< Levitiko 17 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Adonai spoke to Moses [Drawn out], saying,
2 “Uza Aaroni ndi ana ake, pamodzi ndi Aisraeli onse kuti, ‘Chimene Yehova walamula ndi ichi:
“Speak to Aaron [Light-bringer], and to his sons, and to all the children of Israel [God prevails], and say to them: ‘This is the thing which Adonai has enjoined,
3 Mwisraeli aliyense amene apha ngʼombe, mwana wankhosa kapena mbuzi mu msasa kapena kunja kwa msasa,
Whatever man there is of the house of Israel [God prevails], who kills a bull, or lamb, or goat, in the camp, or who kills it outside the camp,
4 mʼmalo mobwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova ndi kuyipereka kuti ikhale nsembe ya Yehova, ameneyo wapalamula mlandu wa magazi, wakhetsa magazi ndipo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
and has not brought it to the door of the Tent of Meeting, to offer it as an offering to Adonai before Adonai’s tabernacle: blood shall be imputed to that man. He has shed blood; and that man shall be cut off from among his people.
5 Izi zili choncho kuti Aisraeli azibwera ndi nyama zawo za nsembe zimene akanaphera ku malo kwina kulikonse. Aisraeli azibwera nazo nyamazo kwa Yehova, kwa wansembe wokhala pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo aziphere pomwepo kuti zikhale nsembe za chiyanjano.
This is to the end that the children of Israel [God prevails] may bring their sacrifices, which they sacrifice in the open field, that they may bring them to Adonai, to the door of the Tent of Meeting, to the priest, and sacrifice them for sacrifices of peace offerings to Adonai.
6 Wansembe awaze magazi ake pa guwa la Yehova limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo atenthe mafuta ake kuti atulutse fungo lokomera Yehova.
The priest shall sprinkle the blood on Adonai’s altar at the door of the Tent of Meeting, and burn the fat for a pleasant aroma to Adonai.
7 Motero asadzapherenso nsembe fano la mbuzi limene amachita nalo zadama. Limeneli ndi lamulo la muyaya kwa iwo ndi mibado ya mʼtsogolo.’”
They shall no more sacrifice their sacrifices to the goat idols, after which they play the prostitute. This shall be a regulation forever to them throughout their generations.’
8 “Uwawuze kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo amene amakhala pakati pawo akapereka nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse
“You shall say to them, ‘Any man there is of the house of Israel [God prevails], or of the strangers who live as foreigners among them, who offers a burnt offering or sacrifice,
9 popanda kubwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano kudzayipereka pamaso pa Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.’”
and does not bring it to the door of the Tent of Meeting, to sacrifice it to Adonai; that man shall be cut off from his people.
10 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene adya magazi, ndidzamufulatira ndipo ndidzamuchotsa pakati pa anthu anzake.
“‘Any man of the house of Israel [God prevails], or of the strangers who live as foreigners among them, who eats any kind of blood, I will set my face against that soul who eats blood, and will cut him off from among his people.
11 Pakuti moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi, ndipo ndawupereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amachotsa machimo chifukwa moyo uli mʼmenemo.
For the life of the flesh is in the blood; and I have given it to you on the altar to make atonement for your souls: for it is the blood that makes atonement by reason of the life.
12 Choncho ndikuwawuza Aisraeli kuti, ‘Pasapezeke aliyense wa inu wodya magazi, ngakhale mlendo wokhala pakati panu.’”
Therefore I have said to the children of Israel [God prevails], “No person among you may eat blood, nor may any stranger who lives as a foreigner among you eat blood.”
13 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene amasaka ndi kupha nyama zakuthengo kapena mbalame zimene amadya, ataye magazi ake pansi ndi kuwakwirira ndi dothi,
“‘Whatever man there is of the children of Israel [God prevails], or of the strangers who live as foreigners among them, who takes in hunting any animal or bird that may be eaten; he shall pour out its blood, and cover it with dust.
14 chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi ake. Nʼchifukwa chake ndinawawuza Aisraeli kuti, ‘Musamadye magazi a cholengedwa chilichonse, chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi. Aliyense wodya magaziwo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
For as to the life of all flesh, its blood is with its life: therefore I said to the children of Israel [God prevails], “You shall not eat the blood of any kind of flesh; for the life of all flesh is its blood. Whoever eats it shall be cut off.”
15 “‘Munthu aliyense, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, amene amadya chilichonse chofa chokha, kapena chojiwa ndi zirombo, achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Kenaka adzakhala woyeretsedwa.
“‘Every person that eats what dies of itself, or that which is torn by animals, whether he is native-born or a foreigner, he shall wash his clothes, and bathe himself in water, and be unclean until the evening: then he shall be clean.
16 Koma ngati sachapa zovala zake ndi kusamba, adzasenzabe machimo ake.’”
But if he does not wash them, or bathe his flesh, then he shall bear his iniquity.’”

< Levitiko 17 >