< Levitiko 17 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke to Moses, saying,
2 “Uza Aaroni ndi ana ake, pamodzi ndi Aisraeli onse kuti, ‘Chimene Yehova walamula ndi ichi:
Speak to Aaron and to his sons, and to all the children of Israel, and thou shalt say to them, This is the word which the Lord has commanded, saying,
3 Mwisraeli aliyense amene apha ngʼombe, mwana wankhosa kapena mbuzi mu msasa kapena kunja kwa msasa,
Every man of the children of Israel, or of the strangers abiding among you, who shall kill a calf, or a sheep, or a goat in the camp, or who shall kill it out of the camp,
4 mʼmalo mobwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova ndi kuyipereka kuti ikhale nsembe ya Yehova, ameneyo wapalamula mlandu wa magazi, wakhetsa magazi ndipo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
and shall not bring it to the door of the tabernacle of witness, so as to sacrifice it for a whole-burnt-offering or peace-offering to the Lord to be acceptable for a sweet-smelling savour: and whosoever shall slay it without, and shall not bring it to the door of the tabernacle of witness, so as to offer it as a gift to the Lord before the tabernacle of the Lord; blood shall be imputed to that man, he has shed blood; that soul shall be cut off from his people.
5 Izi zili choncho kuti Aisraeli azibwera ndi nyama zawo za nsembe zimene akanaphera ku malo kwina kulikonse. Aisraeli azibwera nazo nyamazo kwa Yehova, kwa wansembe wokhala pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo aziphere pomwepo kuti zikhale nsembe za chiyanjano.
That the children of Israel may offer their sacrifices, all that they shall slay in the fields, and bring them to the Lord unto the doors of the tabernacle of witness to the priest, and they shall sacrifice them as a peace-offering to the Lord.
6 Wansembe awaze magazi ake pa guwa la Yehova limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo atenthe mafuta ake kuti atulutse fungo lokomera Yehova.
And the priest shall pour the blood on the altar round about before the Lord by the doors of the tabernacle of witness, and shall offer the fat for a sweet-smelling savour to the Lord.
7 Motero asadzapherenso nsembe fano la mbuzi limene amachita nalo zadama. Limeneli ndi lamulo la muyaya kwa iwo ndi mibado ya mʼtsogolo.’”
And they shall no longer offer their sacrifices to vain [gods] after which they go a whoring; it shall be a perpetual statute to you for your generations.
8 “Uwawuze kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo amene amakhala pakati pawo akapereka nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse
And thou shalt say to them, Whatever man of the children of Israel, or of the sons of the proselytes abiding among you, shall offer a whole-burnt-offering or a sacrifice,
9 popanda kubwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano kudzayipereka pamaso pa Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.’”
and shall not bring it to the door of the tabernacle of witness to sacrifice it to the Lord, that man shall be destroyed from among his people.
10 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene adya magazi, ndidzamufulatira ndipo ndidzamuchotsa pakati pa anthu anzake.
And whatever man of the children of Israel, or of the strangers abiding among you, shall eat any blood, I will even set my face against that soul that eats blood, and will destroy it from its people.
11 Pakuti moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi, ndipo ndawupereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amachotsa machimo chifukwa moyo uli mʼmenemo.
For the life of flesh is its blood, and I have given it to you on the altar to make atonement for your souls; for its blood shall make atonement for the soul.
12 Choncho ndikuwawuza Aisraeli kuti, ‘Pasapezeke aliyense wa inu wodya magazi, ngakhale mlendo wokhala pakati panu.’”
Therefore I said to the children of Israel, No soul of you shall eat blood, and the stranger that abides among you shall not eat blood.
13 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene amasaka ndi kupha nyama zakuthengo kapena mbalame zimene amadya, ataye magazi ake pansi ndi kuwakwirira ndi dothi,
And whatever man of the children of Israel, or of the strangers abiding among you shall take any animal in hunting, beast, or bird, which is eaten, then shall he pour out the blood, and cover it in the dust.
14 chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi ake. Nʼchifukwa chake ndinawawuza Aisraeli kuti, ‘Musamadye magazi a cholengedwa chilichonse, chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi. Aliyense wodya magaziwo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
For the blood of all flesh is its life; and I said to the children of Israel, Ye shall not eat the blood of any flesh, for the life of all flesh is its blood: every one that eats it shall be destroyed.
15 “‘Munthu aliyense, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, amene amadya chilichonse chofa chokha, kapena chojiwa ndi zirombo, achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Kenaka adzakhala woyeretsedwa.
And every soul which eats that which has died of itself, or is taken of beasts, either among the natives or among the strangers, shall wash his garments, and bathe himself in water, and shall be unclean until evening: then shall he be clean.
16 Koma ngati sachapa zovala zake ndi kusamba, adzasenzabe machimo ake.’”
But if he do not wash his garments, and do not bathe his body in water, then shall he bear his iniquity.