< Levitiko 18 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
上主訓示梅瑟說:」
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
你告訴以色列子民說:我是上主你們的天主。
3 Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo.
你們不要仿效你們註過的埃及地的習慣,也不要仿效我正要領你們去的客納罕地的習慣,不要隨從他們的風俗;
4 Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
應執行我的規定,遵守我的法令,依照遵行:我,上主是你們的天主。
5 Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.
你們應遵守我的法令和規定;遵守的人必因此獲得生命:我是上主。婚姻的阻礙
6 “‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.
你們中任何人不可親近血親,去揭漏她的下體:我是上主。
7 “‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.
你不可揭露你父親得下體和你母親的下體:她是你的母親,不可揭露她的下體。
8 “‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.
你父親妻子的下體,你不可揭露,那是你父親的下體。
9 “‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.
你姊妹的下體,不論他是你父親的女兒,或你母親的女兒,或在家生的,或在外生的,你不可揭露她們的下體。
10 “‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.
你兒子的女兒,或你女兒的女兒的下體,你不可揭露,因為她們的下體是你們的下體。
11 “‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.
你不可揭露你父親妻子的女兒的下體,因為她是你父親所生,是你得姊妹,你不可揭露她的下體。
12 “‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.
你父親姊妹的下體,你不可揭露,因為她是你父親的骨肉。
13 “‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.
你母親姊妹的下體,你不可揭露,因為她是你母親的骨肉。
14 “‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.
你父親兄弟的下體,你不可揭露,也不可親近他的妻子;她是你的叔伯母。
15 “‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.
你兒媳的下體,你不可揭露。她是你兒子的妻子,你不可揭露她的下體。
16 “‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.
你兄弟妻子的下體,你不可揭露;那是你兄弟的下體。
17 “‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.
你不可揭露了一女人的下體又揭露她女兒;不可娶她兒子的女兒,或她女兒的女兒,揭露她的下體,她們都是她的血親:這是醜行。
18 “‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.
你不可娶一女人又娶他的姊妹,做她的情敵,在她活著的時候,揭露她姊妹的下體。[違犯貞潔的惡行]
19 “‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.
女人在月經不潔期中,你不可接近,揭露她的下體。
20 “‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.
你近人的妻子你不可與她同寢,為她所沾污。
21 “‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.
你不可使你任何一個子女經火祭獻給摩肋客,亦不可褻瀆你天主的名:我是上主。
22 “‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.
你不可與男人同寢,如同與女人同寢一樣:這是醜惡行為。
23 “‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.
你不可與任何獸類同寢,為牠所淫污,女人亦不可委身與走獸,同牠交合:這是逆性邪惡。
24 “‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera.
你們不可以任何這樣的事玷污自己,因為這些民足以這一些事玷污了自己,我正要由你們面前將他們驅逐;
25 Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo.
甚至連這地也玷汙了,所以我必追究這地上的罪惡,使這地吐棄地上的居民。
26 Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi,
至於你們,應遵守我的法令和規定;不論是本地人,或是寄居在你們中間的外方人,這樣醜惡的事,一件也不許做,
27 pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa.
因為在你們以前住在這地上的人,做過這一切醜惡的事,玷污了這地方。
28 Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.
希望這地不要因你們而再受到玷汙,將你們吐棄,如同吐棄了你們之前的民族。
29 “‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake.
因為,凡做任何一件這樣醜惡的事,這樣的人,都應由民間剷除。
30 Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
所以你們應遵守我的禁令,不可仿效你們以前的人所有的醜惡風俗,免得因此受到玷汙:我,上主是你們的天主。

< Levitiko 18 >