< Levitiko 17 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
HERREN talede til Moses og sagde:
2 “Uza Aaroni ndi ana ake, pamodzi ndi Aisraeli onse kuti, ‘Chimene Yehova walamula ndi ichi:
Tal til Aron og hans Sønner og alle Israeliterne og sig til dem: Dette har HERREN påbudt:
3 Mwisraeli aliyense amene apha ngʼombe, mwana wankhosa kapena mbuzi mu msasa kapena kunja kwa msasa,
Om nogen af Israels Hus slagter et Stykke Hornkvæg, et Får eller en Ged i Lejren, eller han slagter dem uden for Lejren,
4 mʼmalo mobwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova ndi kuyipereka kuti ikhale nsembe ya Yehova, ameneyo wapalamula mlandu wa magazi, wakhetsa magazi ndipo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
uden at bringe dem hen til Åbenbaringsteltets Indgang for at bringe HERREN en Offergave foran HERRENs Bolig, da skal dette tillegnes den Mand som Blodskyld; han har udgydt Blod, og den Mand skal udryddes af sit Folk.
5 Izi zili choncho kuti Aisraeli azibwera ndi nyama zawo za nsembe zimene akanaphera ku malo kwina kulikonse. Aisraeli azibwera nazo nyamazo kwa Yehova, kwa wansembe wokhala pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo aziphere pomwepo kuti zikhale nsembe za chiyanjano.
Dette er anordnet, for at Israeliterne skal bringe deres Slagtofre, som de slagter ude på Marken, til HERREN, til Åbenbaringsteltets Indgang, til Præsten, og ofre dem som Takofre til HERREN.
6 Wansembe awaze magazi ake pa guwa la Yehova limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo atenthe mafuta ake kuti atulutse fungo lokomera Yehova.
Præsten skal da sprænge Blodet på HERRENs Alter ved Indgangen til Åbenbaringsteltet og bringe Fedtet som Røgoffer, en liflig Duft for HERREN.
7 Motero asadzapherenso nsembe fano la mbuzi limene amachita nalo zadama. Limeneli ndi lamulo la muyaya kwa iwo ndi mibado ya mʼtsogolo.’”
Og de må ikke mere ofre deres Slagtofre til Bukketroldene, som de boler med. Det skal være en evig gyldig Anordning for dem fra Slægt til Slægt!
8 “Uwawuze kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo amene amakhala pakati pawo akapereka nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse
Og du skal sige til dem: Om nogen af Israels Hus eller de fremmede, der bor iblandt eder, ofrer et Brændoffer eller Slagtoffer
9 popanda kubwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano kudzayipereka pamaso pa Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.’”
og ikke bringer det hen til Åbenbaringsteltets Indgang for at ofre det til HERREN, da skal den Mand udryddes af sin Slægt.
10 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene adya magazi, ndidzamufulatira ndipo ndidzamuchotsa pakati pa anthu anzake.
Om nogen af Israels Hus eller af de fremmede, der bor iblandt dem, nyder noget Blod, så vender jeg mit Åsyn mod den, der nyder Blodet, og udrydde1 ham af hans Folk.
11 Pakuti moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi, ndipo ndawupereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amachotsa machimo chifukwa moyo uli mʼmenemo.
Thi Kødets Sjæl er i Blodet, og jeg har givet eder det til Brug på Alteret til at skaffe eders Sjæle Soning; thi det er Blodet, som skaffer Soning, fordi det er Sjælen.
12 Choncho ndikuwawuza Aisraeli kuti, ‘Pasapezeke aliyense wa inu wodya magazi, ngakhale mlendo wokhala pakati panu.’”
Derfor har jeg sagt til Israeliterne: Ingen af eder må nyde Blod; heller ikke den fremmede, der bor iblandt eder, må nyde Blod.
13 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene amasaka ndi kupha nyama zakuthengo kapena mbalame zimene amadya, ataye magazi ake pansi ndi kuwakwirira ndi dothi,
Om nogen af Israeliterne eller af de fremmede, der bor iblandt dem, nedlægger et Stykke Vildt eller en Fugl af den Slags, der må spises, da skal han lade Blodet løbe ud og dække det med Jord.
14 chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi ake. Nʼchifukwa chake ndinawawuza Aisraeli kuti, ‘Musamadye magazi a cholengedwa chilichonse, chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi. Aliyense wodya magaziwo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
Thi om alt Køds Sjæl gælder det, at dets Blod er dets Sjæl; derfor har jeg sagt til Israeliterne: I må ikke nyde Blodet af noget som helst Kød, thi alt Køds Sjæl er dets Blod; enhver, der nyder det, skal udryddes.
15 “‘Munthu aliyense, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, amene amadya chilichonse chofa chokha, kapena chojiwa ndi zirombo, achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Kenaka adzakhala woyeretsedwa.
Enhver, der spiser seldøde eller sønderrevne Dyr, det være sig en indfødt eller en fremmed, skal tvætte sine Klæder og bade sig i Vand og være uren til Aften; så er han ren.
16 Koma ngati sachapa zovala zake ndi kusamba, adzasenzabe machimo ake.’”
Men hvis han ikke tvætter sine Klæder og bader sig, skal han undgælde for sin Brøde.