< Levitiko 17 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
I mluvil Hospodin Mojžíšovi, řka:
2 “Uza Aaroni ndi ana ake, pamodzi ndi Aisraeli onse kuti, ‘Chimene Yehova walamula ndi ichi:
Mluv k Aronovi a synům jeho i ke všechněm synům Izraelským, a rci jim: Tato jest věc, kterouž přikázal Hospodin, řka:
3 Mwisraeli aliyense amene apha ngʼombe, mwana wankhosa kapena mbuzi mu msasa kapena kunja kwa msasa,
Kdož by koli z domu Izraelského zabil vola aneb beránka, neb kozu, buď mezi stany, aneb kdož by zabil vně za stany,
4 mʼmalo mobwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova ndi kuyipereka kuti ikhale nsembe ya Yehova, ameneyo wapalamula mlandu wa magazi, wakhetsa magazi ndipo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
A ke dveřím stánku úmluvy nepřivedl by ho, aby obětoval obět Hospodinu před příbytkem Hospodinovým: vinen bude krví, nebo krev vylil; protož vyhlazen bude muž ten z prostředku lidu svého.
5 Izi zili choncho kuti Aisraeli azibwera ndi nyama zawo za nsembe zimene akanaphera ku malo kwina kulikonse. Aisraeli azibwera nazo nyamazo kwa Yehova, kwa wansembe wokhala pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo aziphere pomwepo kuti zikhale nsembe za chiyanjano.
Přivedou tedy synové Izraelští oběti své, kteréž by na poli zabíjeti chtěli, přivedou je, pravím, k Hospodinu ke dveřím stánku úmluvy, k knězi, a obětovati budou oběti pokojné Hospodinu.
6 Wansembe awaze magazi ake pa guwa la Yehova limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo atenthe mafuta ake kuti atulutse fungo lokomera Yehova.
A pokropí kněz krví na oltáři Hospodinovu u dveří stánku úmluvy, a páliti bude tuk u vůni líbeznou Hospodinu.
7 Motero asadzapherenso nsembe fano la mbuzi limene amachita nalo zadama. Limeneli ndi lamulo la muyaya kwa iwo ndi mibado ya mʼtsogolo.’”
A nikoli více nebudou obětovati obětí svých ďáblům, po nichžto odcházejíce, oni smilní. Zákon tento bude jim věčný i všechněm potomkům jejich.
8 “Uwawuze kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo amene amakhala pakati pawo akapereka nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse
Protož povíš jim: Kdož by koli z domu Izraelského aneb z příchozích, kteříž by pohostinu byli mezi vámi, obětoval zápal aneb jinou obět,
9 popanda kubwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano kudzayipereka pamaso pa Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.’”
A ke dveřím stánku úmluvy nepřivedl by jí, aby ji obětoval Hospodinu; tedy vyhlazen bude člověk ten z lidu svého.
10 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene adya magazi, ndidzamufulatira ndipo ndidzamuchotsa pakati pa anthu anzake.
A kdož by koli z domu Izraelského aneb z příchozích, kteříž jsou pohostinu mezi nimi, jedl jakou krev: postavím tvář svou proti člověku tomu, a vyhladím jej z prostředku lidu jeho.
11 Pakuti moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi, ndipo ndawupereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amachotsa machimo chifukwa moyo uli mʼmenemo.
Nebo duše všelikého těla ve krvi jest, já pak oddal jsem vám ji k oltáři, k očišťování duší vašich. Nebo sama krev na duši očišťuje.
12 Choncho ndikuwawuza Aisraeli kuti, ‘Pasapezeke aliyense wa inu wodya magazi, ngakhale mlendo wokhala pakati panu.’”
Protož řekl jsem synům Izraelským: Nižádný z vás nebude jísti krve; ani příchozí, kterýž pohostinu jest mezi vámi, nebude krve jísti.
13 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene amasaka ndi kupha nyama zakuthengo kapena mbalame zimene amadya, ataye magazi ake pansi ndi kuwakwirira ndi dothi,
A kdož by koli z synů Izraelských aneb z příchozích, kteříž jsou pohostinu mezi vámi, honě, ulovil zvíře aneb ptáka, což se jísti může, tedy vycedí krev jeho a zasype ji prstí.
14 chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi ake. Nʼchifukwa chake ndinawawuza Aisraeli kuti, ‘Musamadye magazi a cholengedwa chilichonse, chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi. Aliyense wodya magaziwo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
Nebo duše všelikého těla jest krev jeho, kteráž jest v duši jeho. Protož jsem pověděl synům Izraelským: Krve žádného těla jísti nebudete, nebo duše všelikého těla jest krev jeho; kdož by koli jedl ji, vyhlazen bude.
15 “‘Munthu aliyense, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, amene amadya chilichonse chofa chokha, kapena chojiwa ndi zirombo, achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Kenaka adzakhala woyeretsedwa.
Kdož by pak koli jedl tělo mrtvé aneb udávené, buď on doma zrozený aneb příchozí: zpéře roucha svá, a umyje se vodou, a nečistý bude až do večera, potom pak čistý bude.
16 Koma ngati sachapa zovala zake ndi kusamba, adzasenzabe machimo ake.’”
A pakli nezpéře roucha svého, a těla svého neumyje, tedy ponese nepravost svou.

< Levitiko 17 >