< Levitiko 18 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke to Moses, saying:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Speak to the sons of Israel, and you shall say to them: I am the Lord your God.
3 Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo.
You shall not act according to the custom of the land of Egypt, in which you have lived; nor shall you behave according to the habit of the region of Canaan, into which I will lead you; neither shall you walk in their ordinances.
4 Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
You shall accomplish my judgments, and you shall observe my precepts, and you shall walk in them. I am the Lord your God.
5 Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.
Keep my laws and judgments; when a man does these, he shall live by them. I am the Lord.
6 “‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.
No man shall approach her who is a close blood-relative to him, so as to uncover her nakedness. I am the Lord.
7 “‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.
You shall not expose the nakedness of your father, or the nakedness of your mother. She is your mother; you shall not uncover her nakedness.
8 “‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.
You shall not expose the nakedness of your father’s wife; for it is the nakedness of your father.
9 “‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.
You shall not uncover the nakedness of your sister, whether from father or from mother, whether she was born at home or abroad.
10 “‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.
You shall not uncover the nakedness of your son’s daughter, or your daughter’s daughter; for it is your own nakedness.
11 “‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.
You shall not uncover the nakedness of your father’s wife’s daughter, whom she bore to your father, and who is your sister.
12 “‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.
You shall not expose the nakedness of your father’s sister; for she is the flesh of your father.
13 “‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.
You shall not uncover the nakedness of your mother’s sister, because she is the flesh of your mother.
14 “‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.
You shall not uncover the nakedness of your father’s brother, nor shall you approach his wife, who is joined to you by affinity.
15 “‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.
You shall not uncover the nakedness of your daughter-in-law, for she is your son’s wife; neither shall you expose her dishonor.
16 “‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.
You shall not uncover the nakedness of your brother’s wife; for it is the nakedness of your brother.
17 “‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.
You shall not uncover the nakedness of your wife and her daughter. You shall not take her son’s daughter or her daughter’s daughter, so as to uncover her dishonor; for they are her flesh, and such sexual intercourse is incest.
18 “‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.
You shall not take your wife’s sister as a rival mistress; nor shall you uncover her nakedness, while your wife is still living.
19 “‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.
You shall not approach a woman who is undergoing menstruation, nor shall you uncover her foulness.
20 “‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.
You shall not have sexual intercourse with your neighbor’s wife, nor shall you be defiled by the mingling of seed.
21 “‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.
You shall not give some of your seed to be consecrated to the idol Moloch, nor to pollute the name of your God. I am the Lord.
22 “‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.
You shall not commit sexual acts with a male, in place of sexual intercourse with a female, for this is an abomination.
23 “‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.
You shall not commit sexual acts with any animal, nor shall you be defiled by it. A woman shall not lie down with a beast, nor commit sexual acts with it; for this is wickedness.
24 “‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera.
Do not pollute yourselves with any of these things, by which all of the nations, which I will cast out in your sight, have been contaminated
25 Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo.
and by which the land has been polluted. I will visit the wickedness of the land, so that it may vomit out its inhabitants.
26 Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi,
Keep my ordinances and judgments, and do not do any of these abominations: the native born, as well as the settler, who sojourns among you.
27 pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa.
For all these detestable things were done by the inhabitants of the land who were here before you, and they have polluted it.
28 Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.
Therefore, beware, lest in a similar manner, it may vomit you out as well, if you do these same things, just as it vomited out the people who were before you.
29 “‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake.
Every soul who shall commit any of these abominations shall perish from the midst of his people.
30 Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Keep my commandments. Do not be willing to do the things which have been done by those who were before you, and do not be polluted by these things. I am the Lord your God.