as with a woman: it is an abomination.
23 “‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.
And with any beast shalt thou not lie to defile thyself therewith; neither shall any woman stand before a beast to lie down thereto: it is confusion.
24 “‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera.
Do not defile yourselves through any of these things.; for through all these have become defiled the nations which I cast out before you:
25 Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo.
And the land became defiled; wherefore I have visited its iniquity upon it, and the land itself vomited out its inhabitants.
26 Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi,
Ye shall therefore keep my statutes and my ordinances, and ye shall not commit any of these abominations; neither any of your own nation, nor the stranger that sojourneth among you;
27 pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa.
(For all these abominations have the men of the land done, who were before you, and the land hath become defiled; )
28 Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.
That the land may not vomit you out also, when ye defile it, as it hath vomited out the nations that were before you.
29 “‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake.
For whosoever shall commit any of these abominations, — even the souls that commit them shall be cut off from among their people.
30 Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Therefore shall ye keep my charge, so that ye commit not any one of these abominable customs, which were committed before you, and that ye do not defile yourselves therewith: I am the Lord your God.

< Levitiko 18 >