< Levitiko 18 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Og Herren talede til Mose og sagde:
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Tal til Israels Børn, og du skal sige til dem: Jeg er Herren eders Gud.
3 Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo.
Efter Ægyptens Lands Gerning, hvor I boede, skulle I ikke gøre, og efter Kanaans Lands Gerning, hvor hen jeg vil føre eder, skulle I ikke gøre, og efter deres Skikke skulle I ikke vandre.
4 Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
I skulle gøre efter mine Bud og holde mine Skikke, saa at I vandre i dem; jeg er Herren eders Gud.
5 Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.
Og I skulle holde mine Skikke og mine Bud, hvilke et Menneske skal gøre og leve ved dem; jeg er Herren.
6 “‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.
Ingen af eder skal holde sig nær til sin næste Slægt, til at, blotte dennes Blusel; jeg er Herren.
7 “‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.
Du skal ikke blotte din Faders Blusel eller din Moders Blusel; hun er din Moder, du skal ikke blotte hendes Blusel.
8 “‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.
Du skal ikke blotte din Stivmoders Blusel; det er din Faders Blusel.
9 “‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.
Din Søsters Blusel, din Faders Datter eller din Moders Datter, enten hun er født hjemme eller født ude, deres Blusel skal du ikke blotte.
10 “‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.
Din Sønnedatters eller din Datterdatters Blusel, deres Blusel skal du ikke blotte; thi de ere din Blusel.
11 “‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.
Din Stivmoders Datters Blusel, hun som er din Fader født og er din Søster, hendes Blusel skal du ikke blotte.
12 “‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.
Du skal ikke blotte din Faders Søsters Blusel, hun er din Faders næste Slægt.
13 “‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.
Du skal ikke blotte din Moders Søsters Blusel; thi hun er din Moders næste Slægt.
14 “‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.
Du skal ikke blotte din Farbroders Blusel; du skal ikke holde dig nær til hans Hustru; thi hun er din Faster.
15 “‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.
Du skal ikke blotte din Sønnekvindes Blusel; thi hun er din Søns Hustru, du skal ikke blotte hendes Blusel.
16 “‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.
Du skal ikke blotte din Broders Hustrus Blusel; det er din Broders Blusel.
17 “‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.
Du skal ikke blotte en Hustrus og hendes Datters Blusel; du skal ikke tage hendes Søns Datter eller hendes Datters Datter, at blotte hendes Blusel; thi de ere hendes næste Slægt; det er en Skændsel.
18 “‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.
Og du skal ikke tage en Hustru tillige med hendes Søster, til at vække hendes Skinsyge, at blotte hendes Blusel tillige med hins, medens hun lever.
19 “‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.
Og din Hustru i hendes Urenheds Svaghed, skal du ikke komme nær, til at blotte hendes Blusel.
20 “‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.
Og du skal ikke ligge hos din Næstes Hustru til at avle, til at blive uren ved hende.
21 “‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.
Og af dit Afkom skal du ikke lade nogen gaa igennem Ilden for Molek; og du skal ikke vanhellige din Guds Navn; jeg er Herren.
22 “‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.
Og du skal ikke ligge hos Mandkøn, som man ligger hos en Kvinde; det er en Vederstyggelighed.
23 “‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.
Og du skal ikke beblande dig med noget Kvæg til at besmittes ved det, og ingen Kvinde skal have at skaffe med noget Kvæg til Samleje; det er en Skændighed.
24 “‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera.
Gører eder ikke urene ved alt dette, thi ved alt dette ere Hedningerne, hvilke jeg uddriver for eder, blevne urene.
25 Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo.
Og Landet er blevet urent, og jeg har hjemsøgt dets Misgerning paa det; og Landet skal udspy sine Indbyggere.
26 Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi,
Og I skulle holde mine Skikke og mine Bud og ikke gøre nogen af alle disse Vederstyggeligheder, hverken den indfødte eller den fremmede, som opholder sig midt iblandt eder;
27 pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa.
thi dette Lands Folk, som var før eder, har gjort alle disse Vederstyggeligheder, og Landet er blevet urent;
28 Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.
at Landet ikke skal udspy eder, naar I gøre det urent, lige som det udspyr det Folk, som var før eder.
29 “‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake.
Thi hver den, som gør nogen af alle disse Vederstyggeligheder, de som gøre det, skulle udryddes midt af deres Folk.
30 Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Saa holder det, jeg vil have holdt, at I ikke gøre nogen af de vederstyggelige Skikke, som ere gjorte før eder, at I ikke skulle gøre eder urene ved dem; jeg er Herren eders Gud.

< Levitiko 18 >