< Levitiko 17 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
И рече Господь к Моисею, глаголя:
2 “Uza Aaroni ndi ana ake, pamodzi ndi Aisraeli onse kuti, ‘Chimene Yehova walamula ndi ichi:
глаголи Аарону и сыном его и ко всем сыном Израилевым, и речеши к ним: сие слово еже заповеда Господь, глаголя:
3 Mwisraeli aliyense amene apha ngʼombe, mwana wankhosa kapena mbuzi mu msasa kapena kunja kwa msasa,
человек человек от сынов Израилевых или от пришелец, иже прилежат в вас, иже аще заколет телца или овцу или козу в полце, и иже аще заколет вне полка
4 mʼmalo mobwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova ndi kuyipereka kuti ikhale nsembe ya Yehova, ameneyo wapalamula mlandu wa magazi, wakhetsa magazi ndipo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
и пред двери скинии свидения не принесет, якоже сотворити е во всесожжение или спасение Господу приятно, в воню благовония: и иже аще заколет вне и пред двери скинии свидения не принесет его, яко принести дар Господу пред скинию Господню: и вменится человеку тому кровь: кровь пролиял, да потребится душа она от людий своих:
5 Izi zili choncho kuti Aisraeli azibwera ndi nyama zawo za nsembe zimene akanaphera ku malo kwina kulikonse. Aisraeli azibwera nazo nyamazo kwa Yehova, kwa wansembe wokhala pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo aziphere pomwepo kuti zikhale nsembe za chiyanjano.
яко да принесут сынове Израилевы жертвы своя, елики аще сии заколют на поли, и да принесут я ко Господу к дверем скинии свидения к жерцу, и пожрут я в жертву спасения Господу.
6 Wansembe awaze magazi ake pa guwa la Yehova limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo atenthe mafuta ake kuti atulutse fungo lokomera Yehova.
И да возлиет жрец кровь на олтарь окрест пред Господем у дверий скинии свидения: и да вознесет тук в воню благоухания Господу:
7 Motero asadzapherenso nsembe fano la mbuzi limene amachita nalo zadama. Limeneli ndi lamulo la muyaya kwa iwo ndi mibado ya mʼtsogolo.’”
и да не пожрут ктому жертв своих суетным, имже сами блудодействуют вслед их: законное вечное будет вам в роды вашя.
8 “Uwawuze kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo amene amakhala pakati pawo akapereka nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse
И речеши к ним: человек человек от сынов Израилевых или от сынов пришелцов прилежащих в вас, иже аще сотворит всесожжение или жертву,
9 popanda kubwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano kudzayipereka pamaso pa Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.’”
и к дверем скинии свидения не принесет сотворити е Господви, потребится душа та от людий своих.
10 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene adya magazi, ndidzamufulatira ndipo ndidzamuchotsa pakati pa anthu anzake.
И человек человек от сынов Израилевых или от пришелец прилежащих в вас, иже аще яст всякую кровь, и утвержу лице Мое на душу ядущую кровь, и погублю ю от людий своих:
11 Pakuti moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi, ndipo ndawupereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amachotsa machimo chifukwa moyo uli mʼmenemo.
зане душа всякия плоти кровь его есть, и Аз дах ю вам у олтаря умоляти от душах ваших: кровь бо его вместо души умолит.
12 Choncho ndikuwawuza Aisraeli kuti, ‘Pasapezeke aliyense wa inu wodya magazi, ngakhale mlendo wokhala pakati panu.’”
Сего ради рекох сыном Израилевым: всяка душа от вас да не снест крове, и пришлец прилежащий в вас да не снест крове.
13 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene amasaka ndi kupha nyama zakuthengo kapena mbalame zimene amadya, ataye magazi ake pansi ndi kuwakwirira ndi dothi,
И человек человек от сынов Израилевых или от пришлец прилежащих в вас, иже аще уловит ловитву зверя или птицу, еже ястся: пролиет кровь ея, и покрыет ю землею:
14 chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi ake. Nʼchifukwa chake ndinawawuza Aisraeli kuti, ‘Musamadye magazi a cholengedwa chilichonse, chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi. Aliyense wodya magaziwo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
душа бо всякия плоти кровь его есть. И рекох сыном Израилевым: крове всякия плоти да не снесте, яко душа всякия плоти кровь его есть: всяк ядый ю потребится:
15 “‘Munthu aliyense, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, amene amadya chilichonse chofa chokha, kapena chojiwa ndi zirombo, achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Kenaka adzakhala woyeretsedwa.
и всяка душа яже яст мертвечину или звероядину, от туземец или от пришелец, да исперет ризы своя и да омыет тело водою, и нечист будет до вечера, по сем же чист будет:
16 Koma ngati sachapa zovala zake ndi kusamba, adzasenzabe machimo ake.’”
аше же не исперет риз своих, ни омыет тела водою, то приимет беззаконие свое.